< 2 Mbiri 7 >

1 Solomoni atamaliza kupemphera, moto unatsika kuchokera kumwamba ndi kutentha nsembe zopsereza ndi nsembe zina, ndipo ulemerero wa Yehova unadzaza Nyumba ya Mulunguyo.
Da Salomo havde endt sin Bøn, for Ild ned fra Himmelen og fortærede Brændofferet og Slagtofrene, og HERRENs Herlighed fyldte Templet,
2 Ansembe sanathe kulowa mʼNyumba ya Mulungu chifukwa munadzaza ulemerero wa Yehova.
og Præsterne kunde ikke gå ind i HERRENs Hus, fordi HERRENs Herlighed fyldte det.
3 Aisraeli onse ataona moto ukuchokera kumwamba ndi ulemerero wa Yehova pamwamba pa Nyumba ya Mulungu, anagwada poyalidwa miyalapo ndipo anagunditsa nkhope zawo pansi, ndi kulambira ndi kutamanda Yehova, ponena kuti, “Iye ndi wabwino; chikondi chake chikhala chikhalire”
Og da alle Israeliterne så Ilden og HERRENs Herlighed fare ned over Templet, kastede de sig på Knæ på Stenbroen med Ansigtet mod Jorden og filbad og lovede HERREN med Ordene "thi han er god, og hans Miskundhed varer evindelig!"
4 Tsono mfumu ndi anthu onse anapereka nsembe pamaso pa Yehova.
Kongen ofrede nu sammen med alt Folket Slagtofre for HEERRENs Åsyn.
5 Ndipo mfumu Solomoni anapereka nsembe ngʼombe 22,000, nkhosa ndi mbuzi 120,000. Kotero mfumu ndi anthu onse anachita mwambo wopereka Nyumba kwa Mulungu.
Til Slagtofferet tog Kong Salomo 22.000 Stykker Hornkvæg og 120.000 Stykker Småkvæg. Således indviede Kongen og alt Folket Guds Hus.
6 Ansembe anayimirira mʼmalo mwawo, monganso anachitira Alevi ndi zida zoyimbira za Yehova, zimene Davide anapanga zotamandira Yehova ndipo zimagwiritsidwa ntchito pamene amatamanda, ponena kuti, “Chikondi chake chikhale chikhalire.” Moyangʼanizana ndi Alevi, ansembe amaliza malipenga, ndipo Aisraeli onse anali atayimirira.
Og Præsterne stod på deres Pladser, og Leviterne stød med HERRENs Musikinstrumenter, som Kong David havde ladet lave, for at love HERREN med Davids Lovsangs Ord "thi hans Miskundhed varer evindelig!" og Præsterne stod lige over for dem og blæste i trompeter, og hele Israel stod op:
7 Solomoni anapatula malo a pakati pa bwalo kutsogolo kwa Nyumba ya Yehova ndipo pamenepo anapereka nsembe zopsereza ndi mafuta, zopereka za chiyanjano, chifukwa guwa lansembe lamkuwa limene anapanga panalibe malo woti nʼkuperekerapo nsembe zopsereza, nsembe za ufa ndi mafuta.
Og Salomo helligede den mellemste Del af Forgården foran HERRENs Hus, thi der måtte han ofre Brændofrene og Fedtstykkerne af Takofrene, da Kobberalteret, som Salomo havde ladet lave, ikke kunde rumme Brændofferet, Afgrødeoffret og Fedtstykkerne.
8 Choncho nthawi imeneyi, Solomoni anachita chikondwerero kwa masiku asanu ndi awiri pamodzi ndi Aisraeli onse. Unali msonkhano waukulu, kuyambira ku Lebo Hamati mpaka ku chigwa cha ku Igupto.
Samtidig fejrede Salomo i syv Dage Højtiden sammen med hele Israel, en vældig Forsamling lige fra Egnen ved Hamat og til Ægyptens Bæk.
9 Pa tsiku lachisanu ndi chitatu panali msonkhano, pakuti anachita mwambo wopereka guwa lansembe kwa masiku asanu ndi awiri ndi masiku enanso asanu ndi awiri achikondwerero.
Ottendedagen holdt man festlig Samling, thi de fejrede Alterets Indvielse i syv Dage og Højtiden i syv.
10 Pa tsiku la 23 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, Solomoni anawuza anthu aja kuti apite kwawo. Anthu anali achimwemwe ndi okondwa mʼmitima mwawo chifukwa cha zinthu zabwino zimene Yehova anachitira Davide ndi Solomoni ndiponso anthu ake Aisraeli.
Og på den tre og tyvende Dag i den syvende Måned lod han Folket gå hver til sit, glade og vel til Mode over den Godhed, HERREN havde vist sin Tjenet David og Salomo og sit Folk Israel.
