< Ezekieli 33 >

1 Yehova anandiyankhula nati:
Then the word of Yahweh came to me, saying,
2 “Iwe mwana wa munthu awuze anthu a mtundu wako kuti, ‘Paja zimati ndikatumiza nkhondo mʼdziko anthu a mʼdzikomo amasankha munthu mmodzi pakati pawo kuti akhale mlonda.
“Son of man, declare this to your people; say to them, 'When I bring a sword against any land, then the people of that land take one man from among themselves and make him a watchman for them.
3 Tsono iyeyo amati akaona nkhondo ikubwera amaliza lipenga kuti achenjeze anthuwo.
He looks for the sword as it comes on the land, and he blows his horn to warn the people!
4 Wina aliyense akamva lipenga koma osasamala, mdani uja akabwera nʼkumupha, ndiye kuti wadziphetsa yekha.
If the people hear the sound of the horn but do not pay attention, and if the sword comes and kills them, then each one's blood is on his own head.
5 Iye anamva kulira kwa lipenga koma sanalabadire. Ndiye kuti wadziphetsa yekha. Akanasamala kuchenjeza kwa mlonda akanapulumuka.
If someone hears the sound of the horn and pays no attention, his blood is on him; but if he pays attention, he will save his own life.
6 Koma ngati mlondayo aona lupanga likubwera ndipo osawomba lipengalo kuchenjeza anthu, ndipo lupanga libwera ndi kuchotsa moyo wa mmodzi mwa iwo, munthu ameneyo adzafa chifukwa cha tchimo lake, koma ndidzamuyimba mlandu mlondayo chifukwa cha imfa ya mnzakeyo.’
However, if the watchman sees the sword as it is coming, but if he does not blow the horn, with the result that the people are not warned, and if the sword comes and takes anyone's life, then that person dies in his own sin, but I will require his blood from the watchman.'
7 “Tsono iwe mwana wa munthu, ndakuyika kuti ukhale mlonda wa Aisraeli. Choncho imva mawu amene ndikuyankhula ndipo uwachenjeze.
Now you yourself, son of man! I have made you a watchman for the house of Israel; you will hear the words from my mouth and warn them on my behalf.
8 Ndikawuza munthu woyipa kuti, ‘Iwe munthu woyipa, udzafa ndithu,’ ndipo iwe osayankhula kumuchenjeza kuti aleke njira zake, munthu wochimwayo adzafa chifukwa cha tchimo lake, koma Ine ndidzakuyimba mlandu chifukwa cha imfa yake.
If I say to a wicked person, 'Wicked one, you will surely die!' but if you do not announce this so as to warn the wicked about his way, then he who is wicked will die in his sin, but I will require his blood from your hand!
9 Koma ngati uchenjeza munthu woyipa kuti aleke njira zake, ndipo iye osatero, adzafa chifukwa cha tchimo lake, koma iwe udzapulumutsa moyo wako.
But you, if you warn the wicked about his way, so that he might turn back from it, and if he does not turn back from his way, then he will die in his sin, but you yourself will have saved your own life.
10 “Iwe mwana wa munthu, akumbutse Aisraeli mawu awo akuti, ‘Ife talemedwa ndi zolakwa zathu ndi machimo athu, ndipo tikuwonda chifukwa cha zimene tachita. Kodi tingakhale ndi moyo bwanji?’”
So you, son of man, say to the house of Israel, 'You are saying this, “Our transgressions and our sins are on us, and we are decaying in them! How can we live?”'
11 Uwawuze kuti, Ine Ambuye Yehova ndikuti: “Pali Ine wamoyo, sindikondwera ndi imfa ya munthu woyipa. Ndimakondwera ndikamaona munthu woyipa akuleka zoyipa zake kuti akhale ndi moyo. Tembenukani! Tembenukani, siyani makhalidwe anu oyipa! Muferanji, Inu Aisraeli?
Say to them, 'As I live—this is the Lord Yahweh's declaration—I do not delight in the death of the wicked, for if the wicked repents from his way, then he will live! Repent! Repent from your wicked ways! For why should you die, house of Israel?'
