< 2 Mafumu 13 >

1 Mʼchaka cha 23 cha ufumu wa Yowasi mwana wa Ahaziya mfumu ya Yuda, Yehowahazi, mwana wa Yehu anakhala mfumu ya Israeli mu Samariya, ndipo analamulira zaka 17.
In the twenty-third year of Joash the son of Ahaziah, king of Judah, Jehoahaz the son of Jehu began to reign over Israel in Samaria, and reigned seventeen years.
2 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova potsatira machimo a Yeroboamu mwana Nebati amene anachimwitsa nawo Israeli ndipo iye sanawaleke machimowo.
And he did that which was evil in the sight of Jehovah, and followed the sins of Jeroboam the son of Nebat, with which he made Israel to sin. He did not depart from it.
3 Ndipo Yehova anakwiyira Aisraeli nawayika pansi pa ulamuliro wa Hazaeli mfumu ya Siriya ndi Beni-Hadadi mwana wa Hazaeli masiku awo onse.
And the anger of Jehovah was kindled against Israel, and he delivered them into the hand of Hazael king of Syria, and into the hand of Benhadad the son of Hazael, continually.
4 Tsono Yehowahazi anapempha Yehova kuti amuchitire chifundo ndipo Yehova anamva pempho lake chifukwa anaona momwe mfumu ya Aramu inkapsinjira Aisraeli.
And Jehoahaz besought Jehovah, and Jehovah hearkened to him, for he saw the oppression of Israel, how that the king of Syria oppressed them.
5 Yehova anapatsa Aisraeli munthu woti awapulumutse ndipo anapulumuka mʼdzanja la Aramu. Choncho Aisraeli anakhala mʼnyumba zawo monga ankachitira kale.
(And Jehovah gave Israel a savior, so that they went out from under the hand of the Syrians, and the sons of Israel dwelt in their tents as beforetime.
6 Komabe Aisraeli sanaleke kuchita machimo a nyumba ya Yeroboamu, amene anachimwitsa nawo Israeli. Iwo anapitirira kuchita machimowo. Ndiponso fano la Asera linakhalabe ku Samariya.
Nevertheless they did not depart from the sins of the house of Jeroboam, with which he made Israel to sin, but walked therein. And the Asherah also remained in Samaria.)
7 Yehowahazi sanatsale ndi ankhondo ambiri koma 50 okha okwera pa akavalo, magaleta khumi ndi asilikali oyenda pansi 10,000.
For he did not leave to Jehoahaz of the people except fifty horsemen, and ten chariots, and ten thousand footmen, for the king of Syria destroyed them, and made them like the dust in threshing.
8 Ntchito zina za Yehowahazi ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
Now the rest of the acts of Jehoahaz, and all that he did, and his might, are they not written in the book of the chronicles of the kings of Israel?
9 Yehowahazi anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda mu Samariya. Ndipo Yowasi mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
And Jehoahaz slept with his fathers, and they buried him in Samaria. And Joash his son reigned in his stead.
10 Mʼchaka cha 37 cha Yowasi mfumu ya Yuda, Yehowahazi anakhala mfumu ya Israeli mu Samariya, ndipo analamulira zaka 16.
In the thirty-seventh year of Joash king of Judah, Jehoash the son of Jehoahaz began to reign over Israel in Samaria, and reigned sixteen years.
11 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova ndipo sanaleke kuchita tchimo la Yeroboamu mwana wa Nebati limene anachimwitsa nalo Israeli.
And he did that which was evil in the sight of Jehovah. He did not depart from all the sins of Jeroboam the son of Nebat, with which he made Israel to sin, but he walked therein.
12 Ntchito zina za Yowasi ndi zonse zimene anachita, kuphatikizapo nkhondo yake ndi Amaziya mfumu ya Yuda, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
Now the rest of the acts of Joash, and all that he did, and his might with which he fought against Amaziah king of Judah, are they not written in the book of the chronicles of the kings of Israel?
13 Yowasi anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake ndipo Yeroboamu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake. Yowasi anayikidwa mʼmanda mu Samariya pamodzi ndi mafumu a Israeli.
And Joash slept with his fathers, and Jeroboam sat upon his throne. And Joash was buried in Samaria with the kings of Israel.
14 Tsono Elisa anadwala matenda amene anafa nawo. Yowasi mfumu ya Israeli inapita kukamuona ndipo inamulirira. Iye polira ankanena kuti, “Abambo anga! Abambo anga! Magaleta a Israeli ndi okwerapo ake a Israeli!”
