< Genesis 31 >

1 Yakobo anamva zimene ana aamuna a Labani ankanena kuti, “Yakobo watenga chilichonse cha abambo athu ndipo wapeza chuma chonsechi pogwiritsa ntchito chuma cha abambo athu.”
And he heareth the words of Laban's sons, saying, 'Jacob hath taken all that our father hath; yea, from that which our father hath, he hath made all this honour;'
2 Choncho Yakobo anaona kuti Labani sankamuonetsanso nkhope yabwino monga kale.
and Jacob seeth the face of Laban, and lo, it is not with him as heretofore.
3 Pamenepo Yehova anati kwa Yakobo, “Bwerera ku dziko la makolo ako ndi kwa abale ako, ndipo Ine ndidzakhala nawe.”
And Jehovah saith unto Jacob, 'Turn back unto the land of thy fathers, and to thy kindred, and I am with thee.'
4 Choncho Yakobo anatumiza mawu kukayitana Rakele ndi Leya kuti abwere ku busa kumene ankaweta ziweto zake.
And Jacob sendeth and calleth for Rachel and for Leah to the field unto his flock;
5 Iye anawawuza kuti, “Abambo anu sakundionetsanso nkhope yabwino monga kale, koma Mulungu wa makolo anga wakhala ali nane.
and saith to them, 'I am beholding your father's face — that it is not towards me as heretofore, and the God of my father hath been with me,
6 Inu mukudziwa kuti ndagwirira ntchito abambo anu ndi mphamvu zanga zonse,
and ye — ye have known that with all my power I have served your father,
7 chonsecho abambo anu akhala akundinyenga posintha malipiro anga kakhumi konse. Komabe Mulungu sanalole kuti andichitire choyipa
and your father hath played upon me, and hath changed my hire ten times; and God hath not suffered him to do evil with me.
8 Pamene abambo anu anati, ‘Zamawangamawanga zidzakhala malipiro ako,’ ziweto zonse zinaswa ana amawangamawanga; ndipo pamene anati, ‘Zamichocholozi zidzakhala malipiro ako,’ ziweto zonse zinaswa ana a michocholozi.
'If he say thus: The speckled are thy hire, then bare all the flock speckled ones; and if he say thus: The ring-streaked are thy hire, then bare all the flock ring-streaked;
9 Motero Mulungu walanda abambo anu ziweto zawo ndi kundipatsa.
and God taketh away the substance of your father, and doth give to me.
10 “Pa nthawi imene ziweto zimatenga mawere ndinalota maloto, ndipo ndinaona kuti atonde onse amene ankakwerawo anali amichocholozi, amawangamawanga kapena amathothomathotho
'And it cometh to pass at the time of the flock conceiving, that I lift up mine eyes and see in a dream, and lo, the he-goats, which are going up on the flock, [are] ring-streaked, speckled, and grisled;
11 Kutulo komweko, mngelo wa Mulungu anati, ‘Yakobo.’ Ine ndinayankha, ‘Ee, Ambuye.’
and the messenger of God saith unto me in the dream, Jacob, and I say, Here [am] I.
12 Ndipo iye anati, ‘Tayangʼana ndipo taona kuti atonde onse okwerana ndi ziweto ali amichocholozi, amawangamawanga kapena a mathothomathotho, popeza ndaona zonse zimene Labani wakhala akukuchitira.
'And He saith, Lift up, I pray thee, thine eyes, and see — all the he-goats which are going up on the flock [are] ring-streaked, speckled, and grisled, for I have seen all that Laban is doing to thee;
13 Ine ndine Mulungu amene ndinadza kwa iwe pa Beteli paja. Beteli ndi kumalo kuja kumene unayimika mwala ndi kuwudzoza mafuta, komanso kulumbira kwa Ine. Tsopano choka mʼdziko lino msanga ndi kubwerera ku dziko la kwanu.’”
I [am] the God of Bethel where thou hast anointed a standing pillar, where thou hast vowed a vow to me; now, arise, go out from this land, and turn back unto the land of thy birth.'
14 Pamenepo Rakele ndi Leya anayankha, “Kodi ngati ife tilinso ndi gawo ngati cholowa pa chuma cha abambo athu?
And Rachel answereth — Leah also — and saith to him, 'Have we yet a portion and inheritance in the house of our father?
