< Genesis 33 >

1 Yakobo atakweza maso ake anaona Esau akubwera ndi anthu ake 400. Choncho ana ake anawagawira Leya, Rakele ndi antchito awiri aja.
[Then Jacob joined the rest of his family]. [Later that day] Jacob looked up and saw Esau coming, and there were 400 men with him. [Jacob was worried because of that], so he separated the children. He put Leah’s children with Leah, Rachel’s children with Rachel, and the two female slaves’ children with their mothers.
2 Anayika antchito ndi ana awo patsogolo, kenaka nʼkubwera Leya ndi ana ake, ndipo pambuyo pawo Rakele ndi Yosefe.
He put the two female slaves and their children in front. He put Leah and her children next. He put Rachel and Joseph at the rear.
3 Iye mwini anakhala patsogolo nawerama mpaka kukhudza pansi kasanu ndi kawiri pamene amayandikira mʼbale wake.
He himself went ahead of them all, and as he continued to approach his older brother, he prostrated himself with his face on the ground seven times.
4 Koma Esau anathamanga kukakumana ndi Yakobo ndipo anamukupatira namupsompsona. Onse awiri ankangolira.
But Esau ran to Jacob. He hugged him, put his arms around his neck, and kissed him on the cheek. And they both cried.
5 Kenaka Esau ataona amayi ndi ana awo anamufunsa Yakobo kuti, “Kodi anthu amene uli nawowa ndi a ndani?” Yakobo anayankha kuti, “Awa ndi ana amene Mulungu, mwa kukoma mtima kwake, wapereka kwa mtumiki wanune.”
Then Esau looked up and saw the women and the children. He asked, “Who are these people who are with you?” Jacob replied, “These are the wives and children that God has graciously/kindly given to me.”
6 Tsono antchito aja anayandikira naweramitsa mitu pansi.
Then the female slaves and their children came near and bowed in front of Esau.
7 Kenaka, Leya ndi ana ake anabwera. Nawonso anaweramitsa mitu pansi. Potsiriza pa onse anabwera Yosefe ndi Rakele naweramitsanso mitu yawo pansi.
Then Leah and her children came and bowed down. Finally Joseph and Rachel came near and bowed down.
8 Esau anafunsa kuti, “Kodi gulu la ziweto ndakumana nalo lija ndi layani?” Yakobo anayankha nati, “Mbuye wanga, gulu lija ndi lanu kuti mundikomere mtima.”
Esau asked, “What is the meaning of all the animals that I saw?” Jacob replied, “I am giving them to you, sir, so that you will feel good toward me.”
9 Koma Esau anati, “Mʼbale wanga, ine ndili nazo kale zambiri. Zinthu zakozi sunga.”
But Esau replied, “My [younger] brother, I have enough animals! Keep for yourself the animals that you have!”
10 Yakobo anati, “Chonde musatero. Ngati mwandikomera mtima, landirani mphatso yangayi kuchokera kwa ine. Pakuti ndi mmene mwandirandira bwinomu, ine ndikamaona nkhope yanu ndikuchita ngati ndikuona nkhope ya Mulungu.
But Jacob said, “No, please, if you feel good toward me, accept these gifts from me. You have greeted me very kindly. Seeing your smiling face assures me [that you have forgiven me]. It is like seeing the face of God!
11 Chonde, landirani mphatso imene ndakutengeraniyi, popeza Mulungu wandikomera mtima kwambiri moti ndili ndi zonse zimene ndizifuna.” Ndipo popeza kuti Yakobo anamuwumiriza, Esau analandira.
Please accept these gifts that I have brought to you, because God has acted kindly toward me, and I still have plenty of animals!” Jacob kept on urging him to accept the animals, and finally he accepted them.
12 Ndipo Esau anati, “Tiyeni tizipita; nditsagana nanu.”
Then Esau said, “Let’s continue traveling together, and I will show the road to you.”
13 Koma Yakobo anati kwa iye, “Mbuye wanga, inu mudziwa kuti anawa ndi a nthete ndiponso ndiyenera kusamalira nkhosa ndi ngʼombe zimene zikuyamwitsa ana awo. Ngati ndizimenya kuti zifulumire, tsiku limodzi lokha nyamazo zidzafa.
Jacob [had no intention to go with Esau], but he said, “You know, sir, that the children are weak, and that I must take care of the female sheep and cows that are (sucking their mother’s milk/nursing their young). If I force them to walk fast for a long distance in just one day, the animals will all die.
14 Choncho, mbuye wanga lolani kuti mutsogole. Ine ndiziyenda pangʼonopangʼono pambuyo pa ziwetozi ndi anawa mpaka ndikafika ku Seiri.”
You go ahead of me. I will lead the animals slowly, but I will walk as fast as the children and animals can walk. I will catch up with you in Seir, [in the land where the descendants of Edom live].”
15 Esau anati, “Ndiye bwanji ndikusiyireko ena mwa anthu anga.” Koma Yakobo anati, “Koma muchitiranji zimenezi? Chachikulu nʼkuti mwandilandira bwino, mbuye wanga.”
Esau said, “Then allow me to leave with you some of the men who came with me, [to protect you].” But Jacob replied, “(Why do that?/There is no need to do that!) [RHQ] The only thing that I want is for you to act friendly toward me.”
16 Choncho tsiku limenelo Esau anayamba ulendo wobwerera ku Seiri.
So on that day Esau left to return to Seir.
17 Komabe Yakobo anapita ku Sukoti. Kumeneko anamanga nyumba yake ndi makola a ziweto zake. Nʼchifukwa chake malowa amatchedwa Sukoti.
But [instead of going to Seir], Jacob and his family went to [a place called] Succoth. There he built a house for himself and his family, and built shelters for his livestock. That is the reason they named the place Succoth, [which means ‘shelters’].
18 Mmene ankabwerera kuchokera ku Padanaramu, Yakobo anafika ku Salemu, mzinda wa Sekemu ku Kanaani. Anamanga msasa pamalopo moyangʼanana ndi mzindawo.
[Some time later, ] Jacob and his family left Paddan-Aram [in Mesopotamia], and they traveled safely to the Canaan region. There they set up their tents in a field near Shechem city.
19 Malo amenewo anagula kwa zidzukulu za Hamori, abambo a Sekemu ndi ndalama 100 zasiliva.
One of the leaders of the people in that area was named Hamor. Hamor had several sons. Jacob paid the sons of Hamor 100 pieces of silver for the piece of ground on which they set up their tents.
20 Pamalopo anamanganso guwa lansembe, nalitcha Eli Elohe Israeli.
He built a stone altar there, and named it El-Elohe Israel, [which means ‘God, the God of Israel].’

< Genesis 33 >