< Genesis 10 >

1 Nayi mbiri ya ana a Nowa, Semu, Hamu ndi Yafeti. Ana atatuwa anabereka ana awo chitatha chigumula.
And these are the generations of the sons of Noah: Shem, Ham, and Japheth; and to them were sons born after the flood.
2 Ana aamuna a Yafeti anali: Gomeri, Magogi, Madai, Yavani, Tubala, Mesaki ndi Tirasi.
The sons of Japheth: Gomer, and Magog, and Madai, and Javan, and Tubal, and Meshech, and Tiras.
3 Ana aamuna a Gomeri anali: Asikenazi, Rifati ndi Togarima.
And the sons of Gomer: Ashkenaz, and Riphath, and Togarmah.
4 Ana aamuna a Yavani anali: Elisa, Tarisisi, Kitimu ndi Rodanimu.
And the sons of Javan: Elishah, and Tarshish, Kittim, and Dodanim.
5 (Amenewa ndiwo makolo a anthu okhala mʼmphepete mwa nyanja. Awa ndi ana a Yafeti monga mwa mafuko a mu mitundu yawo, uliwonse ndi chiyankhulo chake).
From these came the distribution of the isles of the nations, according to their lands, every one after his tongue, after their families, in their nations.
6 Ana aamuna a Hamu anali: Kusi, Miziraimu, Puti ndi Kanaani.
And the sons of Ham: Cush, and Mizraim, and Phut, and Canaan.
7 Ana aamuna a Kusi anali: Seba, Havila, Sabita, Raama ndi Sabiteka. Ana aamuna a Raama anali: Seba ndi Dedani.
And the sons of Cush: Seba, and Havilah, and Sabtah, and Raamah, and Sabtecha. And the sons of Raamah: Sheba and Dedan.
8 Kusi anabereka Nimurodi amene anali wankhondo wamphamvu kwambiri pa dziko lapansi.
And Cush begot Nimrod: he began to be mighty on the earth.
9 Iye anali mlenje wamphamvu kwambiri pamaso pa Yehova; nʼchifukwa chake anthu ali ndi chisudzo, chakuti, “Ndiwe mlenje wamphamvu kwambiri pamaso pa Yehova monga Nimurodi.”
He was a mighty hunter before Jehovah; therefore it is said, As Nimrod, the mighty hunter before Jehovah!
10 Malo oyambirira a ufumu wake anali Babeli, Ereki, Akadi ndi Kaline. Malo onsewa anali mʼdziko la Sinara.
And the beginning of his kingdom was Babel, and Erech, and Accad, and Calneh, in the land of Shinar.
11 Atachoka mʼdziko limeneli anapita ku Asiriya kumene anakamanga Ninive, Rehoboti-Iri, Kala,
From that land went out Asshur, and built Nineveh, and Rehoboth-Ir, and Calah,
12 ndi Reseni, mzinda waukulu umene uli pakati pa Ninive ndi Kala.
and Resen, between Nineveh and Calah: this is the great city.
13 Igupto ndiye kholo la Aludi, Aanami, Alehabu, Anafutu,
— And Mizraim begot the Ludim, and the Anamim, and the Lehabim, and the Naphtuhim,
14 Apaturusi, Akasilu ndi Akafitori (kumene kunachokera Afilisti).
and the Pathrusim, and the Casluhim, out of whom came the Philistines, and the Caphtorim.
15 Kanaani anabereka mwana wake wachisamba, Sidoni, ndipo anaberekanso Ahiti;
— And Canaan begot Sidon, his firstborn, and Heth,
16 Ayebusi, Aamori, Agirigasi;
and the Jebusite, and the Amorite, and the Girgashite,
17 Ahivi, Aariki, Asini,
and the Hivite, and the Arkite, and the Sinite,
18 Aaravadi, Azemari ndi Ahamati. Pambuyo pake, mafuko a Akanaani anafalikira ponseponse,
and the Arvadite, and the Zemarite, and the Hamathite. And afterwards the families of the Canaanites spread themselves abroad.
19 mpaka ku malire a Kanaani. Malirewo anachokera ku Sidoni kulowa cha ku Gerari mpaka ku Gaza, ndi kulowa ku Sodomu, Gomora, Adima ndi Zeboimu mpaka ku Lasa.
And the border of the Canaanite was from Sidon, as one goes to Gerar, up to Gazah; as one goes to Sodom, and Gomorrah, and Admah, and Zeboim, up to Lesha.
20 Amenewa ndiwo ana aamuna a Hamu monga mwa mafuko ndi ziyankhulo zawo, mʼmadera omwe amakhala ndi mitundu yawo.
These are the sons of Ham, after their families, after their tongues, in their lands, in their nations.
21 Semu amene anali mkulu wake wa Yafeti nayenso anabereka nakhala kholo la Eberi.
And to Shem — to him also were [sons] born; he is the father of all the sons of Eber, the brother of Japheth the elder.
22 Ana aamuna a Semu anali: Elamu, Asuri, Aripakisadi, Ludi ndi Aramu.
The sons of Shem: Elam, and Asshur, and Arphaxad, and Lud, and Aram.
23 Ana aamuna a Aramu anali: Uzi, Huri, Geteri ndi Mesaki.
And the sons of Aram: Uz, and Hul, and Gether, and Mash.
24 Aripakisadi anabereka Sela, ndipo Selayo anabereka Eberi.
— And Arphaxad begot Shelah; and Shelah begot Eber.
25 A Eberi anabereka ana aamuna awiri: Wina anamutcha Pelegi chifukwa pa nthawiyo anthu a pa dziko lapansi anagawikana. Dzina la mʼbale wake linali Yokitani.
And to Eber were born two sons: the name of the one was Peleg, for in his days was the earth divided; and his brother's name was Joktan.
26 Yokitani anabereka Alimodadi, Selefi, Hazari-Maveti, Yera,
And Joktan begot Almodad, and Sheleph, and Hazarmaveth, and Jerah,
27 Hadoramu, Uzali, Dikila,
and Hadoram, and Uzal, and Diklah,
28 Obali, Abimaeli, Seba,
and Obal, and Abimael, and Sheba,
29 Ofiri, Havila ndi Yobabu. Onsewa anali ana aamuna a Yokitani.
and Ophir, and Havilah, and Jobab: all these were sons of Joktan.
30 Chigawo chimene ankakhala chinayambira ku Mesa mpaka ku Seferi, ku dera la mapiri chakummawa.
And their dwelling was from Mesha, as one goes to Sephar, the eastern mountain.
31 Amenewa ndiwo ana a Semu monga mwa mafuko ndi ziyankhulo zawo, mʼmadera omwe ankakhala ndi mitundu yawo.
These are the sons of Shem, after their families, after their tongues, in their lands, after their nations.
32 Amenewa ndiwo mafuko a ana aamuna a Nowa monga mwa mibado ya mitundu yawo. Mitundu yonse ya anthu inatuluka mwa iwowa ndi kufalikira pa dziko lonse lapansi chitatha chigumula chija.
These are the families of the sons of Noah, after their generations, in their nations. And from these came the distribution of the nations on the earth after the flood.

< Genesis 10 >