< Eksodo 38 >

1 Anapanga guwa lansembe zopsereza lamatabwa amtengo wa mkesha. Linali lofanana mbali zonse. Msinkhu wake masentimita 137, mulitali mwake masentimita 229, mulifupi masentimita 229.
Il fit aussi de bois de Sittim l'autel des holocaustes; et sa longueur était de cinq coudées, et sa largeur de cinq coudées; il était carré; et sa hauteur [était] de trois coudées.
2 Anapanga nyanga imodziimodzi pa ngodya zake zinayizo, kotero kuti nyangazo ndi guwalo zinali chinthu chimodzi, ndipo anakuta guwalo ndi mkuwa.
Et il fit ses cornes à ses quatre coins; ses cornes sortaient de lui, et il le couvrit d'airain.
3 Anapanganso ziwiya zamkuwa izi zogwirira ntchito pa guwalo: miphika, mafosholo, mabeseni owazira magazi, ngowe zokowera nyama ndi zosonkhezera moto.
Il fit aussi tous les ustensiles de l'autel, les chaudrons, les racloirs, les bassins, les fourchettes, [et] les encensoirs; il fit tous ses ustensiles d'airain.
4 Anapanga sefa yachitsulo chamkuwa ya guwa lansembelo kuti ikhale mmunsi mwa khoma la guwa lansembelo, kuchokera pansi mpaka pakati pa khoma la guwalo.
Et il fit pour l'autel une grille d'airain, en forme de treillis, au-dessous de l'enceinte de l'autel, depuis le bas jusques au milieu.
5 Anapanga mphete zamkuwa zinayi ndipo anazilumikiza ku ngodya zinayi za sefa ija kuti zigwire nsichi zonyamulira.
Et il fondit quatre anneaux aux quatre coins de la grille d'airain, pour mettre les barres.
6 Anapanga nsichi zamtengo wa mkesha ndipo anazikuta ndi mkuwa.
Et il fit les barres de bois de Sittim, et les couvrit d'airain.
7 Iwo analowetsa nsichizo mʼmphetemo mbali zonse ziwiri za guwalo kuti azinyamulira. Guwalo linali lamatabwa ndi logoba mʼkati mwake.
Et il fit passer les barres dans les anneaux, aux côtés de l'autel, pour le porter avec elles, le faisant d'ais, et creux.
8 Anapanga beseni lamkuwa lokhala ndi miyendo yamkuwanso kuchokera ku magalasi oyangʼanira nkhope a amayi amene ankatumikira pa chipata cha tenti ya msonkhano.
Il fit aussi la cuve d'airain et son soubassement d'airain des miroirs des femmes qui s'assemblaient par troupes; qui s'assemblaient, [dis-je], par troupes à la porte du Tabernacle d'assignation.
9 Kenaka anapanga bwalo la chihema. Mbali yakummwera inali yotalika mamita 46 ndipo kunali nsalu yotchinga yofewa yosalala yolukidwa bwino.
Il fit aussi un parvis, pour le côté qui regarde vers le Midi, [et] des courtines de fin lin retors, de cent coudées, pour le parvis.
10 Anapanganso mizati makumi awiri, matsinde makumi awiri amkuwa ndi ngowe zasiliva ndi zingwe za mizatiyo.
Et il fit d'airain leurs vingt piliers avec leurs vingt soubassements, [mais] les crochets des piliers et leurs filets étaient d'argent.
11 Mbali yakumpoto inalinso yotalika mamita 46 ndipo inali ndi mizati makumi awiri, matsinde amkuwa makumi awiri, ngowe zasiliva ndi zingwe za mizatiyo.
Et pour le côté du Septentrion, il fit des [courtines] de cent coudées, leurs vingt piliers et leurs vingt soubassements étaient d'airain, mais les crochets des piliers et leurs filets étaient d'argent.
12 Mbali yakumadzulo inali yotalika mamita 23 ndipo inali ndi nsalu yotchinga, mizati khumi ndi matsinde khumi. Inalinso ndi ngowe zasiliva ndi zingwe za mizatiyo.
Et pour le côté de l'Occident, des courtines de cinquante coudées, leurs dix piliers, et leurs dix soubassements; les crochets des piliers et leurs filets étaient d'argent.
13 Mbali yakummawa, kotulukira dzuwa, inalinso yotalika mamita 23.
Et pour le côté de l'Orient droit vers le Levant, [des courtines] de cinquante coudées.
14 Mbali imodzi yachipata kunali nsalu yotchinga yotalika mamita asanu ndi awiri, mizati itatu ndi matsinde atatu,
Il fit pour l'un des côtés quinze coudées de courtines, [et] leurs trois piliers avec leurs trois soubassements;
15 polowera mʼbwalo panali nsalu yotchinga ya mamita asanu ndi awiri pamodzi ndi mizati itatu ndi matsinde atatu.
Et pour l'autre côté, quinze coudées de courtines, afin qu'il y en eût autant deçà que delà de la porte du parvis, [et] leurs trois piliers avec leurs trois soubassements.
16 Katani yonse yotchinga kuzungulira chihema inali yofewa, yosalala ndi yolukidwa bwino.
Il fit donc toutes les courtines du parvis qui étaient tout à l’entour, de fin lin retors.
17 Matsinde amizati anali amkuwa. Ngowe ndi zingwe za mizati zinali zasiliva, ndipo pamwamba pa mizatiyo anakutapo siliva. Choncho mizati yonse ya bwalolo inalumikizidwa ndi zingwe zasiliva.
Il fit aussi d'airain les soubassements des piliers, mais il fit d'argent les crochets des piliers, et les filets, et leurs chapiteaux furent couverts d'argent, et tous les piliers du parvis furent ceints à l’entour d'un filet d'argent.
