< Deuteronomo 32 >

1 Mverani, inu mayiko a mmwamba ndipo ine ndidzayankhula; imva, iwe dziko lapansi, mawu a pakamwa panga.
Give ear, you heavens, and let me speak. Let the earth listen to the words of my mouth.
2 Chiphunzitso changa chigwe ngati mvula ndipo mawu anga atsike ngati mame, ngati mvumbi pa udzu watsopano, ngati mvula yochuluka pa zomera zanthete.
Let my teaching drop down like the rain, let my speech distill like the dew, like the gentle rain on the tender grass, and like the showers on the plants.
3 Ndidzalalikira dzina la Yehova. Aa, tamandani ukulu wa Mulungu wathu!
For I will proclaim the name of Yahweh, and ascribe greatness to our God.
4 Iye ndi Thanthwe, ntchito zake ndi zangwiro, njira zake zonse ndi zolungama. Mulungu wokhulupirika amene salakwitsa, Iye ndiye wolungama ndi wosalakwa.
The Rock, his work is perfect; for all his paths are just. He is the faithful God, without iniquity. He is just and upright.
5 Koma iwo achita mosakhulupirika pamaso pake, iwo si ana akenso, koma iwo ndi mʼbado wachinyengo ndi wokhotakhota.
They have acted corruptly against him. They are not his children. It is their disgrace. They are a perverted and crooked generation.
6 Kodi mukumubwezera Yehova chotere, inu anthu opusa ndi opanda nzeru? Kodi Iye si Atate anu, Mlengi wanu, amene anakupangani ndi kukuwumbani?
Do you reward Yahweh in this way, you foolish and senseless people? Is he not your father, the one who has created you? He made you and established you.
7 Kumbukirani masiku amakedzana; ganizirani za mibado yakalekale. Funsa abambo ako ndipo adzakuwuza, akuluakulu ako, ndipo adzakufotokozera.
Call to mind the days of ancient times, think about the years of many ages past. Ask your father and he will show you, your elders and they will tell you.
8 Pamene Wammwambamwamba anapereka mayiko kwa anthu a mitundu ina kukhala cholowa chawo, pamene analekanitsa anthu onse, anayikira malire anthu onse molingana ndi chiwerengero cha ana a Israeli.
When the Most High gave the nations their inheritance— when he divided all of mankind, and he set the boundaries of the peoples, as he also fixed the number of their gods.
9 Pakuti gawo la Yehova ndi anthu ake, Yakobo ndiye cholowa chake.
For Yahweh's portion is his people; Jacob is his apportioned inheritance.
10 Anamupeza mʼchipululu, ku malo owuma ndi kopanda kanthu. Anamuteteza ndi kumusamalira; anamutchinjiriza ngati mwanadiso wake,
He found him in a desert land, and in the barren and howling wilderness; he shielded him and cared for him, he guarded him as the apple of his eye.
11 ngati chiwombankhanga chimene chimasasula chisa chake nʼkumazungulira pamwamba pa ana ake, chimene chimatambalalitsa mapiko ake kuti chigwire anawo ndi kuwanyamula pa mapiko ake otambalalawo.
As an eagle that guards her nest and flutters over her young, Yahweh spread out his wings and took them, and carried them on his pinions.
12 Yehova yekha ndiye anamutsogolera; popanda thandizo la mulungu wachilendo.
Yahweh alone led him; no foreign god was with him.
13 Anamuyendetsa pamwamba pa mapiri a mʼdziko ndi kumudyetsa zipatso za mʼminda. Anamudyetsa uchi wofula pa thanthwe, ndiponso mafuta ochokera mʼnthaka ya miyala,
He made him ride on high places of the land, and he fed him the fruits of the field; he nourished him with honey from the rock, and oil from the flinty crag.
14 pamodzi ndi chambiko ndi mkaka wochokera ku ngʼombe ndi nkhosa, ndiponso ana ankhosa onenepa ndi mbuzi, pamodzinso ndi nkhosa zazimuna zabwino za ku Basani ndiponso tirigu wabwino kwambiri. Munamwa vinyo wa thovu lofiira.
