< Deuteronomo 32 >

1 Mverani, inu mayiko a mmwamba ndipo ine ndidzayankhula; imva, iwe dziko lapansi, mawu a pakamwa panga.
Slušaj, nebo, govoriæu; i zemlja neka èuje govor usta mojih.
2 Chiphunzitso changa chigwe ngati mvula ndipo mawu anga atsike ngati mame, ngati mvumbi pa udzu watsopano, ngati mvula yochuluka pa zomera zanthete.
Neka se spusti kao dažd nauka moja, i neka padne kao rosa govor moj, kao sitan dažd na mladu travu i kao krupan dažd na odraslu travu.
3 Ndidzalalikira dzina la Yehova. Aa, tamandani ukulu wa Mulungu wathu!
Jer æu javljati ime Gospodnje; velièajte Boga našega.
4 Iye ndi Thanthwe, ntchito zake ndi zangwiro, njira zake zonse ndi zolungama. Mulungu wokhulupirika amene salakwitsa, Iye ndiye wolungama ndi wosalakwa.
Djelo je te stijene savršeno, jer su svi putovi njegovi pravda; Bog je vjeran, bez nepravde; pravedan je i istinit.
5 Koma iwo achita mosakhulupirika pamaso pake, iwo si ana akenso, koma iwo ndi mʼbado wachinyengo ndi wokhotakhota.
Oni se pokvariše prema njemu; njihovo nevaljalstvo nije nevaljalstvo sinova njegovijeh; to je rod zao i pokvaren.
6 Kodi mukumubwezera Yehova chotere, inu anthu opusa ndi opanda nzeru? Kodi Iye si Atate anu, Mlengi wanu, amene anakupangani ndi kukuwumbani?
Tako li vraæate Gospodu, narode ludi i bezumni? nije li on otac tvoj, koji te je zadobio? on te je naèinio i stvorio.
7 Kumbukirani masiku amakedzana; ganizirani za mibado yakalekale. Funsa abambo ako ndipo adzakuwuza, akuluakulu ako, ndipo adzakufotokozera.
Opomeni se negdašnjih dana, pogledajte godine svakoga vijeka; pitaj oca svojega i on æe ti javiti, starije svoje i kazaæe ti.
8 Pamene Wammwambamwamba anapereka mayiko kwa anthu a mitundu ina kukhala cholowa chawo, pamene analekanitsa anthu onse, anayikira malire anthu onse molingana ndi chiwerengero cha ana a Israeli.
Kad višnji razdade našljedstvo narodima, kad razdijeli sinove Adamove, postavi meðe narodima po broju sinova Izrailjevih.
9 Pakuti gawo la Yehova ndi anthu ake, Yakobo ndiye cholowa chake.
Jer je dio Gospodnji narod njegov, Jakov je uže našljedstva njegova.
10 Anamupeza mʼchipululu, ku malo owuma ndi kopanda kanthu. Anamuteteza ndi kumusamalira; anamutchinjiriza ngati mwanadiso wake,
Naðe ga u zemlji pustoj, na mjestu strašnu gdje buèi pustoš; vodi ga unaokolo, uèi ga i èuva kao zjenicu oka svojega.
11 ngati chiwombankhanga chimene chimasasula chisa chake nʼkumazungulira pamwamba pa ana ake, chimene chimatambalalitsa mapiko ake kuti chigwire anawo ndi kuwanyamula pa mapiko ake otambalalawo.
Kao što orao izmamljuje orliæe svoje, diže se nad ptiæima svojim, širi krila svoja, uzima ih i nosi na krilima svojim,
12 Yehova yekha ndiye anamutsogolera; popanda thandizo la mulungu wachilendo.
Tako ga Gospod voðaše, i s njim ne bješe tuðega boga;
13 Anamuyendetsa pamwamba pa mapiri a mʼdziko ndi kumudyetsa zipatso za mʼminda. Anamudyetsa uchi wofula pa thanthwe, ndiponso mafuta ochokera mʼnthaka ya miyala,
Voðaše ga na visine zemaljske da jede rod poljski, i davaše mu da sisa med iz stijene i ulje iz tvrdoga kamena,
14 pamodzi ndi chambiko ndi mkaka wochokera ku ngʼombe ndi nkhosa, ndiponso ana ankhosa onenepa ndi mbuzi, pamodzinso ndi nkhosa zazimuna zabwino za ku Basani ndiponso tirigu wabwino kwambiri. Munamwa vinyo wa thovu lofiira.
