< Genesis 13 >

1 Choncho Abramu pamodzi ndi mkazi wake ndi zonse anali nazo, anachoka ku Igupto kupita ku Negevi. Loti naye anapita nawo.
And Abram went up out of Egypt, he and his wife, and all that he had, and Lot with him, into the south.
2 Abramu anali wolemera kwambiri; anali ndi ziweto ndiponso siliva ndi golide.
And he was very rich in possession of gold and silver.
3 Atachoka ku Negevi, anayenda malo osiyanasiyana mpaka anafika ku Beteli, ku malo a pakati pa Beteli ndi Ai, kuja kumene anamanga tenti poyamba,
And he returned by the way that he came, from the south to Bethel, to the place where before he had pitched his tent between Bethel and Hai:
4 ndiponso kumene Abramu anamangira Yehova guwa lansembe kwa nthawi yoyamba ndi kupemphera mʼdzina la Yehova.
In the place of the altar which he had made before; and there he called upon the name of the Lord.
5 Loti amene ankayendayenda ndi Abramu nayenso anali ndi ziweto zosiyanasiyana ndi matenti.
But Lot also, who was with Abram, had flocks of sheep, and herds of beasts, and tents.
6 Motero dziko linayamba kuwachepera kuti onse nʼkukhala pamodzi, popeza katundu wawo anali wochuluka kwambiri moti sakanatha kukhala pamodzi.
Neither was the land able to bear them, that they might dwell together: for their substance was great, and they could not dwell together.
7 Mikangano inayambika pakati pa abusa a Abramu ndi abusa a Loti. Nthawi imeneyo nʼkuti Akanaani ndi Aperezi akukhalanso mʼdziko lomwelo.
Whereupon also there arose a strife between the herdsmen of Abram and of Lot. And at that time the Chanaanite and the Pherezite dwelled in that country.
8 Tsono Abramu anati kwa Loti, “Pasakhale mikangano pakati pa iwe ndi ine kapena pakati pa abusa ako ndi anga, popeza ndife abale.
Abram therefore said to Lot: Let there be no quarrel, I beseech thee, between me and thee, and between my herdsmen and thy herdsmen: for we are brethren.
9 Kodi dziko lonseli silili pamaso pako? Tiye tisiyane. Iwe ukalowera kumanzere, ine ndilowera kumanja; ukalowera kumanja, ine ndipita kumanzere.”
Behold the whole land is before thee: depart from me I pray thee: if thou wilt go to the left hand, I will take the right: if thou choose the right hand, I will pass to the left.
10 Loti atamwazamwaza maso anaona kuti chigwa chonse cha mtsinje wa Yorodani chinali chothiriridwa bwino ngati munda wa Yehova, kapena ngati dziko la ku Igupto mpaka ku Zowari. (Nthawi iyi nʼkuti Yehova asanawononge Sodomu ndi Gomora).
And Lot, lifting up his eyes, saw all the country about the Jordan, which was watered throughout, before the Lord destroyed Sodom and Gomorrha, as the paradise of the Lord, and like Egypt as one comes to Segor.
11 Choncho Loti anadzisankhira yekha chigwa chonse cha Yorodani nanyamuka kulowera cha kummawa. Choncho anthu awiriwa anasiyana.
And Lot chose to himself the country about the Jordan, and he departed from the east: and they were separated one brother from the other.
12 Abramu anakhala mʼdziko la Kanaani, pamene Loti anakakhala pakati pa mizinda ikuluikulu ya mʼchigwamo. Anamanga tenti yake pafupi ndi Sodomu.
Abram dwelt in the land of Chanaan; and Lot abode in the towns that were about the Jordan, and dwelt in Sodom.
13 Tsono anthu a ku Sodomu anali oyipa ndiponso ankachimwira Yehova kwambiri.
And the men of Sodom were very wicked, and sinners before the face of the Lord, beyond measure.
14 Loti atachoka, Yehova anati kwa Abramu, “Kuchokera pamene ulipo tayangʼanayangʼana cha kumpoto, kummwera, kummawa ndi kumadzulo.
And the Lord said to Abram, after Lot was separated from him: Lift up thy eyes, and look from the place wherein thou now art, to the north and to the south, to the east and to the west.
15 Dziko lonse ukulionalo ndidzalipereka kwa iwe ndi zidzukulu zako mpaka muyaya.
All the land which thou seest, I will give to thee, and to thy seed for ever.
16 Ndidzakupatsa zidzukulu zochuluka ngati fumbi lapansi moti amene angathe kuwerenga fumbilo ndiye kuti angathenso kuwerenga zidzukulu zako.
And I will make thy seed as the dust of the earth: if any man be able to number the dust of the earth, he shall be able to number thy seed also.
17 Dzuka ndipo uyendere dziko lonseli mulitali ndi mulifupi pakuti ndalipereka kwa iwe.”
Arise and walk through the land in the length, and in the breadth thereof: for I will give it to thee.
18 Choncho Abramu anasamutsa tenti yake napita kukakhala pafupi ndi mitengo ikuluikulu ija ya thundu ya ku Mamre ku Hebroni, kumene anamangira Yehova guwa lansembe.
So Abram removing his tent came and dwelt by the vale of Mambre, which is in Hebron: and he built there an altar to the Lord.

< Genesis 13 >