He ate butter from the herd and drank milk from the flock, with fat of lambs, rams of Bashan and goats, with the finest of the wheat— and you drank foaming wine made from the juice of grapes.
15 Yesuruni ananenepa ndi kuyamba kuwukira; atakhuta, ananenepa ndi kukula thupi. Anasiya Mulungu amene anamulenga ndipo anakana Thanthwe ndi Mpulumutsi wake.
But Jeshurun grew fat and kicked— you grew fat, you were too fat, and you had eaten your fill— he abandoned the God who made him, and he rejected the Rock of his salvation.
16 Anamuchititsa nsanje ndi milungu yawo yachilendo ndiponso anamukwiyitsa ndi mafano awo onyansa.
They made Yahweh jealous by their strange gods; with their abominations they angered him.
17 Anapereka nsembe kwa ziwanda zimene si Mulungu, milungu imene sankayidziwa nʼkale lomwe, milungu yongobwera kumene, milungu imene makolo anu sankayiopa.
They sacrificed to demons, which are not God— gods they had not known, gods that recently appeared, gods your fathers did not fear.
18 Inu munasiya Thanthwe limene linakulerani; munayiwala Mulungu amene anakubalani.
You have deserted the Rock, who became your father, and you forgot the God who gave you birth.
19 Yehova anaona zimenezi ndipo anawakana chifukwa ana ake aamuna ndi aakazi anamukwiyitsa.
Yahweh saw this and he rejected them, because his sons and his daughters provoked him so.
20 Iye anati, “Ndidzawabisira nkhope yanga, ndi kuona kuti mathero awo adzakhala otani; pakuti ndi mʼbado wopotoka, ana amene ndi osakhulupirika.
“I will hide my face from them,” he said, “and I will see what their end will be; for they are a perverse generation, children who are unfaithful.
21 Anandichititsa kukhala wansanje pamene ankapembedza chimene si mulungu ndi kundikwiyitsa chifukwa cha mafano awo achabechabe. Ine ndidzawachititsa kuti achite nsanje ndi mtundu wina wopandapake; ndidzawakwiyitsa ndi mtundu wina wachabechabe.
They have made me jealous by what is not god and angered me by their worthless things. I will make them envious by those who are not a people; by a foolish nation I will make them angry.
22 Pakuti mkwiyo wanga wayaka ngati moto, umene umayaka mpaka ku dziko la anthu akufa. Motowo udzanyeketsa dziko lapansi ndi zokolola zake ndipo udzapsereza maziko a mapiri. (Sheol h7585)
For a fire is kindled by my anger and is burning to the lowest Sheol; it is devouring the earth and its harvest; it is setting on fire the foundations of the mountains. (Sheol h7585)
23 “Ndidzawawunjikira masautso ndipo mivi yanga yonse idzathera pa iwo.
I will heap disasters on them; I will shoot all my arrows at them;
24 Ndidzawatumizira njala yoopsa, malungo woopsa ndi nthenda zofa nazo; ndidzawatumizira zirombo zakuthengo zowavuta, ululu wa njoka ya mʼphiri imene imakwawa pa fumbi.
They will be wasted by hunger and devoured by burning heat and bitter destruction; I will send on them the teeth of wild animals, with the poison of things that crawl in the dust.
25 Mʼmisewu lupanga lidzawasandutsa kukhala wopanda ana; mantha adzalamulira nyumba zawo. Anyamata ndi atsikana adzafa, ngakhalenso makanda ndi okalamba.
Outside the sword will bereave, and in the bedrooms terror will do so. It will destroy both young man and virgin, the nursing baby, and the man of gray hairs.
26 Ine ndinanena kuti ndidzawamwaza ndi kuwafafaniza kuti anthu asawakumbukirenso,
I said that I would scatter them far away, that I would make the memory of them to cease from among mankind.