15 Kodi abambo athu samationa ife ngati alendo? Iwo anatigulitsa ndi kuwononga ndalama zonse anazipeza pa ifezo.
have we not been reckoned strangers to him? for he hath sold us, and he also utterly consumeth our money;
16 Chuma chonse chimene Mulungu walanda abambo athu, ndi chathu ndi ana athu. Tsono inu chitani zimene Mulungu wakuwuzani.”
for all the wealth which God hath taken away from our father, it [is] ours, and our children's; and now, all that God hath said unto thee — do.'
17 Pamenepo Yakobo anakonzeka nakweza ana ake ndi akazi ake pa ngamira,
And Jacob riseth, and lifteth up his sons and his wives on the camels,
18 anakusa ziweto zake zonse patsogolo natenga katundu wake yense amene anamupeza ku Padanaramu, ndipo ananyamuka kupita ku Kanaani, ku dziko la abambo ake, Isake.
and leadeth all his cattle, and all his substance which he hath acquired, the cattle of his getting, which he hath acquired in Padan-Aram, to go unto Isaac his father, to the land of Canaan.
19 Labani atachoka pa khomo kupita kukameta nkhosa, mʼmbuyomu Rakele anaba timafano ta milungu ta abambo ake.
And Laban hath gone to shear his flock, and Rachel stealeth the teraphim which her father hath;
20 Komanso nthawi iyi nʼkuti Yakobo atamunamiza Labani Mwaramu posamuwuza zoona kuti afuna kuthawa.
and Jacob deceiveth the heart of Laban the Aramaean, because he hath not declared to him that he is fleeing;
21 Choncho anathawa ndi zonse anali nazo. Ananyamuka nawoloka mtsinje wa Yufurate kupita cha ku Giliyadi, dziko la mapiri.
and he fleeth, he and all that he hath, and riseth, and passeth over the River, and setteth his face [toward] the mount of Gilead.
22 Patapita masiku atatu, Labani anawuzidwa kuti Yakobo wathawa.
And it is told to Laban on the third day that Jacob hath fled,
23 Pomwepo anatengana ndi abale ake namulondola Yakobo kwa masiku asanu ndi awiri ndipo anakamupezera ku Giliyadi, dziko la mapiri.
and he taketh his brethren with him, and pursueth after him a journey of seven days, and overtaketh him in the mount of Gilead.
24 Koma Mulungu anabwera kwa Labani, Mwaramu kutulo usiku nati kwa iye, “Samala kuti usamuopseze Yakobo mwa njira iliyonse.”
And God cometh in unto Laban the Aramaean in a dream of the night, and saith to him, 'Take heed to thyself lest thou speak with Jacob from good unto evil.'
25 Pamene Labani amamupeza Yakobo, nʼkuti Yakobo atamanga matenti ake ku mapiri a dziko la Giliyadi. Nayenso Labani ndi abale ake anamanga matenti awo komweko.
And Laban overtaketh Jacob; and Jacob hath fixed his tent in the mount; and Laban with his brethren have fixed [theirs] in the mount of Gilead.
26 Tsono Labani anati kwa Yakobo, “Kodi ndakuchita chiyani kuti iwe undinamize ndi kutenga ana anga ngati anthu ogwidwa ku nkhondo?
And Laban saith to Jacob, 'What hast thou done that thou dost deceive my heart, and lead away my daughters as captives of the sword?
27 Chifukwa chiyani unandinamiza ndi kuthawa mozemba wosandiwuza? Ukanandiwuza, bwezi titatsanzikana mwa chisangalalo ndi kuyimba nyimbo ndi zisekese ndi azeze.
Why hast thou hidden thyself to flee, and deceivest me, and hast not declared to me, and I send thee away with joy and with songs, with tabret and with harp,
28 Sunandilole kuti ndingopsompsona adzukulu anga ndi ana anga aakazi motsanzikana nawo. Unachita zopusa.
and hast not suffered me to kiss my sons and my daughters? — now thou hast acted foolishly in doing [so];
29 Ndili nayo mphamvu yakukuchita choyipa; koma usiku wapitawu, Mulungu wa abambo ako wandiwuza ine kuti, ‘Usamuopseze Yakobo mwa njira iliyonse.’
my hand is to God to do evil with you, but the God of your father yesternight hath spoken unto me, saying, Take heed to thyself from speaking with Jacob from good unto evil.
30 Ndikudziwa kuti unachoka chifukwa unapukwa kufuna kubwerera kwanu kwa abambo ako. Koma nʼchifukwa chiyani unaba milungu yanga?”
