< 2 Samueli 8 >

1 Patapita nthawi, Davide anagonjetsa Afilisti ndi kuwapambana ndipo analanda Metegi Ama kuchoka mʼmanja mwa Afilistiwo.
Some time later, David’s army attacked the Philistia [army] and defeated them. They took control over the entire Philistia area.
2 Davide anagonjetsanso Amowabu. Iye anawalamula kuti agone pansi mʼmizere itatu pa gulu lililonse ndipo anawayeza ndi chingwe. Pa gulu lililonse ankapha anthu amene anali pa mizere iwiri yoyamba, kusiyapo mzere wachitatu. Kotero Amowabu anakhala pansi pa ulamuliro wa Davide ndipo ankapereka msonkho.
David’s army also defeated the army of the Moab people-group. David forced their soldiers to lie down on the ground [close to each other]. His men killed two out of every three of them. The [other] Moab people [were forced to] accept David as their ruler, and they were forced to give to him [every year the] payment/tax [that he demanded].
3 Komanso Davide anagonjetsa Hadadezeri mwana wa Rehobu, mfumu ya Zoba, pamene anapita kukakhazikitsa ulamuliro wake mʼmbali mwa mtsinje wa Yufurate.
David’s army also defeated [the army of] Hadadezer, the son of Rehob, who ruled [the state of] Zobah [in Syria]. That happened when David went to rule again over the area at [the upper part of] the Euphrates River.
4 Davide analanda magaleta 1,000, anthu 7,000 okwera magaleta pamodzi ndi asilikali oyenda pansi 20,000. Iye anadula mitsempha ya akavalo onse okoka magaleta, koma anasiyapo akavalo 100 okha.
David’s army captured 1,700 of Hadadezer’s soldiers who rode on horses, and 20,000 of his other soldiers. They also crippled/hamstrung most of the horses that pulled the chariots, but they left/spared enough horses to [pull] 100 chariots.
5 Aramu wa ku Damasiko atabwera kudzathandiza Hadadezeri mfumu ya Zoba, Davide anakantha asilikali 22,000.
When [the army of] Syria came from Damascus [city] to help King Hadadezer’s [army], David’s soldiers killed 22,000 of them.
6 Iye anakhazikitsa maboma mu ufumu wa Aramu wa ku Damasiko, ndipo Aaramu anakhala pansi pa ulamuliro wake ndipo ankapereka msonkho. Yehova ankamupatsa chipambano Davide kulikonse kumene ankapita.
Then David stationed (groups of his soldiers/army camps) in their area, and the people of Syria were forced to accept David as their ruler, and to give to David’s government [every year] the payment/tax that he demanded. And Yahweh enabled David’s [army] to win victories wherever they went.
7 Davide anatenga zishango zagolide za akuluakulu ankhondo a Hadadezeri ndi kubwera nazo ku Yerusalemu.
David’s soldiers took the gold shields that were carried by Hadadezer’s officials, and brought them to Jerusalem.
8 Mfumu Davide inatenga mkuwa wambiri kuchokera ku Beta ndi Berotai, mizinda ya Hadadezeri.
They also brought [to Jerusalem] a lot of bronze [that they found] in Betah and Berothai, two cities that King Hadadezer [had previously] ruled.
9 Tou, mfumu ya Hamati atamva kuti Davide wagonjetsa gulu lonse lankhondo la Hadadezeri,
When Toi, the king of the Hamath [city in Syria], heard that David’s [army] had defeated the entire army of King Hadadezer,
10 anatumiza mwana wake Yoramu kwa mfumu Davide kukamulonjera ndi kukamuyamikira chifukwa cha kupambana kwake pa nkhondo yake ndi Hadadezeriyo, amene analinso pa nkhondo ndi Tou. Yoramu anabweretsa ziwiya zasiliva, zagolide ndi zamkuwa.
he sent his son Joram to greet King David and to (congratulate him/say that he was happy) about his army defeating Hadadezer’s army, which Toi’s [army] had fought many times. Joram brought to David many items/gifts made from gold, silver, and bronze.
11 Mfumu Davide inapereka zinthu zimenezi kwa Yehova, monga anachitira ndi siliva ndi golide zochokera ku mayiko onse amene anawagonjetsa:
King David dedicated all those items to Yahweh. He also dedicated the silver and gold which his army had taken from the nations that they had conquered.
12 Edomu ndi Mowabu, Aamoni ndi Afilisti, ndi Aamaleki. Iye anaperekanso zolanda ku nkhondo zochokera kwa Hadadezeri mwana wa Rehobu, mfumu ya Zoba.
They had taken items from the Edom people-group and the Moab people-group, from the Ammon people-group, from the Philistia people, and from [the descendants of] Amalek, as well as from the people that Hadadezer [previously] ruled.
13 Ndipo Davide anatchuka atabwera kokakantha Aedomu 18,000 mu Chigwa cha Mchere.
When David returned [after defeating the armies of Syria], he became more famous because his army killed 18,000 soldiers from the Edom people-group in the Salt Valley [near the Dead Sea].
14 Iye anayika maboma mʼdera lonse la Edomu, ndipo Aedomu onse anakhala pansi pa Davide. Yehova ankapambanitsa Davide kulikonse kumene ankapita.
David stationed (groups of his soldiers/army camps) throughout the Edom area, and forced the people there to accept him as their king. Yahweh enabled David’s [army] to win battles wherever they went.
15 Davide analamulira dziko lonse la Israeli ndipo ankachita zonse mwachilungamo ndi molondola pamaso pa anthu ake onse.
David ruled over all the Israeli people, and he always did for them what was fair and just.
16 Yowabu mwana wa Zeruya anali mkulu wa ankhondo; Yehosafati mwana wa Ahiludi anali mlembi wa zochitika.
Joab was the army commander; Jehoshaphat, the son of Ahilud, was the man who reported to the people everything that David decided that they should do;
17 Zadoki mwana wa Ahitubi ndi Ahimeleki mwana wa Abiatara anali ansembe; Seraya anali mlembi;
Zadok the son of Ahitub and Ahimelech the son of Abiathar were the priests; Seraiah was the official secretary;
18 Benaya mwana wa Yehoyada anali mtsogoleri wa Akereti ndi Apeleti; ndipo ana a Davide anali ansembe.
Benaiah the son of Jehoiada was the commander of (David’s bodyguards/the men who protected the king); and David’s sons were priests (OR, his administrators/advisors).

< 2 Samueli 8 >