< 2 Mbiri 32 >

1 Zitatha zonse zimene Hezekiya anachita mokhulupirika, Senakeribu mfumu ya ku Asiriya anabwera ndi kuthira nkhondo dziko la Yuda. Iye anazinga mizinda yotetezedwa ya Yuda, kuganiza kuti ayigonjetsa.
Po tych sprawach i pewnem ich postanowieniu przyciągnął Sennacheryb, król Assyryjski, a wtargnąwszy do Judzkiej ziemi, położył się obozem przeciw miastom obronnym, a umyślił je sobie dobyć.
2 Pamene Hezekiya anaona kuti Senakeribu wabwera ndipo wakonzeka kuchita nkhondo ndi Yerusalemu,
A widząc Ezechyjasz, że przyciągnął Sennacheryb, a iż twarz swoję obrócił, aby walczył przeciw Jeruzalemowi:
3 iye anakambirana ndi akuluakulu ake pamodzi ndi atsogoleri a gulu lankhondo za kutseka akasupe ochoka ku kasupe amene anali kunja kwa mzinda, ndipo iwo anamuthandiza.
Tedy wszedł w radę z książętami swymi i z rycerstwem swem, aby zatkali źródła wód, które były za miastem; i pomogli mu.
4 Gulu lalikulu la anthu linasonkhana, ndipo anatseka akasupe onse pamodzi ndi mtsinje umene umayenda mʼkati mwa nthakamo. Iwo ankanena kuti, “Nʼchifukwa chiyani mafumu a Asiriya akabwera kuno adzapeze madzi ambiri?”
Bo zebrawszy się lud wielki zatkali wszystkie źródła, i potok, który płynął przez pośrodek ziemi, mówiąc: Czemużby przyszedłszy królowie Assyryjscy mieli znaleść tak wiele wód?
5 Kenaka iye anagwira ntchito molimbika kukonza madera ogumuka a khoma ndi kumangapo msanja. Anamanganso mpanda wina kunja kwa mpanda winawo ndipo anamanga zolimbitsa Milo ku mzinda wa Davide.
A pokrzepiwszy się, pobudował wszystkie mury obalone, i nabudował wież, przytem zewnątrz drugi mur; i zmocnił Mello w mieście Dawidowem, i poczynił broni bardzo wiele, i tarczy.
6 Iye anasankha atsogoleri a ankhondo olamulira anthu ndipo anawasonkhanitsa pamaso pake pa bwalo la chipata cha mzinda ndi kuwalimbikitsa ndi mawu awa:
Postanowił też hetmanów wojennych nad ludem, których zgromadził do siebie na ulicę bramy miejskiej, i mówił łaskawie do nich, a rzekł:
7 “Khalani amphamvu ndi olimba mtima. Musachite mantha kapena kutaya mtima chifukwa cha mfumu ya ku Asiriya ndi gulu lalikulu lankhondo limene ali nalo, pakuti ife tili ndi mphamvu yayikulu kuposa imene ili ndi iye.
Zmacniajcie się, i mężnie sobie poczynajcie; nie bójcie się, ani się lękajcie twarzy króla Assyryjskiego, ani twarzy wszystkiego mnóstwa, które jest z nim; bo większy jest z nami niżeli z nim.
8 Iye ali ndi mphamvu ya anthu basi, koma ife tili ndi Yehova Mulungu wathu kutithandiza ndi kuchita nkhondo zathu.” Ndipo anthu anapeza chilimbikitso kuchokera pa zimene Hezekiya mfumu ya Yuda ananena.
Z nimi jest ramię cielesne; ale z nami jest Pan, Bóg nasz, aby nas ratował i odprawiał wojny nasze. Tedy spoległ lud na słowach Ezechyjasza, króla Judzkiego.
