< Genesis 43 >

1 Njala inakula kwambiri mʼdzikomo.
And the famine was severe in the land.
2 Tsono atatha kudya tirigu yense amene anakatenga ku Igupto, Yakobo anati kwa ana ake aja, “Pitani kuti mukatigulire chakudya china pangʼono.”
And it came to pass, when they had eaten up the grain which they had brought out of Egypt, their father said to them, Go again, buy us a little food.
3 Koma Yuda anati kwa iye, “Munthu uja anatichenjeza monenetsa kuti, ‘Simudzandionanso ine pokhapokha mutabwera ndi mngʼono wanu.’
And Judah spoke to him, saying, The man solemnly protested to us, saying, Ye shall not see my face unless your brother be with you.
4 Mukalola kuti mngʼono wathuyu apite nafe, ndiye ife tidzapita kukakugulirani chakudya.
If thou will send our brother with us, we will go down and buy food for thee,
5 Koma mukapanda kumulola, ife sitipita, chifukwa munthuyo anatiwuza kuti, ‘Simudzandionanso pokhapokha mutabwera ndi mngʼono wanuyo.’”
but if thou will not send him, we will not go down. For the man said to us, Ye shall not see my face unless your brother be with you.
6 Tsono Israeli anafunsa kuti, “Bwanji inu munandiputira mavuto oterewa pomuwuza munthuyo kuti muli ndi mʼbale wanu wina?”
And Israel said, Why did ye deal so ill with me, as to tell the man whether ye had yet a brother?
7 Iwo anayankha, “Munthuyo ankangofunsafunsa za ife ndi za banja lathu. Iye anatifunsa kuti, ‘Kodi abambo anu akanali ndi moyo? Kodi muli ndi mʼbale wanu wina?’ Ife tinkangoyankha mafunso ake. Ife tikanadziwa bwanji kuti adzanena kuti, ‘Mubwere naye kuno mʼbale wanu’?”
And they said, The man asked diligently concerning ourselves, and concerning our kindred, saying, Is your father yet alive? Have ye another brother? And we told him according to the tenor of these words. Could we in any way know that he would say, Bring your brother down?
8 Ndipo Yuda anati kwa Israeli abambo ake, “Muloleni mnyamatayo apite ndi ine, ndipo tinyamuka nthawi yomweyo, kuti ife ndi inu pamodzi ndi ana athu tikhale ndi moyo.
And Judah said to Israel his father, Send the young man with me, and we will arise and go, that we may live, and not die, both we, and thou, and also our little ones.
9 Ine ndidzipereka kuti ndikhale chikole cha moyo wa mnyamatayu. Ine ndidzamuteteza. Ngati sindibwera naye ndi kumupereka kwa inu, ndidzakhala wolakwa pamaso panu moyo wanga wonse.
I will be surety for him, of my hand shall thou require him. If I do not bring him to thee, and set him before thee, then let me bear the blame forever.
10 Mmene zililimu, tikanapanda kuchedwa, bwenzi titapita ndi kubwerako kawiri.”
For unless we had lingered, surely we would have now returned a second time.
11 Tsono abambo awo Israeli anawawuza kuti, “Ngati pafunika kutero, ndiye muchite izi: Ikanimo zipatso zabwino kwambiri za dziko lino mʼmatumba mwanu ndi kumutengera munthuyo ngati mphatso. Mumutengere mafuta wopaka pangʼono, uchi pangʼono, mafuta wonunkhiritsa chakudya, mule, mtedza ndi alimoni.
And their father Israel said to them, If it be so now, do this: Take of the choice fruits of the land in your vessels, and carry a present down to the man, a little balm, and a little honey, spicery and myrrh, nuts, and almonds.
12 Mutenge ndalama zokwanira. Ndalama zina nʼzokamubwezera zija anakuyikirani mʼmatumba anu zija. Mwina anangolakwitsa.
And take double money in your hand, and the money that was returned in the mouth of your sacks carry again in your hand. Perhaps it was an oversight.
13 Mutengeninso mngʼono wanuyu ndi kubwerera kwa munthuyo msanga.
Also take your brother, and arise, go again to the man.
14 Ndipo Mulungu Wamphamvuzonse akuchitireni chifundo pamaso pa munthuyo kuti akamulole mʼbale wanu wina uja ndi Benjamini kuti abwerere ndi inu. Kukakhala kulira, ndine wolira basi.”
And God Almighty give you mercy before the man, that he may release to you your other brother and Benjamin. And if I be bereaved of my sons, I am bereaved.
15 Choncho abale aja anatenga mphatso, ndalama zokwanira ndi Benjamininso. Iwo anafulumira kupita ku Igupto ndipo anakaonekera kwa Yosefe.
And the men took that present, and they took double money in their hand, and Benjamin, and rose up, and went down to Egypt, and stood before Joseph.
16 Yosefe ataona Benjamini ali pamodzi ndi abale ake, anati kwa wantchito wa mʼnyumba mwake, “Atengereni anthu awa ku nyumba kwanga, ndipo uphe nyama ndi kukonza bwino chakudya popeza amenewa adya ndi ine masana ano.”
And when Joseph saw Benjamin with them, he said to the steward of his house, Bring the men into the house, and kill, and make ready, for the men shall dine with me at noon.
17 Wantchitoyo anachita monga momwe Yosefe ananenera, ndipo anawatengera abale aja ku nyumba kwa Yosefe.
And the man did as Joseph bade, and the man brought the men to Joseph's house.
