< 2 Mbiri 9 >

1 Mfumu yayikazi ya ku Seba itamva za kutchuka kwa Solomoni, inabwera mu Yerusalemu kudzamuyesa ndi mafunso okhwima. Inafika ndi gulu lalikulu la ngamira zonyamula zokometsera zakudya, golide wambiri, ndi miyala yokongola. Inafika kwa Solomoni ndipo inayankhula naye zonse zimene zinali mu mtima mwake.
Indlovukazi yeShebha isizwile udumo lukaSolomoni yeza eJerusalema ukuhlola uSolomoni ngemibuzo enzima, ilexuku elikhulu kakhulu, lamakamela ethwele amakha legolide ngobunengi lamatshe aligugu; isifikile kuSolomoni yakhuluma laye konke okwakusenhliziyweni yayo.
2 Solomoni anayankha mafunso ake onse ndipo panalibe kanthu kalikonse kovuta kwa iye komwe sanathe kufotokozera mfumu yayikaziyo.
USolomoni wayichasisela zonke indaba zayo, njalo kwakungekho lutho olwamcatshelayo uSolomoni angaluchasisanga kuyo.
3 Mfumu yayikazi ya ku Seba itaona nzeru za Solomoni komanso nyumba yaufumu imene anamanga,
Indlovukazi yeShebha isibonile inhlakanipho kaSolomoni, lendlu ayeyakhile,
4 chakudya cha pa tebulo pake, moyo wa antchito ake ndi zovala zawo; atumiki opereka zakumwa ndi zovala zawo ndiponso nsembe zopsereza zimene ankapereka ku Nyumba ya Yehova, inathedwa nzeru.
lokudla kwetafula lakhe, lokuhlala kwenceku zakhe, lokuma kwezikhonzi zakhe, lezigqoko zazo, labaphathinkezo bakhe, lezigqoko zabo, lokwenyuka kwakhe enyuka ngakho endlini yeNkosi, kakusabanga lamoya kuyo.
5 Iyo inati kwa mfumu, “Mbiri imene ndinamva ndili ku dziko kwathu, ya zomwe munachita komanso nzeru zanu ndi yoona.
Yasisithi enkosini: Wawuliqiniso umbiko engawuzwa elizweni lami ngendaba zakho langenhlakanipho yakho.
6 Koma sindinakhulupirire zimene ankanena mpaka nditafika ndi kuona ndi maso anga. Kunena zoona sanandiwuze ngakhale theka lomwe la kuchuluka kwa nzeru zanu, pakuti zaposa zimene ndinamva.
Kodwa kangiwakholwanga amazwi abo ngaze ngeza lamehlo ami akubona. Khangela-ke, bengingatshelwanga ingxenye yobukhulu benhlakanipho yakho; uyedlula umbiko engawuzwayo.
7 Ngodala anthu anu! Ngodala atumiki anu amene amayimirira pamaso panu nthawi zonse ndi kumamva nzeru zanu!
Ayajabula amadoda akho, njalo ziyajabula lezizinceku zakho ezimi phambi kwakho njalonjalo zisizwa inhlakanipho yakho.
8 Atamandike Yehova Mulungu wanu amene wakondwera nanu nakukhazikani pa mpando wake waufumu kuti mulamulire mʼmalo mwa Yehova Mulungu wanu. Chifukwa cha chikondi cha Mulungu wanu pa Israeli, ndi khumbo lake kuti akusungeni mpaka muyaya, Iye wayika inu kukhala mfumu yawo kuti mulamulire moyenera ndi mwachilungamo.”
Kabusiswe uJehova uNkulunkulu wakho othokoze ngawe ukukubeka esihlalweni sakhe sobukhosi ukuthi ube yinkosi kuJehova uNkulunkulu wakho. Ngoba uNkulunkulu wakho wamthanda uIsrayeli ukumqinisa kuze kube nininini, ngakho ukubekile waba yinkosi phezu kwabo ukuze wenze isahlulelo lokulunga.
9 Kenaka iyo inapereka kwa mfumu makilogalamu 4,000 a golide, zonunkhira zambirimbiri ndi miyala yokongola. Nʼkale lomwe sikunaonekenso zonunkhiritsa ngati zomwe mfumu yayikazi ya ku Seba inapereka kwa mfumu Solomoni.
Yasinika inkosi igolide elingamathalenta alikhulu lamatshumi amabili, lamakha ngobunengi obukhulu, lamatshe aligugu. Kakuzanga kube khona anjengalawo amakha indlovukazi yeShebha eyawanika inkosi uSolomoni.
10 (Anthu a Hiramu ndi anthu a Solomoni anabweretsa golide kuchokera ku Ofiri ndipo anabweretsanso mitengo ya mʼbawa ndi miyala yokongola.
