< Genesis 16 >

1 Tsono Sarai, mkazi wa Abramu anali asanamuberekere ana Abramuyo. Koma anali ndi wantchito wamkazi wa ku Igupto dzina lake Hagara;
Sarai Abrams wyfe bare him no childerne. But she had an hand mayde an Egiptian whose name was Hagar.
2 ndipo Sarai anati kwa Abramu, “Yehova sanalole kuti ine ndikhale ndi ana. Bwanji mulowe mwa wantchito wanga wamkaziyu kuti mwina ndingaone ana kudzera mwa iyeyu.” Abramu anamvera Sarai.
Wherfore the sayde vnto Abram. Beholde the LORde hath closed me that I can not bere. I praye the goo in vnto my mayde peradueture I shall be multiplyed by meanes of her And Abram herde the voyce of Sarai. Than Sarai
3 Tsono Sarai anatenga Hagara wantchito wake wamkazi wa ku Igupto uja namupereka kwa Abramu mwamuna wake kuti akhale mkazi wake. Izi zinachitika Abramu atakhala ku Kanaani zaka khumi.
Abrams wife toke Hagar hyr mayde the Egitian (after Abram had dwelled. x. yere in the lande of Canaan) and gaue her to hyr husbonde Abram to be his wyfe.
4 Abramu atalowana ndi Hagara, Hagara uja anatenga mimba. Pamene Hagara anadziwa kuti anali woyembekezera anayamba kunyoza mbuye wake Sarai.
And he wente in vnto Hagar and she conceaved. And when she sawe that she had conceyved hyr mastresse was despised in hyr syghte.
5 Pamenepo Sarai anati kwa Abramu, “Inu ndinu amene mwandiputira nkhanza zikundichitikirazi. Ndinakupatsani wantchito wanga wamkazi kuti akhale mkazi wanu, ndiye tsopano wayamba kundinyoza ine chifukwa wadziwa kuti ndi woyembekezera. Yehova ndiye amene aweruze pakati pa inu ndi ine.”
Than sayd Sarai vnto Abram: Thou dost me vnrighte for I haue geuen my mayde in to thy bosome: and now because she seyth that she hath coceaved I am despysed in hyr syghte: the LORde iudge betwene the and me.
6 Abramu anati, “Wantchito wakoyu ali mʼmanja mwako. Chita naye chilichonse chimene ukuganiza kuti ndi chokukomera.” Tsono Sarai anazunza Hagara mpaka anathawa.
Than sayde Abra to Sarai: beholde thy mayde is in thy hande do with hyr as it pleaseth the. And because Sarai fared foule with her she fled from her.
7 Mngelo wa Yehova anamupeza Hagara pafupi ndi chitsime mʼchipululu. Chinali chitsime chimene chili mʼmphepete mwa msewu wopita ku Suri.
And the angell of the LORde founde her besyde a fountayne of water in the wyldernes: euen by a well in the way to Sur.
8 Ndipo mngeloyo anati, “Hagara, iwe wantchito wa Sarai, ukuchokera kuti ndipo ukupita kuti?” Iye anayankha, “Ndikuthawa mbuye wanga Sarai.”
And he sayde: Hagar Sarais mayde whence comest thou and whether wylt thou goo? And she answered: I flee from my mastresse Sarai.
9 Mngelo wa Yehova anamuwuza kuti, “Bwerera kwa mbuye wako ndipo ukamugonjere.
And the angell of the LORde sayde vnto her: returne to thy mastresse agayne and submytte thy selfe vnder her handes.
10 Ndidzakupatsa zidzukulu zambiri zoti munthu sangaziwerenge.”
And the angell of ye LORde sayde vnto her: I will so encrease thy seed that it shall not be numbred for multitude.
11 Mngelo wa Yehova uja anamuwuzanso kuti, “Ndiwe woyembekezera ndipo udzabala mwana wamwamuna. Udzamutcha dzina lake Ismaeli, pakuti Yehova wamva kulira chifukwa cha kuzunzika kwako.
And the LORdes angell sayd further vnto her: se thou art wyth childe and shalt bere a sonne and shalt call his name Ismael: because the LORDE hath herde thy tribulation.
12 Iye adzakhala munthu wa khalidwe ngati mʼmbulu wamisala; adzadana ndi aliyense ndipo anthu onse adzadana naye, adzakhala mwaudani pakati pa abale ake onse.”
He will be a wylde man and his hande will be agenst every man and euery mans hande agenst him. And yet shall he dwell faste by all his brothren.
13 Hagara anatcha Yehova amene anamuyankhula uja dzina loti: “Ndinu Mulungu amene mumandiona,” popeza anati, “Ndakumana ndi Yehova atatha kundikomera mtima.”
And she called the name of the LORde that spake vnto her: thou art the God that lokest on me for she sayde: I haue of a suertie sene here the backe parties of him that seith me.
14 Nʼchifukwa chake chitsime chija chimene chili pakati pa Kadesi ndi Beredi chinatchedwa Beeri-lahai-roi.
Wherfore she called the well the well of the lyuynge that seith me which well is betwene Cades and Bared.
15 Tsono Hagara anamuberekera Abramu mwana wamwamuna ndipo Abramu anamutcha mwanayo Ismaeli.
And Hagar bare Abram a sonne and Abram called his sons name which Hagar bare Ismaell.
16 Pamene Hagara anamubalira Ismaeli nʼkuti Abramuyo ali ndi zaka 86.
And Abram was. lxxxvi. yere olde when Hagar bare him Ismael.

< Genesis 16 >