< Eksodo 23 >

1 “Usafalitse mbiri yabodza. Usathandize munthu wolakwa pomuchitira umboni wonama.
You must not give a false report about anyone. Do not join with a wicked man to be a dishonest witness.
2 “Usatsate gulu la anthu ndi kuchita choyipa. Pamene ukupereka umboni mʼbwalo lamilandu, usakhotetse mlandu chifukwa chofuna kukondweretsa anthu ambiri.
You must not follow a crowd to do evil, nor may you bear witness while siding with the crowd in order to pervert justice.
3 Ndipo poweruza mlandu wa munthu wosauka usamukondere.
You must not show favoritism to a poor man in his lawsuit.
4 “Ngati ukumana ndi ngʼombe kapena bulu wa mdani wako zitasochera, uwonetsetse kuti wazitenga kupita nazo kwa mwini wakeyo.
If you meet your enemy's ox or his donkey going astray, you must bring it back to him.
5 Ngati uwona bulu wa munthu wina amene amakuda atagwa ndi katundu, usamusiye pomwepo, uwonetsetse kuti wamuthandiza.
If you see the donkey of someone who hates you fallen to the ground under its load, you must not leave that person. You must surely help him with his donkey.
6 “Usakhotetse milandu ya anthu osauka.
Do not thrust aside justice for your poor in his lawsuit.
7 Upewe zabodza ndipo usaphetse munthu wosalakwa ndi wolungama, chifukwa Ine sindidzakhululukira wochimwa.
Do not join others in making false accusations, and do not kill the innocent or righteous, for I will not acquit the wicked.
8 “Musamalandire chiphuphu, pakuti chiphuphu chimadetsa mʼmaso anthu oweruza ndi kusintha mawu awo kuti mlandu uyipire osalakwa.
Never take a bribe, for a bribe blinds those who see, and perverts honest people's words.
9 “Usamuzunze mlendo, pakuti inu nomwe mukudziwa mmene amamvera mlendo chifukwa nanunso munali alendo mʼdziko la Igupto.
You must not oppress a foreigner, since you know the life of a foreigner, for you were foreigners in the land of Egypt.
10 “Muzidzala mbewu zanu mʼmunda ndi kumakolola mbewuzo kwa zaka zisanu ndi chimodzi.
For six years you will sow seed on your land and gather in its produce.
11 Koma chaka chachisanu ndi chiwiri muzisiya osalima mindayo kuti anthu osauka pakati panu azipezamo chakudya, ndipo nyama zakuthengo zizidya zotsalazo. Muzichita chimodzimodzi ndi minda ya mpesa ndi mitengo ya olivi.
But in the seventh year you will leave it unplowed and fallow, so that the poor among your people may eat. What they leave, the wild animals will eat. You will do the same with your vineyards and olive orchards.
12 “Muzigwira ntchito masiku asanu ndi limodzi koma tsiku lachisanu ndi chiwiri musagwire ntchito kuti ngʼombe yanu ndi bulu wanu apume ndiponso kuti kapolo wobadwira mʼnyumba yanu ndi mlendo yemwe apezenso mphamvu.
During six days you will do your work, but on the seventh day you must rest. Do this so that your ox and your donkey may have rest, and so that your female slave's son and any foreigner may rest and be refreshed.
13 “Samalani pochita zonse zimene ine ndanena. Musamapemphere kwa milungu ina ndipo mayina awo musamawatchule.
Pay attention to everything that I have said to you. Do not mention the names of other gods, nor let their names be heard from your mouth.
14 “Muzichita zikondwerero zolemekeza Ine katatu pa chaka.
You must travel to hold a festival for me three times every year.
15 “Muzichita Chikondwerero cha Buledi wopanda Yisiti. Kwa masiku asanu ndi awiri muzidya buledi wopanda yisiti monga ndinakulamulirani. Muzichita zimenezi mwezi wa Abibu pa nthawi yomwe ndayika, pakuti mʼmwezi umenewu munatuluka mʼdziko la Igupto. “Pasapezeke munthu wobwera pamaso panga wopanda kanthu mʼmanja.
You are to observe the Festival of Unleavened Bread. As I commanded you, you will eat unleavened bread for seven days. At that time, you will appear before me in the month of Aviv, which is fixed for this purpose. It was in this month that you came out from Egypt. But you must not appear before me empty-handed.
16 “Muzichita Chikondwerero cha Masika pogwiritsa ntchito zipatso zoyambirira kucha zimene munadzala mʼmunda. “Muzichitanso Chikondwerero cha Zokolola pakutha pa chaka, pamene mukututa zokolola zanu mʼmunda.
You must observe the Festival of Harvest, the firstfruits of your labors when you sowed seed in the fields. Also you must observe the Festival of Ingathering at the end of the year, when you gather in your produce from the fields.
17 “Amuna onse azionekera pamaso pa Ambuye Yehova katatu pa chaka.
