< Genesis 20 >

1 Abrahamu anachokako kumeneko napita ku Negevi ndipo anakakhala ku dziko la Gerari, limene lili pakati pa mzinda wa Kadesi ndi mzinda wa Suri. Anakhala ku Gerari kwa kanthawi,
UAbrahama wasesuka lapho waya elizweni leningizimu, wahlala phakathi kweKadeshi leShuri wahlala njengowezizwe eGerari.
2 ndipo Abrahamu ankawawuza za Sara kuti, “Iyeyu ndi mlongo wanga.” Choncho Abimeleki, mfumu wa ku Gerari anamutenga Sara uja.
UAbrahama wasesithi ngoSara umkakhe: Ungudadewethu. UAbhimeleki inkosi yeGerari wathuma-ke, wathatha uSara.
3 Koma usiku, Mulungu anafika kwa Abimeleki kutulo nati, “Ufatu iwe chifukwa cha mkazi amene watengayu popeza ndi wokwatiwa.”
Kodwa uNkulunkulu weza kuAbhimeleki ephutsheni ebusuku, wathi kuye: Khangela, ufile ngenxa yowesifazana omthetheyo, ngoba uganile endodeni.
4 Nthawi imeneyi nʼkuti Abimeleki asanamukhudze mkaziyo, kotero kuti anati, “Ambuye, kodi mudzawonongadi mtundu wolungama?
Kodwa uAbhimeleki wayengasondelanga kuye. Ngakho wathi: Nkosi, uzabhubhisa lesizwe esilungileyo yini?
5 Kodi Abrahamu sanandiwuze kuti iyeyu ndi mlongo wake? Ndiponso mkaziyu ankanena kuti Abrahamu ndi mlongo wake. Choncho ine pochita izi, ndinkachita moona mtima ndiponso mopanda chinyengo.”
Kayisuye yini othe kimi: Ungudadewethu? Laye uqobo wasesithi: Ungumnewethu. Ngobuqotho benhliziyo yami langobuhlophe bezandla zami ngikwenzile lokhu.
6 Tsono kumaloto komweko Mulungu anati kwa iye, “Inde ndikudziwa kuti wachita izi moona mtima, ndipo Ine sindinafune kuti undichimwire. Nʼchifukwa chake sindinakulole kuti umukhudze.
UNkulunkulu wasesithi kuye ephutsheni: Lami sengazile ukuthi ngobuqotho benhliziyo yakho ukwenzile lokhu; lami futhi ngikuvimbele ukuze ungoni kimi; ngenxa yalokhu kangikuvumelanga ukuthi umthinte.
7 Tsopano kabwezere mkaziyo kwa mwamuna wake. Iyeyu ndi mneneri, ndipo adzakupempherera kuti ukhale ndi moyo. Koma ukapanda kukamupereka, udziwiretu kuti udzafa pamodzi ndi onse a pa banja pako.”
Ngakho-ke buyisela umfazi wendoda, ngoba ingumprofethi; njalo izakukhulekela ukuze uphile; kodwa uba ungambuyiseli, yazi ukuthi isibili uzakufa wena labo bonke abangabakho.
8 Mmamawa mwake Abimeleki anayitanitsa akuluakulu ake onse, ndipo atawafotokozera zimene zinachitika, iwo aja anachita mantha kwambiri.
UAbhimeleki wasevuka ekuseni kakhulu, wabiza zonke inceku zakhe, wakhuluma wonke la amazwi endlebeni zazo; njalo amadoda esaba kakhulu.
9 Kenaka Abimeleki anayitana Abrahamu ndipo anati, “Kodi wachita chiyani? Ndakulakwira chiyani kuti undibweretsere ine pamodzi ndi anthu anga chilango chachikulu chotere? Wandichitira zinthu zimene sizinayenera kuchitika.”
UAbhimeleki wasembiza uAbrahama, wathi kuye: Wenzeni kithi? Ngoneni kuwe ukuthi ungilethele mina lombuso wami isono esikhulu? Wenze kimi izenzo ezingafanelanga ukwenziwa.
10 Ndipo Abrahamu anafunsa Abimeleki kuti, “Chifukwa chiyani wachita zimenezi?”
UAbhimeleki wasesithi kuAbrahama: Uboneni, uze wenze into le?
11 Abrahamu anayankha nati, “Ndinkaganiza kuti kuno kulibiretu munthu woopa Mulungu. Ndiye ndimati mwina adzandipha chifukwa cha mkazi wanga.
UAbrahama wasesithi: Ngoba ngacabanga ukuthi: Isibili ukwesaba uNkulunkulu kakukho kulindawo; njalo bazangibulala ngenxa yomkami.
12 Komabe kunena zoona, iyeyu ndi mlongo wangadi, mwana wamkazi wa abambo anga ngakhale kuti si ife a mayi mmodzi. Tsono akhoza kukhala mkazi wanga.
Kanti-ke isibili ungudadewethu, uyindodakazi kababa, kodwa kasiyo indodakazi kamama; wasesiba ngumkami.
13 Ndiye pamene Mulungu anati ndichoke ku nyumba ya abambo anga, ndinawuza mkazi wangayu kuti, ‘Kuti uwonetse kuti ndiwe mkazi wokoma mtima, uziwuza anthu kulikonse kumene tingapite kuti ndine mlongo wako.’”
Kwasekusithi mhla uNkulunkulu engizulisa ngisuka endlini kababa ngasengisithi kuye: Lo ngumusa ozawenza kimi, kuzo zonke indawo esizafika kuzo, uthi ngami: Ungumnewethu.
14 Tsono Abimeleki anapereka nkhosa, ngʼombe ndi antchito aamuna ndi aakazi kwa Abrahamu. Ndipo anamubwezeranso Abrahamu Sara, mkazi wake.
UAbhimeleki wasethatha izimvu lezinkomo lezinceku lezincekukazi, wapha uAbrahama, wambuyisela uSara umkakhe.
15 Tsono Abimeleki anati kwa Abrahamu, “Dziko langa ndi limene ukulionali; ukhale paliponse pamene ufuna.”
UAbhimeleki wasesithi: Khangela, ilizwe lami liphambi kwakho; hlala lapho okuhle khona emehlweni akho.
16 Ndipo kwa Sara, iye anati, “Ndikumupatsa mlongo wakoyu makilogalamu khumi ndi awiri a siliva kutsimikiza kuti iwe ndi wosalakwa pamaso pa onse amene ali ndi iwe; ulibedi mlandu.”
LakuSara wathi: Khangela, ngimnikile umnewenu inhlamvu zesiliva eziyinkulungwane; khangela, uyisisibekelo samehlo kuwe, kuye wonke olawe, labo bonke, njalo ukhuziwe.
17 Tsono Abrahamu anapemphera kwa Mulungu ndipo Mulunguyo anachiritsa Abimeleki, mkazi wake pamodzi ndi adzakazi ake kuti athenso kubereka ana.
UAbrahama wasekhuleka kuNkulunkulu; uNkulunkulu wasemsilisa uAbhimeleki lomkakhe lencekukazi zakhe, ukuze bazale.
18 Paja Yehova nʼkuti atatseka akazi onse a mʼbanja la Abimeleki kuti asabereke ana chifukwa cha Sara, mkazi wa Abrahamu.
Ngoba iNkosi yayizivalile ngokupheleleyo izizalo zonke zabendlu kaAbhimeleki ngenxa kaSara umkaAbrahama.

< Genesis 20 >