< Ezekieli 43 >

1 Pambuyo pake munthuyo anapita nane ku chipinda choyangʼana kummawa,
Afterward he brought me to the gate, even the gate that looks toward the east.
2 ndipo ndinaona ulemerero wa Mulungu wa Israeli ukubwera kuchokera kummawa. Liwu lake linali ngati mkokomo wamadzi, ndipo dziko linawala ndi ulemerero wake.
And, behold, the glory of the God of Israel came from the way of the east. And his voice was like the sound of many waters, and the earth shone with his glory.
3 Masomphenya amene ndinawaonawa anali ngati masomphenya amene ndinawaona pamene Yehova anabwera kudzawononga mzinda ndiponso ngati masomphenya amene ndinawaona ku mtsinje wa Kebara. Ndipo ndinadzigwetsa chafufumimba.
And it was according to the appearance of the vision which I saw, even according to the vision that I saw when I came to destroy the city. And the visions were like the vision that I saw by the river Chebar. And I fell upon my face.
4 Ulemerero wa Yehova unalowa mʼNyumba ya Mulungu kudzera pa chipata choyangʼana kummawa.
And the glory of Jehovah came into the house by the way of the gate whose view is toward the east.
5 Tsono Mzimu unandinyamula nundilowetsa mʼbwalo lamʼkati, ndipo ulemerero wa Yehova unadzaza Nyumba ya Mulungu.
And the Spirit took me up, and brought me into the inner court, and, behold, the glory of Jehovah filled the house.
6 Munthuyo ali chiyimire pambali panga, ndinamva wina akundiyankhula kuchokera mʼNyumba ya Mulungu.
And I heard speaking to me out of the house, and a man stood by me.
7 Iye anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, awa ndi malo a mpando wanga waufumu, ndi malo opondapo mapazi anga. Pano ndiye pamene ndidzakhala pakati pa Aisraeli mpaka muyaya. Aisraeliwa kapena mafumu awo sadzayipitsa dzina langa popembedza milungu ina kapena poyika mitembo ya mafumu awo ku zitunda zachipembedzo.
And he said to me, Son of man, this is the place of my throne, and the place of the soles of my feet, where I will dwell in the midst of the sons of Israel forever. And the house of Israel shall no more defile my holy name, neither they, nor their kings, by their whoredom, and by the dead bodies of their kings in their high places,
8 Ankamanga chiwundo chawo pafupi ndi chiwundo changa, ndiponso mphuthu zawo pafupi ndi mphuthu zanga, nʼkungokhala khoma chabe pakati pa iwowo ndi Ine. Motero anayipitsa dzina langa loyera ndi machitidwe awo onyansa. Choncho Ine ndinawawononga ndili wokwiya.
in their setting of their threshold by my threshold, and their door-post beside my door-post, and there was but the wall between me and them. And they have defiled my holy name by their abominations which they have committed. Therefore I have consumed them in my anger.
9 Tsopano alekeretu kupembedza milungu ina ndipo achotseretu mitembo ya mafumu awo, isakhale pafupi ndi Ine, ndipo Ine ndidzakhala pakati pawo mpaka muyaya.
Now let them put away their whoredom, and the dead bodies of their kings, far from me, and I will dwell in the midst of them forever.
10 “Iwe mwana wa munthu, awuze Aisraeliwa za Nyumba ya Mulunguyi, mamangidwe ake ndipo achite manyazi ndi machimo awo,
Thou, son of man, show the house to the house of Israel, that they may be ashamed of their iniquities, and let them measure the pattern.
11 akachita manyazi ndi zoyipa zonse anachita, uwafotokozera za Nyumba ya Mulungu, mamangidwe ake, makomo ake otulukira ndi makomo olowera, ndiye kuti, mamangidwe ake onse. Uwafotokozerenso malangizo ndi malamulo ake. Uwalembe akuona kuti athe kuwasunga ndi kuwachita.
And if they be ashamed of all that they have done, make known to them the form of the house, and the fashion of it, and the exits of it, and the entrances of it, and all the forms of it, and all the ordinances of it, and all the forms of it, and all the laws of it. And write it in their sight, that they may keep the whole form of it, and all the ordinances of it, and do them.
12 “Limeneli ndi lamulo la Nyumba ya Mulungu imene idzamangidwe pamwamba pa phiri. Malo ake onse ozungulira adzakhala oyera kwambiri. Limeneli ndilo lamulo la Nyumba ya Mulungu.
This is the law of the house. Upon the top of the mountain the whole limit of it round about shall be most holy. Behold, this is the law of the house.
13 “Miyeso ya guwa lansembe ndi iyi: Pa tsinde pake padzakhala ngalande ya masentimita makumi asanu kuzama kwake ndi mulifupi mwake. Mʼphepete mwa ngalandeyo kuzungulira guwa lonse, mudzakhala mkombero wa masentimita 25.
And these are the measures of the altar by cubits (the cubit is a cubit and a handbreadth). The bottom shall be a cubit, and the breadth a cubit, and the border of it by the edge of it round about a span. And this shall be the base of the altar.