All your males must appear before the Lord Yahweh three times every year.
18 “Musapereke magazi anyama ngati nsembe kwa Ine pamodzi ndi chilichonse chimene chili ndi yisiti. “Ndipo musasunge mafuta anyama yansembe ya pa chikondwerero mpaka mmawa.
You must not offer the blood from sacrifices made to me with bread containing yeast. The fat from the sacrifices at my festivals must not remain all night until the morning.
19 “Muzibwera ndi zipatso zoyambirira kucha zabwino kwambiri ku Nyumba ya Yehova Mulungu wanu. “Musamaphike kamwana kambuzi mu mkaka wa mayi wake.
You must bring the choicest firstfruits from your land into my house, the house of Yahweh your God. You must not boil a young goat in its mother's milk.
20 “Taona Ine ndikutuma mngelo wanga patsogolo panu kuti akutetezeni mʼnjiramo ndi kukakufikitsani ku malo amene ndakonza.
I am going to send an angel before you to guard you on the way, and to bring you to the place that I have prepared.
21 Muzimumvera ndi kumvetsetsa zimene akunena. Musamuwukire chifukwa sadzakhululuka kuwukira kwanu, pakuti akuchita zimenezi mʼdzina langa.
Be attentive to him and obey him. Do not provoke him, for he will not pardon your transgressions. My name is on him.
22 Ngati mudzamvera iyeyu ndi kuchita zonse zimene Ine ndikunena, Ine ndidzakhala mdani wa adani anu ndipo ndidzatsutsana ndi onse otsutsana nanu.
If you indeed obey his voice and do everything that I tell you, then I will be an enemy to your enemies and an adversary to your adversaries.
23 Mngelo wanga adzakhala patsogolo panu ndipo adzakufikitsani mʼdziko la Aamori, Ahiti, Aperezi, Akanaani, Ahivi ndi Ayebusi, ndipo ndidzawapheratu onsewo.
My angel will go before you and bring you to the Amorites, Hittites, Perizzites, Canaanites, Hivites, and the Jebusites. I will destroy them.
24 Musagwadire milungu yawo kapena kuyipembedza. Ndipo musatsatire zinthu zomwe amachita. Koma inu mukawononge milungu yawo ndi kuphwasula malo amene amapembedzerapo.
You must not bow down to their gods, worship them, or do as they do. Instead, you must completely overthrow them and smash their stone pillars in pieces.
25 Muzipembedza Yehova Mulungu wanu ndipo adzakudalitsani ndi chakudya ndi madzi ndiponso ndidzachotsa nthenda pakati panu.
You must worship Yahweh your God, and he will bless your bread and water. I will remove sickness from among you.
26 Palibe mkazi amene adzapite padera kapena kukhala wosabereka mʼdziko mwanu. Ndidzakupatsani moyo wautali.
No woman will be barren or will miscarry her young in your land. I will give you long lives.
27 “Ine ndidzawachititsa mantha ndi kusokoneza anthu onse amene adzalimbana ndi inu ndipo adani anu onse adzakuthawani.
I will send fear of myself on those into whose land you advance. I will kill all the people whom you meet. I will make all your enemies turn their backs to you in fright.
28 Ahivi, Akanaani ndi Ahiti adzathawa ngati kuti ndawatumizira mavu.
I will send hornets before you that will drive out the Hivites, Canaanites, and the Hittites from before you.
29 Komabe sindidzawachotseratu onse mʼchaka chimodzi chifukwa dziko lingadzakhale lopanda anthu ndipo nyama zakuthengo zidzakuchulukirani.
I will not drive them out from before you in one year, or the land would become abandoned, and the wild animals would become too many for you.
30 Ndidzawathamangitsa pangʼonopangʼono mpaka inu mutachuluka kokwanira mwakuti nʼkutenga dzikolo.
Instead, I will drive them out little by little from before you until you become fruitful and inherit the land.
31 “Malire a dziko lanu adzakhala kuyambira ku Nyanja Yofiira mpaka ku nyanja ya Afilisti, ndiponso kuyambira ku chipululu mpaka ku mtsinje wa Yufurate. Anthu onse okhala mʼdziko limeneli ndidzawapereka mʼmanja mwanu ndipo mudzawathamangitsa.
I will fix your borders from the Sea of Reeds to the Sea of the Philistines, and from the wilderness to the Euphrates River. I will give you victory over the land's inhabitants. You will drive them out before yourselves.
32 Musachite pangano ndi iwo kapena ndi milungu yawo.
You must not make a covenant with them or with their gods.
33 Asadzakhale mʼdziko lanu chifukwa angadzakuchimwitseni ndi kuyamba kupembedza milungu yawo. Mukadzatero ndiye kuti mwakodwa mu msampha.”
They must not live in your land, or they would make you sin against me. If you worship their gods, this will surely become a trap for you.'”

< Eksodo 23 >