12 “Tsono iwe mwana wa munthu, awuze anthu a mtundu wako kuti, ‘Ngati munthu wolungama achimwa, ndiye kuti ntchito zake zabwino zija sizidzamupulutsa. Koma wochimwa akaleka ntchito zake zoyipazo, sadzalangidwa konse. Ndithu ngati munthu wolungama ayamba kuchimwa sadzatha kukhala ndi moyo chifukwa cha ntchito zake zabwino zija.’
So now you, son of man, say to your people, 'The righteousness of a righteous person will not save him if he sins! The wickedness of a wicked person will not cause him to perish if he repents from his sin! For the righteous person will not be able to live because of his righteousness if he sins.
13 Ngati ndiwuza munthu wolungama kuti adzafa ndithu, koma iyeyo nʼkumadalira ntchito zake zabwino zimene anachita kale ndi kuyamba kuchimwa, ndiye kuti ntchito zake zabwinozo zidzayiwalika. Iye adzafa chifukwa cha machimo ake.
If I say to the righteous, “He will surely live!” and if he trusts in his righteousness and then commits injustice, I will not call to mind any of his righteousness. He will die for the wickedness he committed.
14 Ndipo ngati ndiwuza munthu woyipa kuti, ‘Udzafa ndithu,’ tsono iye nʼkutembenuka kuleka machimo ake ndi kuyamba kuchita zimene Yehova afuna,
So if I say to the wicked, “You will surely die,” but if he then repents from his sins and does what is just and right—
15 monga kubweza chimene anatenga ngati chikole cha ngongole, kubweza chimene anaba, kutsatira malamulo omwe amapereka moyo ndi kuleka kuchita zoyipa, iye adzakhala ndithu ndi moyo; sadzafa.
if he restores the loan guarantee that he wickedly demanded, or if he makes restitution for what he has stolen, and if he walks in the statutes that give life and no longer commits sin—then he will surely live. He will not die.
16 Ndidzakhululuka machimo ake onse anachita. Iye wachita zimene ndi zolungama ndi zoyenera ndipo iye adzakhala ndi moyo ndithu.
None of the sins that he has committed will be called to mind for him. He has acted justly and rightly, and so, he will surely live!
17 “Komabe anthu a mtundu wako akunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Ayi, koma makhalidwe awo ndiwo ali osalungama.
But your people say, “The way of the Lord is not fair!” but it is your ways that are not fair!
18 Ngati munthu wolungama atembenuka ndi kuleka ntchito zake zolungama ndi kuyamba kuchita zoyipa, adzafa nazo.
When the righteous person turns away from his righteousness and commits sin, then he will die in it!
19 Ndipo ngati munthu woyipa atembenuka ndi kuleka ntchito zake zoyipa ndi kuyamba kuchita zolungama ndi zoyenera, iye adzakhala ndi moyo pochita zimenezo.
When the wicked turns away from his wickedness and does what is just and righteous, he will live because of those things!
20 Koma Inu Aisraeli, mukunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Ayi, inu Aisraeli, Ine ndidzaweruza aliyense wa inu potsata ntchito zake.”
But you people say, “The way of the Lord is not fair!” I will judge each of you according to his way, house of Israel!'”
21 Pa tsiku lachisanu la mwezi wakhumi, chaka chakhumi ndi chiwiri cha ukapolo wathu, munthu wina amene anapulumuka ku Yerusalemu anabwera kudzandiwuza kuti, “Mzinda wagwa!”
It happened in the twelfth year, on the fifth day of the tenth month of our captivity, that a fugitive came to me from Jerusalem and said, “The city has been captured!”
22 Tsono madzulo ake munthuyo asanafike, dzanja la Yehova linali pa ine. Koma mmawa mwake munthuyo atabwera Yehova anatsekula pakamwa panga, motero kuti sindinakhalenso wosayankhula.
The hand of Yahweh had been on me in the evening before the fugitive came, and my mouth was opened by the time that he came to me in the dawn. So my mouth was open; I was no longer mute!
