< 2 Samueli 24 >

1 Nthawi inanso Yehova anawakwiyira Aisraeli ndipo anawutsa mtima wa Davide kuti awavutitse ndipo anati, “Pita kawerenge Aisraeli ndi Ayuda.”
And again the anger of Jehovah was kindled against Israel, and he moved David against them, saying, Go, number Israel and Judah.
2 Choncho mfumu inati kwa Yowabu pamodzi ndi atsogoleri a ankhondo amene anali nawo. “Pitani pakati pa mafuko onse a Israeli kuyambira ku Dani mpaka ku Beeriseba kuti mukawerenge anthu omenya nkhondo ndi cholinga choti ndidziwe chiwerengero chawo.”
And the king said to Joab the captain of the army, who was with him, Go now to and fro through all the tribes of Israel, from Dan even to Beersheba, and number ye the people, that I may know the sum of the people.
3 Koma Yowabu anayankha mfumu kuti, “Yehova Mulungu wanu achulukitse ankhondo anu kukhala miyandamiyanda, ndipo alole inu mbuye wanga mfumu mudzazione zimenezi. Koma nʼchifukwa chiyani inu mbuye wanga mfumu mukufuna kuchita zimenezi?”
And Joab said to the king, Now Jehovah thy God add to the people, however many they may be, a hundredfold, and may the eyes of my lord the king see it, but why does my lord the king delight in this thing?
4 Komabe mawu a mfumu anapambana mawu a Yowabu ndi atsogoleri a ankhondo. Choncho anachoka pamaso pa mfumu kupita kukawerenga anthu omenya nkhondo mu Israeli.
Notwithstanding, the king's word prevailed against Joab, and against the captains of the army. And Joab and the captains of the army went out from the presence of the king to number the people of Israel.
5 Atawoloka Yorodani, iwo anamanga misasa yawo pafupi ndi Aroeri kummwera kwa mzinda wa ku chigwa ndipo kenaka iwo anapita ku dziko la Gadi mpaka ku Yazeri.
And they passed over the Jordan, and encamped in Aroer on the right side of the city that is in the middle of the valley of Gad, and to Jazer.
6 Iwo anapita ku Giliyadi ndi ku chigwa cha Tahitimu Hodisi ndipo anapitirira mpaka ku Dani Yaani ndi madera ozungulira Sidoni.
Then they came to Gilead, and to the land of Tahtim-hodshi. And they came to Dan-jaan, and round about to Sidon,
7 Kenaka iwo anapita molunjika linga la ku Turo ndi ku mizinda yonse ya Ahivi ndi Akanaani. Pomaliza anapita ku Beeriseba ku Negevi wa ku Yuda.
and came to the stronghold of Tyre, and to all the cities of the Hivites, and of the Canaanites. And they went out to the south of Judah, at Beersheba.
8 Atayendayenda mʼdziko lonse anabwerera ku Yerusalemu patapita miyezi isanu ndi inayi ndi masiku makumi awiri.
So when they had gone to and fro through all the land, they came to Jerusalem at the end of nine months and twenty days.
9 Yowabu anapereka chiwerengero cha anthu ankhondo kwa mfumu: Mu Israeli munali anthu 800,000 amphamvu amene amadziwa kugwiritsa ntchito lupanga ndipo mu Yuda munali anthu 500,000.
And Joab gave the sum of the numbering of the people to the king. And there were in Israel eight hundred thousand valiant men who drew the sword, and the men of Judah were five hundred thousand men.
10 Davide anatsutsika mu mtima mwake atatha kuwerenga anthuwo ndipo anapemphera kwa Yehova kuti, “Ine ndachimwa kwambiri pa zimene ndachita. Tsono Yehova, ndikupempha kuti mukhululuke kulakwa kwa mtumiki wanu. Ine ndachita zopusa kwambiri.”
And David's heart smote him after he had numbered the people. And David said to Jehovah, I have sinned greatly in that which I have done, but now, O Jehovah, put away, I beseech thee, the iniquity of thy servant, for I have done very foolishly.
11 Davide asanadzuke mmawa mwake mawu a Yehova anafika kwa mneneri Gadi, mlosi wa Davide kuti,
And when David rose up in the morning, the word of Jehovah came to the prophet Gad, David's seer, saying,
12 “Pita ukamuwuze Davide kuti, ‘Yehova akuti, Ine ndikukupatsa zinthu zitatu izi. Usankhepo chimodzi pa zimenezi choti ndikuchitire.’”
Go and speak to David, Thus says Jehovah, I offer thee three things. Choose thee one of them, that I may do it to thee.
13 Choncho Gadi anapita kwa Davide ndipo anati kwa iye, “Kodi mungakonde kuti mʼdziko mwanu mukhale njala kwa zaka zitatu? Kapena kuti mukhale mukuthawa adani anu kwa miyezi itatu? Kapena kuti mʼdziko muno mukhale mliri kwa masiku atatu? Tsopano, ganizirani bwino ndipo musankhe chomwe mudzamuyankhe amene wandituma.”
