< 2 Samueli 12 >

1 Tsono Yehova anatumiza Natani kwa Davide. Atafika kwa Davide anati, “Panali anthu awiri mʼmizinda ina, wina wolemera ndi wina wosauka.
I posla Gospod Natana k Davidu; i on došav k njemu reèe mu: u jednom gradu bijahu dva èovjeka, jedan bogat a drugi siromah.
2 Munthu wolemerayo anali ndi nkhosa ndi ngʼombe zambiri,
Bogati imaše ovaca i goveda vrlo mnogo;
3 koma wosaukayo analibe chilichonse kupatula kankhosa kamodzi kakakazi kamene anakagula. Iye anakasunga ndipo kanakula naye pamodzi ndi ana ake. Kamadya chakudya chake, kamamwera chikho chake ndipo kamagona mʼmanja mwake. Kanali ngati mwana wamkazi kwa iyeyo.
A siromah nemaše ništa do jednu malu ovèicu, koju bješe kupio, i hranjaše je, te odraste uza nj i uz djecu njegovu, i jeðaše od njegova zalogaja, i iz njegove èaše pijaše, i na krilu mu spavaše, i bijaše mu kao kæi.
4 “Ndipo mlendo anafika kwa munthu wolemera uja, koma munthu wolemerayo sanafune kutenga imodzi mwa nkhosa kapena ngʼombe zake kuti akonzere chakudya mlendo amene anafika kwa iye. Mʼmalo mwake anatenga mwana wankhosa wamkazi wa munthu wosauka uja nakonzera chakudya mlendo uja amene anabwera kwa iye.”
A doðe putnik k bogatome èovjeku, a njemu bi žao uzeti iz svojih ovaca ili goveda da zgotovi putniku koji doðe k njemu; nego uze ovcu onoga siromaha, i zgotovi je èovjeku, koji doðe k njemu.
5 Davide anapsa mtima kwambiri chifukwa cha munthuyo ndipo anati kwa Natani, “Pali Yehova, munthu amene anachita zimenezi ayenera kufa basi!
Tada se David vrlo razgnjevi na onoga èovjeka, i reèe Natanu: tako živ bio Gospod, zaslužio je smrt onaj koji je to uèinio.
6 Iye ayenera kulipira mwana wankhosa wamkaziyo kanayi, chifukwa anachita chinthu chimenechi ndipo analibe chifundo.”
I ovcu neka plati uèetvoro, što je to uèinio i nije mu žao bilo.
7 Kenaka Natani anati kwa Davide, “Munthuyo ndinu! Yehova, Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ine ndinakudzoza kukhala mfumu ya Israeli, ndipo ndinakupulumutsa mʼdzanja la Sauli.
Tada reèe Natan Davidu: ti si taj. Ovako veli Gospod Bog Izrailjev: ja sam te pomazao za cara nad Izrailjem, i ja sam te izbavio iz ruku Saulovijeh.
8 Ndinakupatsanso banja la mbuye wako ndiponso akazi a mbuye wako mʼmanja mwako. Ine ndinakupatsanso banja la Israeli ndi Yuda. Ndipo ngati zinthu zonse izi zinali zochepa, Ine ndikanakupatsa zambiri.
I dao sam ti dom gospodara tvojega, i žene gospodara tvojega na krilo tvoje, dao sam ti dom Izrailjev i Judin; i ako je malo, dodao bih ti to i to.
9 Nʼchifukwa chiyani unanyoza mawu a Yehova pochita chimene chili choyipa pamaso pake? Iwe unakantha Uriya Mhiti ndi lupanga ndipo unatenga mkazi wake kukhala wako. Uriyayo unamupha ndi lupanga la Aamoni.
Zašto si prezreo rijeè Gospodnju èineæi što njemu nije po volji? Uriju Hetejina ubio si maèem i uzeo si ženu njegovu sebi za ženu, a njega si ubio maèem sinova Amonovijeh.
10 Ndipo tsopano lupanga silidzachoka pa nyumba yako, chifukwa unandinyoza ine ndi kutenga mkazi wa Uriya Mhiti kukhala wako.’
