< Genesis 36 >

1 Nazi zidzukulu za Esau amene ankatchedwanso Edomu:
Now this is the history of the generations of Esau (that is, Edom).
2 Esau anakwatira akazi atatu a ku Kanaani. Iwowa ndiwo Ada mwana wa Eloni Mhiti; Oholibama mwana wa Ana amene anali mwana wa Zibeoni Mhivi
Esau took his wives from the daughters of Canaan: Adah the daughter of Elon, the Hittite; and Oholibamah the daughter of Anah, the daughter of Zibeon, the Hivite;
3 ndi Basemati mwana wa Ismaeli, amenenso anali mlongo wa Nabayoti.
and Basemath, Ishmael’s daughter, sister of Nebaioth.
4 Ada anaberekera Esau, Elifazi; Basemati anabereka Reueli;
Adah bore to Esau Eliphaz. Basemath bore Reuel.
5 ndipo Oholibama anabereka Yeusi, Yolamu ndi Kora. Amenewa anali ana a Esau amene anabadwira ku Kanaani.
Oholibamah bore Jeush, Jalam, and Korah. These are the sons of Esau, who were born to him in the land of Canaan.
6 Esau anatenga akazi ake, ana ake aamuna ndi aakazi ndi ena onse a pa banja pake. Anatenganso ziweto zake ndi ziweto zake zonse pamodzi ndi katundu wake yense amene anamupata ku Kanaani, ndipo anachoka ku dziko la Kanaani kupatukana ndi mʼbale wake Yakobo.
Esau took his wives, his sons, his daughters, and all the members of his household, with his livestock, all his animals, and all his possessions, which he had gathered in the land of Canaan, and went into a land away from his brother Jacob.
7 Iwo anatero chifukwa dziko limene ankakhalamo silikanakwanira awiriwo. Iwowa anali ndi ziweto zochuluka motero kuti sakanatha kukhala pamodzi.
For their substance was too great for them to dwell together, and the land of their travels couldn’t bear them because of their livestock.
8 Choncho Esau (amene ndi Edomu) anakakhazikika ku dziko la mapiri ku Seiri.
Esau lived in the hill country of Seir. Esau is Edom.
9 Nazi zidzukulu za Esau, kholo la Aedomu amene ankakhala ku Seiri.
This is the history of the generations of Esau the father of the Edomites in the hill country of Seir:
10 Awa ndi mayina a ana aamuna a Esau: Elifazi, mwana wa Ada, mkazi wa Esau, ndi Reueli, mwana wamwamuna wa Basemati, mkazi wa Esau.
these are the names of Esau’s sons: Eliphaz, the son of Adah, the wife of Esau; and Reuel, the son of Basemath, the wife of Esau.
11 Awa ndi mayina a ana a Elifazi: Temani, Omari, Zefo, Gatamu ndi Kenazi.
The sons of Eliphaz were Teman, Omar, Zepho, and Gatam, and Kenaz.
12 Timna anali mzikazi wa Elifazi, mwana wa Esau. Iyeyo anaberekera Elifazi mwana dzina lake Amaleki. Amenewa ndiwo zidzukulu za Ada, mkazi wa Esau.
Timna was concubine to Eliphaz, Esau’s son; and she bore to Eliphaz Amalek. These are the descendants of Adah, Esau’s wife.
13 Awa ndi ana a Reueli: Nahati, Zera, Sama ndi Miza. Amenewa ndi ana a Basemati, mkazi wa Esau.
These are the sons of Reuel: Nahath, Zerah, Shammah, and Mizzah. These were the descendants of Basemath, Esau’s wife.
14 Ana aamuna a Oholibama, mkazi wa Esau, mwana wa Ana ndi mdzukulu wa Zebeoni ndi awa: Yeusi, Yolamu ndi Kora.
These were the sons of Oholibamah, the daughter of Anah, the daughter of Zibeon, Esau’s wife: she bore to Esau Jeush, Jalam, and Korah.
15 Nawa mafumu a zidzukulu za Esau: Mwa ana a Elifazi, mwana woyamba wa Esau panali mafumu awa: Temani, Omari, Zefo, ndi Kenazi,
These are the chiefs of the sons of Esau: the sons of Eliphaz the firstborn of Esau: chief Teman, chief Omar, chief Zepho, chief Kenaz,
16 Kora, Gatamu, ndi Amaleki. Awa anali mafumu mwa ana a Elifazi ku Edomu ndipo onsewa anali zidzukulu za Ada.
chief Korah, chief Gatam, chief Amalek. These are the chiefs who came of Eliphaz in the land of Edom. These are the sons of Adah.
17 Mwa ana a Reueli, mwana wa Esau munali mafumu awa: Nahati, Zera, Sama ndi Miza. Awa anali mafumu mwa ana a Reueli ku Edomu. Iwowa anali zidzukulu za Basemati mkazi wa Esau.
These are the sons of Reuel, Esau’s son: chief Nahath, chief Zerah, chief Shammah, chief Mizzah. These are the chiefs who came of Reuel in the land of Edom. These are the sons of Basemath, Esau’s wife.
18 Mwa ana a Oholibama, mkazi wa Esau munali mafumu awa: Yeusi, Yolamu, ndi Kora. Amenewa anali mafumu mwa ana a mkazi wa Esau, Oholibama, mwana wa Ana.
These are the sons of Oholibamah, Esau’s wife: chief Jeush, chief Jalam, chief Korah. These are the chiefs who came of Oholibamah the daughter of Anah, Esau’s wife.
19 Amenewa ndiwo zidzukulu za Esau (amene ndi Edomu) ndiponso mafumu awo.
These are the sons of Esau (that is, Edom), and these are their chiefs.
