< Genesis 2 >

1 Motero kumwamba, dziko lapansi ndi zonse za mʼmenemo zinatha kulengedwa monga mwa kuchuluka kwawo.
That is the way God created the heavens and the earth.
2 Pofika tsiku lachisanu ndi chiwiri Mulungu anamaliza ntchito zonse zimene ankagwira ndipo pa tsiku lachisanu ndi chiwiri anapumula ku ntchito zake zonse.
By the time it was the seventh day, God had finished the work of creating everything, so he did not work any more on that day.
3 Ndipo Mulungu anadalitsa tsiku lachisanu ndi chiwiri nalipatula, chifukwa pa tsiku limeneli Iye anapumula ku ntchito yonse yolenga imene anayigwira.
God blessed each seventh day, and he set those days apart to be special days, because on the seventh day God did not work any more, after finishing all his work of creating everything.
4 Mbiri ya momwe kumwamba ndi dziko lapansi zinalengedwera pa tsiku lija Yehova Mulungu ankazilenga ndi iyi: Yehova Mulungu atapanga dziko lapansi ndi kumwamba,
That is how God created the heavens and the earth. God, whose name is Yahweh, made the heavens and the earth.
5 zitsamba zinali zisanamere ndipo chomera chilichonse chinali chisanamerenso popeza Yehova Mulungu anali asanagwetse mvula pa dziko lapansi. Panalibe munthu wolima nthaka,
At first there were no plants growing, because Yahweh God had not yet caused rain to fall on the ground. Furthermore, there was no one to till the ground for planting crops.
6 koma kasupe ankatuluka mʼnthaka ndi kuthirira pa dziko lonse.
Instead, mist rose up from the ground, so that it watered the surface of the ground.
7 Tsono Yehova Mulungu anawumba munthu kuchokera ku dothi nawuziramo mpweya wamoyo mʼmphuno mwake ndipo munthuyo anakhala wamoyo.
Then Yahweh God took some soil and formed a man. He breathed into the man’s nostrils his own breath that gives life, and as a result the man became a living person.
8 Kenaka Yehova Mulungu anatsekula munda wa Edeni chakummawa; kumeneko anayikako munthu amene anamupanga uja.
Yahweh God made a park/garden in a place named Eden, which was east of the land of Canaan, and he put there the man that he had created.
9 Ndipo Yehova Mulungu anameretsa mʼmundamo mitengo ya mitundu yonse. Inali mitengo yokongola ndi ya zipatso zokoma. Pakati pa munda uja panali mtengo wopatsa moyo ndi mtengo wopatsa nzeru zodziwitsa chabwino ndi choyipa.
Yahweh God also put there every kind of tree that is beautiful to see and that produced fruit that was good to eat. He also placed in the middle of the park/garden a tree [whose fruit would enable those who ate it] to live forever. He also placed there another tree whose fruit would enable those who ate it to know what actions were good [to do] and what actions were evil [to do].
10 Mtsinje wothirira mundawo unkatuluka mu Edeni; kuchokera apo unkagawikana kukhala mitsinje inayi.
A river flowed from Eden to provide water for the park/garden. Outside of Eden, the river divided into four rivers.
11 Dzina la mtsinje woyamba ndi Pisoni; uwu umazungulira dziko lonse la Havila, kumene kuli golide.
The name of the first river is Pishon. That river flows through all the land of Havilah, where there is gold.
12 (Golide wa ku dziko ili ndi wabwino. Kulinso miyala yokongola ya bedola ndi onikisi).
That gold (is very pure/has no impurities in it). There is [also a sweet-smelling gum called] bdellium, and valuable stones called onyx.
13 Dzina la mtsinje wachiwiri ndi Gihoni; uwu umazungulira dziko lonse la Kusi.
The name of the second river is Gihon. That river flows through all the land of Cain.
14 Dzina la mtsinje wachitatu ndi Tigirisi; umayenda chakummawa kwa Asiriya. Ndipo mtsinje wachinayi ndi Yufurate.
The name of the third river is Tigris. It flows east of [the city of] Asshur. The name of the fourth river is Euphrates.
15 Yehova Mulungu anatenga munthu uja ndi kumuyika mʼmunda wa Edeni kuti awulime ndi kuwusamalira.
Yahweh God took the man and put him in Eden park/garden to till/cultivate it and take care of it.
16 Ndipo Yehova Mulungu analamula munthu uja kuti, “Uzidya zipatso za mu mtengo wina uliwonse mʼmundamu;
But Yahweh said to him, “You must not eat the fruit of the tree that will enable you to know what actions are good to do and what actions are evil to do. If you eat any fruit from that tree, on that day your relationship with me will end. But I will permit you to eat the fruit of any of the other trees in the park/garden.”
17 koma usadye zipatso za mu mtengo wodziwitsa chabwino ndi choyipa, popeza ukadzadya za mu mtengowu udzafa ndithu.”
18 Ndipo Yehova Mulungu anati, “Sibwino kuti munthu akhale yekha. Ndidzamupangira mnzake womuthandiza.”
Then Yahweh God said, “It is not good for this man to be alone. So I will make someone who will be a suitable partner for him.”
19 Kenaka Yehova Mulungu anawumba ndi dothi nyama zonse zakuthengo ndi mbalame zonse zamlengalenga. Ndipo Iye anapita nazo kwa munthu uja kuti akazipatse mayina; ndipo dzina lililonse limene Adamu anapereka ku chamoyo chilichonse, lomwelo linakhala dzina lake.
Yahweh God had taken some soil and had formed from it all kinds of animals and birds, and he brought them to the man to hear what names he would give them.
20 Choncho Adamu anazitcha mayina ziweto zonse, mbalame zamlengalenga ndi nyama zakuthengo zonse. Komabe munthu uja analibe mnzake womuthandiza.
Then the man gave names to all the kinds of livestock and birds and wild animals, but none of these creatures was a partner that was suitable for the man.
21 Tsono Yehova Mulungu anamugonetsa munthu uja tulo tofa nato; ali mtulo chomwecho, Mulungu anachotsa imodzi mwa nthiti zake ndi kutseka pamalopo ndi mnofu.
So Yahweh God caused the man to fall into a deep sleep. While the man was sleeping, Yahweh took out one of the man’s ribs. Then he immediately closed the opening in his body [and healed it].
22 Motero Yehova Mulungu anapanga mkazi ndi nthiti ija imene anatenga kwa munthu uja nabwera naye kwa iye.
Yahweh then made a woman from the rib that he had taken from the man’s body, and he brought her to the man.
23 Munthu uja anati, “Uyu ndiye fupa lochokera ku mafupa anga ndi mnofu wochokera ku mnofu wanga; adzatchedwa ‘mkazi,’ popeza wachokera mwa mwamuna.”
The man exclaimed, “[Wow]! This is truly (someone like me/what I was looking for!) She is truly from my bones and from my flesh. So I will call her woman, because she was taken from me, a man.”
24 Nʼchifukwa chake, mwamuna amasiya abambo ndi amayi ake nakaphatikana ndi mkazi wake ndipo awiriwo amakhala thupi limodzi.
[The first woman was taken from the man’s body, ] so that is why when a man and a woman marry, they must leave their parents. The man will join very closely to his wife, so that the two of them will be as though they are one person.
25 Munthu uja ndi mkazi wakeyo, onse awiri anali maliseche ndipo analibe manyazi.
Although the man and his wife were naked, they were not ashamed about that.

< Genesis 2 >