< Ezekieli 33 >

1 Yehova anandiyankhula nati:
I doszło do mnie słowo PANA mówiące:
2 “Iwe mwana wa munthu awuze anthu a mtundu wako kuti, ‘Paja zimati ndikatumiza nkhondo mʼdziko anthu a mʼdzikomo amasankha munthu mmodzi pakati pawo kuti akhale mlonda.
Synu człowieczy, przemów do synów twego ludu i powiedz im: Gdy sprowadzam miecz na jakąś ziemię, a lud tej ziemi weźmie jakiegoś mężczyznę spośród siebie i ustanowi go sobie stróżem;
3 Tsono iyeyo amati akaona nkhondo ikubwera amaliza lipenga kuti achenjeze anthuwo.
A [on], gdy zobaczy nadciągający miecz na tę ziemię, zadmie w trąbę i ostrzeże lud;
4 Wina aliyense akamva lipenga koma osasamala, mdani uja akabwera nʼkumupha, ndiye kuti wadziphetsa yekha.
A ktoś usłyszy dźwięk trąby i nie przyjmie przestrogi, a miecz przyjdzie i zabierze go, to jego krew spadnie na jego [własną] głowę.
5 Iye anamva kulira kwa lipenga koma sanalabadire. Ndiye kuti wadziphetsa yekha. Akanasamala kuchenjeza kwa mlonda akanapulumuka.
Dźwięk trąby usłyszał, ale nie przyjął przestrogi, jego krew spadnie na niego. Ten jednak, który przyjmie przestrogę, ocali swoją duszę.
6 Koma ngati mlondayo aona lupanga likubwera ndipo osawomba lipengalo kuchenjeza anthu, ndipo lupanga libwera ndi kuchotsa moyo wa mmodzi mwa iwo, munthu ameneyo adzafa chifukwa cha tchimo lake, koma ndidzamuyimba mlandu mlondayo chifukwa cha imfa ya mnzakeyo.’
Ale jeśli stróż zobaczy nadciągający miecz, a nie zadmie w trąbę i ludu nie ostrzeże, a przyjdzie miecz i zabierze kogoś z nich, to ten [jest] porwany w swojej nieprawości, ale jego krwi zażądam z ręki tego stróża.
7 “Tsono iwe mwana wa munthu, ndakuyika kuti ukhale mlonda wa Aisraeli. Choncho imva mawu amene ndikuyankhula ndipo uwachenjeze.
Ciebie, synu człowieczy, ciebie ustanowiłem stróżem dla domu Izraela. Gdy usłyszysz słowo z moich ust, ostrzeżesz go ode mnie.
8 Ndikawuza munthu woyipa kuti, ‘Iwe munthu woyipa, udzafa ndithu,’ ndipo iwe osayankhula kumuchenjeza kuti aleke njira zake, munthu wochimwayo adzafa chifukwa cha tchimo lake, koma Ine ndidzakuyimba mlandu chifukwa cha imfa yake.
Gdy mówię do bezbożnego: Bezbożniku, na pewno umrzesz – a ty mu [tego] nie powiesz, aby przestrzec bezbożnika przed jego drogą, to ten bezbożnik umrze z powodu swojej nieprawości; ale jego krwi zażądam z twojej ręki.
9 Koma ngati uchenjeza munthu woyipa kuti aleke njira zake, ndipo iye osatero, adzafa chifukwa cha tchimo lake, koma iwe udzapulumutsa moyo wako.
Jeśli jednak ostrzeżesz bezbożnego przed jego drogą, aby odwrócił się od niej, a on się nie odwróci od swojej drogi, to umrze on z powodu swojej nieprawości; ale ty ocalisz swoją duszę.
10 “Iwe mwana wa munthu, akumbutse Aisraeli mawu awo akuti, ‘Ife talemedwa ndi zolakwa zathu ndi machimo athu, ndipo tikuwonda chifukwa cha zimene tachita. Kodi tingakhale ndi moyo bwanji?’”
Ty więc, synu człowieczy, mów do domu Izraela: Tak mówicie: Skoro ciążą na nas nasze występki i nasze grzechy, tak że w nich marniejemy, to jakże możemy żyć?
11 Uwawuze kuti, Ine Ambuye Yehova ndikuti: “Pali Ine wamoyo, sindikondwera ndi imfa ya munthu woyipa. Ndimakondwera ndikamaona munthu woyipa akuleka zoyipa zake kuti akhale ndi moyo. Tembenukani! Tembenukani, siyani makhalidwe anu oyipa! Muferanji, Inu Aisraeli?
Powiedz im: Jak żyję, mówi Pan BÓG: Nie pragnę śmierci bezbożnego, ale aby bezbożny odwrócił się od swojej drogi i żył. Odwróćcie się, odwróćcie się od swoich złych dróg. Dlaczego macie umrzeć, domu Izraela?
