< Ezekieli 39 >

1 “Iwe mwana wa munthu, nenera modzudzula Gogi ndi kumuwuza kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: ‘Ine ndikudana nawe, iwe Gogi, kalonga wamkulu wa Mesaki ndi Tubala.
Therefore, thou sonne of man, prophecie against Gog, and say, Thus sayeth the Lord God, Behold, I come against thee, O Gog, ye chiefe prince of Meshech and Tubal.
2 Ine ndidzakuzunguza ndi kukupirikitsira kutsogolo. Ndidzakutenga kuchokera kutali kumpoto ndi kukutumiza kuti ukalimbane ndi anthu a ku mapiri a Israeli.
And I will destroy thee and leaue but the sixt part of thee, and will cause thee to come vp from the North partes and will bring thee vpon the mountaines of Israel:
3 Kenaka Ine ndidzathyola uta wa mʼdzanja lako lamanzere ndipo ndidzagwetsa mivi ya mʼdzanja lako lamanja.
And I will smite thy bowe out of thy left hand, and I will cause thine arrowes to fall out of thy right hand.
4 Udzagwa ku mapiri a ku Israeli, iwe ndi magulu ako onse ankhondo ndiponso mitundu ya anthu imene ili nawe. Ndidzakusandutsa chakudya cha mitundu yonse ya mbalame zodya nyama, ndiponso cha zirombo zakuthengo.
Thou shalt fal vpon the mountaines of Israel, and all thy bands and the people, that is with thee: for I will giue thee vnto the birdes and to euery feathered foule and beast of the fielde to be deuoured.
5 Udzafera pa mtetete kuthengo, pakuti Ine ndayankhula. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
Thou shalt fall vpon the open fielde: for I haue spoken it, sayth the Lord God.
6 Ndidzatumiza moto pa Magogi ndi pa onse amene amakhala mwamtendere mʼmbali mwa nyanja. Choncho adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’
And I will sende a fire on Magog, and among them that dwell safely in the yles, and they shall knowe that I am the Lord.
7 “Ndidzachititsa kuti dzina langa loyera lidziwike pakati pa anthu anga Israeli. Sindidzalola kuti dzina langa liyipitsidwenso, ndipo mitundu ya anthu idzadziwa kuti Ine Yehova ndine Woyera mu Israeli.
So will I make mine holy Name knowen in the middes of my people Israel, and I will not suffer them to pollute mine holy Name any more, and the heathen shall knowe that I am the Lord, the holy one of Israel.
8 Zikubwera! Ndipo zidzachitikadi, ndikutero Ine Ambuye Yehova. Ndiye tsiku limene ndinanena lija.
Beholde, it is come, and it is done, sayeth the Lord God: and this is the day whereof I haue spoken.
9 “Pamenepo okhala mʼmizinda ya Israeli adzatuluka ndipo adzasonkhanitsa zida zankhondo kuti zikhale nkhuni ndipo adzazitentha; zishango ndi lihawo, mauta ndi mivi, zibonga za nkhondo ndi mikondo. Adzazisonkhera moto kwa zaka zisanu ndi ziwiri.
And they that dwell in the cities of Israel, shall goe forth, and shall burne and set fire vpon the weapons, and on the shieldes, and bucklers, vpon the bowes, and vpon the arrowes, and vpon the staues in their handes, and vpon the speares, and they shall burne them with fire seuen yeeres.
10 Iwo sadzatolera nkhuni kuthengo kapena kukadula ku nkhalango, chifukwa adzasonkhera moto zidazo. Ndipo iwo adzafunkha amene anawafunkhawo, ndi kulanda chuma cha amene anawalanda, ndikutero Ine Ambuye Yehova.
So that they shall bring no wood out of the fielde, neither cut downe any out of the forestes: for they shall burne the weapons with fire, and they shall robbe those that robbed them, and spoyle those that spoyled them, sayeth the Lord God.
11 “Pa tsiku limenelo ndidzamupatsa Gogi manda mu Israeli, mʼchigwa cha apaulendo, kummawa kwa Nyanja Yakufa. Mandawo adzatseka njira ya apaulendo, chifukwa Gogi ndi gulu lake lankhondo adzayikidwa kumeneko. Ndipo chigwacho chidzatchedwa chigwa cha gulu lankhondo la Gogi.
And at the same time will I giue vnto Gog a place there for burial in Israel, euen the valley whereby men go towarde the East part of the sea: and it shall cause them that passe by, to stoppe their noses, and there shall they bury Gog with all his multitude: and they shall call it the valley of Hamon-Gog.
12 “Nyumba ya Israeli idzakhala ikukwirira mitembo kwa miyezi isanu ndi iwiri ndi cholinga choyeretsa dziko.
And seuen moneths long shall the house of Israel be burying of the, that they may clense the land.
13 Anthu onse a mʼdzikomo adzakwirira nawo mitembo. Ntchito imeneyo adzatchuka nayo pa tsiku limene ndidzaonetsa ulemerero wanga. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
Yea, all the people of the lande shall burie them, and they shall haue a name when I shall be glorified, saith the Lord God.
14 “Patapita miyezi isanu ndi iwiri adzalemba ntchito anthu ena odzayenda mʼdziko lonse kufunafuna mitembo imene inatsalira nʼkumayikwirira. Choncho adzayeretseratu dzikolo.
And they shall chuse out men to goe continually through the lande with them that trauaile, to bury those that remaine vpon ye ground, and clense it: they shall search to the ende of seuen moneths.
