< Eksodo 23 >

1 “Usafalitse mbiri yabodza. Usathandize munthu wolakwa pomuchitira umboni wonama.
Ungawuphathi umbiko wamanga, ungafaki isandla sakho lomubi ukuze ube ngumfakazi wobubi.
2 “Usatsate gulu la anthu ndi kuchita choyipa. Pamene ukupereka umboni mʼbwalo lamilandu, usakhotetse mlandu chifukwa chofuna kukondweretsa anthu ambiri.
Ungalandeli abanengi ngezinto ezimbi, ungafakazi ecaleni ukuze weyamele kwabanengi uliphambule.
3 Ndipo poweruza mlandu wa munthu wosauka usamukondere.
Lomyanga ungamzweli ecaleni lakhe.
4 “Ngati ukumana ndi ngʼombe kapena bulu wa mdani wako zitasochera, uwonetsetse kuti wazitenga kupita nazo kwa mwini wakeyo.
Uba uhlangana lenkabi yesitha sakho loba ubabhemi waso kuduha, uzakubuyisela lokukubuyisela kuso.
5 Ngati uwona bulu wa munthu wina amene amakuda atagwa ndi katundu, usamusiye pomwepo, uwonetsetse kuti wamuthandiza.
Uba ubona ubabhemi walowo okuzondayo elele ngaphansi komthwalo wakhe, uyekele ukumkhulula, uzamkhulula lokumkhulula laye.
6 “Usakhotetse milandu ya anthu osauka.
Kawuyikuphambula ukwahlulelwa komyanga wakho ecaleni lakhe.
7 Upewe zabodza ndipo usaphetse munthu wosalakwa ndi wolungama, chifukwa Ine sindidzakhululukira wochimwa.
Bana khatshana lendaba yamanga, ungabulali ongelacala lolungileyo, ngoba kangiyikumlungisisa okhohlakeleyo.
8 “Musamalandire chiphuphu, pakuti chiphuphu chimadetsa mʼmaso anthu oweruza ndi kusintha mawu awo kuti mlandu uyipire osalakwa.
Njalo kawuyikwemukela isivalamlomo, ngoba isivalamlomo siphumputhekisa ababonayo, sonakalise amazwi abalungileyo.
9 “Usamuzunze mlendo, pakuti inu nomwe mukudziwa mmene amamvera mlendo chifukwa nanunso munali alendo mʼdziko la Igupto.
Futhi kawuyikumcindezela owezizwe; ngoba lina liyayazi imizwa yowezizwe, ngoba lalingabezizwe elizweni leGibhithe.
10 “Muzidzala mbewu zanu mʼmunda ndi kumakolola mbewuzo kwa zaka zisanu ndi chimodzi.
Njalo iminyaka eyisithupha uzahlanyela isiqinti sakho, ubuthe isivuno saso.
11 Koma chaka chachisanu ndi chiwiri muzisiya osalima mindayo kuti anthu osauka pakati panu azipezamo chakudya, ndipo nyama zakuthengo zizidya zotsalazo. Muzichita chimodzimodzi ndi minda ya mpesa ndi mitengo ya olivi.
Kodwa ngowesikhombisa uzasilalukisa sibe lifusi, ukuze abayanga besizwe sakho badle, lalokho okuseleyo inyamazana zeganga zikudle. Wenze njalo ngesivini sakho lemihlwathi yakho.
12 “Muzigwira ntchito masiku asanu ndi limodzi koma tsiku lachisanu ndi chiwiri musagwire ntchito kuti ngʼombe yanu ndi bulu wanu apume ndiponso kuti kapolo wobadwira mʼnyumba yanu ndi mlendo yemwe apezenso mphamvu.
Insuku eziyisithupha uzakwenza umsebenzi wakho, njalo ngosuku lwesikhombisa uphumule, ukuze kuphumule inkabi yakho labobabhemi bakho, kuvuselele-ke indodana yencekukazi yakho lowezizweni.