14 Kuchokera mʼngalande ya pansi padzakhala mpaka pa phaka lapansi mita imodzi, mulifupi mwake theka la mita. Kuchokera pa phaka lalingʼono mpaka pa phaka lalikulu, msinkhu wake ndi mamita awiri, mulifupi mwake ndi masentimita makumi asanu.
And from the bottom upon the ground to the lower ledge shall be two cubits, and the breadth one cubit. And from the lesser ledge to the greater ledge shall be four cubits, and the breadth a cubit.
15 Malo osonkhapo moto pa guwa, msinkhu wake udzakhala mamita awiri. Pa ngodya iliyonse ya malo osonkhapo motowo panatuluka nyanga imodzi.
And the upper altar shall be four cubits. And from the altar hearth and upward there shall be four horns.
16 Malo osankhalapo moto pa guwa lansembe miyeso yake ndi yofanana mbali zonse. Mulitali mwake mudzakhala mamita asanu ndi limodzi ndipo mulifupi mwake mudzakhalanso mamita asanu ndi limodzi.
And the altar hearth shall be twelve long by twelve broad, square in the four sides of it.
17 Phaka lapamwamba muyeso wake udzakhala wofanana mbali zonse. Mulitali mudzakhala mamita asanu ndi awiri ndiponso mulifupi mwake mudzakhalanso mamita asanu ndi awiri. Mkombero wake udzakhala wa masentimita 25 ndiponso ngalande yake yozungulira idzakhala ya masentimita 25. Makwerero a guwa lansembe adzayangʼana kummawa.”
And the ledge shall be fourteen long by fourteen broad in the four sides of it. And the border about it shall be half a cubit, and the bottom of it shall be a cubit round about. And the steps of it shall look toward the east.
18 Kenaka munthuyo anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, Ambuye Yehova akuti: Guwalo litamangidwa, tsono malamulo awa azidzatsatidwa popereka nsembe zopsereza ndiponso powaza magazi pa guwapo.
And he said to me, Son of man, thus says the lord Jehovah: These are the ordinances of the altar in the day when they shall make it, to offer burnt offerings on it, and to sprinkle blood on it.
19 Udzawapatse ansembe, omwe ndi Alevi, a banja la Zadoki, amene amabwera pafupi nane kudzanditumikira, mwana wangʼombe wamwamuna kuti aperekere nsembe yopepesera machimo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
Thou shall give to the priests the Levites who are of the seed of Zadok, who are near to me, to minister to me, says the lord Jehovah, a young bullock for a sin offering.
20 Udzatengeko magazi ake ena ndi kuwapaka pa nyanga zinayi za pa guwa lansembe, pa ngodya zinayi za phaka ndiponso mozungulira mkombero wonse. Motero udzaliyeretsa ndi kulipatula.
And thou shall take of the blood of it, and put it on the four horns of it, and on the four corners of the ledge, and upon the border round about. Thus thou shall cleanse it and make atonement for it.
21 Udzatenge ngʼombe yayimuna yomwe yaperekedwa ngati nsembe yopepesera machimo, ndipo udzayiwotche pa malo ake enieni mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu, kunja kwa malo opatulika.
Thou shall also take the bullock of the sin offering, and it shall be burnt in the appointed place of the house, outside the sanctuary.
22 “Mmawa mwake udzatenge mbuzi yopanda chilema kuti nayonso iperekedwe ngati nsembe yopepesera machimo. Pambuyo pake idzayeretse guwa lansembe monga unachitira ndi ngʼombe yayimuna ija.
And on the second day thou shall offer a he-goat without blemish for a sin offering. And they shall cleanse the altar, as they cleansed it with the bullock.
23 Utatha kuyeretsa guwa lansembelo, udzatenge mwana wangʼombe wamwamuna wopanda chilema ndiponso nkhosa yayimuna yopanda chilema.
When thou have made an end of cleansing it, thou shall offer a young bullock without blemish, and a ram out of the flock without blemish.
24 Udzapereke zonsezi pamaso pa Yehova, ndipo ansembe adzazithire mchere ndi kuzipereka kuti zikhale nsembe zopsereza kwa Yehova.
And thou shall bring them near before Jehovah, and the priests shall cast salt upon them, and they shall offer them up for a burnt offering to Jehovah.
25 “Kwa masiku asanu ndi awiri, uzidzapereka tsiku ndi tsiku mbuzi yayimuna, mwana wangʼombe, ndiponso nkhosa kuti zikhale nsembe zopepesera machimo. Zonsezi zidzakhale zopanda chilema.
Seven days thou shall prepare each day a goat for a sin offering. They shall also prepare a young bullock, and a ram out of the flock, without blemish.
26 Kwa masiku asanu ndi awiriwo ansembe adzachite mwambo woyeretsa ndi kupatula guwa lansembelo.
Seven days they shall make atonement for the altar and purify it. So they shall consecrate it.
27 Masiku amenewa atatha, kuyambira tsiku lachisanu ndi chitatu, ansembe azipereka nsembe zanu zopsereza ndi nsembe zachiyanjano pa guwa lansembe. Apo ndidzakulandirani. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”
And when they have accomplished the days, it shall be that upon the eighth day, and forward, the priests shall make your burnt offerings upon the altar, and your peace offerings. And I will accept you, says the lord Jehovah.

< Ezekieli 43 >