< 2 Samueli 20 >

1 Ndipo munthu wina wokonda kuyambitsa chisokonezo, dzina lake Seba, mwana wa Bikiri wa fuko la Benjamini, anali komweko. Iye analiza lipenga ndipo anafuwula kuti, “Ife tilibe chathu mu mfumu wa Davide, tilibe gawo mwa mwana wa Yese! Inu Aisraeli aliyense apite ku nyumba kwake!”
Kwasekusenzakala ukuthi kube khona lapho umuntu kaBheliyali, obizo lakhe linguShebha indodana kaBikiri umBhenjamini; wasevuthela uphondo wathi: Kasilasabelo kuDavida, kasilalifa endodaneni kaJese; wonke umuntu emathenteni akhe, Israyeli!
2 Kotero Aisraeli onse anamuthawa Davide ndipo anatsatira Seba mwana wa Bikiri. Koma anthu a ku Yuda anakhala ndi mfumu yawo njira yonse kuchokera ku Yorodani mpaka ku Yerusalemu.
Ngakho wonke umuntu wakoIsrayeli wenyuka wasuka emva kukaDavida, elandela uShebha indodana kaBikiri; kodwa abantu bakoJuda banamathela enkosini yabo, kusukela eJordani kwaze kwaba seJerusalema.
3 Davide atabwerera ku nyumba yake yaufumu ku Yerusalemu, iye anatenga azikazi khumi aja amene anawasiya kuti aziyangʼanira nyumba yaufumu, ndipo anawayika mʼnyumba imene anayikapo mlonda. Iye ankawadyetsa koma sanagone nawonso. Anasungidwa kwa okha mpaka tsiku la kufa kwawo ndipo anakhala ngati akazi amasiye.
UDavida wasefika endlini yakhe eJerusalema; inkosi yathatha abafazi abalitshumi, abafazi abancane, eyayibatshiye ukuze balinde indlu, yababeka endlini elindiweyo, yabanika ukudla, kodwa kayingenanga kubo. Basebevalelwa kwaze kwaba lusuku lokufa kwabo, bephila ebufelokazini.
4 Kenaka mfumu inati kwa Amasa, “Itanitsa ankhondo a Yuda kuti abwere kwa ine pasanathe masiku atatu, ndipo iwe udzakhale nawo.”
Inkosi yasisithi kuAmasa: Biza abantu bakoJuda babuthane kimi ngensuku ezintathu, lawe ube khona lapha.
5 Motero Amasa anakayitana Ayuda, koma anachedwa, napitirira pa nthawi imene mfumu inamuyikira.
UAmasa wasehamba ukubuthanisa uJuda, kodwa waphuza phezu kwesikhathi esimisiweyo ayemmisele sona.
6 Davide anati kwa Abisai, “Tsono Seba mwana wa Bikiri adzatipweteka kuposa momwe Abisalomu anatichitira. Tenga asilikali a mbuye wako ndipo umuthamangitse, mwina adzapeza mizinda yotetezedwa ndi kutithawa ife.”
UDavida wasesithi kuAbishayi: Khathesi uShebha indodana kaBikiri uzasenzela okubi okwedlula uAbisalomu; wena thatha inceku zenkosi yakho, uxotshane laye, hlezi azitholele imizi ebiyelwe ngemithangala, asiphunyuke.
7 Kotero anthu a Yowabu, Akereti ndi Apeleti ndiponso asilikali onse amphamvu anapita motsogozedwa ndi Abisai. Iwo anayenda kuchokera ku Yerusalemu kuthamangitsa Seba mwana wa Bikiri.
Kwasekuphuma emva kwakhe amadoda kaJowabi lamaKerethi lamaPelethi lamaqhawe wonke, basebephuma eJerusalema ukuxotshana loShebha indodana kaBikiri.
8 Ali pa mwala waukulu wa ku Gibiyoni, Amasa anabwera kudzakumana nawo. Yowabu anali atavala chovala chausilikali ndipo pamwamba pa malayawo, mʼchiwuno mwake anavala lamba womangirirapo lupanga lili moyikamo mwakemo. Akuyenda linasololoka kuchoka moyikamo mwake.
