< Ezara 3 >

1 Utafika mwezi wa chisanu ndi chiwiri Aisraeli atakhala kale mʼmidzi yawo, anthu anasonkhana ku Yerusalemu ndi cholinga chimodzi.
Le septième mois approchant, et les enfants d'Israël étant dans leurs villes, le peuple s'assembla à Jérusalem, comme un seul homme.
2 Kenaka Yesuwa mwana wa Yozadaki ndi ansembe anzake pamodzi ndi Zerubabeli mwana wa Sealatieli ndi abale ake anayamba kumanga guwa lansembe la Mulungu wa Israeli. Anatero pofuna kuti aziperekapo nsembe zopsereza monga analembera mʼbuku la Mose, munthu wa Mulungu uja.
Alors Jéshua, fils de Jotsadak, se leva avec ses frères les sacrificateurs, et Zorobabel, fils de Salathiel, avec ses frères; et ils bâtirent l'autel du Dieu d'Israël, pour y offrir les holocaustes ainsi qu'il est écrit dans la loi de Moïse, homme de Dieu.
3 Ndi mantha ndi mantha chifukwa cha anthu a mʼmayikomo, iwo anamanga guwalo pa maziko ake akale, ndipo anapereka nsembe zopsereza kwa Mulungu pa guwapo mmawa ndi madzulo.
Et ils redressèrent l'autel sur ses fondements, car ils étaient sous la crainte des populations du pays; et ils y offrirent des holocaustes à l'Éternel, les holocaustes du matin et du soir.
4 Ankasunga tsiku la chikondwerero cha misasa monga momwe zinalembedwera. Ankaperekanso nsembe za tsiku ndi tsiku monga mwa chiwerengero chake potsata mwambo wake wa tsiku ndi tsiku monga zinalembedwa.
Ils célébrèrent ensuite la fête des tabernacles, ainsi qu'il est écrit, et ils offrirent des holocaustes chaque jour, autant qu'il en fallait selon que l'ordinaire de chaque jour le demandait.
5 Pambuyo pake, ankapereka nsembe zopsereza, nsembe zopereka pa nthawi ya mwezi watsopano ndi za pa masiku onse a chikondwerero oyikidwa kutamandira Yehova, kudzanso nsembe zaufulu zopereka kwa Yehova.
Après cela, ils offrirent l'holocauste continuel, ceux des nouvelles lunes et de toutes les solennités consacrées à l'Éternel, et ceux que chacun présentait volontairement à l'Éternel.
6 Kuyambira pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri, iwo anayambanso kupereka nsembe zopsereza kwa Yehova, ngakhale kuti maziko a Nyumba ya Yehova anali asanamangidwe.
Dès le premier jour du septième mois, ils commencèrent à offrir des holocaustes à l'Éternel, bien que le temple de l'Éternel ne fût pas encore fondé.
7 Ndipo anapereka ndalama kwa amisiri a miyala ndi kwa amisiri a matabwa, ndi chakudya, chakumwa ndi mafuta kwa anthu a ku Sidoni ndi a ku Turo, kuti abweretse mitengo ya mkungudza pa nyanja kuchokera ku Lebanoni mpaka ku Yopa. Zonsezi anachita malinga ndi chilolezo chimene analandira kuchokera kwa Koresi, mfumu ya Peresiya.
Mais ils donnèrent de l'argent aux tailleurs de pierres et aux charpentiers; ils donnèrent aussi à manger et à boire, ainsi que de l'huile, aux Sidoniens et aux Tyriens, afin qu'ils amenassent du bois de cèdre, du Liban à la mer de Japho, selon la permission que Cyrus, roi de Perse, leur en avait donnée.
8 Tsono mu chaka chachiwiri atabwera ku Yerusalemu, ku malo akale a Nyumba ya Yehova, mwezi wachiwiri Zerubabeli mwana wa Sealatieli, Yesuwa mwana wa Yozadaki pamodzi ndi abale awo onse, ansembe, Alevi ndi onse amene anabwera ku Yerusalemu kuchokera ku ukapolo, anayamba kugwira ntchito. Iwo anasankha Alevi a zaka zoyambira makumi awiri kuti aziyangʼanira ntchito ya kumanga Nyumba ya Yehova.
Et la seconde année depuis leur arrivée à la maison de Dieu, à Jérusalem, au second mois, Zorobabel, fils de Salathiel, Jéshua, fils de Jotsadak, et le reste de leurs frères, les sacrificateurs, et les Lévites, et tous ceux qui étaient venus de la captivité à Jérusalem, commencèrent; et ils établirent des Lévites, depuis l'âge de vingt ans et au-dessus, pour présider à l'ouvrage de la maison de l'Éternel.
9 Yesuwa ndi ana ake aamuna kudzanso abale ake, Kadimieli ndi ana ake (ana a Yuda) onse pamodzi anasenza udindo woyangʼanira antchito ku Nyumba ya Mulungu, kuphatikizanso ana a Henadadi komanso Alevi, ana awo ndi abale awo.
Et Jéshua assistait avec ses fils et ses frères, et Kadmiel avec ses fils, enfants de Juda, comme un seul homme, pour diriger ceux qui faisaient l'ouvrage de la maison de Dieu, ainsi que les fils de Hénadad, avec leurs fils et leurs frères, Lévites.
10 Amisiri omanga nyumba atamanga maziko a Nyumba ya Yehova, ansembe anabwera akuyimba malipenga, atavala zovala zaunsembe. Ndipo Alevi, zidzukulu za Asafu, anadza akuyimba matambolini ndi kutenga udindo wawo wotamanda Yehova, potsata malangizo a Davide mfumu ya Aisraeli.
Or, lorsque ceux qui bâtissaient jetèrent les fondements du temple de l'Éternel, on y fit assister les sacrificateurs en costume, avec les trompettes, et les Lévites, fils d'Asaph, avec les cymbales, pour louer l'Éternel, selon l'institution de David, roi d'Israël.
11 Iwo ankayimba motamanda ndi mothokoza Yehova nyimbo iyi: “Yehova ndi wabwino; chikondi chake pa Israeli ndi chamuyaya.” Ndipo anthu onse ankafuwula kwambiri kumutamanda Yehova, chifukwa maziko a Nyumba ya Yehova anali kumangidwa.
Et en louant et en célébrant l'Éternel, ils s'entre-répondaient ainsi: Car il est bon, car sa miséricorde demeure à toujours sur Israël! Et tout le peuple jetait de grands cris de joie, en louant l'Éternel, parce qu'on posait les fondements de la maison de l'Éternel.
12 Koma ambiri mwa ansembe, Alevi ndiponso atsogoleri amabanja, akuluakulu amene anaona Nyumba ya Yehova yakale, analira mokweza pamene anaona maziko a nyumbayi akumangidwa. Komanso ena ambiri ankafuwula mosangalala.
Mais plusieurs des sacrificateurs, et des Lévites, et des chefs des pères, qui étaient âgés, et qui avaient vu la première maison sur son fondement, en se représentant cette maison-ci, pleuraient à haute voix; tandis que beaucoup d'autres élevaient leurs voix avec des cris de réjouissance et avec joie.
13 Choncho panalibe amene ankatha kusiyanitsa liwu lofuwula mokondwerera ndi liwu la anthu olira, chifukwa anthuwo ankafuwula kwambiri. Ndipo liwu lofuwulalo limamveka kutali.
Et l'on ne pouvait discerner la voix des cris de joie d'avec la voix des pleurs du peuple; car le peuple jetait de grands cris, de sorte que leur voix fut entendue bien loin.

< Ezara 3 >