< Deuteronomo 25 >

1 Anthu akasemphana mawu, ayenera kupita ku bwalo la milandu ndipo woweruza adzaweruza mlanduwo. Adzamasula wosalakwa nalanga wolakwa.
If cause is bitwixe ony men, and thei axen iugis, thei schulen yyue the victorie of riytfulnesse to him, whom thei perseyuen to be iust, thei schulen condempne hym of wickidnesse, whom thei perseyuen to be wickid.
2 Munthu akapezeka wolakwa ayenera kukwapulidwa, woweruza amugoneke pansi wolakwayo ndipo akwapulidwe pamaso pake zikoti zochuluka molingana ndi mlandu wake,
Sotheli if thei seen hym that synnede, worthi of betyngis, thei schulen caste him doun, and make to be betun bifor hem; also the maner of betyngis schal be for the mesure of synne,
3 koma asamukwapule zikoti zopitirira makumi anayi. Akakwapulidwa kupitirira apo ndiye kuti mʼbale wanuyo anyozeka pamaso panu.
so oneli that tho passe not the noumbre of fourti, lest thi brother be to-rent viliche bifore thin iyen, and go awei.
4 Musamange ngʼombe pakamwa pamene ikupuntha tirigu.
Thou schalt not bynde the `mouth of the oxe tredynge thi fruytis in the corn floor.
5 Ngati abale akukhala pamodzi ndipo wina mwa iwo akamwalira wosasiya mwana wamwamuna, mkazi wamasiyeyo asakakwatiwe ndi mlendo. Mʼbale wake wa mwamuna wakeyo amukwatire kukwaniritsa chimene akuyenera kuchita kwa mlamu wakeyo.
Whanne britheren dwellen to gidere, and oon of hem is deed with out fre children, the wijf of the deed brother schal not be weddid to anothir man, but his brothir schal take hir, and schal reise seed of his brother.
6 Mwana wamwamuna woyamba amene mayiyo angabereke ayenera kutenga dzina la mwamuna wake womwalirayo kuti dzina lake lisafafanizike mu Israeli.
And he schal clepe the firste gendrid sone `of hir bi the name `of hym, `that is, of the deed brothir, that his name be not don awei fro Israel.
7 Komabe, ngati munthu sakufuna kukwatira mkazi wa mʼbale wakeyo, mkaziyo ayenera kupita kwa akuluakulu ku chipata cha mzinda ndi kukanena kuti, “Mʼbale wake wa mwamuna wanga akukana kupitiriza dzina la mʼbale wake mu Israeli. Iye akukana kulowa chokolo.”
Forsothe if he nyle take the wijf of his brother, which is due to hym bi lawe, the womman schal go to the yate of the citee; and sche schal axe the grettere men in birthe, and sche schal seie, `The brother of myn hosebonde nyle reise seed of his brother in Israel, nethir wole take me in to mariage.
8 Pamenepo akuluakulu a mu mzinda wawowo adzamuyitanitsa nakamba naye. Ngati alimbikirabe kunena kuti, “Ine sindikufuna kumukwatira mkaziyu,”
And anoon thei schulen make hym to be clepid, and thei schulen axe. If he answerith, Y nyle take hir to wijf;
9 mkazi wamasiye wa mʼbale wakeyo adzapita kwa iye pamaso pa akuluakuluwo namuvula nsapato imodzi, adzamulavulire kumaso nʼkunena kuti, “Izi ndi zimene amachitira munthu amene safuna kupitiriza mbiri ya banja la mʼbale wake.”
the womman schal go to hym bifor the eldre men of Israel, and sche schal take awei the schoo, and sche schal spete in to his face, and schal seie, So it schal be doon to the man, that bildith not `the hows of his brother;
10 Mbiri ya banja la munthu ameneyo idzadziwika mu Israeli kuti ndi Banja la Wovulidwa nsapato.
and `the name of hym schal be clepid in Israel, The hows of the man vnschood.
11 Ngati anthu awiri akuchita ndewu ndipo mkazi wa mmodzi wa iwo abwera kudzaleretsa mwamuna wake kwa mnzakeyo natambasula dzanja lake kugwira ku maliseche kwa winayo,
If twei men han strijf bitwixe hem silf, and oon bigynneth to stryue ayens another, and the wijf of `the tother man wole delyuere hir hosebonde fro the hond of the strongere man, and puttith hond, and `takith the schamefast membris `of hym,
12 muyenera kumudula dzanja, osamumvera chisoni.
thou schalt kitte awei `the hond of hir, nether thou schalt be bowid on hir bi ony mercy.
13 Musamakhale ndi miyeso iwiri yosiyana mʼthumba mwanu, wolemera ndi wopepuka.
Thou schalt not haue in the bagge dyuerse weiytis,
14 Musamakhale ndi milingo iwiri yosiyana mʼnyumba mwanu, waukulu ndi waungʼono.
a grettere and a lesse, nether a buyschel more and lesse schal be in thin hows.
15 Muyenera kukhala ndi miyeso ndi milingo yoyenera ndi yosanyenga kuti mukhalitse mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.
Thou schalt haue a iust weiyte and trewe, and an euene buyschel `and trewe schal be to thee, that thou lyue in myche tyme on the lond which thi Lord God schal yyue to thee.
16 Pakuti Yehova Mulungu wanu amanyansidwa ndi aliyense wochita za chinyengo zoterezi.
For the Lord schal haue hym abhomynable that doith these thingis, and he wlatith, `ethir cursith, al vnriytfulnesse.
17 Kumbukirani zimene Aamaleki anakuchitirani pamene munali pa ulendo wochokera ku Igupto.
Haue thou mynde what thingis Amalech dide to thee in the weie, whanne thou yedist out of Egipt;
18 Pamene munali otopa ndi ofowoka, iwo anakumana nanu pa ulendo wanu ndi kukantha onse otsalira mʼmbuyo ndipo iwo sanaope Mulungu.
hou he cam to thee, and killide the laste men of thin oost, that saten wery, whanne thou were disesid with hungur and trauel, and he dredde not God.
19 Pamene Yehova Mulungu wanu akupumulitsani kwa adani onse okuzungulirani mʼdziko limene akupatsani inu ngati cholowa chanu, mudzawafafanize Aamaleki, asadzawakumbukirenso pa dziko lapansi. Musadzayiwale chimenechi!
Therfor whanne thi Lord God hath youe reste to thee, and hath maad suget alle naciouns `bi cumpas, in the lond which he bihiyte to thee, thou schalt do awei `the name of hym vndur heuene; be thou war lest thou foryete.

< Deuteronomo 25 >