13 “Samalani pochita zonse zimene ine ndanena. Musamapemphere kwa milungu ina ndipo mayina awo musamawatchule.
Lezintweni zonke esengizitshilo kini qaphelani, lebizo labanye onkulunkulu lingaliphathi, kaliyikuzwakala emlonyeni wakho.
14 “Muzichita zikondwerero zolemekeza Ine katatu pa chaka.
Kathathu ngomnyaka uzangigcinela umkhosi.
15 “Muzichita Chikondwerero cha Buledi wopanda Yisiti. Kwa masiku asanu ndi awiri muzidya buledi wopanda yisiti monga ndinakulamulirani. Muzichita zimenezi mwezi wa Abibu pa nthawi yomwe ndayika, pakuti mʼmwezi umenewu munatuluka mʼdziko la Igupto. “Pasapezeke munthu wobwera pamaso panga wopanda kanthu mʼmanja.
Umkhosi wesinkwa esingelamvubelo uzawugcina, insuku eziyisikhombisa udle isinkwa esingelamvubelo njengokukulaya kwami, ngesikhathi esimisiweyo senyanga kaAbhibhi; ngoba kuyo waphuma eGibhithe; kabayikubonakala phambi kwami bengaphethe lutho.
16 “Muzichita Chikondwerero cha Masika pogwiritsa ntchito zipatso zoyambirira kucha zimene munadzala mʼmunda. “Muzichitanso Chikondwerero cha Zokolola pakutha pa chaka, pamene mukututa zokolola zanu mʼmunda.
Lomkhosi wesivuno, izithelo zokuqala zomsebenzi wakho, owuhlanyeleyo ensimini; lomkhosi wokubutha ekupheleni komnyaka, lapho usubuthile umsebenzi wakho ensimini.
17 “Amuna onse azionekera pamaso pa Ambuye Yehova katatu pa chaka.
Kathathu ngomnyaka bonke abesilisa bakho bazabonakala phambi kweNkosi uJehova.
18 “Musapereke magazi anyama ngati nsembe kwa Ine pamodzi ndi chilichonse chimene chili ndi yisiti. “Ndipo musasunge mafuta anyama yansembe ya pa chikondwerero mpaka mmawa.
Kawuyikunikela igazi lomhlatshelo wami kanye lesinkwa esilemvubelo. Lamafutha omkhosi wami angalali kuze kuse.
19 “Muzibwera ndi zipatso zoyambirira kucha zabwino kwambiri ku Nyumba ya Yehova Mulungu wanu. “Musamaphike kamwana kambuzi mu mkaka wa mayi wake.
Ikhethelo lezithelo zokuqala zensimu yakho uzaliletha endlini yeNkosi uNkulunkulu wakho. Ungapheki izinyane echagweni lukanina.
20 “Taona Ine ndikutuma mngelo wanga patsogolo panu kuti akutetezeni mʼnjiramo ndi kukakufikitsani ku malo amene ndakonza.
Khangela, ngithuma ingilosi phambi kwakho ukuze ikulondoloze endleleni, ikuse endaweni engiyilungisileyo.
21 Muzimumvera ndi kumvetsetsa zimene akunena. Musamuwukire chifukwa sadzakhululuka kuwukira kwanu, pakuti akuchita zimenezi mʼdzina langa.
Uqaphele phambi kwayo, ulalele ilizwi layo; ungayicunuli, ngoba kayiyikuthethelela iziphambeko zenu; ngoba ibizo lami liphakathi kwayo.
22 Ngati mudzamvera iyeyu ndi kuchita zonse zimene Ine ndikunena, Ine ndidzakhala mdani wa adani anu ndipo ndidzatsutsana ndi onse otsutsana nanu.
Kodwa uba ulalela lokulalela ilizwi layo, wenze konke engikutshoyo, sengizakuba yisitha sezitha zakho, ngiphambane labaphambana lawe.