So Gad came to David, and told him, and said to him, Shall seven years of famine come to thee in thy land? Or will thou flee three months before thy foes while they pursue thee? Or shall there be three days' pestilence in thy land? Now decide, and see what answer I shall return to him who sent me.
14 Davide anati kwa Gadi, “Ine ndavutika kwambiri mu mtima mwanga. Ife atilange ndi Yehova pakuti chifundo chake ndi chachikulu, koma ndisalangidwe ndi anthu.”
And David said to Gad, I am in a great strait. Let us fall now into the hand of Jehovah, for his mercies are great, and let me not fall into the hand of man.
15 Choncho Yehova anabweretsa mliri pa Aisraeli, kuyambira mmawa mpaka pa nthawi imene anafuna mwini wake, ndipo unapha anthu 70,000 kuyambira ku Dani mpaka ku Beeriseba.
So Jehovah sent a pestilence upon Israel from the morning even to the time appointed. And there died of the people from Dan even to Beersheba seventy thousand men.
16 Pamene mngelo anatambasula dzanja lake kuti awononge Yerusalemu, Yehova anamva chisoni chifukwa cha zowawazo ndipo anati kwa mngelo amene ankawononga anthu uja, “Basi kwakwanira! Leka kuwononga.” Nthawi imeneyo mngelo wa Yehova anali atayima pamalo opunthira tirigu a Arauna Myebusi.
And when the agent stretched out his hand toward Jerusalem to destroy it, Jehovah relented of the evil, and said to the agent who destroyed the people, It is enough. Now stay thy hand. And the agent of Jehovah was by the threshing-floor of Araunah the Jebusite.
17 Davide ataona mngelo amene ankakantha anthu uja, anati kwa Yehova, “Ine ndi amene ndachimwa. Ine mʼbusa ndiye ndachita zoyipa. Anthuwa ali ngati nkhosa zosalakwa. Kodi iwowa achita chiyani? Langani ineyo pamodzi ndi banja langa.”
And David spoke to Jehovah when he saw the agent who smote the people, and said, Lo, I have sinned, and I have done perversely, but these sheep, what have they done? Let thy hand, I pray thee, be against me, and against my father's house.
18 Tsiku limenelo Gadi anapita kwa Davide ndi kukanena kuti, “Pitani kamangeni guwa lansembe la Yehova pamalo opunthira tirigu a Arauna Myebusi.”
And Gad came that day to David, and said to him, Go up, rear an altar to Jehovah in the threshing-floor of Araunah the Jebusite.
19 Ndipo Davide anapita monga momwe Yehova anamulamulira kudzera mwa Gadi.
And David went up according to the saying of Gad, as Jehovah commanded.
20 Arauna atayangʼana ndi kuona mfumu ndi anthu ake akubwera kumene kunali iye, iyeyo anatuluka ndi kuwerama pamaso pa mfumu mpaka nkhope yake kugunda pansi.
And Araunah looked forth, and saw the king and his servants coming on toward him. And Araunah went out, and bowed himself before the king with his face to the ground.
21 Arauna anati, “Nʼchifukwa chiyani mbuye wanga mfumu mwabwera kwa mtumiki wanu?” Davide anayankha kuti, “Kudzagula malo ako opunthira tirigu kuti ndimangire Yehova guwa lansembe kuti mliri uli pa anthuwa usiye.”
And Araunah said, Why has my lord the king come to his servant? And David said, To buy the threshing-floor from thee, to build an altar to Jehovah that the plague may be halted from the people.
22 Arauna anati kwa Davide, “Mbuye wanga mfumu mutenge chilichonse chimene chikukondweretseni ndi kuchipereka nsembe. Nazi ngʼombe zazimuna za nsembe yopsereza, nazi zopunthira tirigu ndi magoli angʼombe kuti zikhale nkhuni.
And Araunah said to David, Let my lord the king take and offer up what seems good to him. Behold, the oxen for the burnt offering, and the threshing instruments and the yokes of the oxen for the wood.
23 Inu mfumu, Arauna akupereka zonsezi kwa inu mfumu.” Arauna anatinso kwa iye, “Yehova Mulungu wanu akuvomerezeni.”
All this, O king, Araunah gives to the king. And Araunah said to the king, Jehovah thy God accept thee.
24 Koma mfumu inayankha Arauna kuti, “Ayi, Ine ndikunenetsa kuti ndikulipira. Sindidzapereka kwa Yehova Mulungu wanga nsembe yopsereza imene sindinavutikire.” Kotero Davide anagula malo wopunthira tiriguwo ndi ngʼombe ndipo anapereka kwa Araunayo masekeli asiliva makumi asanu.
And the king said to Araunah, No, but I will truly buy it from thee at a price. Neither will I offer burnt offerings to Jehovah my God which cost me nothing. So David bought the threshing-floor and the oxen for fifty shekels of silver.
25 Davide anamanga guwa lansembe la Yehova pamenepo ndipo anaperekapo nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano. Ndipo Yehova anayankha pempherolo mʼmalo mwa dziko lonse, ndipo mliri unatha pa Aisraeli.
And David built there an altar to Jehovah, and offered burnt offerings and peace offerings. So Jehovah was entreated for the land, and the plague was halted from Israel.

< 2 Samueli 24 >