9 Nthawi ina, pamene Senakeribu mfumu ya ku Asiriya ndi gulu lake lonse lankhondo anali atazinga Lakisi, iye anatumiza atsogoleri ake ankhondo ku Yerusalemu ndi uthenga uwu kwa Hezekiya mfumu ya Yuda ndi anthu onse a ku Yuda amene anali kumeneko:
Potem posłał Sennacheryb, król Assyryjski, sługi swe do Jeruzalemu, (a sam dobywał Lachis, a wszystka moc jego była z nim, ) do Ezechyjasza, króla Judzkiego, i do wszystkich z Judy, którzy byli w Jeruzalemie, mówiąc:
10 “Senakeribu mfumu ya ku Asiriya akuti: Kodi inu mukukhulupirira chiyani, kuti mukukhalabe mu Yerusalemu mutazingidwa?
Tak mówi Sennacheryb, król Assyryjski: W czemże wżdy ufacie, że siedzicie w murach Jeruzalemskich?
11 Pamene Hezekiya akunena kuti ‘Yehova Mulungu wathu adzatipulumutsa kuchoka mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya,’ iye akukusocheretsani, kuti mufe ndi njala ndi ludzu.
Izali Ezechyjasz nie zwodzi was, aby was pomorzył głodem i pragnieniem, mówiąc: Pan, Bóg nasz, wyrwie nas z ręki króla Assyryjskiego?
12 Kodi si Hezekiya amene anachotsa malo opembedzerapo Mulungu ameneyu ndi maguwa ansembe ndi kunena kwa anthu a ku Yuda ndi Yerusalemu kuti, ‘Muzipembedza pa guwa lansembe limodzi ndi kupserezapo nsembe?’
Izali nie ten Ezechyjasz zniósł wyżyny jego, i ołtarze jego, i rozkazał Judzie i Jeruzalemczykom, mówiąc: Przy jednym tylko ołtarzu kłaniać się będziecie, i na nim kadzić?
13 “Kodi inu simukudziwa zimene ine ndi makolo anga tachita kwa anthu a mitundu ina? Kodi milungu ya mitundu imeneyi inatha kupulumutsa dziko lawo kuchoka mʼdzanja langa?
Izali nie wiecie, com uczynił ja i ojcowie moi wszystkim narodom ziemskim? Azaż jakim sposobem mogli bogowie narodów ziemskich wyrwać ziemię swoję z ręki mojej?
14 Kodi ndi milungu iti mwa milungu ya mitundu ina ya anthuwo, imene makolo anga anayiwononga kotheratu, inatha kupulumutsa anthu ake mʼdzanja langa? Nanga tsono Mulungu wanuyo adzakupulumutsani mʼdzanja langa motani?
Któż był ze wszystkich bogów onych narodów, które wytracili ojcowie moi, coby mógł wybawić lud swój z ręki mojej, aby też mógł Bóg wasz wyrwać was z ręki mojej?
15 Choncho inu musalole kuti Hezekiya akunamizeni ndi kukusocheretsani motere. Musamukhulupirire, pakuti palibe mulungu wa mtundu wina uliwonse kapena ufumu wina uliwonse umene unatha kupulumutsa anthu ake kuchoka mʼdzanja langa kapena mʼdzanja la makolo anga. Nanga bwanji Mulungu wanuyo, sadzatha kukupulumutsani kuchoka mʼdzanja langa!”
Przetoż teraz niech was nie zwodzi Ezechyjasz, a niech was na to nie namawia, ani mu wierzcie. Jeźlić nie mógł żaden bóg wszystkich narodów i królestw wyrwać ludu swego z ręki mojej, i z ręki ojców moich, pogotowiu Bóg wasz nie wyrwie was z ręki mojej.
16 Atsogoleri a ankhondo a Senakeribu anapitiriza kuyankhula zotsutsana ndi Yehova Mulungu ndi mtumiki wake Hezekiya.
Nadto jeszcze mówili słudzy jego przeciw Panu Bogu, i przeciwko Ezechyjaszowi słudze jego.
