< 2 Samueli 23 >

1 Nawa mawu otsiriza a Davide: “Mawu a Davide mwana wa Yese, mawu a munthu amene wakwezedwa ndi Wammwambamwamba, munthu wodzozedwa ndi Mulungu wa Yakobo, woyimba nyimbo za Israeli:
Torej to so zadnje Davidove besede. Jesejev sin David je rekel in mož, ki je bil vzdignjen na visoko, maziljenec Jakobovega Boga in prijeten Izraelov psalmist, je rekel:
2 “Mzimu wa Yehova unayankhula kudzera mwa ine; mawu ake anali pakamwa panga.
» Gospodov Duh je govoril po meni in njegova beseda je bila na mojem jeziku.
3 Mulungu wa Israeli anayankhula, Thanthwe la Israeli linati kwa ine: ‘Pamene munthu alamulira anthu mwachilungamo, pamene alamulira moopa Mulungu,
Izraelov Bog je rekel: ›Izraelova skala mi je spregovorila: ›Kdor vlada nad ljudmi, mora biti pravičen, vladajoč v strahu Božjem.‹‹
4 amakhala ngati kuwala kwa mmamawa, mmawa wopanda mitambo, monga kuwala pamene mvula yaleka kugwa imene imameretsa udzu mʼnthaka.’
In on bo kakor svetloba jutra, ko vzhaja sonce, celó brezoblačno jutro, kakor nežna trava, ki poganja iz zemlje, s čistim sijanjem po dežju.
5 “Kodi banja langa silolungama pamaso pa Mulungu? Kodi Iye sanachite pangano losatha ndi ine, lokonzedwa ndi lotetezedwa mbali zonse? Kodi sadzakwaniritsa chipulumutso changa, ndi kundipatsa chokhumba changa chilichonse?
Čeprav moja hiša ni takšna z Bogom, vendar je z menoj sklenil večno zavezo, urejeno v vseh stvareh in zanesljivo. Kajti to je vsa moja rešitev duše in vsa moja želja, čeprav ji on ne daje rasti.
6 Koma anthu oyipa ndiwo ayenera kutayidwa kunja ngati minga, imene sitengedwa ndi manja.
Toda Beliálovi sinovi bodo vsi izmed njih kakor zavrženo trnje, ker ne morejo biti prijeti z rokami,
7 Aliyense amene wayikhudza mingayo amayidula pogwiritsa ntchito chigwandali kapena ndodo ya mkondo; nayitentha pa moto.”
toda človek, ki se jih bo dotaknil, mora biti ograjen z železom in palico sulice, in na istem kraju bodo popolnoma požgani z ognjem.«
8 Nawa mayina a ankhondo amphamvu a Davide: Yosebu-Basebeti wa ku Takemoni mkulu wa atsogoleri a ankhondo atatu. Iye anapha ndi mkondo ankhondo 800 nthawi imodzi.
To so imena mogočnih mož, ki jih je imel David: Tahkemoníjec, ki je sedel na sedežu, glavni izmed poveljnikov; enak je bil Ezničan Adino. Svojo sulico je vzdignil proti osemstotim, ki jih je enkrat pobil.
9 Wotsatana naye anali Eliezara mwana wa Dodo Mwahohi. Monga mmodzi mwa ankhondo atatu amphamvu a Davide, iye anali ndi Davide pamene anazunza Afilisti amene anasonkhana ku Pasi-Damimu kuchita nkhondo. Kenaka ankhondo a Israeli anabwerera mʼmbuyo.
Za njim je bil Eleazar, sin Dodója, Ahóahovca, z Davidom eden izmed treh mogočnih mož, ko so izzivali Filistejce, ki so bili tam skupaj zbrani za boj in Izraelovi možje so odšli proč.
10 Koma iye anayima osasuntha ndipo anakantha Afilisti mpaka mkono wake unatopa ndipo unakanirira ku lupanga lake. Yehova anapereka chigonjetso chachikulu pa tsiku limenelo. Asilikali anabwerera kwa Eliezara, kukatenga katundu wa anthu ophedwa.
