< Genesis 10 >

1 Nayi mbiri ya ana a Nowa, Semu, Hamu ndi Yafeti. Ana atatuwa anabereka ana awo chitatha chigumula.
Voici les générations des fils de Noé: Sem, Cham et Japhet; des fils leur naquirent après le déluge.
2 Ana aamuna a Yafeti anali: Gomeri, Magogi, Madai, Yavani, Tubala, Mesaki ndi Tirasi.
Fils de Japhet: Gomer, Magog, Madaï, Javan, Elisa, Thubal, Mosoch et Thiras.
3 Ana aamuna a Gomeri anali: Asikenazi, Rifati ndi Togarima.
Fils de Gomer: Ascenez, Riphat, et Thogorma.
4 Ana aamuna a Yavani anali: Elisa, Tarisisi, Kitimu ndi Rodanimu.
Fils de Javan: Elisa, Tharsis, Cettim et Dodanim.
5 (Amenewa ndiwo makolo a anthu okhala mʼmphepete mwa nyanja. Awa ndi ana a Yafeti monga mwa mafuko a mu mitundu yawo, uliwonse ndi chiyankhulo chake).
Ceux-ci sont les pères des gentils, qui se partagèrent les îles et les eurent pour territoire, chacun selon sa langue, par tribus, par nations.
6 Ana aamuna a Hamu anali: Kusi, Miziraimu, Puti ndi Kanaani.
Fils de Cham: Chus, Mesraïm, Phuth et Chanaan.
7 Ana aamuna a Kusi anali: Seba, Havila, Sabita, Raama ndi Sabiteka. Ana aamuna a Raama anali: Seba ndi Dedani.
Fils de Chus: Saba, Hevila, Sabatha, Regma et Sabathaca. Fils de Regma: Saba et Dadan.
8 Kusi anabereka Nimurodi amene anali wankhondo wamphamvu kwambiri pa dziko lapansi.
Et Chus engendra Nemrod: celui-ci commença à être puissant sur la terre.
9 Iye anali mlenje wamphamvu kwambiri pamaso pa Yehova; nʼchifukwa chake anthu ali ndi chisudzo, chakuti, “Ndiwe mlenje wamphamvu kwambiri pamaso pa Yehova monga Nimurodi.”
Il était grand chasseur devant le Seigneur; c'est pourquoi l'on dit: Grand chasseur comme Nemrod devant le Seigneur.
10 Malo oyambirira a ufumu wake anali Babeli, Ereki, Akadi ndi Kaline. Malo onsewa anali mʼdziko la Sinara.
Le commencement de son royaume fut Babylone, puis il eut Arach, Archad, Chalané, et la terre de Sennaar.
11 Atachoka mʼdziko limeneli anapita ku Asiriya kumene anakamanga Ninive, Rehoboti-Iri, Kala,
De cette terre sortit Assur, qui bâtit Ninive, et la ville de Rhooboth et Chalé,
12 ndi Reseni, mzinda waukulu umene uli pakati pa Ninive ndi Kala.
Et Ressen, grande ville, entre Ninive et Chalé.
13 Igupto ndiye kholo la Aludi, Aanami, Alehabu, Anafutu,
Mesraïm engendra les Ludim, les Ananim, les Laabim, les Nephtuïm,
14 Apaturusi, Akasilu ndi Akafitori (kumene kunachokera Afilisti).
Les Phétrusim, les Chasluïm (d'où est sorti Philistin) et les Caphtorins.
15 Kanaani anabereka mwana wake wachisamba, Sidoni, ndipo anaberekanso Ahiti;
Chanaan engendra Sidon son premier-né, puis le Hétéen,
16 Ayebusi, Aamori, Agirigasi;
Le Jebuséen, l'Amorrhéen, le Gergéséen,
17 Ahivi, Aariki, Asini,
L'Evéen, l'Arucéen, l'Asennéen,
18 Aaravadi, Azemari ndi Ahamati. Pambuyo pake, mafuko a Akanaani anafalikira ponseponse,
L'Aradien, le Samaréen et l'Amathéen. Après cela, les tribus des Chananéens se dispersèrent.
19 mpaka ku malire a Kanaani. Malirewo anachokera ku Sidoni kulowa cha ku Gerari mpaka ku Gaza, ndi kulowa ku Sodomu, Gomora, Adima ndi Zeboimu mpaka ku Lasa.
Les limites des Chananéens étaient la côte depuis Sidon jusqu'à Gérara et Gaza; puis elles s'étendirent jusqu'à Sodome et Gomorrhe, et passèrent par Adama et Séboïm jusqu'à Léba.
20 Amenewa ndiwo ana aamuna a Hamu monga mwa mafuko ndi ziyankhulo zawo, mʼmadera omwe amakhala ndi mitundu yawo.
Tels furent les fils de Cham et leurs tribus, selon leurs langues, par contrées, et par nations.
21 Semu amene anali mkulu wake wa Yafeti nayenso anabereka nakhala kholo la Eberi.
Sem fut père aussi, et eut Héber de l'un de ses fils, frère de Japhet le plus grand.
22 Ana aamuna a Semu anali: Elamu, Asuri, Aripakisadi, Ludi ndi Aramu.
Fils de Sem: Elam, Assur, Arphaxad, Lud, Aran et Caïnan.
23 Ana aamuna a Aramu anali: Uzi, Huri, Geteri ndi Mesaki.
Fils d'Aram: Hus, Hul, Gether et Mosoch.
24 Aripakisadi anabereka Sela, ndipo Selayo anabereka Eberi.
Arphaxad engendra Salé, et Salé engendra Héber.
25 A Eberi anabereka ana aamuna awiri: Wina anamutcha Pelegi chifukwa pa nthawiyo anthu a pa dziko lapansi anagawikana. Dzina la mʼbale wake linali Yokitani.
D'Héber naquirent deux fils, nommés, l'un Phaleg, parce que de son temps la terre fut partagée, et l'autre Jectan.
26 Yokitani anabereka Alimodadi, Selefi, Hazari-Maveti, Yera,
Or, Jectan engendra Elmodad, Saleph, Asarmoth Jaré,
27 Hadoramu, Uzali, Dikila,
Aduram, Uzal, Décla,
28 Obali, Abimaeli, Seba,
Abimaël, Saba,
29 Ofiri, Havila ndi Yobabu. Onsewa anali ana aamuna a Yokitani.
Ophir, Hévila et Jobab: tels furent les fils de Jectan.
30 Chigawo chimene ankakhala chinayambira ku Mesa mpaka ku Seferi, ku dera la mapiri chakummawa.
Ils habitèrent depuis Messa jusqu'à Séphar, montagne de l'Orient.
31 Amenewa ndiwo ana a Semu monga mwa mafuko ndi ziyankhulo zawo, mʼmadera omwe ankakhala ndi mitundu yawo.
Tels furent les fils de Sem et leurs tribus, selon leurs langues, par contrées et par nations.
32 Amenewa ndiwo mafuko a ana aamuna a Nowa monga mwa mibado ya mitundu yawo. Mitundu yonse ya anthu inatuluka mwa iwowa ndi kufalikira pa dziko lonse lapansi chitatha chigumula chija.
Telles furent les tribus des fils de Noé, par familles et nations; et c'est ainsi que les fils de Noé peuplèrent les pays des nations, sur la terre, après le déluge.

< Genesis 10 >