< 2 Samueli 22 >

1 Davide anayimbira Yehova nyimbo iyi pamene Yehovayo anamupulumutsa mʼdzanja la adani ake onse ndiponso mʼdzanja la Sauli.
Ke LEUM GOD El molella David liki inpaol Saul ac mwet lokoalok pac saya, na David el onkakin on soko inge nu sin LEUM GOD:
2 Iye anati, “Yehova ndiye thanthwe langa, chitetezo changa ndi mpulumutsi wanga.
LEUM GOD El eot ku luk, nien wikla luk, Ac Mwet Lango luk.
3 Mulungu wanga ndiye thanthwe langa, mʼmene ndimathawiramo, chishango changa ndi ndodo yachipulumutso changa. Iye ndi linga langa, pothawirapo panga ndi mpulumutsi wanga. Munandipulumutsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
God luk El mwe loang luk, Ke nga muta yorol nga inse misla. El loangeyu oana sie mwe loeyuk; El lain mwet lokoalok luk ac ase misla nu sik. El mwet lango luk; El loangeyu ac moliyula liki mwe lokoalok.
4 “Ndimayitana Yehova amene ndi woyenera matamando, ndipo ndapulumutsidwa kwa adani anga.
Nga pang nu sin LEUM GOD, Ac El moliyula liki mwet lokoalok luk. Kaksakin LEUM GOD!
5 “Mafunde a imfa anandizinga; mitsinje yothamanga yachiwonongeko inandiopsa kwambiri.
Noa lun misa apinyula; Noa lun kunausten toki nu fuk.
6 Anandimanga ndi zingwe za ku manda; misampha ya imfa inalimbana nane. (Sheol h7585)
Mwe kapir lun misa srumasryula, Ac kulyuk akola in sruokyuwi. (Sheol h7585)
7 “Mʼmasautso anga ndinapemphera kwa Yehova; ndinapemphera kwa Mulungu wanga. Iye ali mʼnyumba yake, anamva mawu anga; kulira kwanga kunafika mʼmakutu ake.
In keok luk, nga pang nu sin LEUM GOD; Nga pang nu sin God luk tuh Elan kasreyu. In tempul lal el lohng pusrek; El porongo ke nga pang Elan kasreyu.
8 “Dziko lapansi linanjenjemera ndi kuchita chivomerezi, maziko a miyamba anagwedezeka; ananjenjemera chifukwa Iye anakwiya.
Na faclu rarrar ac usrusryak; Pwelung yen engyeng uh mukuikui ac kusrusrsrusr Mweyen God El kasrkusrak!
9 Mʼmphuno mwake munatuluka utsi; moto wonyeketsa unatuluka mʼkamwa mwake, makala amoto anali lawilawi mʼkamwa mwake.
Kulasr fofosryak liki infwacl, Sie e in kunausten ac mulut fol sikyak liki oalul.
10 Iye anangʼamba thambo natsika pansi; pansi pa mapazi ake panali mitambo yakuda.
El seya acn lucng ac tufoki, Wi sie pukunyeng lohsr ye nial.
11 Iye anakwera pa Kerubi ndi kuwuluka; nawuluka ndi mphepo mwaliwiro.
El sohksok mui fin cherub; El pwesroul ke poun eng uh.
12 Iye anapanga mdima kukhala chofunda chake, mitambo yakuda ya mlengalenga.
El nokmulla ke lohsr; Pukunyeng matoltol sessesla ke kof raunella.
13 Mʼkuwala kumene kunali pamaso pake munkachokera makala amoto alawilawi.
Mulut fol firiryak liki sarom su oan ye mutal.
14 Yehova anabangula kumwamba ngati bingu, mawu a Wammwambamwamba anamveka ponseponse.
Na LEUM GOD El ngirngir yen engyengu me, Ac pusren God Kulana lohngyuk.
15 Iye anaponya mivi yake, nabalalitsa adani ake, ndi zingʼaningʼani zake anawagonjetsa.
El pisrik pisr natul, ac mwet lokoalok lal fahsrelik; Ke kalmelik lun sarom El oru elos kaingelik.
16 Zigwa za mʼnyanja zinaonekera poyera, ndipo maziko a dziko lapansi anakhala poyera, Yehova atabangula mwaukali, pamene mpweya wamphamvu unatuluka mʼmphuno mwake.
Ke LEUM GOD El kai mwet lokoalok lal Ac ngirla nu selos ke kasrkusrak, Acn loal in meoa wanginla koano, Ac pwelung lun faclu ikakelik.
