< Ezekieli 35 >

1 Yehova anandiyankhula kuti:
И бысть слово Господне ко мне глаголя:
2 “Iwe mwana wa munthu, yangʼana phiri la Seiri; yankhula moliyimba mlandu ndipo
сыне человечь, обрати лице твое к горе Сеир и прорцы на ню и рцы ей:
3 awawuze anthu a kumeneko kuti zimene ndikuyankhula Ine Ambuye Yehova ndi izi: Inu anthu a ku mapiri a Seiri ndikudana nanu. Ndidzatambasula dzanja langa kulimbana nanu, ndipo ndidzasandutsa dziko lanu kukhala chipululu.
сия глаголет Адонаи Господь: се, Аз на тя, горо Сеир, и простру руку Мою на тя и поставлю тя пусту, и опустееши,
4 Mizinda yanu ndidzayisandutsa mabwinja, ndipo dziko lanu lidzasanduka chipululu. Zikadzachitika izi mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
и во градех твоих пустыню сотворю, и ты в пустыню будеши, и уразумееши, яко Аз есмь Господь.
5 “Munali adani a Israeli nthawi zonse, ndipo munkalola kuti Aisraeli aphedwe pa nkhondo pa nthawi ya mavuto awo, pa nthawi imene chilango chawo chinafika pachimake.
Понеже бысть в тебе вражда вечная, и приседела еси дому Израилеву лукавством, рукою врагов с мечем во время печали их и во время неправды, на последок:
6 Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pali Ine wamoyo, ndithu ndidzakukanthani. Imfa idzakulondolani. Popeza sunadane nako kukhetsa magazi, imfa idzakulondola.
сего ради живу Аз, глаголет Адонаи Господь, понеже в крови согрешила еси, и кровь поженет тя, кровь возненавидела еси, и кровь ижденет тя.
7 Phiri la Seiri ndidzalisandutsa chipululu ndipo ndidzapha onse amene amapita nabwerera kumeneko.
И поставлю гору Сеир пусту и опустевшу, и погублю от нея человеки и скоты, (и приходяща и отходяща: )
8 Ndidzaza mapiri ake ndi mitembo. Ophedwa pa nkhondo adzagwera pa zitunda zanu, zigwa zanu ndi mʼmitsinje yanu yonse.
и наполню язвеными твоими холмы твоя и дебри твоя, и на всех полех твоих язвении мечем падут в тебе:
9 Ndidzasandutsa dziko lanu kukhala chipululu mpaka muyaya, ndipo mʼmizinda yanu simudzakhalanso anthu. Zikadzachitika izi mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
и пусту во век поставлю тя, и гради твои не населятся ктому, и уразумееши, яко Аз есмь Господь.
10 “Inu munanena kuti, ‘Mitundu iwiri iyi ya anthu, Yuda ndi Israeli, pamodzi ndi mayiko awo omwe idzakhala yathu.’ Munanena chomwechi ngakhale kuti Ine Yehova ndinali momwemo.
Понеже рекла еси: оба языка и обе стране мои будут, и возму их в наследие, а Господь тамо есть:
11 Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pali Ine wamoyo, ndithu ndidzachita nanu monga munachita ndi anthu a ku Yuda ndi Israeli poonetsa mkwiyo wanu, nsanje yanu ndi chidani chanu pa iwo. Ndikadzakulangani mudzandidziwadi pakati panupo.
сего ради живу Аз, глаголет Адонаи Господь, и сотворю тебе по вражде твоей и по ревности твоей, юже сотворила еси от ненавидения к ним, и познан буду тобою, егда имам тебе судити, и уразумееши, яко Аз есмь Господь.
12 Ndipo mudzadziwa kuti Ine Yehova ndinamva mawu anu onse onyoza amene munanena molimbana ndi mapiri a Israeli. Inu munati, ‘Mapiri a Israeli asanduka bwinja, ndipo aperekedwa kwa ife kuti tiwawononge.’
Слышах глас всех хулений твоих, яже глаголала еси: горы Израилевы пусты даны нам во снедь:
13 Mawu anu amene munayankhula monyada kundinyoza Ine ndinawamva.
и велеречила еси на Мя усты твоими и умножила на Мя словеса, Аз же услышах.
14 Ine Ambuye Yehova ndikuti: Dziko lonse lapansi lidzasangalala pamene ndidzakusandutsani bwinja.
Сего ради тако глаголет Адонаи Господь: во веселии всея земли пусту тя сотворю:
15 Monga momwe inu munasangalala pamene anthu anga Aisraeli anagwa, Inenso ndidzakuchitani chimodzimodzi. Udzasanduka bwinja, iwe Phiri la Seiri, iwe ndi dziko lonse la Edomu. Zikadzatero anthu onse adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
якоже порадовалася еси о наследии дому Израилева, яко погибе, тако сотворю тебе: пуста будеши, горо Сеир, и вся Идумеа потребится, и уведят, яко Аз есмь Господь Бог их.

< Ezekieli 35 >