Futhi izinceku zikaHuramu lenceku zikaSolomoni ezaziletha igolide livela eOfiri, zaseziletha izigodo zama-aligumi lamatshe aligugu.
11 Mfumu inagwiritsa ntchito mitengo ya mʼbawa pokonzera makwerero a Nyumba ya Yehova ndi nyumba yaufumu ndiponso kupangira anthu oyimba apangwe ndi azeze. Zinthu zonga zimenezi sizinaonekeponso mu Yuda).
Inkosi yasisenza ngezigodo zama-aligumi izikhwelo zendlu kaJehova lezendlu yenkosi, lamachacho lezigubhu zezintambo kwabahlabeleli. Kakuzanga kubonwe futhi okunjengalokho mandulo elizweni lakoJuda.
12 Mfumu Solomoni inapereka kwa mfumu yayikazi ya ku Seba zonse zimene inazifuna ndi kuzipempha ndipo Solomoni anayipatsa mfumuyo zoposa zimene iyo inabweretsa kwa Solomoni. Ndipo mfumuyo inabwerera ku dziko lake pamodzi ndi atumiki ake.
Inkosi uSolomoni yasinika indlovukazi yeShebha sonke isifiso sayo eyasicelayo, ngaphandle kwalokho ayekulethe enkosini. Yasiphenduka yaya elizweni layo yona lenceku zayo.
13 Kulemera kwa golide amene Solomoni amalandira pa chaka kunali makilogalamu 23,000,
Isisindo segolide elalifika-ke kuSolomoni ngomnyaka owodwa sasingamathalenta egolide angamakhulu ayisithupha lamatshumi ayisithupha lesithupha,
14 osawerengera amene ankabwera ndi anthu ochita malonda ndi osinthanitsa zinthu. Komanso mafumu onse a ku Arabiya ndi abwanamkubwa a mʼdzikomo amabweretsa golide ndi siliva kwa Solomoni.
ngaphandle kwalokho abakuletha kuvela kubathengisi labathengi; lawo wonke amakhosi eArabhiya lababusi belizwe baletha igolide lesiliva kuSolomoni.
15 Mfumu Solomoni inapanga zishango zazikulu 200 zagolide wosasantha. Mʼchishango chilichonse mumalowa golide wolemera makilogalamu asanu ndi awiri.
Inkosi uSolomoni yasisenza izihlangu ezinkulu ezingamakhulu amabili ngegolide elikhandiweyo; yasebenzisa amashekeli angamakhulu ayisithupha egolide elikhandiweyo esihlangwini esisodwa esikhulu.
16 Iye anapanganso zishango zingʼonozingʼono 300 zagolide wosasantha ndipo chishango chilichonse chimapangidwa ndi golide wolemera makilogalamu atatu. Mfumu inayika zishangozi mʼnyumba yaufumu yotchedwa Nkhalango ya Lebanoni.
Lamahawu angamakhulu amathathu egolide elikhandiweyo; yasebenzisela ihawu elilodwa amashekeli angamakhulu amathathu. Inkosi yakubeka endlini yegusu leLebhanoni.
17 Ndipo mfumu inapanganso mpando waukulu waufumu wa nyanga za njovu ndipo unakutidwa ndi golide woyengeka bwino.
Inkosi yasisenza isihlalo sobukhosi esikhulu ngempondo zendlovu, yasinameka ngegolide elicwengekileyo.
18 Mpando waufumuwo unali ndi makwerero asanu ndi limodzi ndi choyikapo mapazi cholumikizidwa ku mpandowo. Mʼmbali zonse za mpandowo munali zosanjikapo manja, ndi chifanizo cha mkango chitayima posanjikapo manjapo.
Njalo isihlalo sobukhosi sasilezikhwelo eziyisithupha zesihlalo lesenabelo segolide sasixhunywe esihlalweni sobukhosi, lezeyamelo zengalo ngapha langapha endaweni yokuhlala, lezilwane ezimbili zimi eceleni kwezeyamelo zengalo.
19 Mikango khumi ndi iwiri inayimirira pa makwerero asanu ndi imodzi aja. Umodzi mbali ina ya khwerero ndi wina mbali inayo. Palibe mpando wonga uwu umene unapangidwapo mu ufumu wina uliwonse.
Njalo kwakumi izilwane ezilitshumi lambili khona ngapha langapha ezikhwelweni eziyisithupha. Kakuzanga kwenziwe okunjalo lakuwuphi umbuso.
20 Zikho zonse za mfumu Solomoni zinali zagolide, ndiponso zipangizo zonse za ku nyumba yaufumu ya Nkhalango ya Lebanoni zinali zagolide oyengeka bwino. Panalibe chinthu chopangidwa ndi siliva, chifukwa siliva samayesedwa kanthu mʼnthawi ya Solomoni.
