< Ezekieli 5 >

1 Tsiku lina Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, tsopano tenga lupanga lakuthwa ndipo uligwiritse ntchito ngati lumo lometera. Umete tsitsi ndi ndevu zako. Kenaka utenge sikelo ndipo ugawe tsitsilo patatu.
»Ti pa, človeški sin, si vzemi oster nož, vzemi si brivčevo britev in ji povzroči, da gre čez tvojo glavo in po tvoji bradi. Potem si vzemi tehtnico, da stehtaš in razdeliš lase.
2 Kuzinga mzinda kuja kukatha, chimodzi cha zigawo zitatu za tsitsilo uchitenthe pakati pa mzinda. Chigawo chachiwiri uchiduledule ndi lupanga, poyenda muzungulire mzinda wonsewo. Chigawo chachitatu uchimwazire ku mphepo, ndidzachitsata nditasolola lupanga.
Z ognjem boš sežgal tretjino v sredi mesta, ko se dopolnijo dnevi obleganja. Vzel boš tretjino in okoli nje udarjal z nožem. Tretjino boš raztrosil v vetru, jaz pa bom za njimi izvlekel meč.
3 Koma utengeko tsitsi pangʼono, ulimange mu mpindiro wa mkanjo wako.
Od teh boš vzel malo po številu in jih povezal v krajce svojega oblačila.
4 Pa tsitsi limeneli utapepo lina, uliponye pa moto ndi kulitentha. Moto udzayambira pamenepo mpaka ku nyumba yonse ya Israeli.”
Potem ponovno vzemi od teh in jih vrzi v sredo ognja in jih sežgi v ognju, kajti od teh bo prišel ogenj v vso Izraelovo hišo.«
5 Ambuye Yehova akunena kuti, “Uyu ndi Yerusalemu amene ndamuyika pakati pa mitundu ya anthu, ndipo mayiko onse amuzungulira.
Tako govori Gospod Bog: »To je [prestolnica] Jeruzalem. Postavil sem jo v sredo narodov in dežel, ki so naokoli nje.
6 Koma anthu a Yerusalemu aphwanya malamulo anga pochita zoyipa kuposa anthu a mitundu ina. Iwo anandipandukira kupambana anthu ena amene awazungulira. Iwo anakana malamulo anga ndipo sanasunge malangizo anga.
Moje sodbe je spremenila v zlobnost bolj kakor narodi in moje zakone bolj kakor dežele, ki so okoli nje, kajti zavrnili so moje sodbe in moje zakone; niso hodili v njih.«
7 “Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti: Popeza mwakhala osamvera kupambana anthu a mitundu ina amene akuzungulirani, popeza simunatsate malamulo anga kapena kusunga malangizo anga, mʼmalo mwake mwakhala mukutsata makhalidwe a anthu a mitundu ina amene akuzungulirani.
Zato tako govori Gospod Bog: »Ker ste se pomnožili bolj kakor narodi, ki so okoli vas in niste hodili po mojih zakonih niti se niste držali mojih sodb niti niste delali glede na sodbe narodov, ki so naokoli vas, «
8 “Tsono Ambuye Yehova akuti: Ine mwini ndikutsutsana nawe, Yerusalemu, choncho Ine ndidzakulangani. Ine ndidzakulangani anthu a mitundu ina akuona.
zato tako govori Gospod Bog: »Glej jaz, celo jaz, sem zoper tebe in v tvoji sredi bom izvršil sodbe pred očmi narodov.
9 Chifukwa cha ntchito zanu zonyansa ndidzakulangani ndi chilango chimene sindinakulangeni nacho nʼkale lomwe ndipo sindidzakulangani ndi chofanana nacho mʼtsogolomo.
V tebi bom storil to, česar nisem storil in ne bom več storil temu podobnega, zaradi vseh tvojih ogabnosti.
10 Tsono pakati panu makolo adzadya ana awo, ndipo ana adzadya makolo awo. Ndidzakulanga ndipo otsala onse ndidzawabalalitsa ku mphepo zonse zinayi.