Maslo od krava i mlijeko od ovaca s pretilinom od jaganjaca i ovnova Vasanskih i jaraca, sa srcem zrna pšeniènih; i pio si vino, krv od grožða.
15 Yesuruni ananenepa ndi kuyamba kuwukira; atakhuta, ananenepa ndi kukula thupi. Anasiya Mulungu amene anamulenga ndipo anakana Thanthwe ndi Mpulumutsi wake.
Ali se Izrailj ugoji, pa se stade ritati; utio si, udebljao i zasalio; pa ostavi Boga koji ga je stvorio, i prezre stijenu spasenja svojega.
16 Anamuchititsa nsanje ndi milungu yawo yachilendo ndiponso anamukwiyitsa ndi mafano awo onyansa.
Na revnost razdražiše ga tuðim bogovima, gadovima razgnjeviše ga.
17 Anapereka nsembe kwa ziwanda zimene si Mulungu, milungu imene sankayidziwa nʼkale lomwe, milungu yongobwera kumene, milungu imene makolo anu sankayiopa.
Prinosiše žrtve ðavolima, ne Bogu, bogovima, kojih nijesu znali, novim, koji iz bliza doðoše, kojih se nijesu strašili oci vaši.
18 Inu munasiya Thanthwe limene linakulerani; munayiwala Mulungu amene anakubalani.
Stijenu koja te je rodila zaboravio si; zaboravio si Boga stvoritelja svojega.
19 Yehova anaona zimenezi ndipo anawakana chifukwa ana ake aamuna ndi aakazi anamukwiyitsa.
Kad to vidje Gospod, razgnjevi se na sinove svoje i na kæeri svoje,
20 Iye anati, “Ndidzawabisira nkhope yanga, ndi kuona kuti mathero awo adzakhala otani; pakuti ndi mʼbado wopotoka, ana amene ndi osakhulupirika.
I reèe: sakriæu od njih lice svoje, vidjeæu kakav æe im biti pošljedak, jer su rod pokvaren, sinovi u kojima nema vjere.
21 Anandichititsa kukhala wansanje pamene ankapembedza chimene si mulungu ndi kundikwiyitsa chifukwa cha mafano awo achabechabe. Ine ndidzawachititsa kuti achite nsanje ndi mtundu wina wopandapake; ndidzawakwiyitsa ndi mtundu wina wachabechabe.
Oni me razdražiše na revnost onijem što nije Bog, razgnjeviše svojim taštinama; i ja æu njih razdražiti na revnost onijem koji nije narod, narodom ludijem razljutiæu ih.
22 Pakuti mkwiyo wanga wayaka ngati moto, umene umayaka mpaka ku dziko la anthu akufa. Motowo udzanyeketsa dziko lapansi ndi zokolola zake ndipo udzapsereza maziko a mapiri. (Sheol h7585)
Jer se oganj razgorio u gnjevu mojem, i gorjeæe do najdubljega pakla; spaliæe zemlju i rod njezin, i popaliæe temelje brdima. (Sheol h7585)
23 “Ndidzawawunjikira masautso ndipo mivi yanga yonse idzathera pa iwo.
Zgrnuæu na njih zla, strijele svoje pobacaæu na njih.
24 Ndidzawatumizira njala yoopsa, malungo woopsa ndi nthenda zofa nazo; ndidzawatumizira zirombo zakuthengo zowavuta, ululu wa njoka ya mʼphiri imene imakwawa pa fumbi.
Glad æe ih cijediti, vruæice i ljuti pomori proždiraæe ih; i zube zvjerske poslaæu na njih i jed zmija zemaljskih.
25 Mʼmisewu lupanga lidzawasandutsa kukhala wopanda ana; mantha adzalamulira nyumba zawo. Anyamata ndi atsikana adzafa, ngakhalenso makanda ndi okalamba.
Spolja æe ih ubijati maè, a po klijetima strah, i momka i djevojku, dijete na sisi i sijeda èovjeka.
26 Ine ndinanena kuti ndidzawamwaza ndi kuwafafaniza kuti anthu asawakumbukirenso,
Rekao bih: rasijaæu ih po svijem uglovima zemaljskim, uèiniæu da nestane spomena njihova izmeðu ljudi,
27 koma sindinafune kuti adani anga adzandinyoze, mwina adani anga sadzandimvetsetsa ndipo adzanena kuti, ‘Tagonjetsa anthuwa ndife; Yehova sanachite zonsezi.’”