Ta je vstal in udarjal Filistejce, dokler njegova roka ni bila izmučena in se je njegova roka trdno oklenila meča in Gospod je tisti dan izvršil veliko zmago in ljudstvo se je vrnilo za njim, [vendar] samo da plenijo.
11 Wotsatana naye anali Sama mwana wa Age Mharari. Pamene Afilisti anasonkhana pamalo pamene panali munda wa mphodza, ankhondo a Israeli anathawa Afilistiwo.
Za njim je bil Šamá, sin Hararéjca Agaja. Filistejci so bili skupaj zbrani v krdelo, kjer je bil kos polja poln leče in ljudstvo je pobegnilo pred Filistejci.
12 Koma Sama anayima pakati pa mundawo. Iye anawuteteza nakantha Afilistiwo ndipo Yehova anawapambanitsa koposa.
Toda on je stal na sredi polja in ga obranil in pobil Filistejce, in Gospod je izvršil veliko zmago.
13 Pa nthawi yokolola, atatu mwa atsogoleri makumi atatu anabwera kwa Davide ku phanga la Adulamu, pamene gulu la Afilisti linali litamanga misasa mʼchigwa cha Refaimu.
Trije izmed tridesetih vodij so odšli dol in prišli k Davidu v času žetve, k votlini Adulám, in krdelo Filistejcev je taborilo v dolini Rafájim.
14 Nthawi imeneyo Davide anali mu linga, ndipo boma la Afilisti linali ku Betelehemu.
David je bil takrat v utrdbi in garnizija Filistejcev je bila takrat v Betlehemu.
15 Davide analakalaka madzi ndipo anati, “Haa, pakanapezeka munthu wokanditungira madzi a mʼchitsime chomwe chili pafupi ndi chipata cha ku Betelehemu!”
David je hrepenel in rekel: »Oh, da bi mi nekdo dal piti od vode betlehemskega vodnjaka, ki je pri velikih vratih!«
16 Choncho anthu amphamvu atatuwa anadutsa mizere ya Afilisti, natunga madzi amene anali mʼchitsime chomwe chinali pafupi ndi chipata cha ku Betelehemu nabwera nawo kwa Davide. Koma iye anakana kumwa. Mʼmalo mwake anathira pansi pamaso pa Yehova.
Trije mogočni možje so predrli vojsko Filistejcev in zajeli vodo iz betlehemskega vodnjaka, ki je bil pri velikih vratih in jo vzeli ter jo prinesli k Davidu, pa vendar ni hotel piti od nje, temveč jo je izlil Gospodu.
17 Iye anati, “Inu Yehova, musalole kuti ine ndichite chinthu ichi! Kodi awa si magazi a anthu amene anayika miyoyo yawo pachiswe?” Ndipo Davide sanamwe madziwo. Zimenezi ndi zimene anachita anthu amphamvu atatuwo.
Rekel je: »Daleč naj bo od mene, oh Gospod, da bi to storil. Mar ni to kri mož, ki so šli v nevarnosti za svoja življenja?« Zato tega ni hotel piti. Te stvari so storili ti trije mogočni možje.
18 Abisai mʼbale wa Yowabu mwana wa Zeruya ndiye anali mtsogoleri wa anthu atatuwa. Iye anapha ndi mkondo ankhondo 300, choncho iyeyo anali wotchuka pakati pa anthu atatu aja.
Abišáj, Joábov brat, Cerújin sin, je bil vodja med tremi. Svojo sulico je dvignil proti tristotim in jih pobil in imel je ime med tremi.
19 Kodi iyeyo sanali wolemekezeka koposa? Iye anakhala mtsogoleri wawo ngakhale kuti sanali mʼgulu la anthu atatu aja.
Mar ni bil on najbolj častitljiv izmed treh? Zato je bil njihov poveljnik, vendar prvih treh ni dosegel.
20 Benaya mwana wa Yehoyada wa ku Kabizeeli anali munthu wolimba mtima amene anachita zinthu zamphamvu. Iye anakantha ankhondo awiri otchuka a ku Mowabu. Tsiku lina kukuzizira kwambiri, iye analowa mʼdzenje ndi kuphamo mkango.