Sebeselitsheni elikhulu eliseGibeyoni, uAmasa weza phambi kwabo. UJowabi wayebhince isigqoko ayesigqokile, laphezu kwaso kulebhanti elilenkemba ebotshelwe ekhalweni lwakhe isesikhwameni sayo; esaqhubeka inkemba yawa.
9 Yowabu anati kwa Amasa, “Kodi uli bwanji mʼbale wanga?” Kenaka Yowabu anamugwira ndevu Amasa uja ndi dzanja lake lamanja ndi kupsompsona.
UJowabi wasesithi kuAmasa: Uyaphila yini, mfowethu? UJowabi wasebamba uAmasa ngesilevu ngesandla sokunene ukuze amange.
10 Amasa sanayangʼanitsitse lupanga limene linali mʼdzanja la Yowabu, ndipo Yowabu anamubaya nalo mʼmimba ndipo matumbo ake anatuluka ndi kugwera pansi. Popanda kubayanso kachiwiri, Amasa anafa. Ndipo Yowabu ndi mʼbale wake Abisai anathamangitsa Seba mwana wa Bikiri.
Kodwa uAmasa wayengayinanzeleli inkemba eyayisesandleni sikaJowabi; wasemtshaya ngayo kubambo lwesihlanu, wathululela imibilini yakhe emhlabathini, kamphindanga, wafa. UJowabi loAbishayi umfowabo basebexotshana loShebha indodana kaBikiri.
11 Mmodzi mwa ankhondo a Yowabu anakayimirira pafupi ndi mtembo wa Amasa ndipo anati, “Aliyense amene amakonda Yowabu ndi aliyense amene ali wa Davide, atsatire Yowabu!”
Omunye wamajaha kaJowabi wema phansi kwakhe, wathi: Omthandayo uJowabi, longokaDavida, landela uJowabi.
12 Amasa anagona pakati pa msewu atasamba magazi ake, ndipo munthuyo anaona kuti asilikali onse amayima pamenepo. Atazindikira kuti aliyense amene ankafika pamene panali Amasa amayima, iye anamuchotsa mu msewu ndi kumukokera mʼmunda ndipo anamuphimba ndi nsalu.
UAmasa wasegiqika egazini phakathi komgwaqo omkhulu. Lapho lowomuntu ebona ukuthi bonke abantu bayema, wamsusa uAmasa emgwaqweni omkhulu wamusa egangeni, waphosela isembatho phezu kwakhe, lapho ebona ukuthi wonke ofika ngakuye wema.
13 Amasa atachotsedwa pa msewu anthu onse anapita ndi Yowabu kuthamangitsa Seba mwana wa Bikiri.
Esesusiwe emgwaqweni omkhulu, bonke abantu badlula bamlandela uJowabi ukuze baxotshane loShebha indodana kaBikiri.
14 Seba anadutsa mafuko onse a Israeli mpaka ku Abeli ndi Beti-Maaka ndiponso chigawo chonse cha Abeli, amene anasonkhana pamodzi ndi kumutsata iye.
Wasedabula kuzo zonke izizwe zakoIsrayeli, waya eAbeli ngitsho iBeti-Mahaka, lawo wonke amaBeri; basebebuthana bamlandela labo.
15 Ankhondo onse pamodzi ndi Yowabu anafika ndi kumuzungulira Seba mu Abeli-Beti-Maaka. Iwo anapanga mzere wa nkhondo mpaka ku mzinda, ndipo unayangʼanana ndi malo otetezera a kunja. Pamene amalimbana ndi khoma kuti aligwetse,
Basebefika, bamgombolozela eAbeli-Beti-Mahaka; babuthelela idundulu maqondana lomuzi, lema emthangaleni; bonke abantu ababeloJowabi basebewona umduli ukuwuwisela phansi.
16 mayi wina wanzeru anafuwula kuchokera mu mzindawo, “Tamverani! Tamverani! Muwuzeni Yowabu abwere pano kuti ndiyankhule naye.”
Kwasekumemeza owesifazana ohlakaniphileyo phakathi komuzi wathi: Zwanini, zwanini! Ake lithi kuJowabi: Sondela lapha, ukuze ngikhulume lawe.