17 “Ali kumwamba, Iye anatambalitsa dzanja lake ndipo anandigwira; anandivuwula mʼmadzi ozama.
LEUM GOD El saplaki lucng me ac sruokyuwi; El amakinyuyak liki inkof loal.
18 Anandipulumutsa kwa mdani wanga wamphamvu, adani anga amene anali amphamvu kuposa ine.
El moliyula liki mwet lokoalok kulana luk, Ac liki elos nukewa su srungayu. Elos arulana ku likiyu.
19 Adaniwo analimbana nane pamene ndinali pa mavuto, koma Yehova anali thandizo langa.
Ke nga muta in mwe ongoiya, elos lainyu, Tusruktu LEUM GOD El loangeyula.
20 Iye anandipititsa kumalo otakasuka; anandipulumutsa chifukwa amakondwera nane.
El kasreyu ac srukyuyak liki mwe fosrnga; El moliyula mweyen el insewowo sik.
21 “Yehova wandithandiza molingana ndi chilungamo changa; molingana ndi makhalidwe anga abwino, Iye wandipulumutsa.
LEUM GOD El ase lacnen orekma suwohs luk; El akinsewowoyeyu mweyen wangin ma koluk luk.
22 Pakuti ine ndinatsata njira za Yehova; ndilibe mlandu wochoka pamaso pa Mulungu wanga.
Nga akos na ma sap lun LEUM GOD; Nga tiana forla liki God luk.
23 Malamulo ake onse ali pamaso panga, sindinasiye malangizo ake.
Nga karinganang ma sap lal nukewa, Nga tia seakos ma El sapkin.
24 Ndakhala moyo wosalakwa pamaso pake ndipo ndakhala ndi kupewa tchimo.
El etu lah wangin ma sutuu luk, Ac nga sifacna liyeyuyang tuh nga in tia oru ma koluk.
25 Yehova wandipatsa mphotho molingana ndi chilungamo changa, molingana ndi makhalidwe anga abwino pamaso pake.
Ouinge El ase mwe mol nu sik mweyen nga oru ma suwohs, Mweyen El etu lah wangin mwetik.
26 “Kwa wokhulupirika, Inu mumaonetsa kukhulupirika kwanu, kwa anthu amakhalidwe abwino, Inu mumaonetsanso makhalidwe abwino,
O LEUM GOD, kom oaru nu selos su oaru nu sum, Ac kom arulana wo nu selos su moul suwohs.
27 Kwa woyera mtima, Inu mumaonetsa kuyera mtima kwanu, koma kwa anthu achinyengo mumaonetsanso kunyansidwa nawo.
Kom nasnas nu selos su nasnas, A kom kwaselos su koluk.
28 Inu mumapulumutsa anthu odzichepetsa, koma maso anu amatsutsana ndi odzikuza ndipo mumawatsitsa.
Kom molelos su inse pusisel, A kom akpusiselyalos su inse fulat.
29 Inu Yehova, ndinu nyale yanga; Yehova wasandutsa mdima wanga kukhala kuwunika.
LEUM GOD, kom kalem luk; Kom sisla lohsr likiyu.
30 Ndi thandizo lanu nditha kulimbana ndi gulu la ankhondo, ndi Mulungu wanga nditha kuchita zosatheka ndi munthu.
Kom akkeyeyu tuh nga in lain mwet lokoalok luk Ac ase ku nu sik in kutangla loang lalos.
31 “Kunena za Mulungu, zochita zake ndi zangwiro; mawu a Yehova alibe cholakwika. Iye ndi chishango kwa onse amene amathawira kwa iye.
Suwoswoslana orekma lun God se inge, Kas lal arulana pwaye ac fal in lulalfongiyuk! El oana sie mwe loang Nu sin mwet nukewa su suk molela sel.
32 Mulungu wina ndi uti wofanana nanu Yehova? Ndipo ndani amene ndi Thanthwe kupatula Mulungu wathu?
LEUM GOD mukena El God; God mukena El mwe loang lasr.
33 Ndi Mulungu amene anandipatsa mphamvu ndi kulungamitsa njira yanga.
God se inge El nien molela ku luk; El oru inkanek luk in misla ac wo.
34 Iye amasandutsa mapazi anga kukhala ngati ambawala yayikazi; Iye amandithandiza kuyimirira pamwamba pa mapiri.
El akkeye niuk in suwohs oana soko deer; El karinginyu fineol uh.
