< Eksodo 5 >

1 Zitachitika izi, Mose ndi Aaroni anapita kwa Farao ndipo anati, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Aloleni anthu anga apite, kuti akachite chikondwerero cha Ine mʼchipululu.’”
Ensuite Moïse et Aaron se rendirent auprès de Pharaon et lui dirent: " Ainsi parle Yahweh, le Dieu d'Israël: Laisse aller mon peuple, pour qu'il célèbre une fête en mon honneur dans le désert. "
2 Koma Farao anati, “Yehova ndani kuti ine ndimumvere ndi kulola Aisraeli kuti apite? Ine Yehova sindikumudziwa ndipo sindilola kuti Aisraeli apite.”
Pharaon répondit: " Qui est Yahweh pour que j'obéisse à sa voix, en laissant aller Israël? Je ne connais pas Yahweh, et je ne laisserai pas aller Israël. "
3 Ndipo iwo anati, “Mulungu wa Ahebri anakumana nafe. Chonde tiloleni tipite ulendo wa masiku atatu ku chipululu kuti tikapereke nsembe kwa Yehova Mulungu wathu, ngati sititero iye adzatipweteka ndi miliri kapena lupanga.”
Ils dirent: " Le Dieu des Hébreux s'est présenté à nous. Permets-nous de faire trois journées de marche au désert, pour offrir des sacrifices à Yahweh, afin qu'il ne nous frappe pas de la peste ou de l'épée. "
4 Koma mfumu ya Igupto inati, “Mose ndi Aaroni, chifukwa chiyani mukuchititsa anthuwa kuti asagwire ntchito zawo? Bwererani ku ntchito zanu!”
Mais le roi d'Egypte leur dit: " Pourquoi, Moïse et Aaron, détournez-vous le peuple de son ouvrage? Allez à vos corvées! "
5 Ndiponso Farao anati, “Taonani, anthuwa mʼdziko muno alipo ochuluka, ndipo inu mukuwaletsa kugwira ntchito.”
Pharaon dit: " Voici que le peuple du pays est maintenant nombreux, et vous lui feriez interrompre ses corvées! "
6 Pa tsiku lomwelo Farao analamulira akapitawo a thangata ndi anzawo a Chiisraeli amene ankayangʼanira anthu kuti
Ce jour-là même, Pharaon donna cet ordre aux exacteurs du peuple et aux scribes:
7 “Inu musawapatsenso udzu wopangira njerwa monga mumachitira kale, iwo azipita ndi kukatenga udzu wawo.
" Vous ne donnerez plus, comme on l'a fait jusqu'ici, de paille au peuple pour faire des briques; qu'ils aillent eux-mêmes ramasser de la paille.
8 Koma musawachepetsere chiwerengero cha njerwa chomwe munawalamulira kale kuti aziwumba. Iwowa ndi aulesi. Nʼchifukwa chake akulira kuti, ‘Tiloleni tipite tikapereke nsembe kwa Mulungu wathu.’
Néanmoins vous lui imposerez la quantité de briques qu'ils faisaient auparavant, sans en rien retrancher, car ce sont des paresseux; voilà pourquoi ils crient, en disant: Nous voudrions aller faire des sacrifices à notre Dieu.
9 Muwakhawulitse ndi ntchito anthu amenewa kuti azitanganidwa, asakhale ndi mpata omvera zabodza.”
Qu'on charge de travail ces gens-là; qu'ils soient à la besogne et qu'ils ne prêtent plus l'oreille à des paroles de mensonge. "
10 Choncho akapitawo a thangata ndi anzawo a Chiisraeli amene ankayangʼanira anthu anapita kwa anthu aja nati, “‘Farao akuti sadzakupatsaninso udzu.
Les exacteurs du peuple et les scribes vinrent donc dire au peuple: " Ainsi parle Pharaon: Je ne vous donne plus de paille;
11 Mʼmalo mwake mupite mukadzimwetere udzu kulikonse kumene mungawupeze. Komabe ntchito yanu sichepetsedwa.’”
allez vous-mêmes prendre de la paille où vous en trouverez, car on ne retranchera rien de votre tâche. "
12 Kotero anthuwo anamwazikana mʼdziko lonse la Igupto kukamweta udzu.
Le peuple se répandit dans tout le pays d'Egypte pour ramasser du chaume pour en faire de la paille hachée.