Da mi nije do mržnje neprijateljeve, da se ne bi neprijatelji njihovi ponijeli i rekli: ruka se naša uzvisila, a nije Gospod uèinio sve ovo.
28 Iwo ndi mtundu wopanda maganizo, iwo alibe nzeru nʼpangʼono pomwe.
Jer su narod koji propada sa svojih namjera, i nema u njih razuma.
29 Ngati iwo akanakhala anzeru akanamvetsetsa izi ndi kuzindikira kuti mathero awo adzakhala otani!
Kamo da su pametni, da razumiju ovo, i gledaju na pošljedak svoj!
30 Kodi munthu mmodzi akanathamangitsa bwanji anthu 1,000 kapena anthu awiri kuthamangitsa anthu 10,000, kuti awagonjetse, Thanthwe lawo likanapanda kuwagulitsa, Yehova akanapanda kuwataya?
Kako bi jedan gonio tisuæu a dvojica tjerala deset tisuæa, da ih nije stijena njihova prodala i Gospod ih predao?
31 Pakuti thanthwe lawo silofanana ndi Thanthwe lathu, ngakhale adani athu amavomereza zimenezi.
Jer stijena njihova nije kao naša stijena; neprijatelji naši neka budu sudije.
32 Mpesa wawo umachokera ku mpesa wa ku Sodomu ndiponso ku minda ya ku Gomora. Mphesa zawo zili ndi ululu wakupha ndipo maphava ake ndi owawa.
Jer je èokot njihov od èokota Sodomskoga i iz polja Gomorskoga; grožðe je njihovo grožðe otrovno, puca su mu gorka.
33 Vinyo wawo ndi wa ululu wa njoka, ululu woopsa wa mphiri.
Vino je njihovo otrov zmajevski, i ljuti jed aspidin.
34 “Kodi zimenezi sindinazisunge ndi kuzitsekera mʼkatikati mwa chuma changa?
Nije li to sakriveno kod mene, zapeèaæeno u riznicama mojim?
35 Kubwezera chilango nʼkwanga; ndidzawalanga ndine. Pa nthawi yake phazi lawo lidzaterera; tsiku lawo la masautso layandikira ndipo chiwonongeko chawo chikubwera pa iwo mofulumira.”
Moja je osveta i plata, u svoje vrijeme popuznuæe noga njihova, jer je blizu dan propasti njihove, i ide brzo što æe ih zadesiti.
36 Yehova adzaweruza anthu ake ndipo adzachitira atumiki ake chifundo pamene adzaona kuti mphamvu zawo zatha ndipo kuti palibe amene watsala, kapolo kapena mfulu.
Sudiæe Gospod narodu svojemu, i žao æe mu biti sluga njegovijeh, kad vidi da je prošla snaga i da nema ništa ni od uhvaæenoga ni od ostavljenoga.
37 Iye adzanena kuti, “Nanga ili kuti milungu yawo, thanthwe limene ankabisalamo,
I reæi æe: gdje su bogovi njihovi? stijena u koju se uzdaše?
38 milungu imene inkadya mafuta a nsembe zawo ndi kumwa vinyo wa chopereka chawo cha chakumwa?” Iwuzeni ibwere kuti idzakuthandizeni! Ibwere kuti idzakutetezenitu!
Koji salo od žrtava njegovijeh jedoše i piše vino od naljeva njihovijeh. Neka ustanu i pomogu vam, i neka vam budu zaklon.
39 “Onani tsopano kuti Ine ndine Iyeyo! Palibe mulungu wina koma Ine ndekha. Ine ndimapha ndiponso kupereka moyo, ndavulaza ndipo ndidzachiritsa, ndipo palibe angathe kupulumutsa munthu mʼmanja mwanga.
Vidite sada da sam ja, ja sam, i da nema Boga osim mene. Ja ubijam i oživljujem, ranim i iscjeljujem, i nema nikoga ko bi izbavio iz moje ruke.
40 Ndikweza dzanja langa kumwamba ndi kulumbira kuti, ‘Pali Ine wamoyo wamuyaya,
Jer podižem k nebu ruku svoju i kažem: ja sam živ dovijeka.