'And now, thou hast certainly gone, because thou hast been very desirous for the house of thy father; why hast thou stolen my gods?'
31 Yakobo anayankha Labani kuti, “Ine ndinkaopa chifukwa ndinkaganiza kuti mukhoza kundilanda anawa.
And Jacob answereth and saith to Laban, 'Because I was afraid, for I said, Lest thou take violently away thy daughters from me;
32 Koma mukapeza wina aliyense ndi milungu yanu, ameneyo sakhala ndi moyo. Anthu onse akupenya, lozani chilichonse chanu chimene chili ndi ine, ndipo ngati muchipeze tengani. Koma Yakobo sankadziwa kuti Rakele anabadi milunguyo.”
with whomsoever thou findest thy gods — he doth not live; before our brethren discern for thyself what [is] with me, and take to thyself:' and Jacob hath not known that Rachel hath stolen them.
33 Choncho Labani analowadi mu tenti ya Yakobo, ya Leya ndi mʼmatenti a adzakazi awiri aja, koma sanapeze kalikonse. Atatuluka mu tenti ya Leya, analowa ya Rakele.
And Laban goeth into the tent of Jacob, and into the tent of Leah, and into the tent of the two handmaidens, and hath not found; and he goeth out from the tent of Leah, and goeth into the tent of Rachel.
34 Koma Rakele anatengadi milungu ija ndi kuyiika mʼkati mwa chokhalira cha pa ngamira, iye nʼkukhalapo. Choncho Labani anafunafuna mu tenti monse koma wosapeza kanthu.
And Rachel hath taken the teraphim, and putteth them in the furniture of the camel, and sitteth upon them; and Laban feeleth all the tent, and hath not found;
35 Rakele anati kwa abambo ake, “Pepanitu musandikwiyire mbuye wanga chifukwa choti sinditha kuyimirira pamaso panu chifukwa ndili kumwezi.” Choncho Labani anafunafuna koma sanayipeze milungu ija.
and she saith unto her father, 'Let it not be displeasing in the eyes of my lord that I am not able to rise at thy presence, for the way of women [is] on me;' and he searcheth, and hath not found the teraphim.
36 Yakobo anapsa mtima nafunsa Labani mwaukali kuti, “Kodi ndalakwa chiyani? Ndi tchimo lanji limene ndachita kuti muchite kundisaka chonchi?
And it is displeasing to Jacob, and he striveth with Laban; and Jacob answereth and saith to Laban, 'What [is] my transgression? what my sin, that thou hast burned after me?
37 Chifukwa chiyani mwafunyulula katundu wanga? Ndipo mwapeza chiyani cha inu pamenepa? Chimene mwapezapo chiyikeni poyera pamaso pa abale anu ndi anga kuti atiweruze.
for thou hast felt all my vessels: what hast thou found of all the vessels of thy house? set here before my brethren, and thy brethren, and they decide between us both.
38 “Ndakhala nanu kwa zaka makumi awiri tsopano ndipo nkhosa ndi mbuzi zanu sizinapoloze, kapena ine kudyapo nkhosa za mʼkhola mwanu.
'These twenty years I [am] with thee: thy ewes and thy she-goats have not miscarried, and the rams of thy flock I have not eaten;
39 Chiweto chikakhadzulidwa ndi chirombo, sindinkabwera nacho kwa inu. Ineyo ndinkalipira. Inuyo munkandilipiritsa kalikonse kobedwa masana kapena usiku.
the torn I have not brought in unto thee — I, I repay it — from my hand thou dost seek it; I have been deceived by day, and I have been deceived by night;
40 Moyo wanga unali wotere: Dzuwa limanditentha masana ndipo usiku ndimazunzika ndi kuzizira. Tulo sindimalipeza konse.
I have been [thus]: in the day consumed me hath drought, and frost by night, and wander doth my sleep from mine eyes.
41 Zinthu zinali chonchi kwa zaka makumi awiri zimene ndinali mʼnyumba mwanu. Ndinakugwirirani ntchito kwa zaka khumi ndi zinayi chifukwa cha ana anu aakazi awiri ndipo zaka zina zisanu ndi chimodzi chifukwa cha ziweto zanu, ndipo munandisinthira malipiro kakhumi konse.
