< Genesis 38 >

1 Pa nthawi imeneyi, Yuda anasiyana ndi abale ake napita kukakhala ndi munthu wina wa ku Adulamu wotchedwa Hira.
And it came to pass at that time, that Judah went down from his brethren, and turned in to a certain Adullamite, whose name [was] Hirah.
2 Kumeneko, Yuda anaona mwana wamkazi wa munthu wina wa Chikanaani wotchedwa Suwa. Anamukwatira nagona naye malo amodzi.
And Judah saw there a daughter of a certain Canaanite, whose name [was] Shuah; and he took her, and went in to her.
3 Iye anatenga pathupi, nabala mwana wamwamuna amene anamutcha Eri.
And she conceived, and bore a son; and he called his name Er.
4 Anatenganso pathupi nabala mwana wa mwamuna ndipo anamutcha Onani.
And she conceived again, and bore a son; and she called his name Onan.
5 Anaberekanso mwana wina wamwamuna ndipo anamutcha Sela. Ameneyu anabadwa Yuda ali ku Kezibi.
And she yet again conceived, and bore a son; and called his name Shelah: and he was at Chezib, when she bore him.
6 Yuda anamupezera mkazi mwana wake woyamba uja Eri, ndipo dzina la mkaziyo linali Tamara.
And Judah took a wife for Er his first-born, whose name [was] Tamar.
7 Koma ntchito zoyipa za Eri, mwana wachisamba wa Yuda zinayipira Yehova. Choncho Mulungu anamulanga ndi imfa.
And Er, Judah's first-born, was wicked in the sight of the LORD; and the LORD slew him.
8 Pamenepo Yuda anati kwa Onani, “Kwatira mkazi wamasiye wa mʼbale wako. Ulowe chokolo kuti mʼbale wako akhale ndi mwana.”
And Judah said to Onan, Go in to thy brother's wife, and marry her, and raise up seed to thy brother.
9 Koma Onani anadziwa kuti mwanayo sadzakhala wake. Choncho nthawi zonse pamene amagona naye mkaziyo, ankatayira umuna pansi kuti asamuberekere mwana mʼbale wake.
And Onan knew that the seed would not be his: and it came to pass, when he went in to his brother's wife, that he frustrated the purpose, lest he should give seed to his brother.
10 Zimene ankachitazi zinayipira Yehova. Choncho anamulanganso ndi imfa.
And the thing which he did displeased the LORD: wherefore he slew him also.
11 Kenaka Yuda anati kwa mpongozi wake Tamara, “Bwererani ku nyumba ya abambo anu ndi kukhala kumeneko ngati wamasiye mpaka mwana wanga Sela atakula.” Ananena izi chifukwa ankaopa kuti Sela angafenso ngati abale ake aja. Choncho Tamara anapita kukakhala ku nyumba ya abambo ake.
Then said Judah to Tamar his daughter-in-law, Remain a widow at thy father's house, till Shelah my son shall be grown; (for he said, Lest perhaps he die also as his brethren [did]: ) and Tamar went and dwelt in her father's house.
12 Patapita nthawi yayitali, Batishua, mkazi wa Yuda anamwalira. Yuda atatha kulira maliro a mkazi wake, anapita, iyeyu pamodzi ndi bwenzi lake Hira, Mwadulamu uja, ku Timna kumene ankameta nkhosa zawo.
And in process of time, the daughter of Shuah Judah's wife died: and Judah was comforted, and went up to his sheep-shearers to Timnath, he and his friend Hirah the Adullamite.
13 Tamara atamva kuti apongozi ake akupita ku Timna kukameta nkhosa,
And it was told to Tamar, saying, Behold, thy father-in-law goeth up to Timnath, to shear his sheep.
14 iye anavula zovala zake za umasiye, nadziphimba nkhope ndi nsalu kuti asadziwike, ndipo anakhala pansi pa chipata cha ku Enaimu popita ku Timna. Tamara anachita izi chifukwa anaona kuti ngakhale Selayo anali atakula tsopano, iye sanaperekedwe kuti amulowe chokolo.
And she put off from her, her widow's garments, and covered her with a vail, and wrapped herself, and sat in an open place, which [is] by the way to Timnath: for she saw that Shelah was grown, and she was not given to him for a wife.
15 Yuda atamuona anangomuyesa mkazi wadama chabe, chifukwa anadziphimba nkhope.
When Judah saw her, he thought her [to be] a harlot; because she had covered her face.
16 Tsono anapita kwa mkaziyo pamphepete pa msewu paja nati, “Tabwera ndigone nawe.” Apa Yuda sankadziwa kuti mkazi uja anali mpongozi wake. Ndiye mkazi uja anamufunsa Yuda nati, “Mudzandipatsa chiyani kuti ndigone nanu?”
And he turned to her by the way, and said, Come, I pray thee, let me have access to thee; (for he knew not that she [was] his daughter-in-law: ) and she said, What wilt thou give me, that thou mayst have access to me?
