< Ezekieli 46 >

1 “Ambuye Yehova akuti, Chipata chakummawa cha bwalo lamʼkati chizikhala chotseka pa masiku asanu ndi limodzi ogwira ntchito, koma chizitsekulidwa pa tsiku la sabata ndi pa tsiku la chikondwerero cha mwezi watsopano.
The Lord Yahweh says this: The gate of the inner courtyard, facing east, will be shut for the six days of work, but on the Sabbath it will be opened, and on the day of the new moon it will be opened.
2 Mfumu izilowa podzera mʼkhonde la mʼkati la chipata pochokera kunja, nʼkudzayima pafupi ndi nsanamira yapakhomo. Ansembe apereke nsembe yake yopsereza ndi nsembe yake yachiyanjano. Mfumuyo ipembedze pa chiwundo cha pa chipatacho kenaka nʼkutuluka. Koma chipatacho asachitseke mpaka madzulo.
The prince will enter the outer courtyard by the way of the gate and its portico from outside, and he will stand before the doorposts of the inner gate while the priests perform his burnt offering and peace offering. Then he will worship at the threshold of the inner gate and go out, but the gate will not be shut until evening.
3 Anthu a mʼdziko azipembedza pamaso pa Yehova pa khomo la chipata chimenechi pa masiku a sabata ndi pa tsiku la mwezi watsopano.
The people of the land will also worship before Yahweh at the entrance to this gate on the Sabbaths and new moons.
4 Nsembe yopsereza imene mfumu iyenera kupereka kwa Yehova ikhale motere: pa tsiku la Sabata izipereka ana ankhosa aamuna asanu ndi mmodzi wopanda chilema, ndiponso nkhosa yayima yopanda chilema.
The burnt offering that the prince offers to Yahweh on the Sabbath day will be six unblemished lambs and an unblemished ram.
5 Pamodzi ndi nkhosa yayimuna, mfumu izipereka nsembe ya chakudya yokwanira efa imodzi. Pamodzi ndi ana ankhosa, mfumu izipereka monga ikufunira kutero. Iperekenso hini imodzi ya mafuta pa efa iliyonse ya tirigu.
The grain offering with the ram will be an ephah, and the grain offering with the lambs will be what he wishes to give, and a hin of oil with each ephah of grain.
6 Pa tsiku la mwezi watsopano mfumuyo ipereke mwana wangʼombe wamwamuna, ana ankhosa asanu ndi mmodzi ndiponso nkhosa yayimuna, zonsezi zopanda chilema.
On the day of the new moon he must offer an unblemished bull from a herd, six lambs, and an unblemished ram.
7 Ipereke efa imodzi ya tirigu pa ngʼombe yayimuna iliyonse ndiponso efa ina pa nkhosa yayimuna iliyonse. Pa ana ankhosa ipereke tirigu monga ikufunira kutero. Pamodzi ndi efa ya tirigu, ipereke hini imodzi ya mafuta.
He must make a grain offering of an ephah for the bull and an ephah for the ram, and what he wishes to give for the lambs, and a hin of oil for every ephah of grain.
8 Pamene mfumu ikulowa, izidzera mʼkhonde lamʼkati la chipata chakummawa, izitulukiranso pomwepo.
When the prince enters by the way of the gate and its portico, he must leave by the same way.
9 “Anthu a mʼdzikomo akabwera kudzapembedza Yehova pa masiku a chikondwerero, ngati munthu alowera pa chipata chakumpoto atulukire chipata chakummwera. Munthu wolowera chipata chakummwera, atulukire chipata chakumpoto. Munthu asatulukire pomwe walowera, koma atulukire pa chipata choyangʼanana nacho.
But when the people of the land come before Yahweh at the appointed festivals, anyone entering through the north gate to worship must leave through the south gate; and anyone entering through the south gate must leave through the north gate. No one may turn back to the gate through which he entered, for he must go out straight ahead.
10 Mfumu izidzakhala pakati pawo. Anthu akamadzalowa mfumu idzalowa nawo. Anthu akamadzatuluka mfumu idzatuluka nawo.
The prince must be in their midst; when they go in, he must go in, and when they leave, he must leave.
11 “Pa masiku achikondwerero ndi pa masiku ena osankhidwa, zopereka za chakudya zikhale zokwanira efa imodzi pamodzi ndi ngʼombe yayimuna iliyonse, efa imodzinso ndi nkhosa yayimuna, koma pa mwana wankhosa apereke monga angathere. Iperekenso hini imodzi ya mafuta pa efa iliyonse.
At the festivals, the grain offering must be an ephah of grain for the bull and an ephah for the ram, and whatever he wishes to give with the lambs, and a hin of oil for every ephah.
12 Pamene mfumu ikufuna kupereka chopereka chaufulu kwa Yehova, kaya ndi nsembe yopsereza kapena zopereka za chiyanjano, ayitsekulire chipata chakummawa. Iyo ipereke nsembe yopsereza kapena zopereka zake za chiyanjano monga imachitira pa tsiku la Sabata. Kenaka ituluke ndipo mfumuyo itatuluka, atseke chitsekocho.