35 Iye amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo; manja anga amatha kuthyola uta wachitsulo.
El akpahyeyu nu ke mweun Tuh nga in ku in orekmakin mwe pisr kulana.
36 Inu mundipatsa ine chishango chanu cha chigonjetso; mumawerama kuti mundikweze.
O LEUM GOD, kom karinginyu ac moliyula; Kasru lom oru nga in pwengpeng.
37 Inu mwalimbitsa njira yanga kuti ndiyende bwino, kuti mapazi anga asaterereke.
Kom karinginyu tuh nga in tia sruoh, Ac nga soenna ikori.
38 “Ine ndinathamangitsa adani anga ndi kuwakantha; sindinabwerere mpaka iwo atawonongedwa.
Nga ukwe mwet lokoalok luk ac kutangulosla; Nga tia tui nwe ke na nga kunauselosla.
39 Ndinawakantha kotheratu, ndipo sanathe kudzukanso; Iwo anagwera pansi pa mapazi anga.
Nga srunglulosi, ac elos tia ku in tuyak; Elos kutangyukla oan ye mutuk.
40 Inu munandipatsa ine mphamvu yochitira nkhondo; munagwaditsa adani anga pa mapazi anga.
Kom akkeyeyu nu ke mweun Ac ase kutangla fin mwet lokoalok luk.
41 Inu muchititsa kuti adani anga atembenuke ndi kuthawa; ndipo ndinawononga adani anga.
Kom oru mwet lokoalok luk in kaing likiyu; Nga kunauselosla su srungayu.
42 Iwo anafuwula kupempha thandizo, koma panalibe ndi mmodzi yemwe owapulumutsa. Analirira kwa Yehova, koma sanawayankhe.
Elos suk mwet in kasrelos, a wangin mwet molelosla; Elos pang nu sin LEUM GOD, a El tiana topuk.
43 Ine ndinawaperesa ngati fumbi la pa dziko lapansi; ndinawasinja ndipo ndinawapondaponda ngati matope a mʼmisewu.
Nga toanelosi, ac elos ekla oana kutkut; Nga itungulosi oana fohk furarrar inkanek uh.
44 “Inu mwandipulumutsa mʼmanja mwa mitundu ya anthu; Inu mwandisunga kuti ndikhale mtsogoleri wa anthu a mitundu ina. Anthu amene sindikuwadziwa ali pansi pa ulamuliro wanga.
Kom moliyula liki mwet alein nu sik, Ac oakiya tuh nga in leum fin mutunfacl uh; Mwet ma nga tia etu, inge elos orekma nu sik.
45 Alendo amadzipereka okha pamaso panga; akangomva za ine, amandigonjera.
Mwetsac elos srim ye mutuk; Ke elos lohng pusrek, elos akos.
46 Iwo onse anataya mtima; anatuluka mʼmalinga awo akunjenjemera.
Pulaik lalos wanginla Ac elos rarrar ke elos tuku liki pot ku lalos.
47 “Yehova ndi wamoyo! Litamandidwe Thanthwe langa. Akuzike Mulungu, Thanthwe, Mpulumutsi wanga!
LEUM GOD El moul! Kaksakin El su nien molela luk! Fahkelik pwengpeng lun God ku su moliyula!
48 Iye ndi Mulungu amene amabwezera chilango, amene amayika anthu a mitundu yonse pansi pa ulamuliro wanga,
El ase kutangla fin mwet lokoalok luk; El akpusiselye mutunfacl su muta ye kolyuk luk
49 amene amandimasula mʼmanja mwa adani anga. Inu munandikuza kuposa adani anga; munandilanditsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
Ac moliyula liki mwet lokoalok luk. O LEUM GOD, kom ase kutangla fin mwet lokoalok luk Ac liyeyuyang liki mwet sulallal.
50 Choncho ine ndidzakutamandani Inu Yehova, pakati pa anthu a mitundu ina; ndidzayimba nyimbo zotamanda dzina lanu.
Ouinge nga kaksakin kom inmasrlon mutunfacl uh; Nga onkakin on in kaksak nu sum.
51 “Iye amapereka chipambano chachikulu kwa mfumu yake, amaonetsa kukoma mtima kwa wodzozedwa wake, kwa Davide ndi zidzukulu zake kwamuyaya.”
God El sang kutangla lulap nu sin tokosra lal; El akkalemye lungse kawil lal nu sel su el sulela, Aok, nu sel David ac fita lal ma pahtpat.

< 2 Samueli 22 >