27 koma sindinafune kuti adani anga adzandinyoze, mwina adani anga sadzandimvetsetsa ndipo adzanena kuti, ‘Tagonjetsa anthuwa ndife; Yehova sanachite zonsezi.’”
Were it not that I feared the provocation of the enemy, and that their enemies would judge mistakenly, and that they would say, 'Our hand is exalted,' I would have done all this.
28 Iwo ndi mtundu wopanda maganizo, iwo alibe nzeru nʼpangʼono pomwe.
For Israel is a nation devoid of wisdom, and there is no understanding in them.
29 Ngati iwo akanakhala anzeru akanamvetsetsa izi ndi kuzindikira kuti mathero awo adzakhala otani!
Oh, that they were wise, that they understood this, that they would consider their coming fate!
30 Kodi munthu mmodzi akanathamangitsa bwanji anthu 1,000 kapena anthu awiri kuthamangitsa anthu 10,000, kuti awagonjetse, Thanthwe lawo likanapanda kuwagulitsa, Yehova akanapanda kuwataya?
How could one chase a thousand, and two put ten thousand to flight, unless their Rock had sold them, and Yahweh had given them up?
31 Pakuti thanthwe lawo silofanana ndi Thanthwe lathu, ngakhale adani athu amavomereza zimenezi.
For our enemies' rock is not like our Rock, just as even our enemies admit.
32 Mpesa wawo umachokera ku mpesa wa ku Sodomu ndiponso ku minda ya ku Gomora. Mphesa zawo zili ndi ululu wakupha ndipo maphava ake ndi owawa.
For their vine comes from the vine of Sodom, and from the fields of Gomorrah; their grapes are grapes of poison; their clusters are bitter.
33 Vinyo wawo ndi wa ululu wa njoka, ululu woopsa wa mphiri.
Their wine is the poison of serpents and the cruel venom of asps.
34 “Kodi zimenezi sindinazisunge ndi kuzitsekera mʼkatikati mwa chuma changa?
Is not this plan secretly kept by me, sealed up among my treasures?
35 Kubwezera chilango nʼkwanga; ndidzawalanga ndine. Pa nthawi yake phazi lawo lidzaterera; tsiku lawo la masautso layandikira ndipo chiwonongeko chawo chikubwera pa iwo mofulumira.”
Vengeance is mine to give, and recompense, at the time when their foot slips; for the day of disaster for them is near, and the things that are to come on them will hurry to happen.”
36 Yehova adzaweruza anthu ake ndipo adzachitira atumiki ake chifundo pamene adzaona kuti mphamvu zawo zatha ndipo kuti palibe amene watsala, kapolo kapena mfulu.
For Yahweh will give justice to his people, and he will pity his servants. He will see that their power is gone, and no one remains, either slaves or free people.
37 Iye adzanena kuti, “Nanga ili kuti milungu yawo, thanthwe limene ankabisalamo,
Then he will say, “Where are their gods, the rock in whom they took refuge?—
38 milungu imene inkadya mafuta a nsembe zawo ndi kumwa vinyo wa chopereka chawo cha chakumwa?” Iwuzeni ibwere kuti idzakuthandizeni! Ibwere kuti idzakutetezenitu!
The gods who ate the fat of their sacrifices and drank the wine of their drink offerings? Let them rise up and help you; let them be your protection.
39 “Onani tsopano kuti Ine ndine Iyeyo! Palibe mulungu wina koma Ine ndekha. Ine ndimapha ndiponso kupereka moyo, ndavulaza ndipo ndidzachiritsa, ndipo palibe angathe kupulumutsa munthu mʼmanja mwanga.
See now that I, even I, am God, and that there is no god besides me; I kill, and I make alive; I wound, and I heal, and there is no one who can save you from my might.
40 Ndikweza dzanja langa kumwamba ndi kulumbira kuti, ‘Pali Ine wamoyo wamuyaya,
For I lift up my hand to heaven and say, 'As I live forever, I will act.
