< Genesis 18 >

1 Yehova anadza kwa Abrahamu pafupi ndi mitengo ikuluikulu ya thundu ya ku Mamre. Abrahamu nʼkuti atakhala pansi pa khoma la tenti yake masana, dzuwa likutentha.
Poslije mu se javi Gospod u ravnici Mamrijskoj kad sjeðaše na vratima pred šatorom svojim u podne.
2 Tsono Abrahamu atakweza maso ake patali anangoona anthu atatu atayima cha potero. Atawaona, ananyamuka mofulumira kuti awachingamire. Atafika anaweramitsa mutu pansi mwa ulemu nati,
Podigavši oèi svoje pogleda, i gle, tri èovjeka stajahu prema njemu. I ugledavši ih potrèa im na susret ispred vrata šatora svojega, i pokloni se do zemlje;
3 “Ngati mwandikomera mtima, mbuye wanga, musamulambalale mtumiki wanu.
I reèe: Gospode, ako sam našao milost pred tobom, nemoj proæi sluge svojega.
4 Ndikupatseniko timadzi pangʼono kuti nonse musambitse mapazi anu ndi kupumula pansi pa mtengo uwu.
Da vam donesemo malo vode i operite noge, te se naslonite malo pod ovijem drvetom.
5 Tsono ndikutengereniko kachakudya kuti mudye kuti mwina nʼkupezako mphamvu zopitirizira ulendo wanu. Inu mwafika kumalo kwa mtumiki wanu.” Ndipo iwo anamuyankha nati, “Zikomo kwambiri, chita monga wanenera.”
I iznijeæu malo hljeba, te potkrijepite srce svoje, pa onda poðite, kad idete pored sluge svojega. I rekoše: uèini što si kazao.
6 Choncho Abrahamu anafulumira kupita kwa Sara mʼtenti nati, “Tafulumira, tenga mabeseni atatu a ufa wosalala, ukande ndi kupanga buledi.”
I Avram otrèa u šator k Sari, i reèe: brže zamijesi tri kopanje bijeloga brašna i ispeci pogaèe.
7 Kenaka Abrahamu anakatenga mwana wangʼombe wonenepa ndi wofewa bwino ndi kupatsa wantchito wake amene anachita changu kukonza ndiwoyo.
Pa otrèa ka govedima i uhvati tele mlado i dobro, i dade ga momku da ga brže zgotovi.
8 Tsono Abrahamu anatenga chambiko, mkaka ndi mwana wangʼombe wokonzedwa uja nazipereka kwa anthu aja. Alendowo akudya, Abrahamu ankawayangʼana atayimirira pansi pa mtengo.
Pa onda iznese masla i mlijeka i tele koje bješe zgotovio, i postavi im, a sam stajaše pred njima pod drvetom dokle jeðahu.
9 Anthuwo anafunsa Abrahamu kuti, “Mkazi wako Sara ali kuti?” Iye anati, “Ali mu tentimu.”
I oni mu rekoše: gdje je Sara žena tvoja? A on reèe: eno je pod šatorom.
10 Tsono mmodzi mwa iwo anati, “Mosakayikira ndidzabweranso pa nthawi ngati yomwe ino chaka chamawa, ndipo Sara mkazi wako adzakhala ndi mwana wamwamuna.” Koma Sara amene anali kumbuyo kwa Abrahamu pa khoma la tenti ankamva zonsezi.
A jedan izmeðu njih reèe: do godine u ovo doba opet æu doæi k tebi, a Sara æe žena tvoja imati sina. A Sara slušaše na vratima od šatora iza njega.
11 Abrahamu ndi Sara anali okalamba kale ndipo anali ndi zaka zambiri. Sara nʼkuti atapyola kale pa msinkhu oti nʼkubereka.
A Avram i Sara bijahu stari i vremeniti, i u Sare bješe prestalo što biva u žena.
12 Choncho anangoseka nati mu mtima mwake, “Kodi munthu wothayitha ngati ine ndingasangalalenso kugona pamodzi ndi mbuye wanga? Mwamuna wanga nayenso ndi wokalamba.”
Zato se nasmija Sara u sebi govoreæi: pošto sam ostarjela, sad li æe mi doæi radost? a i gospodar mi je star.
13 Ndipo Yehova anati kwa Abrahamu, “Nʼchifukwa chiyani Sara anaseka nʼkumati, ‘Moti ine nʼkudzakhaladi ndi mwana mmene ndakalambiramu?’
Tada reèe Gospod Avramu: što se smije Sara govoreæi: istina li je da æu roditi kad sam ostarjela?
14 Kodi pali chimene chikhoza kumukanika Yehova? Pa nthawi yake, ngati yomwe ino chaka chamawa ndidzabweranso, ndipo Sara adzabala mwana wamwamuna.”
Ima li što teško Gospodu? Do godine u ovo doba opet æu doæi k tebi, a Sara æe imati sina.
15 Koma Sara ndi mantha ananama nati, “Sindinaseke.” Koma Iye anati, “Inde iwe unaseka.”
A Sara udari u bah govoreæi: nijesam se smijala. Jer se uplaši. Ali on reèe: nije istina, nego si se smijala.
16 Kenaka anthu aja ananyamuka ndi kumapita, molunjika ku Sodomu. Ndipo Abrahamu anayenda nawo pamodzi kuwaperekeza.
Potom ustaše ljudi odande, i poðoše put Sodoma; i Avram poðe s njima da ih isprati.
17 Tsono Yehova anati mu mtima mwake, “Kodi ndingamubisire Abrahamu chimene ndikuti ndichite posachedwa?
A Gospod reèe: kako bih tajio od Avrama šta æu uèiniti,
18 Abrahamu adzakhaladi mtundu wa anthu waukulu ndi wamphamvu, ndipo mitundu yonse ya anthu pa dziko lapansi adzadalitsika kudzera mwa iye.