11 Solomoni atatsiriza kumanga Nyumba ya Yehova ndi nyumba yaufumu ndi kukwaniritsa kuchita zonse zimene zinali mu mtima mwake pa Nyumba ya Yehova ndi nyumba yake yaufumu,
Salomo var nu færdig med at opføre HERRENs Hus og Kongens Palads; og alt, hvad Salomo havde sat sig for at udføre ved HERRENs Hus og sit Palads, havde han lykkeligt ført igennem.
12 Yehova anamuonekera usiku ndipo anati: “Ine ndamva pemphero lako ndipo ndadzisankhira malo ano kukhala Nyumba yanga yoperekeramo nsembe.
Da lod HERREN sig til Syne for Salomo om Natten og sagde til ham: "Jeg har hørt din Bøn og udvalgt mig dette Sted til Offersted.
13 “Ine ndikatseka kumwamba kuti mvula isagwe, kapena kulamulira dzombe kuti liwononge dziko, kapena kutumiza mliri pakati pa anthu,
Dersom jeg tillukker Himmelen, så Regnen udebliver, eller jeg opbyder Græshopperne til at æde Landet op, eller jeg sender Pest i mit Folk,
14 ngati anthu anga, amene amatchedwa ndi dzina langa adzichepetsa ndi kupemphera ndi kufunafuna nkhope yanga, nasiya njira zawo zoyipa, pamenepo Ine ndidzamva kumwamba ndipo ndidzakhululuka tchimo lawo ndi kuchiritsa dziko lawo.
og mit Folk, som mit Navn nævnes over, da ydmyger sig, beder og søger mit Åsyn og vender om fra deres onde Veje, så vil jeg høre det i Himmelen og tilgive deres Synd og læge deres Land,
15 Ndipo maso anga adzatsekuka ndi makutu anga adzakhala tcheru kumva mapemphero a pamalo pano.
Nu skal mine Øjne være åbne og mine Ører lytte til Bønnen, der bedes på dette Sted.
16 Ine ndasankha ndipo ndapatula Nyumba yangayi kotero kuti ndidzakhala mʼmenemo kwamuyaya. Maso ndi mtima wanga zidzakhala pano nthawi zonse.
Og nu har jeg udvalgt og billiget dette Hus, for at mit Navn kan bo der til evig Tid, og mine Øjne og mit Hjerte skal være der alle Dage.
17 “Kunena za iwe, ukayenda pamaso panga mokhulupirika monga momwe anachitira abambo ako Davide, ndi kuchita zonse zimene ndakulamula, ndi kusamalitsa malangizo ndi malamulo anga,
Hvis du nu vandrer for mit Åsyn som din Fader David, så du gør alt, hvad. jeg har pålagt dig, og, holder mine Anordninger og Lovbud,
18 Ine ndidzakhazikitsa mpando wako waufumu, monga ndinachitira pangano ndi abambo ako Davide pamene ndinati, ‘Sipadzasowa munthu wolamulira Israeli.’
så vil jeg opretholde din Kongetrone, som jeg tilsagde din Fader David, da jeg sagde: En Efterfølger skal aldrig fattes dig til at herske over Israel.
19 “Koma ngati iwe udzapatuka ndi kutaya malangizo ndi malamulo amene ndakupatsa ndi kupita kukatumikira milungu ina ndi kuyipembedza,
Men hvis I vender eder bort og forlader mine Anordninger og Bud, som jeg har forelagt eder, og går hen og dyrker fremmede Guder og tilbeder dem,
20 pamenepo Ine ndidzazula Aisraeli mʼdziko langa limene ndinawapatsa, ndiponso ndidzayikana Nyumba ino imene ndadzipatulira. Ndipo udzakhala ngati mwambi ndi chinthu chonyozedwa pakati pa anthu onse.
så vil jeg rykke eder op fra mit Land, som jeg gav eder; og dette Hus, som jeg har belliget for mit Navn, vil jeg forkaste fra mit Åsyn og gøre det til Spot og Spe blandt alle Folk,
21 Ndipo ngakhale kuti tsopano Nyumba ya Mulunguyi ndi yokongola kwambiri, onse amene adzadutsa pano adzadabwa kwambiri ndipo adzati, ‘Nʼchifukwa chiyani Yehova wachita chinthu chotere mʼdziko muno ndi pa Nyumba ya Mulunguyi?’
og dette Hus, som var så ophøjet, over det skal enhver, som kommer der forbi, blive slået af Rædsel. Og når man siger: Hvorfor har HERREN handlet således mod dette Land og dette Hus?
22 Anthu adzayankha kuti, ‘Nʼchifukwa chakuti asiya Yehova, Mulungu wa makolo awo, amene anawatulutsa mʼdziko la Igupto ndipo akangamira milungu ina ndi kumayipembedza ndi kuyitumikira. Choncho Iye wabweretsa zovuta zonsezi.’”
skal der svares: Fordi de forlod HERREN, deres Fædres Gud, som førte dem ud af Ægypten, og holdt sig til andre Guder, tilbad og dyrkede dem; derfor har HERREN bragt al denne Elendighed over dem!"

< 2 Mbiri 7 >