Zato bodo v tvoji sredi očetje jedli sinove in sinovi bodo jedli svoje očete. Izvršil bom sodbe v tebi in tvoj celotni preostanek bom razkropil na vse vetrove.
11 Ndithu, pali Ine, akutero Ambuye Yehova Wamoyo, pakuti mwayipitsa Nyumba yanga ndi mafano ano oyipa ndi miyambo yanu yonyansa, Inenso ndidzakulangani. Sindidzakulekererani kapena kukumverani chisoni.
Zato, kakor jaz živim, « govori Gospod Bog, »zagotovo, ker si moje svetišče omadeževala z vsemi svojimi ostudnimi stvarmi in z vsemi svojimi ogabnostmi, zato bom tudi jaz tebe zmanjšal; niti moje oko ne bo prizaneslo, niti ne bom imel nobenega usmiljenja.
12 Chimodzi mwa zigawo zitatu za anthu ako chidzafa ndi mliri, kapena chidzawonongeka ndi njala; chigawo china chidzaphedwa ndi lupanga kunja kwa mzinda, ndipo chigawo china ndidzachibalalitsira ku mphepo zonse zinayi pochita kuchithamangitsa.
Tvoja tretjina bo umrla s kužno boleznijo in z lakoto bodo použiti v tvoji sredi. Tretjina bo padla pod mečem naokoli tebe, tretjino pa bom razkropil na vse vetrove in za njimi bom izvlekel meč.
13 “Ndi mmene udzachitire mkwiyo wanga. Ndikadzatsiriza kuwalanga, pamenepo mtima wanga udzakhala pansi. Adzadziwa kuti Ine Yehova ndinawayankhula mwa nsanje ndikadzawalanga.
Tako bo moja jeza dovršena in svoji razjarjenosti bom povzročil, da počiva nad njimi, jaz pa bom potolažen. Oni pa bodo vedeli, da sem jaz, Gospod, to govoril v svoji gorečnosti, ko sem svojo razjarjenost dovršil v njih.
14 “Ndidzakusandutsa iwe bwinja ndi chinthu chonyozeka pakati pa anthu a mitundu ina amene akuzungulira, ndi kwa onse odutsapo
Poleg tega te bom naredil opustošenje in grajo med narodi, ki so naokoli tebe, pred očmi vseh, ki hodijo mimo.
15 Udzakhala chinthu chonyozeka ndi chonyogodoledwa. Udzakhala chenjezo ndi chinthu choopsa kwa anthu a mitundu ina amene akuzungulira ndikadzakulanga mokwiya ndi mwaukali ndi kugamula mlandu wako mokwiya. Ine Yehova ndayankhula.
Tako bo to graja in zbadljivka, poučevanje in osuplost narodom, ki so naokoli tebe, ko bom v tebi izvršil sodbe v jezi, v razjarjenosti in v besnih ukorih. Jaz, Gospod, sem to govoril.
16 Pamene ndidzakulasa ndi njala yolasa ngati mivi yoopsa ndi yosakaza ndidzatero nʼcholinga choti ndikuwonongeni. Ndidzagwetsa njalayo pa iwe mowirikiza pochepetsa chakudya chako cha tsiku ndi tsiku.
Ko bom nanje poslal zle puščice lakote, ki bodo za njihovo uničenje in ki jih bom poslal, da vas uničijo; in jaz bom razširil lakoto nad vami in zlomil vašo oporo kruha.
17 Ndidzatumiza njala ndi zirombo za kuthengo, ndipo zidzakulanda ana ako. Mliri ndi kuphana zidzakhala pakati pako, ndipo ndidzakubweretsera nkhondo. Ine Yehova ndayankhula.”
Tako bom nad vas poslal lakoto in zle živali in te te bodo oropale in kužna bolezen in kri bosta šla skozte in nadte bom privedel meč. Jaz, Gospod, sem to govoril.«

< Ezekieli 5 >