< Genesis 19 >

1 Angelo awiri aja anafika ku Sodomu madzulo ndipo Loti anali atakhala pansi pa chipata cha mzindawo. Loti atawaona, anayimirira ndi kukakumana nawo ndipo anaweramitsa mutu wake pansi mwaulemu.
And the two angels came to Sodom at even; and Lot sat in the gate of Sodom; and Lot saw them, and rose up to meet them; and he fell down on his face to the earth;
2 Iye anati, “Ambuye wanga, chonde patukirani ku nyumba kwa mtumiki wanu. Mukhoza kusambitsa mapazi anu ndi kugona usiku uno kenaka nʼkumapitirira ndi ulendo wanu mmamawa.” Iwo anati, “Ayi, tigona panja.”
and he said: 'Behold now, my lords, turn aside, I pray you, into your servant's house, and tarry all night, and wash your feet, and ye shall rise up early, and go on your way.' And they said: 'Nay; but we will abide in the broad place all night.'
3 Koma iye anawawumiriza kwambiri kotero kuti anapita naye pamodzi ku nyumba kwake. Anawakonzera chakudya buledi wopanda yisiti ndipo anadya.
And he urged them greatly; and they turned in unto him, and entered into his house; and he made them a feast, and did bake unleavened bread, and they did eat.
4 Alendo aja asanapite kogona, amuna onse achinyamata ndi achikulire ochokera mbali zonse za mzinda wa Sodomu anazinga nyumba ya Loti.
But before they lay down, the men of the city, even the men of Sodom, compassed the house round, both young and old, all the people from every quarter.
5 Iwo anayitana Loti namufunsa kuti, “Ali kuti amuna aja amene afika kuno usiku womwe uno? Atulutse, utipatse kuti tigone nawo malo amodzi.”
And they called unto Lot, and said unto him: 'Where are the men that came in to thee this night? bring them out unto us, that we may know them.'
6 Loti anatuluka panja kukakumana nawo natseka chitseko
And Lot went out unto them to the door, and shut the door after him.
7 ndipo anati, “Ayi anzanga, musachite zinthu zoyipa zotere.
And he said: 'I pray you, my brethren, do not so wickedly.
8 Taonani, ine ndili ndi ana anga akazi awiri amene sanagonepo ndi mwamuna. Mundilole ndikutulutsireni amenewo ndipo muchite nawo zimene mungafune. Koma musachite chilichonse ndi anthuwa, pakuti iwowa ndi alendo anga ndipo ndiyenera kuwatchinjiriza.”
Behold now, I have two daughters that have not known man; let me, I pray you, bring them out unto you, and do ye to them as is good in your eyes; only unto these men do nothing; forasmuch as they are come under the shadow of my roof.'
9 Iwo anayankha kuti, “Tachoka apa tidutse.” Ndipo anati, “Munthu uyu anabwera kuno ngati mlendo chabe, tsono lero akufuna kuti akhale wotiweruza! Tikukhawulitsa kuposa iwowa.” Anapitiriza kumuwumiriza Loti uja nʼkumasunthira kutsogolo kuti athyole chitseko.
And they said: 'Stand back.' And they said: 'This one fellow came in to sojourn, and he will needs play the judge; now will we deal worse with thee, than with them.' And they pressed sore upon the man, even Lot, and drew near to break the door.
10 Koma anthu aja anali mʼkatiwa anasuzumira namukokera Loti uja mʼkati mwa nyumba nʼkutseka chitseko.
But the men put forth their hand, and brought Lot into the house to them, and the door they shut.
11 Kenaka anawachititsa khungu anthu amene anali panja pa nyumba aja, aangʼono ndi aakulu omwe, kuti asaone pa khomo.
And they smote the men that were at the door of the house with blindness, both small and great; so that they wearied themselves to find the door.
12 Anthu awiri aja anati kwa Loti, “Kodi uli ndi wina aliyense pano, kaya ndi akamwini ako, kaya ndi ana ako aamuna kapena aakazi, kapena aliyense mu mzindamu amene ndi anzako? Atulutse onse muno,
And the men said unto Lot: 'Hast thou here any besides? son-in-law, and thy sons, and thy daughters, and whomsoever thou hast in the city; bring them out of the place;
13 chifukwa tiwononga malo ano. Yehova waona kuti kuyipa kwa anthu a mu mzindawu kwakulitsa. Choncho watituma kuti tiwuwononge.”
for we will destroy this place, because the cry of them is waxed great before the LORD; and the LORD hath sent us to destroy it.'
