< Mlaliki 12 >

1 Uzikumbukira mlengi wako masiku a unyamata wako, masiku oyipa asanafike, nthawi isanafike pamene udzanena kuti, “Izi sizikundikondweretsa.”
Tænk På ding Skaber i Ungdommens Dage, førend de onde Dage kommer og Årene nærmer sig, om hvilke du vil sige: "I dem har jeg ikke Behag!"
2 Nthawi ya ukalamba wako, dzuwa ndi kuwala, mwezi ndi nyenyezi zidzada. Mitambo idzabweranso mvula itagwa.
før Sol og Lys og Måne og Stjerner hylles i Mørke og der atter kommer Skyer efter Regn,
3 Nthawi imene manja ako adzanjenjemera, miyendo yako idzafowoka, pamene mano ako adzalephera kutafuna chifukwa ndi owerengeka, ndipo maso ako adzayamba kuchita chidima.
Tiden, da Husets Vogtere bæver, de stærke Mænd bliver krumme, da Møllepigerne svigter, fordi de er få, og de bliver mørke, som kigger ved Gluggerne,
4 Makutu ako adzatsekeka, ndipo sudzamva phokoso lakunja; sudzamvanso kusinja kwa pa mtondo kapena kulira kwa mbalame mmawa.
da begge Gadedørene lukkes, mens Møllen går med dæmpet Lyd, da man står op ved Spurvenes Kvidder og alle Sangens Døtre hvisker,
5 Imeneyi ndiyo nthawi imene anthu amaopa kupita kumalo okwera, amaopa kuyenda mʼmisewu; Mutu umatuwa kuti mbuu, amayenda modzikoka ngati ziwala ndipo chilakolako chimatheratu. Nthawi imeneyo munthu amapita ku nyumba yake yamuyaya ndipo anthu olira maliro amayendayenda mʼmisewu.
da man også ængstes for Bakker, og Rædsler lurer på Vejen, da Mandeltræet blomstrer; Græshoppen slappes og Kapersbærret svigter, nu Mennesket går til sin evige Bolig og Sørgetoget går gennem Gaden,
6 Kumbukira Iye chingwe cha siliva chisanaduke, kapena mbale yagolide isanasweke; mtsuko usanasweke ku kasupe, kapena mkombero usanathyoke ku chitsime.
førend Sølvsnoren brister og Guldskålen brydes itu, før Krukken slås i Stykker ved Kilden og det søndrede Hjul falder ned i Brønden
7 Iyi ndi nthawi imene thupi lidzabwerera ku dothi, kumene linachokera, mzimu udzabwerera kwa Mulungu amene anawupereka.
og Støvet vender tilbage til Jorden som før og Ånden til Gud, som gav den.
8 “Zopanda phindu! Zopandapake!” akutero Mlaliki. “Zonse ndi zopandapake!”
Endeløs Tomhed, sagde Prædikeren, alt er Tomhed.
9 Mlaliki sanali wozindikira zinthu kokha ayi, komanso ankaphunzitsa anthu. Iye ankasinkhasinkha ndi kufufuzafufuza ndi kulemba mwadongosolo miyambi yambiri.
Endnu skal siges, at Prædikeren var viis; han gav også Folket Kundskab; han granskede og ransagede og formede mange Ordsprog.
10 Mlaliki anafufuzafufuza kuti apeze mawu oyenera, ndipo zimene analemba zinali zolondola ndiponso zoona.
Prædikeren søgte at finde Fyndord og optegnede sanddru Lære, Sandhedsord.
11 Mawu a anthu anzeru ali ngati zisonga, zokamba zawo zimene anasonkhanitsa zili ngati misomali yokhomera, yoperekedwa ndi mʼbusa mmodzi.
Som Pigkæppe er de vises Ord, som inddrevne Søm, der sidder tæt; de er givet af en og samme Hyrde.
12 Samalira mwana wanga, za kuwonjezera chilichonse pa zimenezi. Kulemba mabuku ambiri sikutha, ndipo kuphunzira kwambiri kumatopetsa thupi.
Endnu skal siges: Min Søn, var dig! Der er ingen Ende på, som der skrives Bøger, og megen Gransken trætter Legemet.
13 Basi zonse zamveka; mathero a nkhaniyi ndi awa: uziopa Mulungu ndi kusunga malamulo ake, pakuti umenewu ndiwo udindo wa anthu onse.
Enden på Sagen, når alt er hørt, er: Frygt Gud og hold hans Bud! Thi det bør hvert Menneske gøre.
14 Pakuti Mulungu adzaweruza zochita zonse, kuphatikizanso zinthu zonse zobisika, kaya zabwino kapena zoyipa.
Thi hver en Gerning bringer Gud for Retten, når han dømmer alt, hvad der er skjult, være sig godt eller ondt.

< Mlaliki 12 >