< Genesis 15 >

1 Zitatha izi, Yehova anayankhula ndi Abramu mʼmasomphenya nati: “Usaope Abramu. Ine ndili ngati chishango chokutchinjiriza. Mphotho yako idzakhala yayikulu.”
After these things, came the word of Yahweh unto Abram, in a vision saying, —Do not fear Abram, I am a shield to thee, thine exceeding great reward.
2 Koma Abramu anati, “Haa! Ambuye Yehova, mukhoza kundipatsa chiyani popeza ndikanali wopanda mwana ndipo amene adzatenge chuma changa ndi Eliezara wa ku Damasiko?
And Abram said My Lord Yahweh, what canst thou give me, when, I, am going on childless, —and the heir of my house, is Eliezer, of Damascus,
3 Inu simunandipatse ana kotero kuti wantchito wa ku nyumba kwanga ndiye amene adzalowe mʼmalo mwanga.”
And Abram said—Lo, to me, hast thou not given seed, —And lo! a son of my household, is mine heir!
4 Yehova anayankhula naye nati: “Munthu uyu sadzalowa mʼmalo mwako, koma mwana wako weniweni wamwamuna, wobereka wekha ndiye adzalowe mʼmalo mwako.”
And lo! the word of Yahweh [came] unto him, saying, This one, shall not be thine heir: But one who cometh forth of thy body—he shall be thine heir.
5 Yehova anapita naye Abramu panja nati, “Tayangʼana kumwambaku, ndipo chifukwa cha chimenechi uwerenge nyenyezi ngati ungathe kuziwerenga.” Ndipo anamuwuza kuti, “Ndi mmene adzakhalire ana ako ndi zidzukulu zako.”
And he brought him forth abroad and said—Look steadfastly. I pray thee towards the heavens, and number the stars, if thou be able to number, them, And he said to him, Thus, shall be thy seed.
6 Abramu anakhulupirira Yehova, ndipo ichi chinamuchititsa kukhala wolungama.
And he had faith in Yahweh, —so he reckoned it to him as righteousness.
7 Ndipo anamuwuza kuti, “Ine ndine Yehova amene ndinakuchotsa iwe ku mzinda wa Uri wa ku Akaldeya kuti ndikupatse dziko ili kuti likhale lako.”
And he said unto him, —I, am Yahweh, who brought thee forth out of Ur of the Chaldees, to give thee this land to inherit it.
8 Koma Abramu anati, “Haa! Ambuye Yehova, kodi ndingadziwe bwanji kuti lidzakhaladi langa?”
And he said, My Lord Yahweh, whereby, can I know that I shall inherit it?
9 Kotero Yehova anati kwa iye, “Kanditengere kamsoti kangʼombe ka zaka zitatu, kamsoti ka mbuzi ka zaka zitatu, ndi nkhosa yayimuna ya zaka zitatu pamodzi ndi nkhunda ndi kamwana ka njiwa.”
And he said unto him, Take for me a heifer three years old, and a she-goat three years old, and a ram three years old, and a turtle-dove and a young pigeon.
10 Abramu anabweretsadi zonsezi nadula chilichonse pakati nʼkuzindandalika, chidutswa chilichonse kuyangʼanana ndi chinzake; koma njiwa ndi nkhunda sanazidule pakati.
So he took for him all these, and divided them, in the midst, and placed each piece over against its fellow, but the birds, divided he not.
11 Pamene miphamba inabwera kuti itole nyama ija, Abramu anayipirikitsa.
Then came down the birds of prey upon the carcass, and Abram drove them away.
12 Pamene dzuwa limalowa Abramu anagona tulo tofa nato ndipo mdima wandiweyani ndi wochititsa mantha unamuphimba.
And it came to pass when, the sun, was about to go in, and, a deep sleep, had fallen upon Abram, lo! a terror a great darkness, was falling upon him.
13 Tsono Yehova anati kwa iye, “Uyenera kudziwa mosakayika kuti zidzukulu zako zidzakhala alendo mʼdziko lachilendo ndipo zidzakhala akapolo ndi kuzunzidwa zaka 400.
And he said to Abram—Thou must surely know, that, sojourners, will thy seed become in a land not theirs, and shall serve them and they will humble them, four hundred years;
14 Koma ndidzalanga dziko limene zidzukulu zako zidzagwireko ukapolo ndipo pambuyo pake iwo adzatulukamo ndi chuma chambiri.
moreover also, the nation whom they will serve, I, am going to judge, and after that, shall they come forth with great substance.
15 Komabe iweyo udzamwalira mu mtendere ndi kuyikidwa mʼmanda utakalamba bwino.
But, thou, shalt go in unto thy fathers in peace, thou shalt be buried in a good old age.
16 Patapita mibado inayi, adzukulu ako adzabwereranso kuno popeza tchimo la Aamori silinafike pachimake kuti alangidwe.”
And, in the fourth generation, shall they return hither, —for not complete, is the iniquity of the Amorites, as yet,
17 Dzuwa litalowa ndipo mdima utagwa, panaoneka mʼphika wofuka nthunzi ya moto ndi sakali yoyaka ndipo zinadutsa pakati pa zidutswa za nyama zija.
So it came to pass when, the sun, had gone in, and, a thick darkness, had come on, that lo there was a smoking hearth and torch of fire, which passed through between these pieces.
18 Pa tsiku limenelo, Yehova anachita pangano ndi Abramu nati, “Ndikulonjeza kuti ndidzapereka dziko ili kwa zidzukulu zako, kuchokera ku mtsinje wa ku Igupto mpaka ku mtsinje waukulu wa Yufurate.
In that day, did Yahweh solemnise with Abram a covenant, saying, —To thy seed, have I given this land, from the river of Egypt as far as the great river—the river Euphrates:
19 Ndidzakupatsani dziko la Akeni, Akenizi, Akadimoni,
the Kenite, and the Kenizzite, and the Kadmonite;
20 Ahiti, Aperezi, Arefaimu,
and the Hittite and the Perizzite, and the Rephaim;
21 Aamori, Akanaani, Agirigasi ndi Ayebusi.”
and the Amorite, and the Canaanite, and the Girgashite, and the Jebusite.

< Genesis 15 >