< Machitidwe a Atumwi 2 >

1 Litafika tsiku la chikondwerero cha Pentekosite, onse anali pamodzi.
Nalyahafiha isiku elye Pentekoste, bhonti bhabhongene pandwemo.
2 Mwadzidzidzi kunamveka mkokomo kuchokera kumwamba ngati wa mphepo yamphamvu, ndipo inadzaza nyumba yonse imene amakhala.
Gwahabhafumila ungulumo afume humwanya neshi ugwihala ehali. Gwamema munyumba yonti mwabhakheye.
3 Iwo anaona zinthu zokhala ngati malilime amoto ogawikana ndipo anakhala pa aliyense wa iwo.
Zyahabhafumila emele neshi, zigabhanyishe nabhe pamwanya ya shila muntu (pitwe).
4 Ndipo onse anadzazidwa ndi Mzimu Woyera, nayamba kuyankhula mu ziyankhulo zina, monga Mzimu Woyerayo anawayankhulitsa.
Bhonti bhapata Umpepo Ufinjile bhahanda ayanje enjango ezyenje neshi Umpepo shasungwilwe umwene.
5 Ayuda woopa Mulungu ochokera ku mayiko onse a dziko lapansi ankakhala mu Yerusalemu nthawi imeneyi.
Bhahali ayahudi bhabhakhalaga mu Yelusalemu bhabhaputaga bhabhafuma shila nsi pansi.
6 Utamveka mkokomo uja, gulu la anthu linasonkhana. Anthuwo anadabwa chifukwa aliyense anawamva atumwiwo akuyankhula ziyankhulo zosiyanasiyana.
Ungulumo gula nabhahunvwa abhantu bhahabhungana ahwenze atejelezye bhahabha ne wasiwasi shila muntu ahumnwizye bhayanga hunjango yakwe yuyo.
7 Mothedwa nzeru anafunsana kuti, “Kodi anthu onse amene akuyankhulawa si Agalileya?
bhonti bhahaswiga bhahaga ebha bhonti se bha hu Galilaya bhabha yanga epa?
8 Nanga bwanji aliyense wa ife akuwamva iwo mu chinenero cha kwawo?
Yeenu ate tibhumvwa hunjango yetu yatapipwe nayo?
9 Apanti, Amedi ndi Aelami; okhala ku Mesopotamiya, ku Yudeya ndi ku Kapadokiya, ku Ponto ndi ku Asiya,
Waparthia na Waamedi na Waelamu, nebho bhabhakhala hu Mesopotamia, no Uyahudi, na Kapadokia, no hu Ponto nu hu Asia,
10 ku Frugiya ndi Pamfiliya, ku Igupto ndi ku madera a ku Libiya kufupi ndi ku Kurene; alendo ochokera ku Roma,
hu Frigia, Pamfilia, no hu Misri, na hula hu Libya paka hu Kirene, na bhajenu bhonti bhabhafumile hu Rumi,
11 Ayuda ndi otsatira chipembedzo cha Chiyuda onse pamodzi; Akrete ndi Aarabu, ife tonse tikuwamva akuyankhula za ntchito zodabwitsa za Mulungu mu ziyankhulo zathu.”
Ayahudi na bhaongofu, Abhakrete bhonti tubhomvwa nazyo bhatambula embombo engosi Ungulubhi zyabhomba.”
12 Modabwa ndi mothedwa nzeru anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Zimenezi zikutanthauzanji?”
Bhonti bhaswiga sebhahazyaganya mwitwe; hahanda abhuzanye bhene, “Eshi hwa huje yeenu?”
13 Koma ena anawaseka nati, “Aledzera vinyo watsopano.”
Lelo bhamo bhahatanila bhahaga, “Ebha bhakholilwe.”