Now Elisha was fallen sick of his sickness of which he died. And Joash the king of Israel came down to him, and wept over him, and said, My father, my father, the chariots of Israel and the horsemen of it!
15 Elisa anamuwuza kuti, “Tenga uta ndi mivi.” Ndipo anaterodi.
And Elisha said to him, Take bow and arrows. And he took to him bow and arrows.
16 Elisa anawuza mfumu ya Israeli kuti, “Tenga uta mʼdzanja lako.” Pamene anatenga utawo, Elisa anayika manja ake pa manja a mfumuyo.
And he said to the king of Israel, Put thy hand upon the bow. And he put his hand upon it. And Elisha laid his hands upon the king's hands.
17 Elisa anamuwuza kuti, “Tsekula zenera.” Ndipo anatsekuladi. Elisa anati, “Ponya muviwo!” Ndipo anaponyadi. Elisa anati, “Muvi wa chigonjetso cha Yehova, muvi wogonjetsera Aaramu! Iwe udzawawononga kwathunthu Aaramu ku Afeki.”
And he said, Open the window eastward. And he opened it. Then Elisha said, Shoot. And he shot. And he said, Jehovah's arrow of victory, even the arrow of victory over Syria, for thou shall smite the Syrians in Aphek till thou have consumed them.
18 Kenaka Elisa anati, “Tenga mivi.” Ndipo mfumu inatenga miviyo. Iye anati, “Lasa pansi.” Mfumu inalasa pansi miviyo katatu nʼkuleka.
And he said, Take the arrows. And he took them. And he said to the king of Israel, Smite upon the ground. And he smote thrice, and stopped.
19 Munthu wa Mulungu anapsera mtima mfumuyo ndipo anati, “Ukanalasa pansi kasanu kapena kasanu nʼkamodzi. Pamenepo ukanatha kuwagonjetsa Aaramu ndi kuwawononga kwathunthu. Koma tsopano udzawagonjetsa katatu kokha.”
And the man of God was angry with him, and said, Thou should have smitten five or six times. Then thou would have smitten Syria till thou had consumed it, whereas now thou shall smite Syria but thrice.
20 Elisa anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda. Tsono magulu a ankhondo a Amowabu ankabwera kudzalowa ndi kudzathira nkhondo dzikolo nthawi ya dzinja.
And Elisha died, and they buried him. Now the bands of the Moabites invaded the land at the coming in of the year.
21 Tsiku lina Aisraeli ena akukayika maliro mʼmanda, mwadzidzidzi anaona gulu lankhondo ndipo munthu womwalirayo anamuponyera mʼmanda a Elisa. Pamene mtembowo unakhudza mafupa a Elisa, munthu wakufayo anatsitsimuka nayimirira.
And it came to pass, as they were burying a man, that, behold, they spied a band, and they cast the man into the sepulcher of Elisha. And as soon as the man touched the bones of Elisha, he revived, and stood up on his feet.
22 Hazaeli mfumu ya Aramu inazunza Aisraeli nthawi yonse ya ulamuliro wa Yehowahazi.
And Hazael king of Syria oppressed Israel all the days of Jehoahaz.
23 Koma Yehova anawachitira chifundo Aisraeliwo ndi kukhudzika ndi zomwe zinkawachitikira chifukwa cha pangano lake ndi Abrahamu, Isake ndi Yakobo. Mpaka lero lino Iye sanafune kuwawononga kapena kuwachotsa pamaso pake.
But Jehovah was gracious to them, and had compassion on them, and had respect to them, because of his covenant with Abraham, Isaac, and Jacob, and would not destroy them, neither did he cast them from his presence as yet.
24 Hazaeli mfumu ya Aramu inamwalira ndipo mwana wake Beni-Hadadi analowa ufumu mʼmalo mwake.
And Hazael king of Syria died, and Benhadad his son reigned in his stead.
25 Pamenepo Yowasi mwana wa Yehowahazi analandanso kwa Beni-Hadadi mwana wa Hazaeli mizinda yonse imene iye analanda Yehowahazi abambo ake. Yehowasi anagonjetsa Beni-Hadadi katatu ndipo anatenganso mizinda ya Israeli.
And Jehoash the son of Jehoahaz again took out of the hand of Benhadad the son of Hazael the cities, which he had taken out of the hand of Jehoahaz his father by war. Three times Joash smote him, and recovered the cities of Israel.

< 2 Mafumu 13 >