< 2 Samueli 22 >

1 Davide anayimbira Yehova nyimbo iyi pamene Yehovayo anamupulumutsa mʼdzanja la adani ake onse ndiponso mʼdzanja la Sauli.
E falou David ao Senhor as palavras deste cântico, no dia em que o Senhor o livrou das mãos de todos os seus inimigos e das mãos de Saul.
2 Iye anati, “Yehova ndiye thanthwe langa, chitetezo changa ndi mpulumutsi wanga.
Disse pois: O Senhor é o meu rochedo, e o meu lugar forte, e o meu libertador.
3 Mulungu wanga ndiye thanthwe langa, mʼmene ndimathawiramo, chishango changa ndi ndodo yachipulumutso changa. Iye ndi linga langa, pothawirapo panga ndi mpulumutsi wanga. Munandipulumutsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
Deus é o meu rochedo, nele confiarei: o meu escudo, e a força da minha salvação, o meu alto retiro, e o meu refúgio. O meu Salvador, de violência me salvaste.
4 “Ndimayitana Yehova amene ndi woyenera matamando, ndipo ndapulumutsidwa kwa adani anga.
O Senhor, digno de louvor, invoquei, e de meus inimigos fiquei livre.
5 “Mafunde a imfa anandizinga; mitsinje yothamanga yachiwonongeko inandiopsa kwambiri.
Porque me cercaram as ondas de morte: as torrentes de Belial me assombraram.
6 Anandimanga ndi zingwe za ku manda; misampha ya imfa inalimbana nane. (Sheol h7585)
Cordas do inferno me cingiram; encontraram-me laços de morte. (Sheol h7585)
7 “Mʼmasautso anga ndinapemphera kwa Yehova; ndinapemphera kwa Mulungu wanga. Iye ali mʼnyumba yake, anamva mawu anga; kulira kwanga kunafika mʼmakutu ake.
Estando em angústia, invoquei ao Senhor, e a meu Deus clamei: do seu templo ouviu ele a minha voz, e o meu clamor chegou aos seus ouvidos.
8 “Dziko lapansi linanjenjemera ndi kuchita chivomerezi, maziko a miyamba anagwedezeka; ananjenjemera chifukwa Iye anakwiya.
Então se abalou e tremeu a terra, os fundamentos dos céus se moveram e abalaram, porque ele se irou.
9 Mʼmphuno mwake munatuluka utsi; moto wonyeketsa unatuluka mʼkamwa mwake, makala amoto anali lawilawi mʼkamwa mwake.
Subiu o fumo de seus narizes, e da sua boca um fogo devorador: carvões se incenderam dele.
10 Iye anangʼamba thambo natsika pansi; pansi pa mapazi ake panali mitambo yakuda.
E abaixou os céus, e desceu: e uma escuridão havia debaixo de seus pés.
11 Iye anakwera pa Kerubi ndi kuwuluka; nawuluka ndi mphepo mwaliwiro.
E subiu sobre um cherubim, e voou: e foi visto sobre as asas do vento.
12 Iye anapanga mdima kukhala chofunda chake, mitambo yakuda ya mlengalenga.
E por tendas pôs as trevas ao redor de si: ajuntamento de águas, nuvens dos céus.
13 Mʼkuwala kumene kunali pamaso pake munkachokera makala amoto alawilawi.
Pelo resplendor da sua presença brasas de fogo se accendem.
14 Yehova anabangula kumwamba ngati bingu, mawu a Wammwambamwamba anamveka ponseponse.
Trovejou desde os céus o Senhor: e o altíssimo fez soar a sua voz.
15 Iye anaponya mivi yake, nabalalitsa adani ake, ndi zingʼaningʼani zake anawagonjetsa.
E disparou flechas, e os dissipou: raios e os perturbou.
16 Zigwa za mʼnyanja zinaonekera poyera, ndipo maziko a dziko lapansi anakhala poyera, Yehova atabangula mwaukali, pamene mpweya wamphamvu unatuluka mʼmphuno mwake.
E apareceram as profundezas do mar, os fundamentos do mundo se descobriram: pela repreensão do Senhor, pelo sopro do vento dos seus narizes.
