< Mlaliki 7 >

1 Mbiri yabwino ndi yopambana mafuta onunkhira bwino, ndipo tsiku lomwalira ndi lopambana tsiku lobadwa.
Lepsze jest imię dobre, niżeli maść wyborna; a dzień śmierci, niż dzień narodzenia.
2 Kuli bwino kupita ku nyumba yamaliro kusiyana ndi kupita ku nyumba yamadyerero: Pakuti imfa ndiye mathero a munthu aliyense; anthu amoyo azichisunga chimenechi mʼmitima mwawo.
Lepiej iść do domu żałoby, niż iść do domu biesiady, przeto, iż tam widzimy koniec każdego człowieka, a żyjący składa to do serca swego.
3 Chisoni nʼchabwino kusiyana ndi kuseka, pakuti nkhope yakugwa ndi yabwino chifukwa imakonza mtima.
Lepszy jest smutek, niżeli śmiech; bo przez smutek twarzy naprawia się serce.
4 Mtima wa munthu wanzeru nthawi zonse umalingalira za imfa, koma mitima ya zitsiru imalingalira za chisangalalo.
Serce mądrych w domu żałoby; ale serce głupich w domu wesela.
5 Kuli bwino kumva kudzudzula kwa munthu wanzeru kusiyana ndi kumvera mayamiko a zitsiru.
Lepiej jest słuchać gromienia mądrego, niżeli słuchać pieśni głupich.
6 Kuseka kwa zitsiru kuli ngati kuthetheka kwa moto kunsi kwa mʼphika, izinso ndi zopandapake.
Bo jaki jest trzask ciernia pod garncem, tak jest śmiech głupiego; i toć jest marność.
7 Kuzunza ena kumasandutsa munthu wanzeru kukhala chitsiru, ndipo chiphuphu chimawononga mtima.
Zaiste ucisk przywodzi mądrego do szaleństwa, a dar zaślepia serce.
8 Mathero ake a chinthu ndi abwino kupambana chiyambi chake, ndipo kufatsa nʼkwabwino kupambana kudzikuza.
Lepsze jest dokończenie rzeczy, niżeli początek jej; lepszy jest człowiek cierpliwego ducha, niż ducha wyniosłego.
9 Usamafulumire kukwiya mu mtima mwako, pakuti mkwiyo ndi bwenzi la zitsiru.
Nie bądź porywczy w duchu twym do gniewu; bo gniew w zanadrzyu głupich odpoczywa.
10 Usamafunse kuti, “Nʼchifukwa chiyani masiku amakedzana anali abwino kupambana masiku ano?” pakuti si chinthu chanzeru kufunsa mafunso oterewa.
Nie mów: Cóż to jest, że dni pierwsze lepsze były, niż teraźniejsze? Bobyś się o tem nie mądrze pytał.
11 Nzeru ngati cholowa, ndi chinthu chabwino ndipo imapindulitsa wamoyo aliyense pansi pano.
Dobra jest mądrość przy majętności, i jest pożteczna tym, którzy widzą słońce.
12 Nzeru ndi chitetezo, monganso ndalama zili chitetezo, koma phindu la chidziwitso ndi ili: kuti nzeru zimasunga moyo wa munthu amene ali nazo nzeruzo.
Albowiem pod cieniem mądrości, i pod cieniem srebra odpoczywa człowiek, a wszakże przedniejsza jest umiejętność mądrości; bo przynosi żywot tym, którzy ją mają.
13 Taganizirani zimene Mulungu wazichita: ndani angathe kuwongola chinthu chimene Iye anachipanga chokhota?
Przypatrz się sprawie Bożej; bo któż może wyprostować, co on skrzywi?
14 Pamene zinthu zili bwino, sangalala; koma pamene zinthu sizili bwino, ganizira bwino: Mulungu ndiye anapanga nthawi yabwinoyo, ndiponso nthawi imene si yabwinoyo. Choncho munthu sangathe kuzindikira chilichonse cha mʼtsogolo mwake.
W dzień dobry zażywaj dobra, w dzień zły miej się na pieczy: boć ten uczynił Bóg przeciwko owemu, dlatego, aby nie doszedł człowiek tego, co nastanie po nim.
15 Pa moyo wanga wopanda phinduwu ndaona zinthu ziwiri izi: munthu wolungama akuwonongeka mʼchilungamo chake, ndipo munthu woyipa akukhala moyo wautali mʼzoyipa zake.
Tom wszystko widział za dni marności mojej: Bywa sprawiedliwy, który ginie z sprawiedliwością swoją; także bywa niezbożnik, który długo żyje we złości swojej.
