< 2 Samueli 4 >

1 Isiboseti mwana wa Sauli atamva kuti Abineri waphedwa ku Hebroni, anataya mtima ndipo Aisraeli onse anachita mantha kwambiri.
And when Saul's son, heard that Abner was dead in Hebron, his hands became feeble, and all the Israelites were troubled.
2 Koma Isiboseti anali ndi anthu akuluakulu awiri amene ankatsogolera magulu a ankhondo. Mmodzi mwa iwo dzina lake linali Baana ndipo mnzakeyo anali Rekabu. Iwo anali ana a Rimoni wa banja la Beeroti wa fuko la Benjamini Beeroti. Iwo ankatengedwa ngati mbali imodzi ya Benjamini,
And Saul's son had two men who were captains of bands. The name of the one was Baanah, and the name of the other Rechab, the sons of Rimmon the Beerothite, of the sons of Benjamin, for Beeroth also is reckoned to Benjamin.
3 chifukwa anthu a ku Beeroti anathawira ku Gitaimu ndipo akhala ali kumeneko ngati alendo mpaka lero lino.
And the Beerothites fled to Gittaim, and have been sojourners there until this day.
4 (Yonatani mwana wa Sauli anali ndi mwana wamwamuna amene anali wolumala mapazi ake onse awiri. Iye anali ndi zaka zisanu pamene nkhani ya Sauli ndi Yonatani inamveka kuchokera ku Yezireeli. Amene amamulera anamunyamula ndi kuthawa naye, koma pamene amachita zinthu mofulumira mwanayo anagwa ndipo analumala. Dzina lake linali Mefiboseti).
Now Jonathan, Saul's son, had a son who was lame in his feet. He was five years old when the news came of Saul and Jonathan out of Jezreel, and his nurse took him up, and fled. And it came to pass, as she made haste to flee, that he fell, and became lame. And his name was Mephibosheth.
5 Choncho Rekabu ndi Baana ana a Rimoni wa ku Beeroti ananyamuka kupita ku nyumba ya Isi-Boseti, ndipo anafika nthawi ya masana kukutentha pamene iye amapumula.
And the sons of Rimmon the Beerothite, Rechab and Baanah, went, and came about the heat of the day to the house of Ish-bosheth, as he took his rest at noon.
6 Iwo analowa mʼchipinda chamʼkati ngati kuti amakatenga tirigu, ndipo anamulasa mʼmimba. Kenaka Rekabu ndi mʼbale wake Baana anathawa.
And they came there into the midst of the house as though they would have fetched wheat, and they smote him in the body. And Rechab and Baanah his brother escaped.
7 Iwo analowa mʼnyumbamo iye akugona pa bedi mʼchipinda chake. Atamulasa ndi kumupha, anadula mutu wake nʼkuwutenga, nayenda usiku wonse mʼnjira yopita ku Araba.
Now when they came into the house, as he lay on his bed in his bedchamber, they smote him, and killed him, and beheaded him, and took his head, and went by the way of the Arabah all night.
8 Iwo anabweretsa mutu wa Isi-Boseti kwa Davide ku Hebroni ndipo anati kwa mfumu, “Nawu mutu wa Isiboseti mwana wa Sauli, mdani wanu, amene anafuna kukuphani. Lero lino Yehova wabwezera mbuye wanga mfumu adani anu, Sauli ndi ana ake.”
And they brought the head of Ish-bosheth to David to Hebron, and said to the king, Behold, the head of Ish-bosheth, the son of Saul, thine enemy, who sought thy life. And Jehovah has avenged my lord the king this day of Saul, and of his seed.
9 Davide anayankha Rekabu ndi mʼbale wake Baana, ana a Rimoni wa ku Beeroti kuti, “Pali Yehova wamoyo, amene wandipulumutsa ku mavuto anga onse,
And David answered Rechab and Baanah his brother, the sons of Rimmon the Beerothite, and said to them, As Jehovah lives, who has redeemed my soul out of all adversity,
10 pamene munthu wina anandiwuza kuti, ‘Sauli wafa’ ndipo ankaganiza kuti wabweretsa nkhani yabwino, ine ndinamugwira ndi kumupha ku Zikilagi. Iyi inali mphotho imene ndinapereka kwa iyeyo chifukwa cha uthenga wake!
when he who told me, saying, Behold, Saul is dead, thinking to have brought good news, I took hold of him, and killed him in Ziklag, which was the reward I gave him for his news.
11 Nanji pamene anthu oyipa apha munthu wosalakwa ali mʼnyumba mwake ndiponso pa bedi lake! Kodi ine ndingaleke kukulangani ndi kukuchotsani pa dziko lapansi pano?”
How much more, when evil men have slain a righteous man in his own house upon his bed, shall I not now require his blood of your hand, and take you away from the earth?
12 Kotero Davide analamulira ankhondo ake, ndipo anawapha. Iwo anawadula manja ndi mapazi ndi kupachika matupi awo pa dziwe la ku Hebroni. Koma anatenga mutu wa Isi-Boseti nawuyika mʼmanda a Abineri ku Hebroni.
And David commanded his young men, and they killed them, and cut off their hands and their feet, and hanged them up beside the pool in Hebron. But they took the head of Ish-bosheth, and buried it in the grave of Abner in Hebron.

< 2 Samueli 4 >