12 “Tsono iwe mwana wa munthu, awuze anthu a mtundu wako kuti, ‘Ngati munthu wolungama achimwa, ndiye kuti ntchito zake zabwino zija sizidzamupulutsa. Koma wochimwa akaleka ntchito zake zoyipazo, sadzalangidwa konse. Ndithu ngati munthu wolungama ayamba kuchimwa sadzatha kukhala ndi moyo chifukwa cha ntchito zake zabwino zija.’
Ty więc, synu człowieczy, mów do synów swego ludu: Sprawiedliwość sprawiedliwego nie wybawi go w dniu jego przestępstwa, a bezbożność bezbożnego nie zgubi go w dniu, kiedy się odwróci od swojej bezbożności. Sprawiedliwy nie będzie mógł żyć dzięki swojej [sprawiedliwości] w dniu, kiedy zgrzeszy.
13 Ngati ndiwuza munthu wolungama kuti adzafa ndithu, koma iyeyo nʼkumadalira ntchito zake zabwino zimene anachita kale ndi kuyamba kuchimwa, ndiye kuti ntchito zake zabwinozo zidzayiwalika. Iye adzafa chifukwa cha machimo ake.
Jeśli powiem sprawiedliwemu: Na pewno będziesz żyć, a on, polegając na swojej sprawiedliwości, uczyni nieprawość, to żadna jego sprawiedliwość nie będzie wspomniana, ale umrze z powodu swojej nieprawości, którą uczynił.
14 Ndipo ngati ndiwuza munthu woyipa kuti, ‘Udzafa ndithu,’ tsono iye nʼkutembenuka kuleka machimo ake ndi kuyamba kuchita zimene Yehova afuna,
A jeśli powiem bezbożnemu: Na pewno umrzesz, a on odwróci się od swego grzechu i uczyni to, co prawe i sprawiedliwe;
15 monga kubweza chimene anatenga ngati chikole cha ngongole, kubweza chimene anaba, kutsatira malamulo omwe amapereka moyo ndi kuleka kuchita zoyipa, iye adzakhala ndithu ndi moyo; sadzafa.
Jeśli bezbożny zwróci zastaw, odda to, co wydarł, i będzie chodził według praw życia, nie czyniąc nieprawości, na pewno będzie żył i nie umrze.
16 Ndidzakhululuka machimo ake onse anachita. Iye wachita zimene ndi zolungama ndi zoyenera ndipo iye adzakhala ndi moyo ndithu.
Żadne jego grzechy, które popełnił, nie będą mu wspominane. Czynił to, co prawe i sprawiedliwe; na pewno będzie żył.
17 “Komabe anthu a mtundu wako akunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Ayi, koma makhalidwe awo ndiwo ali osalungama.
Lecz synowie twego ludu mówią: Droga Pana nie jest słuszna, choć to ich droga nie jest słuszna.
18 Ngati munthu wolungama atembenuka ndi kuleka ntchito zake zolungama ndi kuyamba kuchita zoyipa, adzafa nazo.
Jeśli sprawiedliwy odwróci się od swojej sprawiedliwości i będzie czynił nieprawość, to umrze z jej powodu.
19 Ndipo ngati munthu woyipa atembenuka ndi kuleka ntchito zake zoyipa ndi kuyamba kuchita zolungama ndi zoyenera, iye adzakhala ndi moyo pochita zimenezo.
Ale jeśli bezbożny odwróci się od swojej bezbożności i będzie czynił to, co prawe i sprawiedliwe, to dzięki temu będzie żył.
20 Koma Inu Aisraeli, mukunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Ayi, inu Aisraeli, Ine ndidzaweruza aliyense wa inu potsata ntchito zake.”
Wy jednak mówicie: Droga Pana nie jest słuszna. Domu Izraela, będę sądził każdego z was według jego drogi.
21 Pa tsiku lachisanu la mwezi wakhumi, chaka chakhumi ndi chiwiri cha ukapolo wathu, munthu wina amene anapulumuka ku Yerusalemu anabwera kudzandiwuza kuti, “Mzinda wagwa!”
I stało się w dwunastym roku naszego uprowadzenia, w dziesiątym [miesiącu], piątego [dnia] tego miesiąca, że przyszedł do mnie jeden zbieg z Jerozolimy, mówiąc: Zdobyto miasto.
22 Tsono madzulo ake munthuyo asanafike, dzanja la Yehova linali pa ine. Koma mmawa mwake munthuyo atabwera Yehova anatsekula pakamwa panga, motero kuti sindinakhalenso wosayankhula.
A ręka PANA była nade mną wieczorem, zanim przyszedł ten zbieg, i otworzyła moje usta, aż ten przyszedł do mnie rano. Otworzyła moje usta i nie byłem już niemy.