15 Poyenda mʼdzikomo azidzati akaona fupa la munthu azidzayikapo chizindikiro pambali pake mpaka okumba manda atakalikwirira fupalo ku chigwa cha gulu lankhondo la Gogi.
And the trauailers that passe through the land, if any see a mans bone, then shall he set vp a signe by it, till the buriers haue buried it, in the valley of Hamon-Gog.
16 (Komwekonso kudzakhala mzinda wotchedwa Gulu la nkhondo). Ndipo potero adzayeretsa dziko.
And also the name of the citie shalbe Hamonah: thus shall they clense the land.
17 “Tsono iwe mwana wa munthu, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Itana mbalame za mitundu yonse ndi zirombo zonse zakuthengo ndipo uziwuze kuti, ‘Sonkhanani ndipo bwerani kuchokera ku mbali zonse ku nsembe imene ndikukonzerani inu, nsembe yayikulu pa mapiri a Israeli. Kumeneko inu mudzadya mnofu ndi kumwa magazi.
And thou sonne of man, thus sayeth the Lord God, Speake vnto euery feathered foule, and to all the beastes of the fielde, Assemble your selues, and come gather your selues on euery side to my sacrifice: for I do sacrifice a great sacrifice for you vpon the mountaines of Israel, that ye may eate flesh, and drinke blood.
18 Mudzadya mnofu wa anthu ankhondo amphamvu ndi kumwa magazi a akalonga a dziko lapansi. Onsewo anaphedwa ngati nkhosa zazimuna, ana ankhosa onenepa, mbuzi ndiponso ngati ngʼombe zazimuna zonenepa za ku Basani.
Ye shall eate the flesh of the valiant, and drink the blood of the princes of the earth, of the weathers, of the lambes, and of the goates, and of bullockes, euen of all fat beastes of Bashan.
19 Ku phwando lansembe limene ndikukonzera inulo, mudzadya zonona mpaka kukhuta ndi kumwa magazi mpaka kuledzera.
And ye shall eate fat till you be full, and drinke blood, till ye be drunken of my sacrifice, which I haue sacrificed for you.
20 Pa tebulo langa mudzakhuta pakudya akavalo ndi okwerapo ake, anthu amphamvu ndi asilikali amitundumitundu,’ ndikutero Ine Ambuye Yehova.
Thus you shalbe filled at my table with horses and chariots, with valiant men, and with al men of warre, sayth the Lord God.
21 “Ine ndidzaonetsa ulemerero wanga pakati pa anthu a mitundu ina, ndipo adzaona mmene ndidzawalangire ndikadzayika dzanja langa pa iwo.
And I wil set my glory among the heathe, and all the heathen shall see my iudgement, that I haue executed, and mine hand, which I haue layed vpon them.
22 Kuyambira tsiku limenelo mpaka mʼtsogolo Aisraeli adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo.
So the house of Israel shall knowe, that I am the Lord their God from that day and so forth.
23 Ndipo anthu a mitundu ina adzadziwa kuti anthu a Israeli anatengedwa ukapolo chifukwa cha tchimo lawo, chifukwa anali osakhulupirika kwa Ine. Choncho Ine ndinawabisira nkhope yanga ndi kuwapereka kwa adani awo. Motero anaphedwa pa nkhondo.
And the heathen shall knowe, that ye house of Israel went into captiuitie for their iniquitie, because they trespassed against me: therefore hid I my face from them, and gaue them into ye hand of their enemies: so fell they all by the sword.
24 Ndinawachita zimenezi chifukwa cha kunyansa kwawo ndi zolakwa zawo, ndipo ndinawabisira nkhope yanga.
According to their vncleannes, and according to their transgressions haue I done vnto the, and hid my face from them.
25 “Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Tsopano ndidzakhazikanso pa bwino banja la Yakobo. Ndidzachitira chifundo Aisraeli onse, ndipo ndidzateteza dzina langa loyera.
Therefore thus sayth the Lord God, Nowe will I bring againe the captiuitie of Iaakob, and haue compassion vpon the whole house of Israel, and wil be ielous for mine holy Name,
26 Anthuwo akadzakhala mwamtendere mʼdziko lawo popanda wina wowaopseza, pamenepo adzayiwala zamanyazi zawo zimene zinawachitikira chifukwa chosandikhulupirira Ine.
After that they haue borne their shame, and all their transgression, whereby they haue transgressed against me, whe they dwelt safely in their land, and without feare of any.
27 Ndidzawabwezeranso kwawo kuchokera pakati pa anthu a mitundu ina ndipo ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku mayiko a adani awo. Poteropo ndidzaonetsa pamaso pa anthu a mitundu yambiri kuti ndine Woyera.
When I haue brought them againe from the people, and gathered them out of their enemies landes, and am sanctified in them in the sight of many nations,
28 Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo, ngakhale kuti ndinawapereka ku ukapolo pakati pa anthu a mitundu ina. Ine ndidzawasonkhanitsanso ku dziko lawo osasiyako wina mʼmbuyo.
Then shall they know, that I am the Lord their God, which caused them to be led into captiuitie among the heathen: but I haue gathered them vnto their owne land, and haue left none of them any more there,
29 Ine sindidzawabisiranso nkhope yanga, pakuti ndidzathira Mzimu wanga pa Aisraeli. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”
Neither wil I hide my face any more from them: for I haue powred out my Spirit vpon the house of Israel, sayth the Lord God.

< Ezekieli 39 >