16 Usakhale wolungama kwambiri kapena wanzeru kwambiri, udziwonongerenji wekha?
Nie bądź nazbyt sprawiedliwym, ani nazbyt mądrym; przeczżebyś miał do zguby przychodzić?
17 Usakhale woyipa kwambiri, ndipo usakhale chitsiru, uferenji nthawi yako isanakwane?
Nie bądź nader niepobożnym, ani nazbyt głupim; przeczżebyś miał umrzeć przed czasem swoim?
18 Nʼkwabwino kuti utsate njira imodzi, ndipo usataye njira inayo. Munthu amene amaopa Mulungu adzapewa zinthu ziwiri zonsezi.
Dobra jest, abyś się owego trzymał, a tego się nie puszczał; kto się boi Boga, uchodzi tego wszystkiego.
19 Nzeru zimapereka mphamvu zambiri kwa munthu wanzeru kupambana olamulira khumi a mu mzinda.
Mądrość umacnia mądrego więcej, niżeli dziesięć książąt, którzy są w mieście.
20 Palibe munthu wolungama pa dziko lapansi amene amachita zabwino zokhazokha ndipo sachimwa.
Zaiste niemasz człowieka sprawiedliwego na ziemi, któryby czynił dobrze, a nie grzeszył.
21 Usamamvetsere mawu onse amene anthu amayankhula, mwina udzamva wantchito wako akukutukwana,
Nie do wszystkich też słów, które mówią ludzie przykładaj serca twego; i niech cię to nie obchodzi, choćciby i sługa twój złorzeczył.
22 pakuti iwe ukudziwa mu mtima mwako kuti nthawi zambiri iwenso unatukwanapo ena.
Boć wie serce twoje, żeś i ty częstokroć drugim złorzeczył.
23 Zonsezi ndinaziyesa ndi nzeru zanga ndipo ndinati, “Ine ndatsimikiza mu mtima mwanga kuti ndikhale wanzeru,” koma nzeruyo inanditalikira.
Wszystkiegom tego doświadczył mądrością, i rzekłem: Będę mądrym; aleć się mądrość oddaliła odemnie.
24 Nzeru zimene zilipo, zili kutali ndipo ndi zozama kwambiri, ndani angathe kuzidziwa?
A co dalekiego, i co bardzo głębokiego jest, któż to znajdzie?
25 Kotero ndinayikapo mtima wanga kuti ndidziwe, ndifufuze ndi kumafunafuna nzeru ndi mmene zinthu zimakhalira ndipo ndinafunanso kudziwa kuyipa kwa uchitsiru ndiponso kupusa kwake kwa misala.
Wszystkom ja przeszedł myślą swoją, abym poznał i wybadał się, i wynalazł mądrość i rozum, a żebym poznał niezbożność, głupstwo, i błąd, i szaleństwo.
26 Ndinapeza kanthu kowawa kupambana imfa, mkazi amene ali ngati khoka, amene mtima wake uli ngati khwekhwe, ndipo manja ake ali ngati maunyolo. Munthu amene amakondweretsa Mulungu adzathawa mkaziyo, koma mkaziyo adzakola munthu wochimwa.
I znalazłem rzecz gorzciejszą nad śmierć, to jest, taką niewiastę, której serce jest jako sieci i sidło, a ręce jej jako pęta. Kto się Bogu podoba, wolny będzie od niej; ale grzesznik będzie od niej pojmany.
27 Mlaliki akunena kuti, “Taonani, chimene ndinachipeza ndi ichi: “Kuwonjezera chinthu china pa china kuti ndidziwe mmene zinthu zimachitikira,
Otom to znalazł, (mówi kaznodzieja, ) stosując jedno z drugiem, abym doszedł umiejętności.
28 pamene ine ndinali kufufuzabe koma osapeza kanthu, ndinapeza munthu mmodzi wolungama pakati pa anthu 1,000, koma pakati pawo panalibepo mkazi mmodzi wolungama.
Czego zaś nad to szukała dusza moja, tedym nie znalazł. Męża jednego z tysiąca znalazłem; alem niewiasty między temi wszystkiemi nie znalazł.
29 Chokhacho chimene ndinachipeza ndi ichi: Mulungu analenga munthu, anamupatsa mtima wolungama, koma anthu anatsatira njira zawozawo zambirimbiri.”
To tylko obacz, com znalazł, że stworzył Bóg człowieka dobrego; ale oni udali się za rozmaitemi myślami. Któż może z mądrym porównać? a kto może wyłożyć każdą rzecz?

< Mlaliki 7 >