18 Tsono anthu aja anachita mantha ataona kuti akuwatengera ku nyumba kwa Yosefe. Mʼmaganizo awo ankanena kuti, “Atibweretsa kuno chifukwa cha ndalama zija zinabwezeredwa mʼmatumba athu poyamba paja. Ameneyu akufuna kuti atipanikize ndi kutigwira ukapolo natilanda abulu athu.”
And the men were afraid, because they were brought to Joseph's house, and they said, We are brought in because of the money that was returned in our sacks at the first time, that he may seek occasion against us, and fall upon us, and take us for bondmen, and our donkeys.
19 Choncho atafika pa khomo la nyumba ya Yosefe anamuyandikira wantchito wa Yosefe nayankhula naye kuti,
And they came near to the steward of Joseph's house, and they spoke to him at the door of the house,
20 “Pepani mbuye wathu, ife tinabweranso ulendo woyamba kudzagula chakudya
and said, Oh, my lord, we indeed came down at the first time to buy food.
21 koma titafika pa malo ena kuti tigone, tinatsekula matumba athu ndipo aliyense wa ife anapeza ndalama zake momwe zinalili zili pakamwa pa thumba lake. Ndiye tabwerera nazo.
And it came to pass, when we came to the lodging place, that we opened our sacks, and, behold, every man's money was in the mouth of his sack, our money in full weight. And we have brought it again in our hand.
22 Tabweretsanso ndalama zina kuti tigule chakudya. Sitikudziwa kuti kaya ndani anayika ndalamazo mʼmatumba athu.”
And we have brought other money down in our hand to buy food. We know not who put our money in our sacks.
23 Koma iye anati, “Mitima yanu ikhale pansi ndipo musachite mantha. Mulungu wanu, Mulungu wa abambo anu, anakuyikirani chumacho mʼmatumba anu. Ine ndinalandira ndalama zanu.” Ndipo anakawatulutsira Simeoni.
And he said, Peace be to you, fear not. Your God, and the God of your father, has given you treasure in your sacks. I had your money. And he brought Simeon out to them.
24 Wantchito uja anawalowetsa anthuwo mʼnyumba ya Yosefe, nawapatsa madzi kuti asambe mapazi awo. Anadyetsanso abulu awo.
And the man brought the men into Joseph's house, and gave them water, and they washed their feet. And he gave their donkeys provender.
25 Abale aja anakonzeratu mphatso zawo zija kuti adzapereke kwa Yosefe, popeza anamva kuti Yosefe adzadya komweko masana.
And they made ready the present against Joseph's coming at noon, for they heard that they should eat bread there.
26 Yosefe atafika ku nyumbako, iwo anapereka mphatso zija namuweramira pansi.
And when Joseph came home, they brought him the present which was in their hand into the house, and bowed down themselves to him to the earth.
27 Yosefe anawafunsa za moyo wawo kenaka anati, “Kodi abambo anu wokalamba amene munkandiwuza aja ali bwanji? Ali ndi moyobe?”
And he asked them of their welfare, and said, Is your father well, the old man of whom ye spoke? Is he yet alive?
28 Iwo anayankha kuti, “Mtumiki wanu abambo athu akanali ndi moyo ndipo ali bwino.” Ndipo anamugwadira namuweramira pansi.
And they said, Thy servant our father is well; he is yet alive. And they bowed the head, and made obeisance.
29 Pomwazamwaza maso Yosefe anaona Benjamini, mʼbale wake weniweni wa bere limodzi, ndipo anafunsa, “Kodi uyu ndiye mʼbale wanu wamngʼono kwambiri amene munkandiwuza uja?” Kenaka anati, “Ambuye akukomere mtima mwana wanga.”
And he lifted up his eyes, and saw Benjamin his brother, his mother's son, and said, Is this your youngest brother, of whom ye spoke to me? And he said, God be gracious to thee, my son.
30 Kenaka Yosefe anafulumira kutuluka chifukwa mtima wake unadzaza ndi chifundo cha mngʼono wake ndipo anafuna kulira. Tsono anakalowa mʼchipinda chakechake nakalira kumeneko.
And Joseph made haste, for his heart yearned over his brother, and he sought where to weep. And he entered into his chamber, and wept there.
31 Atatha kupukuta misozi mʼmaso mwake anatuluka, ndipo modzilimbitsa analamula kuti chakudya chibwere.
And he washed his face, and came out. And he restrained himself, and said, Set on bread.
32 Anamupatsira Yosefe chakudya payekha, abale ake aja pawokha, ndiponso Aigupto amene ankadya pamodzi ndi iye nawonso pawokha. Izi zinali choncho chifukwa Aigupto ankanyansidwa kudya pamodzi ndi Ahebri.
And they set on for him by himself, and for them by themselves, and for the Egyptians, who ate with him, by themselves, because the Egyptians might not eat bread with the Hebrews, for that is an abomination to the Egyptians.
33 Abale aja anawakhazika patsogolo pa Yosefe. Iwo anawakhazika monga mwa mabadwidwe awo kuyambira woyamba kubadwa mpaka wotsirizira; ndipo ankangoyangʼanitsitsana modabwa.
And they sat before him, the firstborn according to his birthright, and the youngest according to his youth. And the men marveled one with another.
34 Tsono ankawagawira chakudya kuchokera pa tebulo la Yosefe. Koma chakudya cha Benjamini chinkaposa cha ena onsewa kasanu. Motero anadya ndi kumwa mpaka kukhuta, ndipo anasangalala pamodzi ndi Yosefe.
And he took and sent portions to them from before him, but Benjamin's portion was five times so much as any of theirs. And they drank, and were merry with him.

< Genesis 43 >