< Ezekieli 11 >

1 Pamenepo Mzimu wa Mulungu unandinyamula ndi kubwera nane ku chipata cha kummawa cha Nyumba ya Yehova. Kumeneko pa khomo la chipata panali anthu 25, ndipo ndinaona pakati pawo atsogoleri awa: Yaazaniya mwana wa Azuri ndi Pelatiya mwana wa Benaya.
Lapho-ke uMoya wangiphakamisela phezulu wangisa esangweni lendlu kaThixo elikhangele empumalanga. Khonapho ekungeneni kwesango kwakulamadoda angamatshumi amabili lanhlanu, njalo phakathi kwawo ngabona uJazaniya indodana ka-Azuri kanye loPhelathiya indodana kaBhenayiya, abakhokheli babantu.
2 Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, awa ndi anthu amene akukonza zoyipa ndi kupereka malangizo oyipa mu mzindamo.
UThixo wathi kimi, “Ndodana yomuntu, laba yibo abantu abenza amacebo amabi, benika lezeluleko ezimbi kulelidolobho.
3 Iwo amawuza anthu kuti, ‘Nthawi sinafike yoti timange Nyumba? Mzindawu uli ngati mʼphika umene uli pa moto ndipo ife tili ngati nyama mu mʼphikamo.
Bathi, ‘Masinyane nje akuyikuba yiso na isikhathi sokwakha izindlu? Idolobho leli liyimbiza yokupheka, njalo thina siyinyama.’
4 Choncho iwe mwana wa munthu, unenere mowadzudzula. Nenera ndithu.’”
Ngakho-ke phrofetha okubi ngabo; phrofetha ndodana yomuntu.”
5 Ndipo Mzimu wa Yehova unandigwera ndipo unandiwuza kuti, “Unene kuti zimene akunena Yehova ndi izi. Iye akuti. ‘Izi ndi zimene mukunena, Inu Aisraeli, koma Ine ndikudziwa zimene zili mu mtima mwanu.’
Lapho-ke uMoya kaThixo weza kimi wangitshela ukuba ngithi, Nanku okutshiwo nguThixo: “Lokho yikho wena okutshoyo, wena ndlu ka-Israyeli, kodwa mina ngiyakwazi okusengqondweni yakho.
6 Mwapha anthu ambiri mu mzinda muno ndipo mwadzaza misewu yake ndi mitembo.
Sewabulala abantu abanengi phakathi kwedolobho leli wagcwalisa imigwaqo yalo ngabafileyo.”
7 “Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti, ‘Mitembo imene mwayiponya mʼmisewuyo ndiyo nyama ndipo mzinda uno ndiwo mʼphika, koma Ine ndidzakuthamangitsanimo.
Ngakho-ke nanku okutshiwo nguThixo Wobukhosi: “Izidumbu oziphosele lapho ziyinyama njalo idolobho leli liyimbiza, kodwa wena ngizakuxotshela ngaphandle kwalo.
8 Inu mumaopa lupanga, koma lupangalo ndi limene ndidzakubweretsereni, akutero Ambuye.
Inkemba uyayesaba, njalo inkemba yiyo engizayiletha ukuba imelane lawe, kutsho uThixo Wobukhosi.
9 Ine ndidzakuthamangitsani mu mzinda ndipo ndidzakuperekani mʼdzanja la alendo kuti akulangeni.
Ngizakuxotshela ngaphandle kwedolobho ngikunikele kwabezizweni ngiphinde ngikujezise.
10 Mudzaphedwa ndi lupanga ndipo ndidzakulangani mpaka kumalire a Israeli. Pamenepo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
Uzabulawa ngenkemba, njalo ngizakwahlulela emingceleni yako-Israyeli. Lapho-ke uzakwazi ukuthi mina nginguThixo.
11 Mzinda uno sudzakhala ngati mʼphika wokutetezani ndipo simudzakhalanso ngati nyama ya mʼmenemo. Ndidzakulangani mpaka kumalire a Israeli.
Idolobho leli kaliyikuba yimbiza yakho, kumbe wena ube yinyama phakathi kwalo; ngizakwahlulela emingceleni yako-Israyeli.
12 Ndipo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova. Inu simunatsatire malangizo anga kapena kusunga malamulo anga koma mwakhala mukutsata zochita za mitundu ina ya anthu imene yakuzungulirani.’”
Njalo uzakwazi ukuthi mina nginguThixo, ngoba izimiso zami kawuzilandelanga kumbe wagcina imithetho yami kodwa ulandele izenzo zezizwe ezikuhanqileyo.”
13 Tsono pamene ndinkanenera, Pelatiya mwana wa Benaya anafa. Pomwepo ndinadzigwetsa pansi chafufumimba ndipo ndinafuwula ndi mawu aakulu kuti “Mayo, Ambuye Yehova! Kodi mudzawatheratu Aisraeli onse otsala?”