14 Koma Petro anayimirira pamodzi ndi atumwi khumi ndi mmodziwo ndipo anakweza mawu ake nayankhula kwa gulu la anthu nati: “Ayuda anzanga, ndi nonse amene muli mu Yerusalemu, mvetsetsani izi ndipo tcherani khutu ku zimene ndikunena.
Lelo uPetro ahimilila pandwemo na bhala ilongo na woka nabhabhule huje mwe mubhantu mwenti mwa mukhala hu Yudea namwe mwenti mwamukhala epa pa Yerusalemu, muntejelezye enongwa zyane muzizingatizye humoyo genyu.
15 Kunena zoona, anthu awa sanaledzere ayi, monga momwe mukuganizira, pakuti ino ndi 9 koloko mmawa!
Abhantu ebha sebhakholilwe neshi shamuibha, esala ezi saa tatu zyashampwiti.
16 Koma izi ndi zimene ananena Mneneri Yoweli kuti:
Lelo mumanye huje ezi zyazila zyazyayangwilwe no ukuwe uYoeli;
17 “‘Mulungu akuti, mʼmasiku otsiriza ndidzakhuthulira Mzimu wanga pa anthu onse. Ana anu aamuna ndi aakazi adzanenera, anyamata anu adzaona masomphenya, nkhalamba zanu zidzalota maloto.
Zyaibha ensiku ezya humalishilo; ayanga Ungulubhi, naibhitila Umpepo Ufinjile abhantu bhonti. Abhana bhenyu asahala na lendu bhaikuwa, abhana bhenyu bhailola embonesyo, na gogolo bhailota enjozi.
18 Ngakhalenso pa antchito anga aamuna ndi aakazi, ndidzakhuthulira Mzimu wanga masiku amenewo, ndipo iwo adzanenera.
Nantele abhomba mbombo bhane abhashe ehaibhitila Umpepo wane bhope bhaikuwa.
19 Ndipo ndidzaonetsa zodabwitsa mlengalenga ndi zizindikiro pa dziko lapansi pano, ndizo magazi, moto ndi utsi watolotolo.
Naibhalanga enswijizyo humwanya ne mbonesyo pansi pa dunia, idanda, umwoto, na tukusye elyosi.
20 Dzuwa lidzadetsedwa ndipo mwezi udzaoneka ngati magazi lisanafike tsiku lalikulu ndi laulemerero la Ambuye.
Ni sanya lyaigaluha hisi no mwezi abhe lidanda, salisele ahwinze isiku Igosi lya Ngulubhi.
21 Ndipo aliyense amene adzayitana pa dzina la Ambuye adzapulumuka.’
ehaibha shila muntu yailikwizya itawa la Ngulubhi ayokoha.'
22 “Inu Aisraeli mverani mawu awa; Yesu wa ku Nazareti anali munthu amene anaperekedwa kwa inu ndi Mulungu. Ndipo Mulungu anakutsimikizirani zimenezi ndi zamphamvu, zodabwitsa ndi zizindikiro zimene anachita mwa Iye pakati panu, monga inu mukudziwa.
Mubhantu mubhi Israeli, umvwi enongwa ezi: U Yesu wa hu Nazareti, Ungulubhi yabhasaluliye na hulete hulimwe ne mbombo engosi Ungulubhi zyabhombile ashilile hwa mwene, namwe mwazilolile namwe muzimenye zyonti zyabhombile-
23 Yesu ameneyu anaperekedwa kwa inu mwa kufuna ndi kudziwiratu kwa Mulungu; ndipo inu mothandizidwa ndi anthu oyipa, munamupha Iye pomupachika pa mtanda.
Lelo hunongwa ya mapango gakwe gapanjile afume hale nenjele zyakwe Ungulubhi, aje aihufumya humakhono ga bhantu aabhibhi ananzi, namwe mwahabuda,
24 Koma Mulungu anamuukitsa kwa akufa, kumumasula Iye ku zowawa za imfa, chifukwa kunali kosatheka kuti agwiridwe ndi imfa.