41 pamene ndidzanola lupanga langa lonyezimira ndipo dzanja liligwira pakubweretsa chiweruzo, ndidzabwezera chilango adani anga ndi kulanga onse odana nane.
When I sharpen my glittering sword, and when my hand begins to bring justice, I will render vengeance on my enemies, and I will pay back those who hate me.
42 Mivi yanga idzakhuta magazi awo pamene lupanga langa lidzawononga mnofu: magazi a anthu ophedwa ndi ogwidwa ukapolo, mitu ya atsogoleri a adani.’”
I will make my arrows drunk with blood, and my sword will devour flesh with the blood of the killed and the captives, and from the heads of the leaders of the enemy.'”
43 Kondwerani, inu mitundu yonse ya anthu pamodzi ndi anthu ake, pakuti Iye adzabwezera chilango anthu amene anapha atumiki ake; adzabwezera chilango adani ake ndipo adzakhululukira dziko lake ndi la anthu ake.
Rejoice, you nations, with God's people, for he will avenge the blood of his servants; he will render vengeance on his enemies, and he will make atonement for his land, for his people.
44 Mose anabwera ndi Yoswa mwana wa Nuni ndipo anayankhula mawu onsewa mʼnyimbo anthu akumva.
Moses came and recited all the words of this song in the ears of the people, he, and Joshua son of Nun.
45 Mose atatsiriza kunena mawu onsewa pamtima kwa Aisraeli,
Then Moses finished reciting all these words to all Israel.
46 iye anawawuza kuti, “Muwasunge bwino mu mtima mwanu, mawu onse amene lero lino ndikukuwuzani kuti mudzawuze ana anu, kuti adzamvere mosamalitsa mawu onse a malamulo amenewa.
He said to them, “Fix your mind on all the words that I have witnessed to you today, so that you may command your children to keep them, all the words of this law.
47 Mawuwa sikuti ndi mawu achabe kwa inu. Mawuwa ndi moyo wanu. Mukawamvera mudzakhala ndi moyo wautali mʼdziko limene mukukalitenga kukhala lanu mukawoloka Yorodani.”
For this is no trivial matter for you, because it is your life, and through this thing you will prolong your days in the land that you are going over the Jordan to possess.”
48 Tsiku lomwelo Yehova anawuza Mose kuti,
Yahweh spoke to Moses on that same day and said,
49 “Pita ku mapiri a ku Abarimu ukakwere pa Phiri la Nebo ku Mowabu, moyangʼanana ndi Yeriko, ndipo ukaone dziko la Kanaani, dziko limene ndikulipereka kwa Aisraeli kukhala lawo.
“Go up into this range of the mountains of Abarim, up Mount Nebo, which is in the land of Moab, opposite Jericho. You will look at the land of Canaan, which I am giving to the people of Israel as their possession.
50 Iwe udzafera pa phiri limenelo ndipo udzapita kumene makolo ako anapita, monga mʼbale wako Aaroni anafera pa phiri la Hori ndipo anakakhala ndi anthu a mtundu wake.
You will die on the mountain that you go up, and you will be gathered to your people, as Aaron your fellow Israelite died on Mount Hor and was gathered to his people.
51 Chifukwa chake nʼchakuti inu nonse awiri simunakhulupirike kwa Ine pamaso pa Aisraeli pa madzi a Meriba ku Kadesi mʼchipululu cha Zini chifukwa simunandilemekeze kokwanira pakati pa Aisraeli.
This will happen because you were unfaithful to me among the people of Israel at the waters of Meribah in Kadesh, in the wilderness of Zin; because you did not treat me with honor and respect among the people of Israel.
52 Choncho udzalionera kutali dziko limene ndikupereka kwa Aisraeli. Sudzalowa mʼdziko limene ndi kulipereka kwa Aisraeli.”
For you will see the land before you, but you will not go there, into the land that I am giving to the people of Israel.”

< Deuteronomo 32 >