< Genesis 49 >

1 Pambuyo pake Yakobo anayitanitsa ana ake aamuna nati: Sonkhanani pamodzi kuti ndikuwuzeni zimene zidzakuchitikireni mʼmasiku a mʼtsogolo.
Then Jacob called for his sons, and said: “Gather yourselves together, that I may tell you what will happen to you in the future.
2 “Bwerani ndipo imvani mawu anga, inu ana a Yakobo; mverani abambo anu Israeli.
Assemble yourselves and listen, you sons of Jacob. Listen to Israel, your father.
3 “Rubeni, ndiwe woyamba kubadwa; mphamvu yanga ndiponso chizindikiro choyamba cha mphamvu zanga, wopambana pa ulemerero ndi mphamvu.
Reuben, you are my firstborn, my might, and the beginning of my strength, outstanding in dignity, and outstanding in power.
4 Wokokoma ngati madzi a chigumula, koma sudzakhalanso wopambana, iwe unagona pa bedi la abambo ako, ndithu unayipitsa bedi la mdzakazi wake.
Uncontrollable as rushing water, you will not have the preeminence, because you went up to your father's bed. Then you defiled it; you went up to my couch.
5 “Simeoni ndi Levi ndi pachibale pawo, anachitira nkhanza anthu amene anachita nawo pangano.
Simeon and Levi are brothers. Weapons of violence are their swords.
6 Iwe moyo wanga, usakhale nawo pa misonkhano yawo ya mseri, kapena kugwirizana nawo mʼmabwalo awo, pakuti anapha anthu mu mkwiyo wawo ndipo anapundula ngʼombe zamphongo monga kunawakomera.
O my soul, do not come into their council; do not join in their meetings, for my heart has too much honor for that. For in their anger they killed men. It was for pleasure that they hamstrung oxen.
7 Matemberero awagwere chifukwa cha mkwiyo wawo woopsa chonchi ndi ukali wawo wankhanza choterewu! Ine ndidzawabalalitsa mʼdziko la Yakobo ndi kuwamwaza iwo mʼdziko la Israeli.
May their anger be cursed, for it was fierce—and their fury, for it was cruel. I will divide them in Jacob and scatter them in Israel.
8 “Yuda, ndiwe amene abale ako adzatamanda; dzanja lako lidzagwira pa khosi pa adani ako; abale ako adzakugwadira iwe.
Judah, your brothers will praise you. Your hand will be on the neck of your enemies. Your father's sons will bow down before you.
9 Yuda ali ngati mwana wa mkango; umabwerera ku malo ako ndi zofunkha, mwana wanga. Monga mkango, amadziwongola ndi kugona pansi, ndipo ngati mkango waukazi, ndani angalimbe mtima kumudzutsa?
Judah is a lion's cub. My son, you have gone up from your victims. He stooped down, he crouched like a lion, like a lioness. Who would dare to awaken him?
10 Ndodo yaufumu sidzachoka mwa Yuda, udzawupanirira ulamuliro motero kuti palibe amene adzawuchotse, mpaka mwini wake weniweni atabwera ndipo mitundu yonse ya anthu idzamumvera.
The scepter will not depart from Judah, nor the ruler's staff from between his feet, until Shiloh comes. The nations will obey him.
11 Ndiye amene amamangirira bulu wake wamkazi kumtengo wa mpesa, ndi mwana wa bulu ku nthambi ya mpesa wabwino. Ndi iye amene amachapa zovala zake mu vinyo; ndi mkanjo wake mu vinyo wofiira ngati magazi.
Binding his donkey to the vine, and his donkey's colt to the choice vine, he has washed his garments in wine, and his robe in the blood of grapes.
12 Maso ake adzakhala akuda chifukwa cha vinyo, mano ake woyera chifukwa cha mkaka.
His eyes will be as dark as wine, and his teeth as white as milk.
13 “Zebuloni adzakhala mʼmphepete mwa nyanja; adzakhala pa dooko la sitima zapamadzi; malire ake adzafika ku Sidoni.
Zebulun will live by the shore of the sea. He will be a harbor for ships, and his border will extend to Sidon.
14 “Isakara ali ngati bulu wamphamvu wogona pansi pakati pa makola.
Issachar is a strong donkey, lying down between the sheepfolds.
15 Ataona ubwino wake wa pamalo pake popumira ndi kukongola kwa dziko lake, iye anaweramutsa msana kuti anyamule katundu wake ndipo anasanduka wogwira ntchito ya ukapolo.
He sees a good resting place and the pleasant land. He will bend his shoulder to the burden and become a servant for the task.
16 “Dani adzaweruza mwachilungamo anthu ake monga limodzi mwa mafuko a anthu a mu Israeli.
Dan will judge his people as one of the tribes of Israel.