23 Mngelo wanga adzakhala patsogolo panu ndipo adzakufikitsani mʼdziko la Aamori, Ahiti, Aperezi, Akanaani, Ahivi ndi Ayebusi, ndipo ndidzawapheratu onsewo.
Ngoba ingilosi yami izahamba phambi kwakho, ikungenise kumaAmori lamaHethi lamaPerizi lamaKhanani lamaHivi lamaJebusi. Njalo ngizababhubhisa.
24 Musagwadire milungu yawo kapena kuyipembedza. Ndipo musatsatire zinthu zomwe amachita. Koma inu mukawononge milungu yawo ndi kuphwasula malo amene amapembedzerapo.
Ungakhothameli onkulunkulu babo, ungabakhonzi, ungenzi njengemisebenzi yabo; kodwa ubachithe lokubachitha, ubhidlize lokubhidliza izinsika zabo eziyizithombe.
25 Muzipembedza Yehova Mulungu wanu ndipo adzakudalitsani ndi chakudya ndi madzi ndiponso ndidzachotsa nthenda pakati panu.
Lizakhonza-ke iNkosi uNkulunkulu wenu; njalo izabusisa ukudla kwakho lamanzi akho, njalo ngisuse isifo phakathi kwakho.
26 Palibe mkazi amene adzapite padera kapena kukhala wosabereka mʼdziko mwanu. Ndidzakupatsani moyo wautali.
Kakuyikuba khona okuphunzayo lokuyinyumba elizweni lakho. Ngizaphelelisa inani lensuku zakho.
27 “Ine ndidzawachititsa mantha ndi kusokoneza anthu onse amene adzalimbana ndi inu ndipo adani anu onse adzakuthawani.
Ngizathumela ukwesabeka kwami phambi kwakho, ngiphambanise bonke abantu ozafika kubo, ngenze izitha zakho zonke zikunike isiphundu.
28 Ahivi, Akanaani ndi Ahiti adzathawa ngati kuti ndawatumizira mavu.
Ngizathumela olonyovu phambi kwakho abazaxotsha amaHivi, amaKhanani lamaHethi phambi kwakho.
29 Komabe sindidzawachotseratu onse mʼchaka chimodzi chifukwa dziko lingadzakhale lopanda anthu ndipo nyama zakuthengo zidzakuchulukirani.
Kangiyikubaxotsha phambi kwakho ngomnyaka owodwa, hlezi ilizwe libe ngamanxiwa, lenyamazana zeganga zikwandele.
30 Ndidzawathamangitsa pangʼonopangʼono mpaka inu mutachuluka kokwanira mwakuti nʼkutenga dzikolo.
Ngizabaxotsha phambi kwakho kancinyane kancinyane, uze wande, udle ilifa lelizwe.
31 “Malire a dziko lanu adzakhala kuyambira ku Nyanja Yofiira mpaka ku nyanja ya Afilisti, ndiponso kuyambira ku chipululu mpaka ku mtsinje wa Yufurate. Anthu onse okhala mʼdziko limeneli ndidzawapereka mʼmanja mwanu ndipo mudzawathamangitsa.
Njalo ngizamisa imingcele yakho kusukela eLwandle oluBomvu kuze kufike elwandle lwamaFilisti, njalo kusukela enkangala kuze kufike emfuleni; ngoba ngizanikela esandleni sakho abakhileyo belizwe; uzabaxotsha phambi kwakho.
32 Musachite pangano ndi iwo kapena ndi milungu yawo.
Ungenzi isivumelwano labo labonkulunkulu babo.
33 Asadzakhale mʼdziko lanu chifukwa angadzakuchimwitseni ndi kuyamba kupembedza milungu yawo. Mukadzatero ndiye kuti mwakodwa mu msampha.”
Kabayikuhlala elizweni lakho, hlezi bakwenze ukuthi wone kimi; uba ukhonza onkulunkulu babo, ngeqiniso kuzakuba yisifu kuwe.

< Eksodo 23 >