Jojadájev sin Benajá, sin hrabrega moža iz Kabceéla, ki je storil mnogo dejanj, je usmrtil dva, levom podobna moža iz Moába. Odšel je tudi dol in ubil leva v sredi jame v času snega.
21 Ndipo iye anakanthanso Mwigupto wamkulu msinkhu. Ngakhale kuti Mwiguptoyo anali ndi mkondo mʼdzanja mwake, Benaya anapita kukamenyana naye ali ndi chibonga chokha mʼmanja. Iye analanda mkondo mʼdzanja la Mwiguptoyo ndi kumupha ndi mkondo wake womwe.
Ubil je Egipčana, čednega moža. Egipčan je imel v svoji roki sulico, toda dol k njemu je šel s palico in iztrgal sulico iz Egipčanove roke in ga ubil z njegovo lastno sulico.
22 Izi ndi zamphamvu zimene Benaya mwana wa Yehoyada anachita. Iyeyo analinso wotchuka ngati anthu atatu amphamvu aja.
Te stvari je storil Jojadájev sin Benajá in imel je ime med tremi mogočnimi možmi.
23 Iye ankalemekezedwa kuposa wina aliyense mwa anthu makumi atatu aja, koma sanali mʼgulu la anthu atatu aja. Ndipo Davide anamuyika kukhala woyangʼanira asilikali omuteteza.
Bil je častitljivejši od tridesetih, vendar prvih treh ni dosegel. In David ga je postavil nad svojo stražo.
24 Mʼgulu la anthu makumi atatu aja munalinso awa: Asaheli mʼbale wa Yowabu, Elihanani mwana wa Dodo wa ku Betelehemu,
Joábov brat Asaél je bil eden izmed tridesetih: Dodójev sin Elhanán iz Betlehema,
25 Sama Mharodi, Elika Mherodi,
Haródec Šamá, Haródec Eliká,
26 Helezi Mpaliti, Ira mwana wa Ikesi wa ku Tekowa,
Paltičan Helec, Irá, sin Tekójčana Ikéša,
27 Abiezeri wa ku Anatoti, Sibekai Mhusati,
Anatóčan Abiézer, Hušán Mebunáj,
28 Zalimoni Mwahohi, Maharai Mnetofa,
Ahóahovec Calmón, Netófčan Mahráj,
29 Heledi mwana wa Baana Mnetofa, Itai mwana wa Ribai wa ku Gibeya ku Benjamini,
Heleb, sin Netófčana Baanája, Ribájev sin Itáj iz Gíbee Benjaminovih otrok,
30 Benaya Mpiratoni, Hidayi wa ku zigwa za Gaasi.
Piratónec Benajá, Hidáj iz Gáaševih potokov,
31 Abi-Aliboni Mwaribati, Azimaveti Mbarihumi,
Arbatéjec Abialbón, Barhuméjec Azmávet,
32 Eliyahiba Msaaliboni, ana a Yaseni, Yonatani,
Šaalbónec Eljahbá, izmed Jašénovih sinov Jonatan,
33 mwana wa Sama Mharari, Ahiamu mwana wa Sarari Mharari,
Hararéjec Šamá, Ahiám, sin Hararéjca Šarárja,
34 Elifeleti mwana wa Ahasibai Mmaakati, Eliamu mwana wa Ahitofele Mgiloni,
Elifélet, sin Ahasbája, sin Maahčána, Eliám, sin Gilčana Ahitófela,
35 Heziro wa ku Karimeli, Paarai Mwaribi,
Karmélčan Hecrai, Arbéjec Paarai,
36 Igala mwana wa Natani wa ku Zoba, mwana wa Hagiri,
Natánov sin Jigál iz Cobe, Gádovec Baní,
37 Zeleki Mwamoni, Naharai wa ku Beeroti, mnyamata wonyamula zida za Yowabu mwana wa Zeruya,
Amónec Celek, Beeróčan Nahráj, nosilec bojne opreme Cerújinega sina Joába,
38 Ira Mwitiri, Garebu Mwitiri,
Jéterjevec Irá, Jéterjevec Garéb,
39 ndi Uriya Mhiti. Onse pamodzi analipo 37.
Hetejec Urijá; skupaj sedemintrideset.

< 2 Samueli 23 >