< 2 Petro 3 >

1 Inu okondedwa, iyi ndi kalata yanga yachiwiri kwa inu. Ine ndalemba makalata onse awiri kuti ndikukumbutseni ndi kukutsitsimutsani ndi cholinga choti muzilingalira moyenera.
Dette er nu alt det annet brev jeg skriver til eder, I elskede, for atter ved påminnelse å vekke eders rene hu
2 Ndikufuna kuti mukumbukire mawu amene anayankhulidwa kale ndi aneneri oyera mtima ndiponso lamulo limene Ambuye ndi Mpulumutsi wathu analipereka kudzera mwa atumwi.
til å minnes de ord som forut er talt av de hellige profeter, og Herrens og frelserens bud, som eders apostler har forkynt,
3 Poyamba mudziwe kuti mʼmasiku otsiriza kudzafika anthu onyoza, adzanyoza ndi kutsata zilakolako zawo zoyipa.
idet I først og fremst vet dette at i de siste dager skal det komme spottere med spott, som farer frem efter sine egne lyster
4 Iwo adzati, “Kodi suja Ambuye analonjeza kuti adzabweranso? Nanga ali kuti? Lija nʼkale anamwalira makolo athu, koma zinthu zonse zili monga anazilengera poyamba paja.”
og sier: Hvor er løftet om hans gjenkomst? for fra den tid fedrene sov inn, vedblir jo alle ting som de var fra skapningens begynnelse.
5 Koma iwo akuyiwala dala kuti Mulungu atanena mawu, kumwamba kunakhalapo ndipo analenga dziko lapansi ndi madzi.
For de som påstår dette, er blinde for at det fra gammel tid var himler og en jord som var blitt til ut av vann og gjennem vann ved Guds ord,
6 Ndi madzinso achigumula, dziko lapansi la masiku amenewo linawonongedwa.
og derved gikk den verden som da var, under i vannflommen.
7 Dziko la kumwamba ndi lapansi la masiku ano akulisunga ndi mawu omwewo kuti adzalitentha ndi moto. Akuzisunga mpaka tsiku limene adzaweruza ndi kuwononga anthu onse osapembedza Mulungu.
Men de himler som nu er, og jorden er ved det samme ord spart til ilden, idet de opholdes inntil den dag da de ugudelige mennesker skal dømmes og gå fortapt.
8 Koma abale okondedwa, musayiwale chinthu chimodzi ichi: Kuti pamaso pa Ambuye tsiku limodzi lili ngati zaka 1,000, ndipo zaka 1,000 zili ngati tsiku limodzi!
Men dette ene må I ikke være blinde for, I elskede, at én dag er i Herrens øine som tusen år, og tusen år som én dag.
9 Ambuye sazengereza kuchita zimene analonjeza, monga ena amaganizira. Iwo akukulezerani mtima, sakufuna kuti aliyense awonongeke, koma akufuna kuti aliyense alape.
Herren er ikke sen med løftet, således som nogen akter det for senhet, men han har langmodighet med eder, da han ikke vil at nogen skal fortapes, men at alle skal komme til omvendelse.
10 Koma tsiku la Ambuye lidzafika ngati mbala. Pa tsikuli zinthu zakumwamba zidzachoka ndi phokoso lalikulu. Zinthu zonse zidzawonongedwa ndi moto, ndipo dziko lapansi ndi zonse zili mʼmenemo zidzapsa.
Men Herrens dag skal komme som en tyv, og da skal himlene forgå med stort brak, og himmellegemene skal komme i brand og opløses, og jorden og tingene på den skal opbrennes.
11 Popeza kuti zinthu zonse zidzawonongedwa motere, kodi inu muyenera kukhala anthu otani? Muyenera kukhala moyo wachiyero ndi opembedza Mulungu
Da nu alt dette opløses, hvor må I da strebe efter hellig ferd og gudsfrykt,
12 pamene mukuyembekezera tsiku la Mulungu ndi kufulumiza kufika kwake. Pa tsiku limeneli zinthu zakumwamba zidzawonongedwa ndi moto, ndipo zidzasungunuka ndi kutentha.
idet I venter på og fremskynder Guds dags komme, hvorved himlene skal opløses i ild og himmellegemene smelte i brand!
13 Koma ife tikudikira kumwamba kwatsopano ndi dziko lapansi latsopano, zimene Mulungu analonjeza, mʼmene chilungamo chidzakhalamo.
Men vi venter efter hans løfte nye himler og en ny jord, hvor rettferdighet bor.
14 Chomwecho okondedwa, popeza inu mukudikira zimenezi, chitani changu kuti mukhale wopanda chilema kuti mukhale pa mtendere ndi Iye.
Derfor, elskede, da I venter dette, så legg vinn på å bli funnet uten flekk og lyte for ham i fred,
15 Zindikirani kuti kuleza mtima kwa Ambuye kukutanthauza chipulumutso, monga momwe mʼbale wathu wokondedwa Paulo anakulemberaninso ndi nzeru zimene Mulungu anamupatsa.
og akt vår Herres langmodighet for frelse, således som og vår elskede bror Paulus har skrevet til eder efter den visdom som er ham gitt,
16 Iye walemba chimodzimodzi makalata ake onse, kuyankhula za zinthu izi. Mʼmakalata ake mumakhala zinthu zina zovuta kuzimvetsa, zimene anthu osadziwa ndi osakhazikika amazipotoza, monga amachita ndi malemba ena onse, potero akudziwononga okha.
likesom og i alle sine brev når han i dem taler om dette; i dem er det noget som er svært å skjønne, og som de ulærde og ubefestede tyder vrangt, som de og gjør med de andre skrifter, til sin egen undergang.
17 Nʼchifukwa chake, abale okondedwa, popeza mukuzidziwa kale zimenezi, chenjerani kuti musatengeke ndi zolakwa za anthu osaweruzika, mungagwe ndi kuchoka pamalo otetezedwa.
Så må da I, elskede, som forut vet dette, ta eder i vare at I ikke skal bli revet med av de ugudeliges forvillelse og falle ut av eders egen faste stand;
18 Koma kulani mu chisomo ndi mʼchidziwitso cha Ambuye ndi Mpulumutsi wathu Yesu Khristu. Kwa Iye kukhale ulemerero tsopano mpaka muyaya. Ameni. (aiōn g165)
men voks i nåde og kjennskap til vår Herre og frelser Jesus Kristus! Ham være æren både nu og til evig tid! Amen. (aiōn g165)

< 2 Petro 3 >

The World is Destroyed by Water
The World is Destroyed by Water