< Amosi 2 >

1 Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Mowabu akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza anatentha mafupa a mfumu ya ku Edomu, mpaka kuwasandutsa phulusa,
Så sier Herren: For tre misgjerninger av Moab, ja for fire vil jeg ikke ta det tilbake - fordi de brente Edom-kongens ben til kalk;
2 Ine ndidzatumiza moto pa Mowabu, umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za ku Keriyoti. Mowabu adzafera pakati pa nkhondo yoopsa, mʼkati mwa mfuwu wa nkhondo ndi kuliza malipenga.
men jeg vil sende ild mot Moab, og den skal fortære Kerijots palasser, og Moab skal dø under krigsbulder, under hærskrik, under basunens lyd,
3 Ndidzawononga wolamulira wake ndi kupha akuluakulu onse amene ali pamodzi ndi iye,” akutero Yehova.
og jeg vil utrydde dommeren av deres land, og alle dets fyrster vil jeg drepe sammen med ham, sier Herren.
4 Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Yuda akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza iwo akana lamulo la Yehova ndipo sanasunge malangizo ake, popeza asocheretsedwa ndi milungu yabodza, milungu imene makolo awo ankayitsatira,
Så sier Herren: For tre misgjerninger av Juda, ja for fire vil jeg ikke ta det tilbake - fordi de foraktet Herrens lov og ikke holdt hans bud, og deres løgnguder, som deres fedre hadde fulgt, førte dem vill;
5 Ine ndidzatumiza moto pa Yuda, umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za ku Yerusalemu.”
men jeg vil sende ild mot Juda, og den skal fortære Jerusalems palasser.
6 Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Israeli akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Iwo amagulitsa anthu olungama ndi siliva, ndi osauka ndi nsapato.
Så sier Herren: For tre misgjerninger av Israel, ja for fire vil jeg ikke ta det tilbake - fordi de selger den uskyldige for penger og den fattige for et par sko,
7 Amapondereza anthu osauka ngati akuponda fumbi, ndipo sawaweruza mwachilungamo anthu oponderezedwa. Abambo ndi mwana wawo amagonana ndi mtsikana mmodzi yemweyo, ndipo potero amanyozetsa dzina langa loyera.
de som higer efter å se støv på de ringes hode og bøier retten for de saktmodige. En mann og hans far går til samme pike, så de vanhelliger mitt hellige navn.
8 Anthuwo amakagonana mʼmbali mwa guwa lililonse la nsembe pa zovala zimene anatenga ngati chikole. Mʼnyumba ya mulungu wawo amamweramo vinyo amene analipiritsa anthu pa milandu.
På pantsatte klær strekker de sig ved hvert alter, og vin som de har tatt som bøter, drikker de i sin Guds hus.
9 “Ine ndinawononga Aamori pamaso pawo, ngakhale iwo anali anthu ataliatali ngati mikungudza ndiponso amphamvu ngati mitengo ya thundu. Ndinawononga zipatso zawo ndiponso mizu yawo.
Og jeg utryddet da amorittene foran dem, de som var høie som sedertrær og sterke som eketrær, og jeg ødela deres frukt oventil og deres røtter nedentil,
10 “Ine ndinakutulutsani ku Igupto, ndipo ndinakutsogolerani mʼchipululu kwa zaka makumi anayi, kudzakupatsani dziko la Aamori.
og jeg førte eder op fra Egyptens land, og jeg ledet eder i ørkenen i firti år, forat I skulde få amorittens land til eiendom,
11 Ine ndinawutsanso ena mwa ana ako kuti akhale aneneri, ndi ena mwa anyamata ako kuti akhale anaziri. Kodi si choncho, inu Aisraeli?” akutero Yehova.
og jeg opvakte nogen av eders sønner til profeter, og nogen av eders unge menn til nasireere. Er det ikke så, I Israels barn? sier Herren.
12 “Koma inu munawamwetsa vinyo anaziri aja, ndipo munalamula aneneri kuti asanenere.
Men I fikk nasireerne til å drikke vin, og I forbød profetene å profetere.
13 “Tsono Ine ndidzakupsinjani monga imapsinjikira ngolo imene yadzaza ndi tirigu.
Se, jeg vil knuge eder ned, likesom en vogn full av kornbånd knuger allting ned;
14 Munthu waliwiro sadzatha kuthawa, munthu wamphamvu sadzakhalanso ndi nyonga, wankhondo sadzapulumutsa moyo wake.
den raske skal intet tilfluktssted finne, og den sterke ikke kunne gjøre bruk av sin kraft, og helten ikke berge sitt liv;
15 Munthu wa uta sadzalimbika, msilikali wothamanga kwambiri sadzapulumuka, ndipo wokwera pa akavalo sadzapulumutsa moyo wake.
bueskytteren skal ikke holde stand, den som er lett på foten, skal ikke berge sitt liv, og heller ikke rytteren på sin hest,
16 Ngakhale asilikali olimba mtima kwambiri adzathawa ali maliseche pa tsikulo,” akutero Yehova.
den modigste iblandt heltene skal flykte naken på den dag, sier Herren.

< Amosi 2 >