20 Awa ndi ana a Seiri Mhori, amene ankakhala mʼdzikomo: Lotani, Sobala, Zibeoni, Ana,
These are the sons of Seir the Horite, the inhabitants of the land: Lotan, Shobal, Zibeon, Anah,
21 Disoni, Ezeri ndi Disani. Amenewa ndiwo ana a Seiri a ku Edomu ndipo analinso mafumu a Ahori.
Dishon, Ezer, and Dishan. These are the chiefs who came of the Horites, the children of Seir in the land of Edom.
22 Ana aamuna a Lotani anali awa: Hori ndi Homamu. Timna anali mlongo wake wa Lotani.
The children of Lotan were Hori and Heman. Lotan’s sister was Timna.
23 Ana aamuna a Sobala anali awa: Alivani, Manahati, Ebala, Sefo ndi Onamu.
These are the children of Shobal: Alvan, Manahath, Ebal, Shepho, and Onam.
24 Ana aamuna a Zibeoni anali awa: Ayiwa ndi Ana. Uyu ndi Ana amene anapeza akasupe a madzi amoto mʼchipululu pamene ankadyetsa abulu abambo wake Zibeoni.
These are the children of Zibeon: Aiah and Anah. This is Anah who found the hot springs in the wilderness, as he fed the donkeys of Zibeon his father.
25 Ana a Ana anali: Disoni ndi Oholibama mwana wake wamkazi.
These are the children of Anah: Dishon and Oholibamah, the daughter of Anah.
26 Ana aamuna a Disoni anali awa: Hemudani, Esibani, Itirani ndi Kerani.
These are the children of Dishon: Hemdan, Eshban, Ithran, and Cheran.
27 Ana aamuna a Ezeri anali awa: Bilihani, Zaavani ndi Akani.
These are the children of Ezer: Bilhan, Zaavan, and Akan.
28 Ana aamuna a Disani anali awa: Uzi ndi Arani.
These are the children of Dishan: Uz and Aran.
29 Mafumu a Ahori anali awa: Lotani, Sobala, Zibeoni, Ana,
These are the chiefs who came of the Horites: chief Lotan, chief Shobal, chief Zibeon, chief Anah,
30 Disoni, Ezeri ndi Disani. Amenewa ndiwo mafumu a Ahori, monga mwa mafuko awo, mʼdziko la Seiri.
chief Dishon, chief Ezer, and chief Dishan. These are the chiefs who came of the Horites, according to their chiefs in the land of Seir.
31 Awa ndi mafumu amene ankalamulira dziko la Edomu, mfumu iliyonse ya Israeli isanayambe kulamulira kumeneko:
These are the kings who reigned in the land of Edom, before any king reigned over the children of Israel.
32 Bela mwana wa Beori anakhala mfumu ya ku Edomu. Mzinda wake ankawutcha Dinihaba.
Bela, the son of Beor, reigned in Edom. The name of his city was Dinhabah.
33 Bela atamwalira, Yobabu mwana wa Zera wochokera ku Bozira analowa ufumu mʼmalo mwake.
Bela died, and Jobab, the son of Zerah of Bozrah, reigned in his place.
34 Atafa Yobabu, Husamu wochokera ku dziko la Atemani, analowa mʼmalo mwake ngati mfumu.
Jobab died, and Husham of the land of the Temanites reigned in his place.
35 Husamu atamwalira, Hadadi mwana wa Bedadi, amene anagonjetsa Amidiyani mʼdziko la Mowabu, analowa ufumu mʼmalo mwake. Mzinda wake unkatchedwa Aviti.
Husham died, and Hadad, the son of Bedad, who struck Midian in the field of Moab, reigned in his place. The name of his city was Avith.
36 Hadadi atamwalira, Samila wochokera ku Masireka, analowa ufumu mʼmalo mwake.
Hadad died, and Samlah of Masrekah reigned in his place.
37 Samila atamwalira, Sauli wochokera ku Rehoboti wa ku Mtsinje, analowa ufumu mʼmalo mwake.
Samlah died, and Shaul of Rehoboth by the river, reigned in his place.
38 Sauli atamwalira, Baala-Hanani, mwana wa Akibori analowa ufumu mʼmalo mwake.
Shaul died, and Baal Hanan the son of Achbor reigned in his place.
39 Pamene Baala-Hanani mwana wa Akibori anamwalira, Hadari analowa ufumu mʼmalo mwake. Mzinda wake unkatchedwa Pau, ndipo dzina la mkazi wake linali Mehatabeli, mwana wamkazi wa Matiredi, mwana wamkazi wa Me-Zahabu.
Baal Hanan the son of Achbor died, and Hadar reigned in his place. The name of his city was Pau. His wife’s name was Mehetabel, the daughter of Matred, the daughter of Mezahab.
40 Mayina a mafumu ochokera mwa zidzukulu za Esau malingana ndi mafuko awo ndi malo a fuko lililonse anali awa: Timna, Aliva, Yeteti,
These are the names of the chiefs who came from Esau, according to their families, after their places, and by their names: chief Timna, chief Alvah, chief Jetheth,
41 Oholibama, Ela, Pinoni,
chief Oholibamah, chief Elah, chief Pinon,
42 Kenazi, Temani, Mibezari,
chief Kenaz, chief Teman, chief Mibzar,
43 Magidieli ndi Iramu. Awa anali mafumu a ku Edomu molingana ndi malo awo okhala mʼdzikomo. Umenewu ndi mndandanda wa mʼbado wa Esau, kholo la Aedomu.
chief Magdiel, and chief Iram. These are the chiefs of Edom, according to their habitations in the land of their possession. This is Esau, the father of the Edomites.

< Genesis 36 >