< 2 Akorinto 6 >

1 Pogwira naye ntchito pamodzi, tikukudandaulirani kuti musangolandira chisomo cha Mulungu pachabe.
Споспешствующе же и молим, не вотще благодать Божию прияти вам.
2 Pakuti akunena kuti, “Pa nthawi yanga yabwino yokomera anthu mtima ndinakumvera, ndipo pa nthawi yopulumutsa ndinakuthandiza. Taonani, ndikukuwuzani kuti, ino ndiyo nthawi yabwino ya Ambuye, lero ndiye tsiku la chipulumutso.”
Глаголет бо: во время приятно послушах тебе, и в день спасения помогох ти. Се ныне время благоприятно, се ныне день спасения.
3 Ife sitikuyika chokhumudwitsa pa njira ya wina aliyense, kuti utumiki wathu usanyozeke.
Ни едино ни в чемже дающе претыкание, да служение безпорочно будет,
4 Mʼmalo mwake, mwanjira iliyonse timasonyeza kuti ndife atumiki a Mulungu popirira kwambiri mʼmasautso, mʼzowawa ndi mʼzodetsa nkhawa.
но во всем представляюще себе якоже Божия слуги, в терпении мнозе, в скорбех, в бедах, в теснотах,
5 Pomenyedwa, kuponyedwa mʼndende ndi mʼzipolowe. Pogwira ntchito mwamphamvu, posagona usiku onse, posowa chakudya;
в ранах, в темницах, в нестроениих, в трудех, во бдениих, в пощениих,
6 pokhala moyo woyera mtima, pomvetsa zinthu, wokoma mtima ndi wachifundo mwa Mzimu Woyera ndi mwachikondi choonadi
во очищении, в разуме, в долготерпении, в благости, в Дусе Святе, в любви нелицемерне,
7 ndi poyankhula choonadi mwamphamvu ya Mulungu. Zida zimene zili mʼdzanja lamanja ndi lamanzere ndizo chilungamo.
в словеси истины, в силе Божией, оружии правды десными и шуими,
8 Timatumikira Mulungu ngakhale ena amatinyoza ndi ena amatilemekeza, ena amatinenera chipongwe, enanso amatiyamikira. Ena amatitenga kukhala ngati onena zoona, ndipo enanso amatitenga kukhala ngati onena zabodza.
славою и безчестием, гаждением и благохвалением: яко лестцы, и истинни:
9 Amatiyesa osadziwika komatu ndife odziwika kwambiri. Amatiyesa wooneka ngati tikufa, koma tikupitirirabe ndi moyo, okanthidwa, koma osaphedwa.
яко незнаеми, и познаваеми: яко умирающе, и се живи есмы: яко наказуеми, а не умерщвляеми:
10 Amatiyesa achisoni, koma ndife achimwemwe nthawi zonse, aumphawi, koma olemeretsa ambiri; wopanda kanthu, koma tili ndi zonse.
яко скорбяще, присно же радующеся: яко нищи, а многи богатяще: яко ничтоже имуще, а вся содержаще.
11 Tayankhula momasuka kwa inu, Akorinto, ndipo tanena zonse za kumtima kwathu.
Уста наша отверзошася к вам, Коринфяне, сердце наше распространися.
12 Ife sitikukubisirani chikondi chathu pa inu, koma inu mukubisa chikondi chanu pa ife.
Не тесно вмещаетеся в нас, утесняетеся же во утробах ваших.
13 Pofuna kufanana zochita ndi kuyankhula monga kwa ana anga, nanunso muzinena za kukhosi kwanu.
Тожде же возмездие, якоже чадом глаголю, распространитеся и вы.
14 Musamasenze goli pamodzi ndi osakhulupirira. Kodi pali mgwirizano wanji pakati pa kulungama ndi kusalungama? Kapena kodi pali mgwirizano wanji pakati pa kuwala ndi mdima?
Не бывайте удобь преложни ко иному ярму, якоже невернии. Кое бо причастие правде к беззаконию? Или кое общение свету ко тьме?
15 Pali mgwirizano wanji pakati pa Khristu ndi Beliyali? Kapena munthu wokhulupirira angayanjane bwanji ndi munthu wosakhulupirira?
Кое же согласие Христови с Велиаром? Или кая часть верну с неверным?
16 Pali mgwirizano wanji pakati pa Nyumba ya Mulungu ndi nyumba ya mafano? Popezatu ndife Nyumba ya Mulungu wamoyo. Monga Mulungu wanena kuti, “Ndidzakhala mwa iwo ndipo ndidzayendayenda pakati pawo, ndipo ndidzakhala Mulungu wawo, ndipo adzakhala anthu anga.”
Или кое сложение церкви Божией со идолы? Вы бо есте церкви Бога жива, якоже рече Бог: яко вселюся в них и похожду, и буду им Бог, и тии будут Мне людие.
17 Nʼchifukwa chake “Tulukani pakati pawo ndi kudzipatula, akutero Ambuye. Musakhudze chodetsedwa chilichonse, ndipo ndidzakulandirani.”
Темже изыдите от среды их и отлучитеся, глаголет Господь, и нечистоте не прикасайтеся, и Аз прииму вы:
18 Ndipo “Ndidzakhala Atate anu, ndipo inu mudzakhala ana anga aamuna ndi aakazi, akutero Ambuye, Wamphamvuzonse.”
и буду вам во Отца, и вы будете Мне в сыны и дщери, глаголет Господь Вседержитель.

< 2 Akorinto 6 >