17 Iye anati, “Ndidzakutumizira kamwana kambuzi ka mʼkhola mwanga.” Mkaziyo anayankha kuti, “Chabwino, ndavomera, koma mungandipatse chikole mpaka mutanditumizira mbuziyo?”
And he said, I will send [thee] a kid from the flock: and she said, Wilt thou give [me] a pledge, till thou sendest [it]?
18 Iye anati, “Ndikupatse chikole chanji?” Mkaziyo anayankha, “Mundipatse mphete yanuyo, chingwe chanucho pamodzi ndi ndodo imene ili mʼdzanja lanulo.” Choncho anazipereka kwa iye nagona naye ndipo anatenga pathupi.
And he said, What pledge shall I give thee? and she said, Thy signet, and thy bracelets, and thy staff that [is] in thy hand: and he gave [them to] her, and came in to her, and she conceived by him.
19 Kenaka Tamara anachoka, navula nsalu anadziphimba nayo ija, navalanso zovala zake za umasiye zija.
And she arose and went her way and laid by her vail from her, and put on the garments of her widowhood.
20 Tsono Yuda anatuma bwenzi lake Mwadulamu uja ndi kamwana kambuzi kaja kuti akapereke kwa mkazi wadama uja, ndi kuti akatero amubwezere chikole chake chija. Koma atafika sanamupezepo.
And Judah sent the kid by the hand of his friend the Adullamite, to receive [his] pledge from the woman's hand: but he found her not.
21 Anawafunsa anthu a komweko, “Kodi mkazi wadama uja amene ankakhala pambali pa msewu wa ku Enaimu, ali kuti?” Iwo anayankha, “Sipanakhalepo mkazi wa dama aliyense pano.”
Then he asked the men of that place, saying, where [is] the harlot that [was] openly by the way-side? and they said, There was no harlot in this [place].
22 Choncho anabwerera kwa Yuda nati, “Sindinamupeze mkazi uja. Kuwonjeza apo, anthu a kumeneko amati, ‘Sipanakhalepo mkazi wadama pano.’”
And he returned to Judah, and said, I cannot find her; and also the men of the place said, [that] there was no harlot in this [place].
23 Pamenepo Yuda anati, “Mulekeni atenge zinthuzo zikhale zake, kuopa kuti anthu angatiseke. Ine sindinalakwe, ndinamutumizira kamwana kambuzika, koma simunamupeze.”
And Judah said, Let her take [it] to her, lest we be shamed: behold, I sent this kid, and thou hast not found her.
24 Patapita miyezi itatu, Yuda anawuzidwa kuti, “Mpongozi wanu Tamara anachita zadama, ndipo zotsatira zake nʼzakuti ali ndi pathupi.” Yuda anati, “Kamutulutseni ndipo mukamutenthe kuti afe!”
And it came to pass about three months after, that it was told to Judah, saying, Tamar thy daughter-in-law hath played the harlot; and also, behold she [is] with child by lewdness: and Judah said, Bring her forth, and let her be burnt.
25 Akumutulutsa, iye anatuma mawu kwa apongozi ake. Anati, “Ndili ndi pathupi pa munthu amene ndi mwini wake wa zinthu izi. Taziyangʼanitsitsani, kodi mwini wa khoza, chingwe ndi ndodo yoyenderayi ndi yani?”
When she [was] brought forth, she sent to her father-in-law, saying, By the man whose these [are], am I with child: and she said, Discern, I pray thee, whose [are] these, the signet, and bracelets, and staff.
26 Yuda anazizindikira zinthuzo ndipo anati, “Uyu ndi wolungama kuposa ine, chifukwa sindinamupereke kwa mwana wanga Sela.” Ndipo Yuda sanagone nayenso.
And Judah acknowledged [them], and said She hath been more righteous than I; because that I gave her not to Shelah my son: and he knew her again no more.
27 Pamene Tamara nthawi inamukwanira yoti abeleke, mʼmimbamo munali mapasa.
And it came to pass in the time of her travail, that behold, twins [were] in her womb.
28 Pamene ankabereka, mmodzi wa iwo anatulutsa dzanja lake. Choncho mzamba anatenga kawulusi kofiira nakamangirira pa mkono pa mwanayo nati, “Uyu ndiye anayamba kubadwa.”
And it came to pass when she travailed, that [the one] put out [his] hand; and the midwife took and bound upon his hand a scarlet thread, saying, This came out first.
29 Koma pamene anabweza mkonowo, mʼbale wake anabadwa ndipo mzamba anati, “Wachita kudziphotcholera wekha njira chonchi!” Ndipo anamutcha Perezi.
And it came to pass as he drew back his hand, that behold, his brother came out; and she said, How hast thou broken forth? [this] breach [be] upon thee: therefore his name was called Pharez.
30 Pambuyo pake mʼbale wake amene anali ndi ulusi wofiira pa mkono wake uja anabadwa ndipo anapatsidwa dzina lakuti Zera.
And afterwards came out his brother that had the scarlet thread upon his hand; and his name was called Zarah.

< Genesis 38 >