17 Mfumunso inalemba makalata onyoza Yehova, Mulungu wa Israeli, ndipo inanena zotsutsana naye izi: “Monga momwe milungu ya anthu a mayiko ena sinathe kuwapulumutsa kuchoka mʼdzanja langa, chonchonso Mulungu wa Hezekiya sadzapulumutsa anthu ake kuchoka mʼdzanja langa.”
Listy też pisał, urągając Panu, Bogu Izraelskiemu, a mówiąc przeciwko niemu temi słowy: Jako bogowie narodów ziemskich nie wyrwali ludu swego z ręki mojej, tak nie wyrwie Bóg Ezechyjaszowy ludu swego z ręki mojej.
18 Kenaka iwo anafuwula mu Chihebri kwa anthu a mu Yerusalemu amene anali pa khoma, kuwaopseza ndi kuwachititsa mantha ndi cholinga choti alande mzindawo.
I wołali głosem wielkim po żydowsku przeciwko ludowi Jeruzalemskiemu, który był na murach, strasząc go i trwożąc go, aby tak miasto wzięli.
19 Iwo anayankhula za Mulungu wa Yerusalemu monga anayankhulira za milungu ya anthu ena a pa dziko lapansi, ntchito ya manja a anthu.
A mówili przeciw Bogu Jeruzalemskiemu, jako przeciw bogom narodów ziemskich, którzy są robotą rąk ludzkich.
20 Mfumu Hezekiya ndi mneneri Yesaya mwana wa Amozi anafuwulira kumwamba mʼpemphero chifukwa cha zimenezi.
Tedy się modlił Ezechyjasz król, i Izajasz prorok, syn Amosa, dla tego, i krzyczeli ku niebu.
21 Ndipo Yehova anatumiza mngelo amene anadzapha anthu onse odziwa nkhondo ndi atsogoleri ndiponso oyangʼanira misasa ya mfumu ya ku Asiriya. Choncho Senakeribu anabwerera kwawo wamanyazi. Ndipo atalowa mʼnyumba ya mulungu wake, ena mwa ana ake anamupha ndi lupanga.
I posłał Pan Anioła, który wytracił każdego mocarza w wojsku, i wodza, i hetmana w obozie króla Assyryjskiego. I wrócił się z pohańbieniem twarzy do ziemi swojej. A gdy wszedł do domu boga swego, ci, którzy wyszli z żywota jego, tam go zabili mie czem.
22 Kotero Yehova anapulumutsa Hezekiya ndi anthu a ku Yerusalemu kuchoka mʼdzanja la Senakeribu mfumu ya ku Asiriya ndi mʼdzanja la anthu ena. Yehova anawateteza ku mbali zonse.
A tak wybawił Pan Ezechyjasza i obywateli Jeruzalemskich z rąk Sennacheryba, króla Assyryjskiego, i z rąk wszystkich, a sprawił im pokój zewsząd.
23 Anthu ambiri anabweretsa zopereka kwa Yehova ku Yerusalemu ndi mphatso zamtengowapatali kwa Hezekiya mfumu ya Yuda. Kuyambira nthawi imeneyo Hezekiya ankalemekezedwa kwambiri ndi mitundu ina yonse.
Tedy wiele ich przynosiło Panu dary do Jeruzalemu i upominki kosztowne Ezechyjaszowi, królowi Judzkiemu; i wywyższony jest w oczach wszystkich narodów potem.
24 Pa nthawi imeneyo Hezekiya anadwala ndipo anali pafupi kufa. Iye anapemphera kwa Yehova, amene anamuyankha ndi kumupatsa chizindikiro chodabwitsa.
W one dni zachorował Ezechyjasz aż na śmierć, i modlił się Panu; który mówił do niego, a dał mu znak.
25 Koma Hezekiya anali ndi mtima wonyada ndipo sanachite molingana ndi kukoma mtima kumene Mulungu anamuonetsera. Choncho mkwiyo wa Yehova unali pa iye ndi pa Yuda ndi Yerusalemu.