17 Yowabu anayandikira kumene kunali mayiyo, ndipo iye anafunsa kuti, “Kodi ndinu Yowabu?” Iye anayankha kuti, “Ndine.” Mayiyo anati, “Tamverani zimene mtumiki wanu akuti anene.” Yowabu anayankha kuti, “Ndikumvetsera.”
Esesondele kuye, owesifazana wathi: Nguwe uJowabi yini? Yena wathi: Nginguye. Wasesithi kuye: Zwana amazwi encekukazi yakho. Wasesithi: Ngiyezwa.
18 Iye anapitiriza kunena kuti, “Kalekale ankanena kuti, ‘Kapeze yankho lako ku Abeli,’ ndipo nkhani imathera pamenepo.
Wasekhuluma esithi: Endulo babejwayele ukukhuluma besithi: Kababuze lokubuza eAbeli; basebeqeda ngokunjalo.
19 Ife ndife anthu a mtendere ndi okhulupirika mu Israeli. Inu mukufuna kuwononga mzinda umene ndi mayi mu Israeli. Nʼchifukwa chiyani mukufuna kufafaniza cholowa cha Yehova?”
Ngingowabokuthula, owabathembekileyo bakoIsrayeli; udinga ukuchitha umuzi lonina koIsrayeli. Uginyelani ilifa leNkosi?
20 Yowabu anayankha kuti, “Ayi ndisatero. Ine sindikufuna kuwufafaniza kapena kuwuwononga.
UJowabi wasephendula wathi: Kakube khatshana, kakube khatshana lami ukuthi ngiginye loba ngichithe.
21 Nkhani simeneyo ayi. Koma munthu wina wa ku dziko lamapiri la Efereimu, dzina lake Seba mwana wa Bikiri, wawukira mfumu Davide. Muperekeni munthuyo ndipo ine ndidzachoka pa mzinda uno.” Mayiyo anati kwa Yowabu, “Mutu wake tikuponyerani pa khoma pano.”
Udaba kalunjalo; kodwa umuntu wasentabeni yakoEfrayimi, nguShebha indodana kaBikiri ibizo lakhe, uphakamisile isandla sakhe emelene lenkosi, emelene loDavida; nikelani yena kuphela, ngizasuka emzini. Owesifazana wasesithi kuJowabi: Khangela, ikhanda lakhe lizaphoselwa kuwe ngaphezu komduli.
22 Ndipo mayiyo anapita kwa anthu onse ndi malangizo ake anzeru, ndipo anadula mutu wa Seba mwana wa Bikiri ndipo anawuponya kwa Yowabu. Kotero iye analiza lipenga ndipo anthu ake anachoka pa mzindawo, aliyense nʼkubwerera kwawo. Ndipo Yowabu anabwerera kwa mfumu ku Yerusalemu.
Owesifazana wasesiya ngenhlakanipho yakhe ebantwini bonke. Basebequma ikhanda likaShebha indodana kaBikiri, baliphosela kuJowabi. Wasevuthela uphondo, bahlakazeka besuka kulowomuzi, ngulowo lalowo waya emathenteni akhe. UJowabi wasebuyela eJerusalema enkosini.
23 Yowabu ndiye amalamulira gulu lonse la ankhondo. Benaya mwana wa Yehoyada amalamulira Akereti ndi Apeleti.
Njalo uJowabi wayephezu kwebutho lonke lakoIsrayeli; loBhenaya indodana kaJehoyada wayephezu kwamaKerethi laphezu kwamaPelethi;
24 Adoramu amayangʼanira anthu ogwira ntchito ya thangata, Yehosafati mwana wa Ahiludi anali mlembi wa zochitika,
loAdoniramu wayephezu kwezibhalwa; loJehoshafathi indodana kaAhiludi wayengumabhalane;
25 Seva anali mlembi wa mfumu. Zadoki ndi Abiatara anali ansembe
loSheva wayengumbhali; loZadoki loAbhiyatha babengabapristi;
26 ndipo Ira wa ku Yairi anali wansembe wa Davide.
loIra laye umJayiri wayengumpristi kaDavida.

< 2 Samueli 20 >