23 Ndipo Yehova anandiyankhula kuti:
I doszło do mnie słowo PANA mówiące:
24 “Iwe mwana wa munthu, anthu amene akukhala mʼmizinda ya mabwinja ya dziko la Israeli akunena kuti, ‘Abrahamu anali munthu mmodzi yekha, ndipo anamupatsa dziko lonse. Koma ife tilipo ambiri, motero tsono dzikolo ndi lathu.’
Synu człowieczy, mieszkańcy tych spustoszonych miejsc w ziemi Izraela mówią: Abraham był jeden i wziął ziemię w posiadanie. Ale nas jest wielu, nam więc dana jest ta ziemia w posiadanie.
25 Choncho iwe uwawuze kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti, ‘Inu mumadya nyama ili ndi magazi ake, ndipo mumapembedza mafano ndi kukhetsa magazi, kodi tsono inu nʼkulandira dzikoli?
Dlatego mów do nich: Tak mówi Pan BÓG: Jadacie z krwią, podnosicie swe oczy ku swoim bożkom i przelewacie krew, a ziemię chcielibyście wziąć w posiadanie?
26 Mumadalira lupanga lanu, mumachita zinthu zonyansa, ndipo aliyense wa inu amachita chigololo ndi mkazi wa mnzake. Kodi inu nʼkulandira dzikoli?’
Opieracie się na swoim mieczu, popełniacie obrzydliwość i każdy plugawi żonę swego bliźniego, a ziemię chcielibyście wziąć w posiadanie?
27 “Uwawuze kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti, ‘Ndithu pali Ine wamoyo, anthu amene anatsala mʼmizinda ya mabwinja adzaphedwa ndi lupanga, amene ali ku midzi ndidzawapereka kuti adzadyedwe ndi zirombo zakuthengo, ndipo amene ali mʼmalinga ndi mʼmapanga adzafa ndi mliri.
Tak im powiedz: Tak mówi Pan BÓG: Jak żyję, ci, którzy są w spustoszonych miejscach, polegną od miecza, a [kto jest na] otwartym polu, tego wydam zwierzętom na pożarcie, a ci, którzy są w warowniach lub w jaskiniach, umrą od zarazy.
28 Ndidzalisandutsa chipululu dzikolo, ndipo mphamvu zake zimene amanyadira zidzatheratu, ndipo mapiri a Yerusalemu adzasanduka chipululu, kotero kuti palibe amene adzatha kudutsako.
I wydam ziemię na wielkie spustoszenie, i ustanie pycha jej mocy; spustoszeją góry Izraela i nikt przez nie nie będzie przechodził.
29 Ndikadzasandutsa dzikolo chipululu chifukwa cha zonyansa zimene ankachita, pamenepo ndiye adzadziwa kuti ndine Yehova.’
I poznają, że ja jestem PANEM, gdy wydam [ich] ziemię na wielkie spustoszenie z powodu wszystkich ich obrzydliwości, które czynili.
30 “Koma kunena za iwe, mwana wa munthu, anthu a mtundu wako akumayankhula za iwe akakhala pa makoma a mzinda ndi pa makomo a nyumba zawo. Akumawuzana kuti, ‘Tiyeni tikamve uthenga umene wachokera kwa Yehova.’
Ale co do ciebie, synu człowieczy, synowie twego ludu często rozmawiają o tobie przy murach i w drzwiach domów, i mówi jeden do drugiego, każdy do swego bliźniego: Chodźcie i posłuchajcie, co za słowo wyszło od PANA.
31 Anthu anga amabwera kwa iwe, monga momwe amachitira nthawi zonse anthu anga, ndipo amakhala pansi pamaso pako kumvetsera mawu ako. Koma zimene akumvazo sazichita. Zokamba zawo zimaonetsa chikondi, koma mitima yawo imakhala pa phindu lawo.
I przychodzą do ciebie, tak zwykł przychodzić lud, zasiadają przed tobą [jak] mój lud i słuchają twoich słów, ale ich nie wypełniają. Mają bowiem miłość na ustach, lecz ich serce podąża za niegodziwym zyskiem.
32 Kunena zoona, kwa iwowo sindiwe kanthu konse, ndiwe munthu wamba chabe womangoyimba nyimbo zachikondi ndi liwu lokoma poyimba zeze. Kumva amamva mawu ako koma sawagwiritsa ntchito.
A oto jesteś dla nich jak urokliwa pieśń [tego, który] ma piękny głos i cudownie gra. Słuchają bowiem twoich słów, ale ich nie wykonują.
33 “Koma zonsezi zikadzachitika, ndipo zidzachitika ndithu, pamenepo adzadziwa kuti mneneri anali pakati pawo.”
Lecz gdy to nadejdzie – oto nadejdzie – wtedy poznają, że prorok był pośród nich.

< Ezekieli 33 >