Ale nie według dobrodziejstw sobie uczynionych sprawował się Ezechyjasz, bo się wyniosło serce jego; przetoż powstał przeciw niemu gniew, i przeciw Judzie, i przeciw Jeruzalemowi.
26 Koma kenaka Hezekiya analapa za kunyada kwakeko, monga anachitanso anthu a mu Yerusalemu. Choncho mkwiyo wa Yehova sunafike pa iwo pa nthawi ya Hezekiya.
Ale gdy się upokorzył Ezechyjasz (bo się było wyniosło serce jego) on i obywatele Jeruzalemscy, nie przyszedł na nich gniew Pański za dni Ezechyjaszowych.
27 Hezekiya anali ndi chuma ndi ulemu wambiri ndipo anamanga nyumba zosungiramo chuma cha siliva wake ndi golide ndi za miyala yokongola, zokometsera zakudya, zishango ndi mtundu uliwonse wa zinthu zamtengowapatali.
A miał Ezechyjasz bogactwa i sławę bardzo wielką; bo sobie zebrał skarby srebra i złota, i kamieni drogich, i rzeczy wonnych, i rynsztunku, i wszelakiego naczynia kosztownego.
28 Iye anamanganso nyumba zosungiramo tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta a olivi, ndiponso anamanga nyumba zodyeramo ngʼombe zosiyanasiyana, ndi makola a nkhosa.
Miał też szpichlerze dla urodzajów zboża i wina, i oliwy, i obory dla bydeł, i zwierzyniec dla rozmaitych zwierząt.
29 Iyeyo anamanga midzi ndipo anali ndi nkhosa ndi ngʼombe zambiri, pakuti Mulungu anamupatsa chuma chambiri.
Miasta też sobie pobudował, i miał stada owiec, i wołów mnóstwo; albowiem mu dał Bóg majętność bardzo wielką.
30 Ndi Hezekiya amene anatseka ku mtunda kwa kasupe wa Gihoni, ndi kumuwongolera kuti madzi ake apite mbali ya kumadzulo kwa Mzinda wa Davide. Iye ankachita bwino pa ntchito iliyonse imene ankagwira.
Ten też Ezechyjasz zatkał źródło wód w Gichonie wyższe, a przywiódł je dołem na zachód słońca ku miastu Dawidowemu; i szczęściło się Ezechyjaszowi we wszystkich sprawach jego.
31 Koma pamene nthumwi zotumizidwa ndi atsogoleri a ku Babuloni zinabwera kudzamufunsa za chizindikiro chozizwitsa chimene chinachitika mʼdzikomo, Mulungu anamusiya yekha, kumuyesa kuti adziwe zonse zimene zinali mu mtima mwake.
A wszakże dla posłów książąt Babilońskich, którzy byli posłani do niego, aby go pytali o znak, który się był stał w ziemi, opuścił go Bóg, aby go kusił, a iżby wiedziano wszystko, co było w sercu jego.
32 Zina ndi zina zokhudza ulamuliro wa Hezekiya ndi ntchito za kudzipereka kwake zalembedwa mʼmasomphenya a Yesaya mwana wa Amozi, mʼbuku la mafumu a Yuda ndi Israeli.
Ale inne sprawy Ezechyjaszowe, i dobroczynności jego, napisane są w widzeniu Izajasza proroka, syna Amosowego, i w księgach królów Judzkich i Izraelskich.
33 Hezekiya anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pa phiri pamene pali manda a zidzukulu za Davide. Ayuda onse ndi anthu a mu Yerusalemu anamulemekeza atamwalira. Ndipo Manase mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
I zasnął Ezechyjasz z ojcami swymi, i pogrzebiony jest nad grobami synów Dawidowych. I wyrządzili mu wszystek Juda i obywatele Jeruzalemscy uczciwość przy śmierci jego. A królował Manases, syn jego, miasto niego.

< 2 Mbiri 32 >