Zato neæe se odmaæi maè od doma tvojega dovijeka, što si me prezreo i uzeo ženu Urije Hetejina da ti bude žena.
11 “Yehova akuti, ‘Ine ndidzabweretsa tsoka pa iwe lochokera mʼbanja lako. Ndidzatenga akazi ako iwe ukuona ndi kuwapereka kwa wina amene ali pafupi nawe, ndipo iye adzagona ndi akazi ako masanasana Aisraeli onse akuona.
Ovako veli Gospod: evo, ja æu podignuti na te zlo iz doma tvojega, i uzeæu žene tvoje na tvoje oèi, i daæu ih bližnjemu tvojemu, te æe spavati sa ženama tvojim na vidiku svakomu.
12 Iwe unachita zimenezi mwamseri koma Ine ndidzachita izi masanasana Aisraeli onse akuona.’”
Jer ti si uèinio tajno, ali æu ja ovo uèiniti pred svijem Izrailjem i svakomu na vidiku.
13 Kenaka Davide anati kwa Natani, “Ine ndachimwira Yehova.” Natani anayankha kuti, “Yehova wachotsa tchimo lanu. Simufa ayi.
Tada reèe David Natanu: sagriješih Gospodu. A Natan reèe Davidu: i Gospod je pronio grijeh tvoj; neæeš umrijeti.
14 Komabe, popeza pochita zimenezi mwachititsa kuti adani a Yehova amunyoze, mwana amene akubalireniyo adzafa.”
Ali što si tijem djelom dao priliku neprijateljima Gospodnjim da hule, zato æe ti umrijeti sin koji ti se rodio.
15 Natani atapita kwawo, Yehova anakantha mwana amene mkazi wa Uriya anabereka ndipo anayamba kudwala.
Potom Natan otide svojoj kuæi. A Gospod udari dijete koje rodi žena Urijina Davidu, te se razbolje na smrt.
16 Davide anapempherera mwanayo kwa Mulungu. Iye anasala chakudya ndipo analowa mʼnyumba mwake nagona pansi usiku wonse.
I David se moljaše Bogu za dijete, i pošæaše se David, i došavši ležaše preko noæ na zemlji.
17 Akuluakulu a banja lake anayima pambali pake kuti amudzutse, koma iye anakana, ndipo sanadye chakudya chilichonse pamodzi ndi iwo.
I starješine doma njegova ustaše oko njega da ga podignu sa zemlje, ali on ne htje, niti jede što s njima.
18 Mwana anamwalira pa tsiku lachisanu ndi chiwiri. Antchito a Davide anaopa kumuwuza kuti mwanayo wamwalira, popeza ankaganiza kuti, “Pamene mwanayu anali ndi moyo, ife tinayankhula Davide koma sanatimvere. Nanga tingamuwuze bwanji kuti mwana wamwalira? Mwina atha kudzipweteka.”
A kad bi sedmi dan, umrije dijete; i ne smijahu sluge Davidove javiti mu da je dijete umrlo, jer govorahu: evo, dok dijete bijaše živo, govorasmo mu, pa nas ne htje poslušati; a kako æemo mu kazati: umrlo je dijete? hoæe ga ucvijeliti.
19 Davide anaona kuti antchito ake amanongʼonezana pakati pawo ndipo anazindikira kuti mwanayo wamwalira. Iye anafunsa kuti, “Kodi mwanayo wamwalira?” Iwo anayankha kuti, “Inde wamwalira.”
A David videæi gdje sluge njegove šapæu meðu sobom, dosjeti se da je umrlo dijete; i reèe David slugama svojim: je li umrlo dijete? A oni rekoše: umrlo je.
20 Ndipo Davide anayimirira. Anakasamba nadzola mafuta ndi kusintha zovala zake. Pambuyo pake anapita ku nyumba ya Yehova kukapembedza. Kenaka anapita ku nyumba kwake ndipo atapempha chakudya anamupatsa nadya.
Tada David usta sa zemlje, i umi se, i namaza se i preobuèe se; i otide u dom Gospodnji, i pokloni se. Potom opet doðe kuæi svojoj, i zaiska da mu donesu da jede; i jede.