Ungulubhi umwene ahazyusya ahayefwa enfwa muhati yakwe kwa sababu seyaweze hene aje enfwa etabhaale.
25 Pakuti Davide ananena za Iye kuti, “‘Ndinaona Ambuye pamaso panga nthawi zonse. Chifukwa Iye ali kudzanja langa lamanja, Ine sindidzagwedezeka.
U Daudi ayanjile ajile, 'Nahalolile Ugosi wane hwitagalila lyane, umwene ali hukhono gwane ulilo sembahwogope.
26 Chifukwa chake mtima wanga ndi wokondwa ndipo lilime langa likukondwera; thupi langanso lidzakhala ndi chiyembekezo.
Umwoyo gwane gwahasungwa nu mele gwane gwasungwilwe. Gwope ubili gwane gwaikhala ni khone.
27 Chifukwa simudzasiya moyo wanga kumalo a anthu akufa, ku manda, kapena kulekerera Woyerayo kuti awole. (Hadēs g86)
Subhaguleshe umwoyo gwane gubhale hwazimu, nantele subhahuleshe ubhomba mbombo waho alole uvunzu. (Hadēs g86)
28 Inu munandidziwitsa ine njira zamoyo; Inu mudzandidzaza ndi chimwemwe pamaso panu.’
Awe umbunisizye idala elye womi; ubhandeshe ememe uluseshelo humaso gaho.'
29 “Abale, ine ndikuwuzani motsimikiza kuti kholo lathu Davide anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda, ndipo manda ake alipo lero lino.
Bhaholo, bhane enjanje ezya ise wetu u Daudi: umwene afwiye asyelelwe nenkungwa yakwe ehweli hulite mpaka asanyunu eshi.
30 Koma iye anali mneneri ndipo anadziwa kuti Mulungu analonjeza ndi lumbiro kuti adzayika mmodzi wa zidzukulu zake pa mpando waufumu.
Umwene ali kuwe na amenye huje Ungulubhi alapile hundapo zyakwe huje ahaihubhiha umo umwana wakwe hwitengo lyakwe elye umwene.
31 Davide ataoneratu zimene zinali mʼtsogolo anayankhula za kuuka kwa Khristu, kuti Iye sanasiyidwe mʼmanda, ndipo thupi lake silinawole. (Hadēs g86)
Eli alilolile shansele, nantele ayanjile huje aizyuha uYesu Kilisiti, 'sigalehwilwe hwazimu nu bili gwakwe sigagwavundile.' (Hadēs g86)
32 Mulungu wamuukitsa Yesu ameneyu, ndipo ife ndife mboni za zimenezi.
Unu uYesu - Ungulubhi azyusizye, nate tili bhaketi bhakwe.
33 Khristu anakwezedwa kukhala kudzanja lamanja la Mulungu, nalandira Mzimu Woyera amene Atate anamulonjeza, ndipo watipatsa ife zimene mukuona ndi kumvazi.
Eshi uYesu ali hukhono ulilo ugwa Ngulubhi, nantele ayejeleye ulaganyo ulwa Umpepo Ufinjile afume hwa Yise wakwe, asuhinye ululagano olu hulite neshi shamulola na hwumvwe.
34 Pakuti si Davide anakwera kumwamba koma iye akuti, “‘Ambuye anawuza Ambuye anga kuti: Khala kudzanja langa lamanja
Umwene uDaudi sigalushile abhale humwanya, lelo ajile, 'OGOSI (Ungulubhi) wane ayanjile hwa Gosi wane,
35 mpaka nditasandutsa adani ako kukhala chopondapo mapazi ako.’
“khala hukhono gwane ulilo, mpaka nehaibhabheha elyakhalile na khanyena manama gaho.
36 “Nʼchifukwa chake, Aisraeli onse adziwe ndithu kuti, Yesu amene inu munamupachika, Mulungu wamuyika kukhala Ambuye ndiponso Mpulumutsi.”