17 “Ali kumwamba, Iye anatambalitsa dzanja lake ndipo anandigwira; anandivuwula mʼmadzi ozama.
Desde o alto enviou, e me tomou: tirou-me das muitas águas.
18 Anandipulumutsa kwa mdani wanga wamphamvu, adani anga amene anali amphamvu kuposa ine.
Livrou-me do meu possante inimigo, e daqueles que me tinham ódio, porque eram mais fortes do que eu.
19 Adaniwo analimbana nane pamene ndinali pa mavuto, koma Yehova anali thandizo langa.
Encontraram-me no dia da minha calamidade: porém o Senhor se fez o meu esteio.
20 Iye anandipititsa kumalo otakasuka; anandipulumutsa chifukwa amakondwera nane.
E tirou-me à largura, e arrebatou-me dali; porque tinha prazer em mim.
21 “Yehova wandithandiza molingana ndi chilungamo changa; molingana ndi makhalidwe anga abwino, Iye wandipulumutsa.
Recompensou-me o Senhor conforme à minha justiça: conforme à pureza de minhas mãos me retribuiu.
22 Pakuti ine ndinatsata njira za Yehova; ndilibe mlandu wochoka pamaso pa Mulungu wanga.
Porque guardei os caminhos do Senhor: e não me apartei impiamente do meu Deus.
23 Malamulo ake onse ali pamaso panga, sindinasiye malangizo ake.
Porque todos os seus juízos estavam diante de mim: e de seus estatutos me não desviei.
24 Ndakhala moyo wosalakwa pamaso pake ndipo ndakhala ndi kupewa tchimo.
Porém fui sincero perante ele: e guardei-me da minha iniquidade.
25 Yehova wandipatsa mphotho molingana ndi chilungamo changa, molingana ndi makhalidwe anga abwino pamaso pake.
E me retribuiu o Senhor conforme à minha justiça, conforme à minha pureza diante dos seus olhos.
26 “Kwa wokhulupirika, Inu mumaonetsa kukhulupirika kwanu, kwa anthu amakhalidwe abwino, Inu mumaonetsanso makhalidwe abwino,
Com o benigno te mostras benigno: com o varão sincero te mostras sincero.
27 Kwa woyera mtima, Inu mumaonetsa kuyera mtima kwanu, koma kwa anthu achinyengo mumaonetsanso kunyansidwa nawo.
Com o puro te mostras puro: mas com o perverso te mostras avesso.
28 Inu mumapulumutsa anthu odzichepetsa, koma maso anu amatsutsana ndi odzikuza ndipo mumawatsitsa.
E o povo aflito livras: mas teus olhos são contra os altivos, e tu os abaterás.
29 Inu Yehova, ndinu nyale yanga; Yehova wasandutsa mdima wanga kukhala kuwunika.
Porque tu, Senhor, és a minha candeia: e o Senhor esclarece as minhas trevas.
30 Ndi thandizo lanu nditha kulimbana ndi gulu la ankhondo, ndi Mulungu wanga nditha kuchita zosatheka ndi munthu.
Porque contigo passo pelo meio dum esquadrão: pelo meu Deus salto um muro.
31 “Kunena za Mulungu, zochita zake ndi zangwiro; mawu a Yehova alibe cholakwika. Iye ndi chishango kwa onse amene amathawira kwa iye.
O caminho de Deus é perfeito, e a palavra do Senhor refinada; e é o escudo de todos os que nele confiam.
32 Mulungu wina ndi uti wofanana nanu Yehova? Ndipo ndani amene ndi Thanthwe kupatula Mulungu wathu?
Porque, quem é Deus, senão o Senhor? e quem é rochedo, senão o nosso Deus?
33 Ndi Mulungu amene anandipatsa mphamvu ndi kulungamitsa njira yanga.
Deus é a minha fortaleza e a minha força, e ele perfeitamente desembaraça o meu caminho.
34 Iye amasandutsa mapazi anga kukhala ngati ambawala yayikazi; Iye amandithandiza kuyimirira pamwamba pa mapiri.
Faz ele os meus pés como os das cervas, e me põe sobre as minhas alturas.