41 pamene ndidzanola lupanga langa lonyezimira ndipo dzanja liligwira pakubweretsa chiweruzo, ndidzabwezera chilango adani anga ndi kulanga onse odana nane.
Ako naoštrim sjajni maè svoj i uzmem u ruku sud, uèiniæu osvetu na neprijateljima svojim i vratiæu onima koji mrze na me.
42 Mivi yanga idzakhuta magazi awo pamene lupanga langa lidzawononga mnofu: magazi a anthu ophedwa ndi ogwidwa ukapolo, mitu ya atsogoleri a adani.’”
Opojiæu strijele svoje krvlju, i maè æe se moj najesti mesa, krvlju isjeèenijeh i zarobljenijeh, kad poènem osvetu na neprijateljima.
43 Kondwerani, inu mitundu yonse ya anthu pamodzi ndi anthu ake, pakuti Iye adzabwezera chilango anthu amene anapha atumiki ake; adzabwezera chilango adani ake ndipo adzakhululukira dziko lake ndi la anthu ake.
Veselite se narodi s narodom njegovijem, jer æe pokajati krv sluga svojih, i osvetiæe se neprijateljima svojim, i oèistiæe zemlju svoju i narod svoj.
44 Mose anabwera ndi Yoswa mwana wa Nuni ndipo anayankhula mawu onsewa mʼnyimbo anthu akumva.
I doðe Mojsije i izgovori sve rijeèi pjesme ove narodu, on i Isus sin Navin.
45 Mose atatsiriza kunena mawu onsewa pamtima kwa Aisraeli,
A kad izgovori Mojsije sve rijeèi ove svemu Izrailju,
46 iye anawawuza kuti, “Muwasunge bwino mu mtima mwanu, mawu onse amene lero lino ndikukuwuzani kuti mudzawuze ana anu, kuti adzamvere mosamalitsa mawu onse a malamulo amenewa.
Reèe im: privijte srce svoje k svijem rijeèima koje vam ja danas zasvjedoèavam, i kazujte ih sinovima svojim da bi držali sve rijeèi ovoga zakona i tvorili ih.
47 Mawuwa sikuti ndi mawu achabe kwa inu. Mawuwa ndi moyo wanu. Mukawamvera mudzakhala ndi moyo wautali mʼdziko limene mukukalitenga kukhala lanu mukawoloka Yorodani.”
Jer nije prazna rijeè da za nju ne marite, nego je život vaš; i tom æete rijeèju produljiti dane svoje na zemlji, u koju idete preko Jordana da je naslijedite.
48 Tsiku lomwelo Yehova anawuza Mose kuti,
U isti dan reèe Gospod Mojsiju govoreæi:
49 “Pita ku mapiri a ku Abarimu ukakwere pa Phiri la Nebo ku Mowabu, moyangʼanana ndi Yeriko, ndipo ukaone dziko la Kanaani, dziko limene ndikulipereka kwa Aisraeli kukhala lawo.
Izidi na ovu goru Avarimsku, na goru Navav, koja je u zemlji Moavskoj prema Jerihonu, i vidi zemlju Hanansku koju dajem sinovima Izrailjevijem u državu.
50 Iwe udzafera pa phiri limenelo ndipo udzapita kumene makolo ako anapita, monga mʼbale wako Aaroni anafera pa phiri la Hori ndipo anakakhala ndi anthu a mtundu wake.
I umri na gori na koju izideš, i priberi s k rodu svojemu, kao što je umro Aron brat tvoj na gori Oru i pribrao se k rodu svojemu.
51 Chifukwa chake nʼchakuti inu nonse awiri simunakhulupirike kwa Ine pamaso pa Aisraeli pa madzi a Meriba ku Kadesi mʼchipululu cha Zini chifukwa simunandilemekeze kokwanira pakati pa Aisraeli.
Jer mi zgriješiste meðu sinovima Izrailjevijem na vodi od svaðe u Kadisu, u pustinji Sinu, što me ne proslaviste meðu sinovima Izrailjevijem.
52 Choncho udzalionera kutali dziko limene ndikupereka kwa Aisraeli. Sudzalowa mʼdziko limene ndi kulipereka kwa Aisraeli.”
Pred sobom æeš vidjeti zemlju, ali neæeš u nju uæi, u zemlju koju dajem sinovima Izrailjevijem.

< Deuteronomo 32 >