< 2 Mafumu 15 >

1 Mʼchaka cha 27 cha Yeroboamu mfumu ya Israeli, Azariya mwana wa Amaziya mfumu ya Yuda anayamba kulamulira.
Godine dvadeset sedme carovanja Jerovoamova nad Izrailjem zacari se Azarija sin Amasijin nad Judom.
2 Iye anakhala mfumu ali ndi zaka 16 ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 52. Amayi ake anali Yekoliya wa ku Yerusalemu.
Bješe mu šesnaest godina kad se zacari, i carova pedeset i dvije godine u Jerusalimu. Materi mu bješe ime Jeholija, iz Jerusalima.
3 Iyeyo anachita zabwino pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Amaziya abambo ake.
On èinjaše što je pravo pred Gospodom sasvijem kao što je èinio Amasija otac njegov.
4 Komabe malo opembedzerako mafano sanawachotse ndipo anthu anapitirizabe kupereka nsembe ndi kufukiza lubani kumeneko.
Ali visine ne biše oborene: narod još prinošaše žrtve i kaðaše na visinama.
5 Ndipo Yehova analanga mfumu ndi nthenda ya khate mpaka tsiku limene inamwalira. Tsono mfumuyo inkakhala mʼnyumba yakeyake yapadera. Mwana wake Yotamu ndiye amene ankayangʼanira nyumba ya mfumu ndiponso ndiye amene ankalamulira anthu mʼdzikomo.
A Gospod udari cara, te bi gubav do smrti svoje; i življaše u odvojenom domu; a Jotam sin carev upravljaše dvorom i suðaše narodu u zemlji.
6 Ntchito zina za Azariya ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
A ostala djela Azarijina i sve što je èinio, nije li to zapisano u dnevniku careva Judinijeh?
7 Azariya anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide. Ndipo Yotamu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
I poèinu Azarija kod otaca svojih, i pogreboše ga kod otaca njegovijeh u gradu Davidovu; a na njegovo se mjesto zacari Jotam sin njegov.
8 Mʼchaka cha 38 cha Azariya mfumu ya Yuda, Zekariya mwana wa Yeroboamu anakhala mfumu ya Israeli ku Samariya ndipo analamulira miyezi isanu ndi umodzi.
Trideset osme godine carovanja Azarijina nad Judom zacari se Zaharija sin Jerovoamov nad Izrailjem u Samariji, i carova šest mjeseca.
9 Ndipo iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova monga anachitira makolo ake. Iye sanaleke machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, amene anachimwitsa nawo Israeli.
I èinjaše što je zlo pred Gospodom kao što su èinili oci njegovi; ne otstupi od grijehova Jerovoama sina Navatova, kojima navede na grijeh Izrailja.
10 Salumu mwana wa Yabesi anachitira chiwembu Zekariya. Anamukantha anthu akuona, namupha, ndipo analowa ufumu mʼmalo mwake.
I pobuni se na nj Salum sin Javisov, i ubi ga pred narodom i pogubi ga, i zacari se na njegovo mjesto.
11 Ntchito zina za Zekariya, zinalembedwa mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli.
A ostala djela Zaharijina, eno zapisana su u dnevniku careva Izrailjevijeh.
12 Awa ndiwo mawu a Yehova amene anayankhula kwa Yehu kuti, “Ana ako adzalamulira Israeli mpaka mʼbado wachinayi.”
To je rijeè Gospodnja koju reèe Juju govoreæi: sinovi tvoji do èetvrtoga koljena sjedeæe na prijestolu Izrailjevu. I zbi se tako.
13 Salumu mwana wa Yabesi anakhala mfumu mʼchaka cha 39 cha ulamuliro wa Uziya mfumu ya Yuda ndipo analamulira mu Samariya mwezi umodzi.
Salum sin Javisov zacari se trideset devete godine carovanja Ozijina nad Judom, a carova mjesec dana u Samariji.
14 Ndipo Menahemu mwana wa Gadi anachoka ku Tiriza napita ku Samariya nakantha Salumu mwana wa Yabesi ku Samariya, namupha ndipo iye analowa ufumu mʼmalo mwake.