'This [is] to me twenty years in thy house: I have served thee fourteen years for thy two daughters, and six years for thy flock; and thou changest my hire ten times;
42 Akanapanda kukhala nane Mulungu wa abambo anga, Mulungu wa Abrahamu ndi Mulungu amene Isake ankamuopa, mosakayika inu mukanandichotsa chimanjamanja. Koma Mulungu waona zovuta zanga ndi kulimbikira ntchito kwanga, ndipo usiku wapitawu anakudzudzulani.”
unless the God of my father, the God of Abraham, and the Fear of Isaac, had been for me, surely now empty thou hadst sent me away; mine affliction and the labour of my hands hath God seen, and reproveth yesternight.'
43 Labani anayankha Yakobo nati, “Ana aakaziwa ndi anga, ana awo ndi anganso. Ziwetozi ndi zanga. Chilichonse ukuona apa ndi changa. Koma tsopano ndingachite chiyani ndi ana anga aakaziwa kapena ndi ana awo?
And Laban answereth and saith unto Jacob, 'The daughters [are] my daughters, and the sons my sons, and the flock my flock, and all that thou art seeing [is] mine; and to my daughters — what do I to these to-day, or to their sons whom they have born?
44 Tsono, tiye tichite pangano pakati pa iwe ndi ine, ndipo likhale mboni pakati pathu.”
and now, come, let us make a covenant, I and thou, and it hath been for a witness between me and thee.'
45 Choncho Yakobo anayimiritsa mwala ngati chipilala.
And Jacob taketh a stone, and lifteth it up [for] a standing pillar;
46 Nati kwa abale ake, “Tutani miyala ina.” Choncho anawunjika miyalayo, ndipo anadya chakudya atakhala pa mbali pa muluwo.
and Jacob saith to his brethren, 'Gather stones,' and they take stones, and make a heap; and they eat there on the heap;
47 Labani anawutcha muluwo Yegara-sahaduta, ndipo Yakobo anawutcha Galeeda.
and Laban calleth it Jegar-Sahadutha; and Jacob hath called it Galeed.
48 Labani anati, “Mulu uwu ndi mboni pakati pa inu ndi ine lero.” Ndi chifukwa chake unatchedwa Galeeda.
And Laban saith, 'This heap [is] witness between me and thee to-day;' therefore hath he called its name Galeed;
49 Unatchedwanso Mizipa, chifukwa iye anati, “Yehova aonetsetsa kuti palibe mmodzi mwa ife adzaswe panganoli ngakhale titatalikirana.
Mizpah also, for he said, 'Jehovah doth watch between me and thee, for we are hidden one from another;
50 Ngati ukazunza ana anga kapena kukwatira akazi enanso, ngakhale kuti palibe wina amene ali nafe pano, koma kumbukira kuti Mulungu ndiye mboni pakati pathu.”
if thou afflict my daughters, or take wives beside my daughters — there is no man with us — see, God [is] witness between me and thee.'
51 Labani anatinso kwa Yakobo, “Taona pano pali miyala ndi chipilala chimene ndayimika pakati pa iwe ndi ine.
And Laban saith to Jacob, 'Lo, this heap, and lo, the standing pillar which I have cast between me and thee;
52 Mulu wa miyala uwu ndi chipilalachi ndi mboni. Ine sindidzadutsa mulu wa miyalawu kudzalimbana ndi iwe. Iwenso usadzadutse mulu wa miyalawu kudzalimbana nane.
this heap [is] witness, and the standing pillar [is] witness, that I do not pass over this heap unto thee, and that thou dost not pass over this heap and this standing pillar unto me — for evil;
53 Mulungu wa Abrahamu ndi Mulungu wa Nahori ndiye adzatiweruze.” Choncho Yakobo analumbira mʼdzina la Mulungu amene Isake, abambo ake ankamuopa.
the God of Abraham and the God of Nahor, doth judge between us — the God of their father,' and Jacob sweareth by the Fear of his father Isaac.
54 Yakobo anapereka nsembe pa phiri paja, ndipo anayitana abale ake kuti adzadye chakudya. Atadya chakudya anagona pa phiri pomwepo.
And Jacob sacrificeth a sacrifice in the mount, and calleth to his brethren to eat bread, and they eat bread, and lodge in the mount;
55 Mmamawa wake, Labani anapsompsona zidzukulu zake ndi ana ake nawadalitsa. Kenaka ananyamuka kubwerera ku mudzi.
and Laban riseth early in the morning, and kisseth his sons and his daughters, and blesseth them; and Laban goeth on, and turneth back to his place.

< Genesis 31 >