Lazo zonke izitsha zokunatha zenkosi uSolomoni zazingezegolide, lezitsha zonke zendlu yegusu leLebhanoni zazingezegolide elicwengekileyo; isiliva sasingabalwa njengolutho ensukwini zikaSolomoni.
21 Mfumu inali ndi sitima zambiri zapamadzi zimene zimayendetsedwa ndi antchito a Hiramu. Zimabwera kamodzi pa zaka zitatu zilizonse zitanyamula golide, siliva ndi nyanga za njovu, ndiponso anyani ndi apusi.
Ngoba imikhumbi yenkosi yaya eTarshishi lezinceku zikaHuramu; kanye ngeminyaka emithathu imikhumbi yeTarshishi yeza ithwele igolide, lesiliva, impondo zezindlovu, lezindwangu, lamaphigaga.
22 Mfumu Solomoni anapambana mafumu ena onse a dziko lapansi pa chuma ndi nzeru.
Inkosi uSolomoni yaba nkulu kulawo wonke amakhosi omhlaba ngenotho langenhlakanipho.
23 Mafumu onse a dziko lapansi ankafunafuna kuonana ndi Solomoni kuti adzamve nzeru zimene Mulungu anayika mu mtima mwake.
Lawo wonke amakhosi omhlaba adinga ubuso bukaSolomoni ukuzwa inhlakanipho yakhe uNkulunkulu ayeyifake enhliziyweni yakhe.
24 Chaka ndi chaka, aliyense amene amabwera, amabweretsa mphatso monga zipangizo zasiliva ndi golide, mikanjo, zida zankhondo ndi zokometsera zakudya komanso akavalo ndi abulu.
Aseletha, ngulowo lalowo isipho sakhe, izitsha zesiliva, lezitsha zegolide, lezembatho, izikhali, lamakha, amabhiza, lezimbongolo; into yomnyaka ngomnyaka wayo.
25 Solomoni anali ndi zipinda 4,000 zodyeramo akavalo ndi magaleta, ndi akavalo 12,000 amene amawasunga mʼmizinda yosungira magaleta ndiponso ena anali ndi iye ku Yerusalemu.
Njalo uSolomoni wayelezindlwana zamabhiza lezinqola ezizinkulungwane ezine, labagadi bamabhiza abazinkulungwane ezilitshumi lambili; wasekubeka emizini yezinqola, njalo lenkosini eJerusalema.
26 Iye ankalamulira mafumu onse kuyambira ku mtsinje wa Yufurate mpaka ku dziko la Afilisti, kukafika ku malire a dziko la Igupto.
Wasebusa phezu kwawo wonke amakhosi kusukela eMfuleni kuze kube selizweni lamaFilisti, njalo kuze kube semngceleni weGibhithe.
27 Mfumu inasandutsa siliva kukhala wambiri ngati miyala wamba mu Yerusalemu ndipo mikungudza kukhala yochuluka ngati mitengo ya mkuyu ya ku zigwa.
Inkosi yasisenza isiliva eJerusalema laba njengamatshe, lemisedari wayenza yaba njengemikhiwa yesikhamore esesihotsheni, ngobunengi.
28 Solomoni ankayitanitsa akavalo ake kuchokera ku Igupto ndi mayiko ena onse.
Basebekhuphela uSolomoni amabhiza eGibhithe lemazweni wonke.
29 Tsono ntchito zina zonse za Solomoni, kuyambira pachiyambi mpaka kumaliza, kodi sizinalembedwa mʼbuku la mbiri la mneneri Natani, ndi mʼbuku la uneneri wa Ahiya wa ku Silo ndi mʼbuku la masomphenya a mlosi Ido, lokamba za Yeroboamu mwana wa Nebati?
Ezinye-ke zezindaba zikaSolomoni, ezokuqala lezokucina, kazibhalwanga yini emazwini kaNathani umprofethi, lakusiprofetho sikaAhiya umShilo, lemibonweni kaYedi umboni mayelana loJerobhowamu indodana kaNebati?
30 Solomoni analamulira Aisraeli onse ku Yerusalemu zaka makumi anayi.
USolomoni wasebusa eJerusalema phezu kukaIsrayeli wonke iminyaka engamatshumi amane.
31 Ndipo anamwalira nagona ndi makolo ake. Anayikidwa mʼmanda mu mzinda wa Davide abambo ake. Ndipo Rehobowamu, mwana wake, analowa ufumu mʼmalo mwake.
USolomoni waselala laboyise, basebemngcwaba emzini kaDavida uyise. URehobhowamu indodana yakhe wasesiba yinkosi esikhundleni sakhe.

< 2 Mbiri 9 >