13 Akapitawo a thangata aja anawafulumiza anthu aja nati, “Malizani kugwira ntchito yanu ya tsiku ndi tsiku monga mmene zinalili pamene munkapatsidwa udzu.”
Les exacteurs les pressaient, en disant: " Achevez vos travaux, ce qui est fixé pour chaque jour, comme lorsqu'on avait de la paille. "
14 Akapitawo a thangata a Farao ankawamenya oyangʼanira anzawo a Chiisraeli aja nawapanikiza kuti, “Chifukwa chiyani lero simunawumbe chiwerengero chovomerezeka cha njerwa monga chakale chija?”
On battit les scribes des enfants d'Israël, que les exacteurs de Pharaon avaient établis sur eux; on disait: " Pourquoi n'avez-vous pas achevé hier et aujourd'hui votre tâche de briques, comme précédemment? "
15 Pamenepo oyangʼanira anzawo a Chiisraeli aja anapita kukadandaula kwa Farao kuti, “Chifukwa chiyani mwachitira antchito anu zotere?
Les scribes des enfants d'Israël allèrent se plaindre à Pharaon, en disant: " Pourquoi en agis-tu ainsi envers tes serviteurs?
16 Antchito anu sakupatsidwa udzu, komabe akutiwuza kuti, ‘Umbani njerwa!’ Antchito anu akumenyedwa, koma cholakwa sichili ndi anthu anu.”
On ne fournit pas de paille à tes serviteurs, et l'on nous dit: Faites des briques! Et voici, tes serviteurs sont battus, et ton peuple se trouve en faute. "
17 Farao anati, “Ulesi, inu ndinu alesi! Nʼchifukwa chake mukumanena kuti, ‘Mutilole tipite kukapereka nsembe kwa Yehova.’
Pharaon répondit: " Vous êtes des paresseux, des paresseux! Voilà pourquoi vous dites: Nous voudrions aller offrir des sacrifices à Yahweh.
18 Pitani tsopano kuntchito. Simudzapatsidwanso udzu komabe muyenera kuwumba muyeso wanu wovomerezeka wa njerwa.”
Et maintenant, allez travailler; on ne vous donnera pas de paille, et vous livrerez la même quantité de briques. "
19 Oyangʼanira anzawo a Chiisraeli anazindikira kuti ali pa mavuto pamene anawuzidwa kuti, “Musachepetse chiwerengero cha njerwa chimene muyenera kuwumba tsiku lililonse.”
Les scribes des enfants d'Israël virent leur cruelle situation, puisqu'on leur disait: " Vous ne retrancherez rien de vos briques; chaque jour la tâche du jour! "
20 Atachoka pamaso pa Farao, anakumana ndi Mose ndi Aaroni akuwadikira,
Ayant trouvé Moïse et Aaron, qui se tenaient là pour les attendre à leur sortie de chez Pharaon,
21 ndipo iwo anati, “Yehova akupenyeni ndi kukuweruzani popeza mwachititsa Farao ndi nduna zake kuti anyansidwe nafe ndipo mwayika lupanga mʼmanja mwawo kuti atiphe.”
ils leur dirent: " Que Yahweh vous voie, et qu'il juge, vous qui avez changé en aversion notre faveur aux yeux de Pharaon et de ses serviteurs, et qui avez mis dans leurs mains une épée pour nous tuer. "
22 Mose anabwerera kwa Yehova ndipo anati, “Chonde Ambuye, chifukwa chiyani mukuzunza anthu anu? Kodi munanditumira zimenezi?
Alors Moïse retourna vers Yahweh, et dit: " Seigneur, pourquoi avez-vous fait du mal à ce peuple? pourquoi donc m'avez-vous envoyé?
23 Chipitireni changa kwa Farao kukamuyankhula mʼdzina lanu, iye wakhala akuzunza anthuwa, ndipo inu simunawapulumutse konse anthu anu.”
Depuis que je suis allé vers Pharaon pour parler en votre nom, il maltraite ce peuple, et vous n'avez en aucune manière délivré votre peuple. "

< Eksodo 5 >