Aisraeli bhonti bhamanye huje uYesu unu yabhabudile Ungulubhi abhishile aje abhe Gosi ashile Agosi bhonti abhamunsi.”
37 Anthu atamva zimenezi, anatsutsika kwambiri mu mtima ndipo anati kwa Petro ndi atumwi enawo, “Abale, kodi ife tichite chiyani?”
Nabhumvwa isho enongwa zyabhalasa humwoyo gabho, bhabhabhuzya aPetro na bhamwabho tikhonzye wili eshi?”
38 Petro anawayankha kuti, “Lapani ndipo mubatizidwe aliyense wa inu, mʼdzina la Yesu Khristu kuti machimo anu akhululukidwe. Ndipo mudzalandira mphatso ya Mzimu Woyera.
U Petro waga, “Mulambe mwoziwe, shila muntu hwitawa lya Yesu Kristi muposhele ulusajilo ulwe mbibhi zyenyu, namwe mubhaposhe Umpepo Ufinjile.
39 Pakuti lonjezoli ndi lanu ndi ana anu ndiponso la onse amene ali kutali, ndi iwo onse amene Ambuye Mulungu wathu adzawayitane.”
Olu olulagano lwenyu na bhana bhenyu na bhantu bhabhali uhutali na bhaala bhonti bhabhaikwiziwa nu Ngulubhi aje bhinze.”
40 Petro anawachenjeza ndi mawu ena ambiri, ndipo anawadandaulira iwo kuti, “Mudzipulumutse ku mʼbado owonongeka uno.”
Hunongwa ezya mwabho ajile hwi ponii na bhantu bhensiku ezi abhe mbibhi.”
41 Iwo amene anawulandira uthenga wake anabatizidwa ndipo tsiku lomwelo miyoyo pafupifupi 3,000 inawonjezedwa ku gulu lawo.
Abhantu bhazyeteha enongwa zila bhoziwa abhantu elfu zitatu ikanisa lyahonjelela.
42 Iwo ankasonkhana pamodzi kuphunzitsidwa ndi atumwi, pachiyanjano, pachakudya ndi popemphera.
Bhahendelela adiile mumanyizyo zya atumwe bha Yesu bhali nu umoja, bhalyanga pandwimo na puute pandwimo.
43 Aliyense ankachita mantha chifukwa cha zodabwitsa ndi zizindikiro zambiri zimene atumwi ankachita.
Uwoga wahabhinjila abhantu ne mbombo ezyaswijizye zyahabhoneha Ungulubhi zyabhombile ashilile hwa tumwe bhakwe.
44 Okhulupirira onse anali pamodzi ndipo aliyense ankapereka zinthu zake kuti zikhale za onse.
Bhonti bhabhahitishie izu lya Ngulubhi bhahakhalaga pandwimo ne vintu vyabhali navyo vyali vya bhonti,
45 Ankagulitsa minda yawo ndi katundu wawo, ndi kugawira kwa aliyense molingana ndi zosowa zake.
evintu vyabhali navyo bhakazyaga bhagabhilaga shila muntu shahanzaga.
46 Tsiku ndi tsiku ankasonkhana pamodzi pa bwalo la pa Nyumba ya Mulungu. Ankadya pamodzi mʼnyumba zawo mwasangala ndi mtima woona.
Ensiku zyonti bhali nu mwoyo gumo mushibhanza, bhamensulaga amabumunda mukhaya nalye eshalye shobho nuluseshelo nu mwoyo ugolosu;
47 Ankayamika Mulungu ndipo anthu onse ankawakomera mtima. Ndipo tsiku ndi tsiku Ambuye ankawonjezera ena pa chiwerengero cha olandira chipulumutso.
bhalumbaga Ungulubhi bhakonde lwe na bhanti bhonti. Shila lisiku abhantu bhahonjelelelaga mushibhanza bhaala bhabhahokahaga.

< Machitidwe a Atumwi 2 >