17 Dani adzakhala ngati njoka ya mʼmphepete mwa msewu, songo yokhala mʼnjira imene imaluma chidendene cha kavalo kuti wokwerapoyo agwe chagada.
Dan will be a snake beside the road, a poisonous snake in the path that bites the horse's heels, so that his rider falls backward.
18 “Ndikuyembekeza chipulumutso chanu Yehova.
I wait for your salvation, Yahweh.
19 “Gadi adzachitidwa chiwembu ndi gulu la amaliwongo, koma iye adzawathamangitsa.
Gad—raiders will attack him, but he will attack them at their heels.
20 “Dziko la Aseri lidzabereka chakudya chokoma, ndipo iye adzapereka chakudya kwa mafumu.
Asher's food will be rich, and he will provide royal delicacies.
21 “Nafutali ali ngati mbawala yayikazi yokhala ndi ana okongola kwambiri.
Naphtali is a doe let loose; he will have beautiful fawns.
22 “Yosefe ali ngati mtengo wobereka zipatso, mtengo wobereka zipatso pafupi ndi kasupe, nthambi zake zimayanga pa chipupa cha mwala.
Joseph is a fruitful bough, a fruitful bough near a spring, whose branches climb over the wall.
23 Alenje a uta anamuchita chiwembu mwankhanza; anamuthamangitsa ndi mauta awo.
The archers will attack him and shoot at him and harass him.
24 Koma uta wake sunagwedezeke, ndi manja ake amphamvu aja analimbika, chifukwa cha mphamvu za Mulungu Wamphamvu wa Yakobo, chifukwa ali Mʼbusa ndi Thanthwe la Israeli.
But his bow will remain steady, and his hands will be skillful because of the hands of the Mighty One of Jacob, because of the name of the Shepherd, the Rock of Israel.
25 Chifukwa cha Mulungu wa makolo ako amene amakuthandiza; chifukwa cha Mulungu Wamphamvu, amene amakudalitsa ndi mvula yochokera kumwamba, ndi madzi otumphuka pansi pa nthaka, ndipo amakudalitsa pokupatsa ana ambiri ndi ngʼombe zambiri.
The God of your father will help you and the Almighty God will bless you with blessings of the sky above, blessings of the deep that lies beneath, and blessings of the breasts and womb.
26 Madalitso a kholo lako ndi amphamvu kuposa madalitso a mapiri akale oposa zabwino za ku zitunda zamgonagona. Zonse izi zikhale pamutu pa Yosefe, pa mphumi pa wopatulika uja amene anapatulidwa pakati pa abale ake.
The blessings of your father are greater than the blessings of the ancient mountains or the desirable things of the ancient hills. May they be on the head of Joseph, even upon the crown of the head of the prince of his brothers.
27 “Benjamini ali ngati mʼmbulu wolusa; umene mmawa umapha ndi kudya zofunkha, ndipo madzulo umagawa zofunkhazo,”
Benjamin is a hungry wolf. In the morning he will devour the prey, and in the evening he will divide the plunder.”
28 Onse awa ndi mafuko khumi ndi awiri a Israeli, ndipo zimenezi ndi zomwe abambo awo ananena pamene anawadalitsa, kuwapatsa aliyense madalitso ake womuyenera iye.
These are the twelve tribes of Israel. This is what their father said to them when he blessed them. Each one he blessed with an appropriate blessing.
29 Kenaka Yakobo analamula ana ake nati: “Ine ndatsala pangʼono kufa. Tsono mukandiyike pamodzi ndi makolo anga mʼphanga la mʼmunda wa Efroni Mhiti.
Then he instructed them and said to them, “I am about to go to my people. Bury me with my forefathers in the cave that is in the field of Ephron the Hittite,
30 Ili ndi phanga la mʼmunda wa Makipela, pafupi ndi Mamre mʼdziko la Kanaani. Abrahamu anagula phangalo pamodzi ndi munda womwe kwa Efroni Mhiti kuti pakhale manda.
in the cave that is in the field of Machpelah, which is near Mamre in the land of Canaan, the field that Abraham bought for a burial place from Ephron the Hittite.
31 Kumeneko kunayikidwa Abrahamu ndi mkazi wake Sara, Isake ndi mkazi wake Rebeka ndipo ndinayikakonso Leya.
There they buried Abraham and Sarah his wife; there they buried Isaac and Rebekah his wife; and there I buried Leah.
32 Munda ndi manda amene ali mʼmenemo zinagulidwa kwa Ahiti.”
The field and the cave that is in it were purchased from the people of Heth.”
33 Yakobo atamaliza kupereka malangizo kwa ana ake, anabwezera miyendo yake pa bedi, namwalira ndipo anakakhala ndi anthu a mtundu wake.
When Jacob finished these instructions to his sons, he pulled his feet into the bed, breathed his last, and went to his people.

< Genesis 49 >