14 Choncho Loti anatuluka nayankhula ndi akamwini ake amene anali kuyembekezera kukwatira ana ake akazi nati, “Fulumirani, tiyeni tichoke pa malo ano chifukwa Yehova watsala pangʼono kuwononga mzindawu.” Koma akamwini akewo ankayesa kuti akungoselewula.
And Lot went out, and spoke unto his sons-in-law, who married his daughters, and said: 'Up, get you out of this place; for the LORD will destroy the city.' But he seemed unto his sons-in-law as one that jested.
15 Mmene kumacha, angelo aja anamufulumizitsa Loti nati, “Nyamuka, tenga mkazi wako ndi ana ako aakazi awiriwo, ndipo mutuluke mu mzindawo kuopa kuti mungaphedwe pamodzi nawo.”
And when the morning arose, then the angels hastened Lot, saying: 'Arise, take thy wife, and thy two daughters that are here; lest thou be swept away in the iniquity of the city.'
16 Koma Loti ankakayikabe. Koma Yehova anawachitira chifundo motero kuti anthu aja anagwira mkazi wake ndi ana ake aakazi aja nawatsogolera bwinobwino kuwatulutsa mu mzindawo.
But he lingered; and the men laid hold upon his hand, and upon the hand of his wife, and upon the hand of his two daughters; the LORD being merciful unto him. And they brought him forth, and set him without the city.
17 Atangowatulutsa, mmodzi wa angelowo anati, “Thawani kuti mudzipulumutse, musachewuke, musayime pena paliponse mʼchigwamo! Thawirani ku mapiri kuopa kuti mungawonongeke!”
And it came to pass, when they had brought them forth abroad, that he said: 'Escape for thy life; look not behind thee, neither stay thou in all the Plain; escape to the mountain, lest thou be swept away.'
18 Koma Loti anawawuza kuti, “Ayi, ambuye anga chonde musatero!
And Lot said unto them: 'Oh, not so, my lord;
19 Taonani, Inu mwachitira mtumiki wanu chifundo, ndipo mwaonetsa kukoma mtima kwanu pondipulumutsa. Sindingathawire ku mapiri chifukwa chiwonongekochi chikhoza kundipeza ndisanafike ku mapiriko ndipo ndingafe.
behold now, thy servant hath found grace in thy sight, and thou hast magnified thy mercy, which thou hast shown unto me in saving my life; and I cannot escape to the mountain, lest the evil overtake me, and I die.
20 Koma, chapafupi pomwepa pali mudzi woti ndikhoza kuthamanga nʼkukafikako. Mundilole ndithawireko, ndi waungʼono kwambiri, si choncho? Mukatero, moyo wanga upulumuka.”
Behold now, this city is near to flee unto, and it is a little one; oh, let me escape thither — is it not a little one? — and my soul shall live.'
21 Mngeloyo anati kwa iye, “Chabwino, ndavomeranso pempho lako, sindiwononga mudzi ukunenawo.
And he said unto him: 'See, I have accepted thee concerning this thing also, that I will not overthrow the city of which thou hast spoken.
22 Koma uthawireko mofulumira chifukwa sindichita kena kalikonse mpaka utafikako.” (Nʼchifukwa chake mudziwo unatchedwa Zowari).
Hasten thou, escape thither; for I cannot do any thing till thou be come thither.' — Therefore the name of the city was called Zoar. —
23 Pamene Loti amafika ku Zowari, nʼkuti dzuwa litatuluka.
The sun was risen upon the earth when Lot came unto Zoar.
24 Ndiye Yehova anathira sulufule wamoto wochokera kumwamba kwa Yehova pa Sodomu ndi Gomora.
Then the LORD caused to rain upon Sodom and upon Gomorrah brimstone and fire from the LORD out of heaven;
25 Kotero, anawononga mizindayo, chigwa chonse pamodzi ndi onse okhala mʼmizindayo. Anawononganso zomera zonse za mʼdzikolo.
and He overthrow those cities, and all the Plain, and all the inhabitants of the cities, and that which grew upon the ground.