Jer Menajim sin Gadijev iz Terse podiže se i doðe u Samariju i ubi Saluma sina Javisova u Samariji, i pogubi ga, i zacari se na njegovo mjesto.
15 Ntchito zina za Salumu ndiponso za chiwembu chimene anachita, zinalembedwa mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli.
A ostala djela Salumova i buna koju podiže, eto, to je zapisano u dnevniku careva Izrailjevijeh.
16 Nthawi imeneyo Menahemu, kuchokera ku Tiriza, anakathira nkhondo mzinda wa Tipisa ndi anthu onse amene anali mʼmenemo ndi dera lonse lozungulira chifukwa iwo anakana kutsekula zipata zawo. Iye anatenga katundu yense mu mzinda wa Tipisa ndi kutumbula akazi onse oyembekezera.
Tada Menajim raskopa Tapsu i pobi sve koji bijahu u njoj i u meðama njezinijem od Terse, jer mu ne otvoriše, zato ih pobi i sve trudne žene njihove raspori.
17 Mʼchaka cha 39 cha Azariya mfumu ya Yuda, Menahemu mwana wa Gadi anakhala mfumu ya Israeli ndipo analamulira mu Samariya zaka khumi.
Godine trideset devete carovanja Azarijina nad Judom zacari se Menajim sin Gadijev nad Izrailjem, i carova deset godina u Samariji.
18 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova. Nthawi yonse ya ulamuliro wake sanasiye machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, amene anachimwitsa nawo Israeli.
I èinjaše što je zlo pred Gospodom, ne otstupi svega vijeka svojega od grijehova Jerovoama sina Navatova, kojima navede na grijeh Izrailja.
19 Tsono Puli mfumu ya ku Asiriya inadzathira nkhondo dzikolo ndipo Menahemu anapatsa Puliyo makilogalamu 34,000 a siliva kuti amuthandize ndi kulimbikitsa ufumu wake.
Tada Ful car Asirski udari na zemlju, a Menajim dade Fulu tisuæu talanata srebra da bi mu pomogao da utvrdi carstvo u svojoj ruci.
20 Menahemu anapeza ndalamazo kudzera mu msonkho umene ankakhometsa Aisraeli. Munthu aliyense wachuma ankapereka masekeli a siliva makumi asanu kwa mfumu ya ku Asiriya. Choncho mfumu ya ku Asiriya inabwerera ndipo sinakhalenso mʼdzikomo.
A te novce uze Menajim od Izrailja, od svijeh bogatijeh ljudi, da ih da caru Asirskom, od svakoga po pedeset sikala. Tako se vrati car Asirski, i ne zabavi se ondje u zemlji.
21 Ntchito zina za Menahemu ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
A ostala djela Menajimova i što je god èinio, nije li zapisano u dnevniku careva Izrailjevijeh?
22 Menahemu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake. Ndipo Pekahiya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
I poèinu Menajim kod otaca svojih, a na njegovo se mjesto zacari Fakija sin njegov.
23 Mʼchaka cha makumi asanu a Azariya mfumu ya Yuda, Pekahiya mwana wa Menahemu anakhala mfumu ya Israeli mu Samariya ndipo analamulira zaka ziwiri.
Godine pedesete carovanja Azarijina nad Judom zacari se Fakija sin Menajimov nad Izrailjem u Samariji, i carova dvije godine.
24 Pekahiya anachita zoyipa pamaso pa Yehova. Iye sanaleke machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, omwe anachimwitsa nawo Israeli.
I èinjaše što je zlo pred Gospodom, ne otstupi od grijehova Jerovoama sina Navatova, kojima navede na grijeh Izrailja.
25 Ndipo Peka mwana wa Remaliya, mtsogoleri wake wa ankhondo, anamuchita chiwembu. Iye pamodzi ndi anthu makumi asanu a ku Giliyadi anapha Pekahiya pamodzi ndi Arigobu ndi Ariyeli mʼchipinda choteteza nyumba ya mfumu mu Samariya. Kotero Peka anapha Pekahiya ndipo analowa ufumu mʼmalo mwake.