When the prince gives a freewill offering, either a burnt offering or a peace offering to Yahweh, the gate facing east will be opened for him. He will offer his burnt offering offering or his peace offering as he does it on the Sabbath day. Then he must go out, and after he has gone out the gate will be shut.
13 “Tsiku lililonse nthawi ya mmawa azipereka kwa Yehova mwana wankhosa wa chaka chimodzi.
In addition, you will give an unblemished lamb one year old as a burnt offering to Yahweh daily; you will do this morning after morning.
14 Pamodzi ndi nyamayo aziperekanso mmawa uliwonse chopereka cha chakudya chokwanira chimodzi mwa zigawo zisanu ndi chimodzi za efa. Aziperekanso chimodzi mwa zigawo zitatu za hini ya mafuta okandira ufa wosalala. Chopereka cha chakudya chimenechi chiziperekedwa kwa Yehova nthawi zonse mwa lamulo.
You will give a grain offering with it morning after morning, a sixth of an ephah and a third of a hin of oil to moisten the flour of the grain offering for Yahweh, according to a permanent statute.
15 Motero azipereka mwana wankhosa ndi chopereka cha chakudya ndi mafuta mmawa uliwonse kuti zikhale nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku.
They will prepare the lamb, the grain offering, and the oil morning after morning, a permanent burnt offering.
16 “‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ngati kalonga apereka mphatso chigawo cha cholowa chake kwa mmodzi mwa ana ake, mphatsoyo idzakhala ya ana akewo. Idzakhala yawo chifukwa ndi cholowa chawo.
The Lord Yahweh says this: If the prince gives a gift to any of his sons, it is his inheritance. It will be the property of his sons, it is an inheritance.
17 Koma ngati ipereka mphatso yotere kuchokera pa cholowa chake kwa mmodzi mwa antchito ake, mphatsoyo idzakhala ya wantchitoyo mpaka chaka chaufulu. Pambuyo pake idzabwereranso kwa kalongayo chifukwa cholowa chake ndi cha ana ake.
But if he gives a gift from his inheritance to one of his servants, then it will be that servant's until the year of liberty, and then it will return to the prince. His inheritance will certainly be for his sons.
18 Kalonga asalande cholowa chilichonse cha anthu, kuwachotsa mʼdera lawo la dziko. Iye apereke kwa ana ake cholowa chawo chochokera pa chuma chakechake, kuti pasapezeke ndi mmodzi yemwe mwa anthu anga wolandidwa chuma chake.’”
The prince will not take the people's inheritance away from their own property; he must provide for his sons from his own property so that my people will not be scattered, each man from his own property.'”
19 Kenaka munthu uja anandidzeretsa pa khomo la pambali pa chipata nandilowetsa ku zipinda za ansembe zoyangʼana kumpoto. Ndipo ndinaona kumeneko malo chakumadzulo kwa zipindazo.
Next the man brought me through the entrance at the gate to the holy rooms for the priests, which faced north and behold! There was a place toward the west.
20 Munthuyo anandiwuza kuti, “Awa ndi malo amene ansembe adzaphikirapo nsembe yopepesera kupalamula ndi nsembe yopepesera machimo. Kumenekonso azidzawotcherako chopereka cha chakudya. Sadzatuluka nazo zoyerazi mʼbwalo lakunja kuopa kuti angapatsireko kuyera anthu ena.”
He said to me, “This is the place where the priests must boil the guilt offering and the sin offering and where they must bake the grain offering. They must not bring the offerings into the outer courtyard, for then the people would be consecrated.”
21 Pambuyo pake anandilowetsa mʼbwalo lakunja napita nane ku ngodya zinayi za bwalolo. Ndipo ndinaona mʼkati mwa ngodya iliyonse bwalo lina.
Then he brought me to the outer courtyard and he led me past the four corners of that courtyard, and I saw that in at every corner of the courtyard there was a another court.
22 Motero pa ngodya zinayi za bwalo panalinso mabwalo ena angʼonoangʼono. Mabwalo amenewa anali ofanana. Mulitali mwake munali mamita makumi awiri ndipo mulifupi mwake munali mamita khumi ndi asanu.
In the four corners of the outer courtyard there were four small courtyards, forty cubits in length and thirty in width. There the same dimensions for all four of the courtyards.
23 Kuzungulira mabwalo anayi angʼonoangʼono aja panali mpanda wamiyala, ndi malo asonkhapo moto omangidwa mʼmunsi mwa mpandawo mozungulira.
There was a row made of stone all around the four of them, and cooking hearths were under the stone row.
24 Munthuyo anandiwuza kuti, “Izi ndi zipinda zophikiramo. Mʼmenemu anthu otumikira ku Nyumba ya Mulungu adzaphikiramo nyama za nsembe za anthu.”
The man said to me, “These are the places where the temple servants will boil the people's sacrifices.”

< Ezekieli 46 >