Kwathi lapho ngisaphrofitha, uPhelathiya indodana kaBhenayiya wafa. Ngakho ngathi mbo phansi ngobuso ngakhala ngelizwi eliphezulu ngisithi, “Awu, Thixo Wobukhosi! Uzaqothula insalela ka-Israyeli na?”
14 Yehova anayankhula nane kuti,
Ilizwi likaThixo lafika kimi lisithi:
15 “Anthu okhala ku Yerusalemu akuwanena abale ako, anthu a ku ukapolo, onse a banja la Israeli, kuti, ‘Anthu onse amene anatengedwa ukapolo ali kutali ndi Yehova. Dziko lanu Yehova anatipatsa kuti likhale lathulathu.’”
“Ndodana yomuntu, abafowenu, abafowenu abayizihlobo zakho zegazi kanye lendlu yonke ka-Israyeli, yibo labo abantu baseJerusalema abathe ngabo: ‘Bakhatshana loThixo kakhulu; ilizwe leli saliphiwa ukuba libe yilifa lethu.’”
16 “Nʼchifukwa chake nena kwa anzako a ku ukapolo kuti, ‘Ambuye Yehova akuti: Ine ndinawatumiza kutali pakati pa anthu a mitundu ina. Ndinawabalalitsa ku mayiko ambiri. Komabe ndakhala ndikuwasunga ku mayiko kumene anapitako!’
“Ngakho-ke wothi: ‘Nanku okutshiwo nguThixo Wobukhosi: Lanxa ngabasa khatshana phakathi kwezizwe njalo ngabahlakazela phakathi kwamazwe, ikanti okwesikhatshana ngibe yindlu engcwele kubo emazweni abaye kuwo.’
17 “Nʼchifukwa chake uwawuze zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena kuti, Ndidzawasonkhanitsa kuchokera kwa anthu a mitundu inayo ndi kuwasonkhanitsira pamodzi kuchokera ku mayiko kumene ndinawabalalitsirako. Pambuyo pake ndidzawapatsa dziko la Israeli.
Ngakho-ke wothi: ‘Nanku okutshiwo nguThixo Wobukhosi: Ngizakubutha ezizweni ngikubuyise ngikususa emazweni owawuhlakazekele kuwo, njalo ngizakunika ilizwe lako-Israyeli futhi.’
18 “Akadzalowa mʼdzikomo adzachotsa mafano awo onse oyipa ndi onyansa.
Bazabuyela kulo basuse zonke izifanekiso zalo ezihlazisayo kanye lezithombe ezenyanyekayo.
19 Ndidzawapatsa mtima watsopano ndipo ndidzayika mzimu watsopano mwa iwo. Ndidzachotsa mtima wowuma ngati mwala mwa iwo, ndipo ndidzawapatsa mtima wofewa ngati mnofu.
Ngizabanika inhliziyo engehlukananga ngifake lomoya omutsha phakathi kwabo; ngizasusa kubo inhliziyo yabo yelitshe ngibaphe inhliziyo yenyama.
20 Motero adzatsata malamulo anga ndipo adzasunga mosamala malamulo anga. Adzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wawo.
Lapho-ke bazalandela izimiso zami baqaphele ukugcina imithetho yami. Bazakuba ngabantu bami, lami ngizakuba nguNkulunkulu wabo.
21 Koma kunena za amene akupembedza mafano oyipa ndi onyansa, ndidzawalanga chifukwa cha zimene achita. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”
Kodwa labo abanhliziyo zabo zinikelwe ezifanekisweni zabo ezihlazisayo lasezithombeni ezenyanyekayo, lokhu abakwenzileyo ngizakwehlisela phezu kwamakhanda abo, kutsho Thixo Wobukhosi.”
22 Tsono akerubi aja anatambasula mapiko awo kuyamba kuwuluka, mikombero ili mʼmbali mwawo. Ulemerero wa Mulungu wa Israeli unali pamwamba pawo.
Lapho-ke amakherubhi, ayelamavili emaceleni, elula impiko zawo, njalo inkazimulo kaNkulunkulu ka-Israyeli yayingaphezu kwawo.
23 Ulemerero wa Yehova unakwera ndi kusiya mzindawo ndipo unakayima pa phiri cha kummawa kwake kwa mzindawo.
Inkazimulo kaThixo yaya phezulu isuka phakathi kwedolobho yayakuma ngaphezu kwentaba ngasempumalanga kwedolobho.
24 Pambuyo pake Mzimu wa Mulungu unandinyamula ndi kukandifikitsa. Zimenezi zinkachitika mʼmasomphenya monga mmene Mzimu wa Mulungu unkandionetsera. Kenaka masomphenya amene ndinkawaonawo anayamba kuzimirira.
UMoya wangiphakamisela phezulu wangisa kwabathunjiweyo eBhabhiloni ngombono owawulethwe nguMoya kaNkulunkulu. Emva kwalokho umbono engangiwubonile wasuka kimi,
25 Ndipo ndinafotokozera akapolowo zonse zimene Yehova anandionetsa.
ngasengitshela abathunjiweyo konke Thixo ayengitshengise khona.

< Ezekieli 11 >