I pobuni se na nj Fekaj sin Remalijin, vojvoda njegov, i ubi ga u Samariji u carskom dvoru, s Argovom i Arijem i s pedeset ljudi sinova Galadovijeh; i ubivši ga zacari se na njegovo mjesto.
26 Ntchito zina za Pekahiya ndi zonse zimene anachita zinalembedwa mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli.
A ostala djela Fakijina i što je god èinio, eno je zapisano u dnevniku careva Izrailjevijeh.
27 Mʼchaka cha 52 cha Azariya mfumu ya Yuda, Peka mwana wa Remaliya anakhala mfumu ya Israeli ku Samariya ndipo analamulira zaka makumi awiri.
Godine pedeset druge Azarije cara Judina zacari se Fekaj sin Remalijin nad Izrailjem u Samariji, i carova dvadeset godina.
28 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova. Sanaleke machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, amene anachimwitsa nawo Israeli.
I èinjaše što je zlo pred Gospodom, ne otstupi od grijehova Jerovoama sina Navatova, kojima navede na grijeh Izrailja.
29 Nthawi ya Peka mfumu ya Israeli, Tigilati-Pileseri mfumu ya ku Asiriya anabwera ndi kudzalanda Iyoni, Abeli-Beti-Maaka, Yanowa, Kedesi ndi Hazori. Mfumu ya ku Asiriya inatenga Giliyadi ndi Galileya, kuphatikizanso madera onse a Nafutali ndipo anatumiza Aisraeli ku Asiriya.
U vrijeme Fekaja cara Izrailjeva doðe Teglat-Felasar car Asirski, i uze Ijon i Avel-Vetmahu i Janoh i Kedes i Asor i Galad i Galileju, svu zemlju Neftalimovu, i preseli narod odande u Asiriju.
30 Kenaka Hoseya mwana wa Ela anachitira chiwembu Peka mwana wa Remaliya. Anamukantha ndi kumupha ndipo anakhala mfumu mʼmalo mwake mʼchaka makumi awiri cha Yotamu mwana wa Uziya.
Tada se pobuni Osija sin Ilin na Fekaja sina Remalijina i ubi ga i pogubi ga, i zacari se na njegovo mjesto dvadesete godine Jotama sina Ozijina.
31 Ntchito zina za Peka ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
A ostala djela Fekajeva i sve što je èinio, eno je zapisano u dnevniku careva Izrailjevijeh.
32 Mʼchaka chachiwiri cha Peka mwana wa Remaliya mfumu ya Israeli, Yotamu mwana wa Uziya mfumu ya Yuda anayamba kulamulira.
Druge godine carovanja Fekaja sina Remalijina nad Izrailjem zacari se Jotam sin Ozijin nad Judom.
33 Iye anakhala mfumu ali ndi zaka 25 ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 16. Amayi ake anali Yerusa mwana wa Zadoki.
Bijaše mu dvadeset i pet godina kad poèe carovati, i carova šesnaest godina u Jerusalimu. Materi mu bješe ime Jerusa, kæi Sadokova.
34 Iye anachita zabwino pamaso pa Yehova monga anachitira Uziya abambo ake.
I èinjaše što je pravo pred Gospodom, sasvijem èinjaše kako je èinio Ozija otac njegov.
35 Komabe malo opembedzera mafano sanawachotse ndipo anthu anapitiriza kupereka nsembe ndi kufukiza lubani kumeneko.
Ali visine ne biše oborene: narod još prinošaše žrtve i kaðaše na visinama. On naèini najviša vrata na domu Gospodnjem.
36 Ntchito zina za Yotamu ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
A ostala djela Jotamova i sve što je èinio, nije li zapisano u dnevniku careva Judinijeh?
37 (Nthawi imeneyo, Yehova anayamba kumatuma Rezini mfumu ya Aaramu ndi Peka mwana wa Remaliya kudzamenyana ndi Yuda).
U to vrijeme poèe Gospod puštati na Judu Resina cara Sirskoga i Fekaja sina Remalijina.
38 Yotamu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide abambo ake. Ndipo Ahazi mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
I Jotam poèinu kod otaca svojih, i bi pogreben kod otaca svojih u gradu Davida oca svojega; a na njegovo se mjesto zacari Ahaz sin njegov.

< 2 Mafumu 15 >