35 Iye amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo; manja anga amatha kuthyola uta wachitsulo.
Instrui as minhas mãos para a peleja, de maneira que um arco de cobre se quebra pelos meus braços.
36 Inu mundipatsa ine chishango chanu cha chigonjetso; mumawerama kuti mundikweze.
Também me deste o escudo da tua salvação, e pela tua brandura me vieste a engrandecer.
37 Inu mwalimbitsa njira yanga kuti ndiyende bwino, kuti mapazi anga asaterereke.
Alargaste os meus passos debaixo de mim, e não vacilaram os meus artelhos.
38 “Ine ndinathamangitsa adani anga ndi kuwakantha; sindinabwerere mpaka iwo atawonongedwa.
Persegui os meus inimigos, e os derrotei, e nunca me tornei até que os consumisse.
39 Ndinawakantha kotheratu, ndipo sanathe kudzukanso; Iwo anagwera pansi pa mapazi anga.
E os consumi, e os atravessei, de modo que nunca mais se levantaram, mas cairam debaixo dos meus pés.
40 Inu munandipatsa ine mphamvu yochitira nkhondo; munagwaditsa adani anga pa mapazi anga.
Porque me cingiste de força para a peleja, fizeste abater-se debaixo de mim os que se levantaram contra mim.
41 Inu muchititsa kuti adani anga atembenuke ndi kuthawa; ndipo ndinawononga adani anga.
E deste-me o pescoço de meus inimigos, daqueles que me tinham ódio, e os destruí.
42 Iwo anafuwula kupempha thandizo, koma panalibe ndi mmodzi yemwe owapulumutsa. Analirira kwa Yehova, koma sanawayankhe.
Olharam, porém não houve libertador: sim, para o Senhor, porém não lhes respondeu.
43 Ine ndinawaperesa ngati fumbi la pa dziko lapansi; ndinawasinja ndipo ndinawapondaponda ngati matope a mʼmisewu.
Então os moí como o pó da terra; como a lama das ruas os trilhei e dissipei.
44 “Inu mwandipulumutsa mʼmanja mwa mitundu ya anthu; Inu mwandisunga kuti ndikhale mtsogoleri wa anthu a mitundu ina. Anthu amene sindikuwadziwa ali pansi pa ulamuliro wanga.
Também me livraste das contendas do meu povo; guardaste-me para cabeça das nações; o povo que não conhecia me servirá.
45 Alendo amadzipereka okha pamaso panga; akangomva za ine, amandigonjera.
Os filhos de estranhos se me sujeitaram; ouvindo a minha voz, me obedeceram.
46 Iwo onse anataya mtima; anatuluka mʼmalinga awo akunjenjemera.
Os filhos de estranhos descairam; e, cingindo-se, sairam dos seus encerramentos.
47 “Yehova ndi wamoyo! Litamandidwe Thanthwe langa. Akuzike Mulungu, Thanthwe, Mpulumutsi wanga!
Vive o Senhor, e bendito seja o meu rochedo; e exaltado seja Deus, a rocha da minha salvação:
48 Iye ndi Mulungu amene amabwezera chilango, amene amayika anthu a mitundu yonse pansi pa ulamuliro wanga,
O Deus que me dá inteira vingança, e sujeita os povos debaixo de mim.
49 amene amandimasula mʼmanja mwa adani anga. Inu munandikuza kuposa adani anga; munandilanditsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
E o que me tira dentre os meus inimigos: e tu me exaltas sobre os que contra mim se levantam; do homem violento me livras.
50 Choncho ine ndidzakutamandani Inu Yehova, pakati pa anthu a mitundu ina; ndidzayimba nyimbo zotamanda dzina lanu.
Por isso, ó Senhor, te louvarei entre as gentes, e entoarei louvores ao teu nome.
51 “Iye amapereka chipambano chachikulu kwa mfumu yake, amaonetsa kukoma mtima kwa wodzozedwa wake, kwa Davide ndi zidzukulu zake kwamuyaya.”
Ele é a torre das salvações do seu rei, e usa de benignidade com o seu ungido, com David, e com a sua semente para sempre.

< 2 Samueli 22 >