Kad æe od Avrama postati velik i silan narod, i u njemu æe se blagosloviti svi narodi na zemlji?
19 Pakuti ndasankha iyeyu kuti adzatsogolere ana ake ndi a pa banja lake, kuti asunge mawu a Yehova pochita zoyenera ndi zachilungamo. Choncho Yehova adzachita kwa Abrahamu chimene anamulonjeza iye.”
Jer znam da æe zapovjediti sinovima svojima i domu svojemu nakon sebe da se drže putova Gospodnjih i da èine što je pravo i dobro, da bi Gospod navršio na Avramu što mu je obeæao.
20 Ndipo Yehova anati kwa Abrahamu, “Kulirira Gomora kwakula ndipo tchimo lawo lafika poyipa kwambiri
I reèe Gospod: vika je u Sodomu i Gomoru velika, i grijeh je njihov grdan.
21 choncho ndikuti ndipiteko ndikaone ngati zimene achita zilidi zoyipa monga mmene madandawulo andipezera Ine. Ngati sizili choncho, ndikadziwa.”
Zato æu siæi da vidim eda li sve èine kao što vika doðe preda me; ako li nije tako, da znam.
22 Anthu aja anatembenuka nʼkumapita, kulowera ku Sodomu, koma Abrahamu anali chiyimirire pamaso pa Yehova.
I ljudi okrenuvši se poðoše put Sodoma; ali Avram još stajaše pred Gospodom,
23 Kenaka Abrahamu anasendera kufupi ndi Iye nati, “Kodi mudzawonongera kumodzi wolungama ndi woyipa?
I pristupiv Avram reèe: hoæeš li pogubiti i pravednoga s nepravednim?
24 Nanga bwanji patakhala anthu makumi asanu olungama mu mzindamo? Kodi mudzawonongadi onse osausiyako mzindawo chifukwa cha anthu makumi asanu olungama omwe ali mʼmenemo?
Može biti da ima pedeset pravednika u gradu; hoæeš li i njih pogubiti, i neæeš oprostiti mjestu za onijeh pedeset pravednika što su u njemu?
25 Ndithu simungachite zimenezi, kupha anthu olungama pamodzi ndi oyipa. Nʼzosatheka kuti inu nʼkufananitsa olungama ndi oyipa. Kodi woweruza wa dziko lapansi nʼkulephera kuchita chilungamo?”
Nemoj to èiniti, ni gubiti pravednika s nepravednikom, da bude pravedniku kao i nepravedniku; nemoj; eda li sudija cijele zemlje neæe suditi pravo?
26 Yehova anati, “Nditapeza anthu makumi asanu olungama mu mzinda wa Sodomu, ndidzasiya malo onsewo osawawononga chifukwa cha iwo.”
I reèe Gospod: ako naðem u Sodomu pedeset pravednika u gradu, oprostiæu cijelom mjestu njih radi.
27 Ndipo Abrahamu anayankhulanso nati, “Tsono poti ndalimba mtima kuyankhula ndi Ambuye, ngakhale kuti ndine fumbi ndi phulusa chabe,
A Avram odgovori i reèe: gle, sada bih progovorio Gospodu, ako i jesam prah i pepeo.
28 bwanji anthu olungama atacheperapo ndi asanu pa anthu makumi asanu? Kodi mudzawononga mzinda wonse chifukwa cha asanuwo?” Iye anati, “Nditapezamo anthu 45, sindidzawuwononga.”
Može biti pravednika pedeset manje pet, hoæeš li za ovijeh pet zatrti sav grad? Odgovori: neæu, ako naðem èetrdeset i pet.
29 Kenakanso anayankhula kwa Iye nati, “Bwanji atangopezekamo anthu 40 okha?” Iye anayankha, “Chifukwa cha anthu 40 amenewa, sindidzatero.”
I stade dalje govoriti, i reèe: može biti da æe se naæi èetrdeset. Reèe: neæu radi onijeh èetrdeset.
30 Ndipo Abrahamu anati, “Pepanitu musandipsere mtima Ambuye, koma mundilole kuti ndiyankhule. Nanga mutapezekamo anthu makumi atatu okha?” Iye anayankha, “Sindidzatero ngati atapezekamo anthu makumi atatu.”
Potom reèe: nemoj se gnjeviti, Gospode, što æu reæi; može biti da æe se naæi trideset. I reèe: neæu, ako naðem trideset.
31 Abrahamu anati, “Tsono poti ndalimba mtima chonchi kumayankhula ndi Ambuye, bwanji atangopezeka anthu makumi awiri okha?” Iye anati, “Chifukwa cha anthu makumi awiriwo, sindidzawuwononga.”
Opet reèe: gle, sada bih progovorio Gospodu; može biti da æe se naæi dvadeset. Reèe: neæu ih pogubiti za onijeh dvadeset.
32 Kenaka Abrahamu anati, “Pepani Ambuye musandipsere mtima, ndingoyankhula kamodzi kokhaka basi. Bwanji atangopezeka khumi okha mʼmenemo?” Iye anayankha nati, “Chifukwa cha khumiwo, sindidzawuwononga.”
Najposlije reèe: nemoj se gnjeviti, Gospode, što æu još jednom progovoriti; može biti da æe se naæi deset. Reèe: neæu ih pogubiti radi onijeh deset.
33 Yehova atatsiriza kuyankhula ndi Abrahamu, anachoka ndipo Abrahamu anabwerera ku nyumba yake.
I Gospod otide svršivši razgovor s Avramom; a Avram se vrati na svoje mjesto.

< Genesis 18 >