21 Antchito ake anamufunsa kuti, “Chifukwa chiyani mukuchita zinthu motere? Pamene mwana anali ndi moyo, munkasala chakudya ndi kulira, koma tsopano pamene mwana wamwalira inu mukudzuka ndi kudya!”
A sluge njegove rekoše mu: šta to radiš? dok bijaše dijete živo, postio si i plakao; a kad umrije dijete, ustao si i jedeš.
22 Iye anayankha kuti, “Pamene mwana anali ndi moyo ine ndinkasala zakudya ndi kulira. Ine ndinkaganiza kuti, ‘Akudziwa ndani? Yehova atha kundikomera mtima kuti mwanayo akhale ndi moyo.’
A on reèe: dok dijete bijaše živo, postio sam i plakao, jer govorah: ko zna, može se smilovati Gospod na me da dijete ostane živo.
23 Koma tsopano wamwalira ndisaliranji chakudya? Kodi ndingathe kumubwezanso? Ine ndidzapita kumene kuli iyeko, koma iye sadzabwerera kwa ine.”
A sada umrlo je; što bih postio? mogu li ga povratiti? ja æu otiæi k njemu, ali on neæe se vratiti k meni.
24 Ndipo Davide anatonthoza mkazi wake Batiseba, napita kwa iye ndi kugona naye. Iye anabereka mwana wamwamuna, ndipo anamutcha dzina lake Solomoni. Yehova ankamukonda iye.
Potom David utješi Vitsaveju ženu svoju, i otide k njoj, i leže s njom. I ona rodi sina, kojemu nadje ime Solomun. I mio bješe Gospodu.
25 Ndipo chifukwa chakuti Yehova ankamukonda iyeyo, Yehovayo anatumiza mawu kwa mneneri Natani kuti akamutchule Yedidiya.
I posla Natana proroka, te mu nadje ime Jedidija, radi Gospoda.
26 Pa nthawi imeneyi Yowabu anamenyana ndi Raba ku Amoni ndipo analanda nsanja yaufumu.
A Joav bijuæi Ravu sinova Amonovih, uze carski grad.
27 Ndipo Yowabu anatumiza amithenga kwa Davide kukanena kuti, “Ine ndamenyana ndi Raba ndipo ndatenga zitsime zake za madzi.
I posla poslanike k Davidu, i reèe: bih Ravu, i uzeh grad na vodi.
28 Ndipo tsopano sonkhanitsani asilikali onse ndipo muzungulire mzindawo ndi kuwulanda.”
Nego sada skupi ostali narod, i stani u oko prema gradu, i uzmi ga, da ga ne bih ja uzeo i moje se ime spominjalo na njemu.
29 Kotero Davide anasonkhanitsa ankhondo onse ndipo anapita ku Raba kukawuthira nkhondo ndi kuwulanda.
I David skupiv sav narod otide na Ravu, i udari na nju, i uze je.
30 Davide anachotsa chipewa chaufumu pamutu pa mfumu yawo ndipo Davide anavala chipewacho. Chipewacho chinkalemera makilogalamu asanu agolide, ndiponso chinali ndi miyala yokongola. Iye anatenga katundu wambiri kuchokera mu mzindawo,
I uze caru njihovu s glave krunu, u kojoj bješe talanat zlata, s dragim kamenjem, i metnuše je na glavu Davidu, i odnese iz grada plijen vrlo velik.
31 ndipo anatulutsa anthu amene anali mʼmenemo, nawayika kuti azigwira ntchito ya macheka, yosula makasu ndi nkhwangwa, ndiponso yowomba njerwa. Davide anachita izi ndi mizinda yonse ya Aamoni. Kenaka iye pamodzi ndi gulu lake lonse lankhondo anabwerera ku Yerusalemu.
A narod koji bijaše u njemu izvede i metnu ih pod pile i pod brane gvozdene i pod sjekire gvozdene, i sagna ih u peæi gdje se opeke peku. I tako uèini svijem gradovima sinova Amonovijeh. Potom se vrati David sa svijem narodom u Jerusalim.

< 2 Samueli 12 >