23 Ndipo Yehova anandiyankhula kuti:
Then the word of Yahweh came to me, saying,
24 “Iwe mwana wa munthu, anthu amene akukhala mʼmizinda ya mabwinja ya dziko la Israeli akunena kuti, ‘Abrahamu anali munthu mmodzi yekha, ndipo anamupatsa dziko lonse. Koma ife tilipo ambiri, motero tsono dzikolo ndi lathu.’
“Son of man, the ones inhabiting those ruins in the land of Israel are talking and say, 'Abraham was only one person, and he inherited the land, but we are many! The land has been given to us as a possession.'
25 Choncho iwe uwawuze kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti, ‘Inu mumadya nyama ili ndi magazi ake, ndipo mumapembedza mafano ndi kukhetsa magazi, kodi tsono inu nʼkulandira dzikoli?
Therefore say to them, 'The Lord Yahweh says this: You eat blood, and you lift up your eyes towards your idols, then you pour out people's blood. Should you really possess the land?
26 Mumadalira lupanga lanu, mumachita zinthu zonyansa, ndipo aliyense wa inu amachita chigololo ndi mkazi wa mnzake. Kodi inu nʼkulandira dzikoli?’
You have depended on your swords and have done disgusting things; each man defiles his neighbor's wife. Should you really possess the land?'
27 “Uwawuze kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti, ‘Ndithu pali Ine wamoyo, anthu amene anatsala mʼmizinda ya mabwinja adzaphedwa ndi lupanga, amene ali ku midzi ndidzawapereka kuti adzadyedwe ndi zirombo zakuthengo, ndipo amene ali mʼmalinga ndi mʼmapanga adzafa ndi mliri.
You will say this to them, 'The Lord Yahweh says this: As I live, surely the ones in the ruins will fall by the sword, and I will give those in the fields to the living creatures as food, and those in fortresses and in caves will die of plagues.
28 Ndidzalisandutsa chipululu dzikolo, ndipo mphamvu zake zimene amanyadira zidzatheratu, ndipo mapiri a Yerusalemu adzasanduka chipululu, kotero kuti palibe amene adzatha kudutsako.
Then I will turn the land into a desolation and a horror, and the pride of its might will end, for the mountains of Israel will be deserted, and there will be no one to pass through them.'
29 Ndikadzasandutsa dzikolo chipululu chifukwa cha zonyansa zimene ankachita, pamenepo ndiye adzadziwa kuti ndine Yehova.’
So they will know that I am Yahweh, when I make the land a desolation and a waste because of all the abominations that they have done.
30 “Koma kunena za iwe, mwana wa munthu, anthu a mtundu wako akumayankhula za iwe akakhala pa makoma a mzinda ndi pa makomo a nyumba zawo. Akumawuzana kuti, ‘Tiyeni tikamve uthenga umene wachokera kwa Yehova.’
So now you, son of man—your people are saying things about you beside the walls and the gates of the houses, and each says to one another—each man to his brother, 'Let us go and listen to the prophet's word that comes out from Yahweh!'
31 Anthu anga amabwera kwa iwe, monga momwe amachitira nthawi zonse anthu anga, ndipo amakhala pansi pamaso pako kumvetsera mawu ako. Koma zimene akumvazo sazichita. Zokamba zawo zimaonetsa chikondi, koma mitima yawo imakhala pa phindu lawo.
So my people will come to you, as they often do, and will sit in front of you and listen to your words, but they will not obey them. Right words are in their mouths, but their hearts are going after unjust profit.
32 Kunena zoona, kwa iwowo sindiwe kanthu konse, ndiwe munthu wamba chabe womangoyimba nyimbo zachikondi ndi liwu lokoma poyimba zeze. Kumva amamva mawu ako koma sawagwiritsa ntchito.
For you are like a lovely song to them, a beautiful sound that is well played on a stringed instrument, so they will listen to your words, but none of them will obey them.
33 “Koma zonsezi zikadzachitika, ndipo zidzachitika ndithu, pamenepo adzadziwa kuti mneneri anali pakati pawo.”
So when all of this happens—behold! it will happen!—then they will know that a prophet has been among them.”

< Ezekieli 33 >