18 Nsalu yotchinga ya pa chipata inali yamtundu wa mtambo, yapepo ndi yofiira, yofewa yosalala ndi yopangidwa ndi anthu aluso. Nsaluyo inali yotalika mamita asanu ndi anayi, molingana ndi nsalu zotchinga bwalo. Msinkhu wake unali masentimita 229,
Et il fit la tapisserie de la porte du parvis de pourpre, d'écarlate, et de cramoisi, et de fin lin retors, d'ouvrage de broderie, de la longueur de vingt coudées, et de la hauteur, qui était la largeur, de cinq coudées; à la correspondance des courtines du parvis.
19 pamodzi ndi mizati yake inayi ndi matsinde amkuwa anayi. Ngowe ndi zingwe zake zinali za siliva, ndipo pamwamba pake pa mzati anakutapo ndi siliva.
Et ses quatre piliers avec leurs soubassements, d'airain, et leurs crochets, d'argent; la couverture aussi de leurs chapiteaux et leurs filets, d'argent.
20 Zikhomo za chihema ndi zina zonse zozungulira chihemacho zinali zamkuwa.
Et tous les pieux du Tabernacle et du parvis à l’entour, d'airain.
21 Chiwerengero cha zipangizo zimene anagwiritsa ntchito popanga chihema, chihema chaumboni, zimene Mose analamulira Alevi kuti alembe motsogozedwa ndi Itamara mwana wa Aaroni, wansembe, chinali ichi:
C'est ici le compte des choses qui furent employées au pavillon, [savoir] au pavillon du Témoignage, selon que le compte en fut fait par le commandement de Moïse, à quoi furent employés les Lévites, sous la conduite d'Ithamar, fils d'Aaron, sacrificateur.
22 Bezaleli mwana wa Uri, mwana wa Huzi wa fuko la Yuda anapanga chilichonse Yehova analamulira Mose,
Et Betsaléel, fils d'Uri, fils de Hur, de la Tribu de Juda, fit toutes les choses que l'Eternel avait commandées à Moïse.
23 pamodzi ndi Oholiabu mwana wa Ahisamaki, wa fuko la Dani, wa luso la zopangapanga ndi kulemba mapulani, ndi wopanga nsalu zolukidwa bwino za mtundu wa mtambo, yapepo ndi zofiira, zofewa ndi zosalala.
Et avec lui Aholiab fils d'Ahisamac, de la Tribu de Dan, les ouvriers, et ceux qui travaillaient en ouvrage exquis, et les brodeurs en pourpre, en écarlate, en cramoisi, et en fin lin.
24 Golide yense wochokera ku nsembe yoweyula amene anagwiritsa ntchito pa ntchito yonse yopanga malo wopatulika anali wolemera makilogalamu 1,000 potsata miyeso ya kumalo wopatulika.
Tout l'or qui fut employé pour l'ouvrage, [savoir] pour tout l'ouvrage du Sanctuaire, qui était de l'or d'oblation, [fut] de vingt-neuf talents, et de sept cent trente sicles, selon le sicle du Sanctuaire.
25 Siliva wochokera ku gulu lonse la anthu anali wolemerera makilogalamu 3,430, potsata miyeso ya ku malo wopatulika.
Et l'argent de ceux de l'assemblée qui furent dénombrés, fut de cent talents, et mille sept cent soixante et quinze sicles, selon le sicle du Sanctuaire:
26 Munthu aliyense amapereka beka imodzi, kufanana ngati makilogalamu 6, potsata muyeso wa ku malo wopatulika. Kuchokera kwa aliyense amene anawerengedwa kuyambira zaka 20 kapena kuposerapo, amuna onse analipo 603,550.
Un demi-sicle par tête, la moitié d'un sicle selon le sicle du Sanctuaire; tous ceux qui passèrent par le dénombrement depuis l'âge de vingt ans et au-dessus, furent six cent trois mille cinq cent cinquante.
27 Anagwiritsa ntchito siliva wolemera makilogalamu 3,400 kupanga matsinde 100 a ku malo wopatulika ndi makatani, ndipo makilogalamu 34 kupanga tsinde limodzi.
Il y eut donc cent talents d'argent pour fondre les soubassements du Sanctuaire, et les soubassements du voile, [savoir] cent soubassements de cent talents, un talent pour chaque soubassement.
28 Makilogalamu otsalawo anagwiritsa ntchito popanga ngowe zamzati kukutira pamwamba pa mizati ndiponso kupanga zingwe zake.
Mais des mille sept cent soixante et quinze [sicles], il fit les crochets pour les piliers, et il couvrit leurs chapiteaux, et en fit des filets à l’entour.
29 Mkuwa ochokera ku nsembe yoweyula unali makilogalamu 2,425.
L'airain d'oblation fut de soixante et dix talents, et deux mille quatre cents sicles;
30 Iwo anawugwiritsa ntchito popanga matsinde a pa chipata cha tenti ya msonkhano, guwa la mkuwa pamodzi ndi sefa yake ndiponso ziwiya zonse,
Dont on fit les soubassements de la porte du Tabernacle d'assignation, et l'autel d'airain avec sa grille d'airain, et tous les ustensiles de l'autel;
31 matsinde ozungulira bwalo ndiponso a pa chipata pake, ndi zikhomo zonse za tentiyo ndi matsinde a malo wozungulirapo.
Et les soubassements du parvis à l’entour, et les soubassements de la porte du parvis, et tous les pieux du pavillon, et tous les pieux du parvis à l’entour.

< Eksodo 38 >