26 Koma mkazi wa Loti anachewuka ndipo anasanduka mwala wa mchere.
But his wife looked back from behind him, and she became a pillar of salt.
27 Mmawa mwake, Abrahamu ananyamuka nabwerera kumalo kumene anakumana ndi Yehova kuja.
And Abraham got up early in the morning to the place where he had stood before the LORD.
28 Anayangʼana kumunsi ku Sodomu, Gomora ndi ku dziko lonse la ku chigwa, ndipo anaona chiwutsi chikufuka mʼdzikolo ngati chikuchokera mʼngʼanjo.
And he looked out toward Sodom and Gomorrah, and toward all the land of the Plain, and beheld, and, lo, the smoke of the land went up as the smoke of a furnace.
29 Choncho Mulungu anawononga mizinda ya ku chigwa, koma anakumbukira pemphero la Abrahamu natulutsa Loti ku sulufule ndi moto zimene zinawononga mizinda ya kumene Loti amakhalako.
And it came to pass, when God destroyed the cities of the Plain, that God remembered Abraham, and sent Lot out of the midst of the overthrow, when He overthrew the cities in which Lot dwelt.
30 Loti ndi ana ake awiri aakazi anachoka ku Zowari nakakhala ku mapiri, chifukwa amachita mantha kukhala ku Zowari. Iye ndi ana ake awiri ankakhala mʼphanga.
And Lot went up out of Zoar, and dwelt in the mountain, and his two daughters with him; for he feared to dwell in Zoar; and he dwelt in a cave, he and his two daughters.
31 Tsiku lina mwana wake wamkazi wamkulu anawuza mngʼono wake kuti, “Abambo athu ndi wokalamba ndipo palibe mwamuna aliyense pano woti atikwatire ndi kubereka ana monga mwa chikhalidwe cha pa dziko lonse lapansi.
And the first-born said unto the younger: 'Our father is old, and there is not a man in the earth to come in unto us after the manner of all the earth.
32 Tiye tiwamwetse vinyo ndipo tigone nawo. Tikatero mtundu wathu udzakhalapobe.”
Come, let us make our father drink wine, and we will lie with him, that we may preserve seed of our father.'
33 Usiku umenewo analedzeretsa vinyo abambo awo, ndipo wamkuluyo analowa nagona naye. Abambo awo samadziwa kanthu pamene mwanayo anagona naye kapena pamene anadzuka.
And they made their father drink wine that night. And the first-born went in, and lay with her father; and he knew not when she lay down, nor when she arose.
34 Tsiku linali mwana wamkazi wamkulu uja anati kwa mngʼono wake, “Usiku wathawu ine ndinagona ndi abambo anga. Tiye tiwaledzeretsenso vinyo usiku uno ndipo iwe upite ndi kugona nawo ndipo mtundu wathu udzakhalapobe.”
And it came to pass on the morrow, that the first-born said unto the younger: 'Behold, I lay yesternight with my father. Let us make him drink wine this night also; and go thou in, and lie with him, that we may preserve seed of our father.'
35 Choncho analedzeranso vinyo abambo awo usiku umenewonso, ndipo mwana wamkazi wamngʼono anapita nagona nawo. Abambo awo sanadziwenso kanthu pamene mwanayo anagona naye kapena pamene anadzuka.
And they made their father drink wine that night also. And the younger arose, and lay with him; and he knew not when she lay down, nor when she arose.
36 Choncho ana onse awiri a Loti aja anatenga pathupi pa abambo awo.
Thus were both the daughters of Lot with child by their father.
37 Mwana wamkazi wamkulu uja anabereka mwana wa mwamuna ndipo anamutcha Mowabu. Iyeyo ndiye kholo la Amowabu onse.
And the first-born bore a son, and called his name Moab — the same is the father of the Moabites unto this day.
38 Mwana wamkazi wamngʼono naye anabereka mwana wamwamuna, ndipo anamutcha iye Beni-Ammi. Iyeyu ndiye kholo la Aamoni onse.
And the younger, she also bore a son, and called his name Ben-ammi — the same is the father of the children of Ammon unto this day.

< Genesis 19 >